< 2 Mbiri 35 >

1 Yosiya anachita chikondwerero cha Paska wa Yehova mu Yerusalemu, ndipo mwana wankhosa wa Paska anaphedwa pa tsiku la khumi ndi chinayi la mwezi woyamba.
Josiah held a Passover for the Lord in Jerusalem, and the Passover lamb was killed on the fourteenth day of the first month.
2 Iye anasankha ansembe pa maudindo awo ndipo anawalimbikitsa pa ntchito ya mʼnyumba ya Yehova.
He assigned the priests to their respective duties and encouraged them in their ministry at the Lord's Temple.
3 Iye anati kwa Alevi amene amalangiza Aisraeli onse omwe anadzipatula kwa Yehova: Ikani bokosi lopatulika mʼNyumba ya Mulungu amene Solomoni mwana wa Davide mfumu ya Israeli anamanga. Lisamanyamulidwe pa mapewa anu. Tsopano tumikirani Yehova Mulungu wanu ndi anthu ake Aisraeli.
Josiah told the Levites who taught all Israel and were holy to the Lord, “Place the holy Ark in the Temple built by Solomon, son of David, king of Israel. It's not necessary for you to carry it around on your shoulders any more. Your responsibility now is to serve the Lord your God and his people Israel.
4 Mukhale mʼmagulu anu molingana ndi mabanja anu, molingana ndi momwe analembera Davide mfumu ya Israeli ndiponso mwana wake Solomoni.
Get yourselves ready for service in your divisions, by families, according to the instructions given by David, king of Israel, and his son Solomon.
5 “Muziyima ku malo opatulika pamodzi ndi gulu la Alevi oyimira gulu lililonse lalingʼono la mabanja a abale anu amene ndi anthu wamba.
Then you are to stand in the sanctuary to assist the lay people according to family divisions, following the assignments according to your Levite family divisions.
6 Muzipha ana ankhosa a Paska, muzidzipatula nokha ndi kuwakonzera abale anu ana ankhosa awo, kuchita zimene Yehova analamulira mwa Mose.”
Sacrifice the Passover lambs, purify yourselves, and be ready to help the people who come to fulfill the requirements given by the Lord through Moses.”
7 Yosiya anapereka kwa anthu wamba onse ana ankhosa ndi ana ambuzi okwanira 30,000 ndi ngʼombe zazimuna 3,000, zopereka za Paska zonse zochokera pa chuma chake cha mfumu.
Josiah contributed as Passover offerings for all the people who were present 30,000 lambs and goats, and 3,000 bulls, all from his own flocks and herds.
8 Akuluakulu akenso anapereka mwaufulu kwa anthu ndi kwa ansembe ndi Alevi. Hilikiya, Zekariya ndi Yehieli oyangʼanira ntchito ya mʼNyumba ya Mulungu anapereka kwa ansembe zopereka za Paska 2,600 ndi ngʼombe 300.
His officials contributed freely to the people, to the priests, and to the Levites. Hilkiah, Zechariah, and Jehiel, who were in charge of God's Temple, gave the priests as Passover offerings 2,600 Passover lambs and 300 bulls.
9 Konaniya nayenso pamodzi ndi Semaya ndi Netaneli, abale ake ndi Hasabiya, Yeiyeli ndi Yozabadi, atsogoleri a Alevi, anapereka nsembe za Paska 5,000 ndi ngʼombe 500 kwa Alevi.
The leaders of the Levites, Conaniah, and Shemaiah and Nethanel his brothers, and Hashabiah and Jeiel and Jozabad, gave the Levites as Passover offerings 5,000 lambs and young goats and 500 bulls.
10 Mwambo unakonzedwa ndipo ansembe anayima pamalo pawo pamodzi ndi Alevi mʼmagulu awo monga mfumu inalamulira.
Once the preparations had been completed, the priests stood where they had been assigned and the Levites took their places in their divisions as the king had ordered.
11 Ana ankhosa a Paska anaphedwa ndipo ansembe anawaza magazi amene anaperekedwa kwa iwo pamene Alevi anali kusenda nyamazo.
They killed the Passover lambs, the priests sprinkled the blood they were given on the altar, while the Levites skinned the sacrifices.
12 Iwo anayika padera nsembe zopsereza kuti azipereke kwa magulu angʼonoangʼono a mabanja a anthu kuti apereke kwa Yehova monga zinalembedwa mʼbuku la Mose. Ndipo anachita chimodzimodzi ndi ngʼombe.
They put to one side the burnt offerings to be given to the families of the lay people, by division, to offer to the Lord, as required in the Book of Moses. They did the same thing with the bulls.
13 Anawotcha nyama za Paska monga momwe zinalembedwera ndi kuwiritsa zopereka zopatulika mʼmiphika, mʼmitsuko ndi mʼziwaya ndipo anazipereka mofulumira kwa anthu onse.
They roasted the Passover sacrifices on the fire as requires, and they boiled the holy offerings in pots, caldrons, and pans, and took them quickly to the lay people.
14 Izi zitatha, anakonza zawo ndi za ansembe chifukwa ansembe, zidzukulu za Aaroni, anali otanganidwa kupereka nsembe zopsereza ndi mafuta a nyama mpaka madzulo. Choncho Alevi amakonza zawo ndi za ansembe, ana a Aaroni.
After that they prepared food from the offerings for themselves and for the priests, because the priests, the descendants of Aaron, were busy presenting burnt offerings and fat until night came. So the Levites did this work for themselves and for the priests, the descendants of Aaron.
15 Anthu oyimba nyimbo, zidzukulu za Asafu, anali pa malo awo potsata zomwe analemba Davide, Asafu, Hemani ndi Yedutuni mlosi wa mfumu. Alonda apazipata anali pa chipata chilichonse ndipo kunali kosafunika kuti achoke pa ntchito yawo, poti abale awo Alevi ankawakonzera zonse.
The singers, the descendants of Asaph, were in their places following the instructions given by David, Asaph, Heman, and Jeduthun, the king's seer. The gatekeepers in charge at each gate did not need to leave, because their fellow Levites provided for them.
16 Kotero pa nthawi imeneyi ntchito yonse ya Yehova ya chikondwerero cha Paska ndi nsembe zopsereza pa guwa la Yehova inachitika monga analamulira mfumu Yosiya.
So on that day the whole Passover service of the Lord was took place, including the presenting of burnt offerings on the altar of the Lord, as King Josiah had ordered.
17 Aisraeli amene analipo anachita chikondwerero cha Paska pa nthawi imeneyi ndi kuchita mwambo wa chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti, kwa masiku asanu ndi awiri.
The Israelites who were there also celebrated Passover at that time, and also the Feast of Unleavened Bread for the following seven days.
18 Paska yofanana ndi iyi sinachitikepo ku Israeli kuyambira nthawi ya Samueli ndipo palibe mmodzi mwa mafumu a Israeli anachitapo chikondwerero cha Paska ngati anachitira Yosiya pamodzi ndi ansembe, Alevi ndi Ayuda onse ndi Aisraeli amene anali pamodzi ndi anthu a mu Yerusalemu.
No Passover like this had been held in Israel since the time of Samuel the prophet. None of the kings of Israel had ever held a Passover like the one that Josiah observed with the priests, the Levites, all of Judah, the Israelites who were there, and the people of Jerusalem.
19 Chikondwerero cha Paska ichi chinachitika mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Yosiya.
This Passover was observed in the eighteenth year of the reign of Josiah.
20 Zimenezi zitachitika, pamene Yosiya anakonzanso Nyumba ya Mulungu, Neko mfumu ya Igupto inapita kukachita nkhondo ku Karikemesi ku mtsinje wa Yufurate, ndipo Yosiya anapita kukamenyana naye.
After all this work that Josiah had carried out in restoring the Temple, King Neco of Egypt was leading his army to fight at Carchemish near the Euphrates, and Josiah went to confront him.
21 Koma Neko anatumiza amithenga kwa iye kunena kuti, “Kodi pali mkangano wanji pakati pa iwe ndi ine, iwe mfumu ya Yuda? Ine sindikuthira nkhondo iwe pa nthawi ino, koma nyumba imene ndili nayo pa nkhondo. Mulungu wandiwuza kuti ndifulumize choncho leka kutsutsana ndi Mulungu amene ali ndi ine, mwina adzakuwononga.”
Neco sent messengers to him, saying, “What argument is there between you and me, king of Judah? I have not come to attack you today, because I'm fighting with another kingdom. God told me I should hurry, so stop obstructing God, who is with me, or he'll destroy you!”
22 Komabe Yosiya sanatembenuke kumusiya iyeyo, koma anadzizimbayitsa ndi kukalowa mʼnkhondo. Iye sanamvere zimene Neko ananena molamulidwa ndi Mulungu koma anapita kukamenyana naye ku chigwa ku Megido.
But Josiah did not turn away and leave. Instead, he disguised himself so he could fight Neco in battle. He ignored Neco's message that came from God, and went to fight him on the Plain of Megiddo.
23 Anthu oponya mivi analasa mfumu Yosiya, ndipo iye anawuza akuluakulu ake, “Chotseni. Ndavulazidwa kwambiri.”
There archers shot King Josiah. He called out those beside him, “Get me out of the battle, because I'm badly wounded!”
24 Choncho anamuchotsa iye mʼgaleta lake, ndipo anamuyika mʼgaleta lina limene anali nalo ndipo anabwera naye ku Yerusalemu kumene anamwalirira. Iye anayikidwa mʼmanda a makolo ake. Ndipo Ayuda ndi Yerusalemu yense anamulira.
So they carried him out of his chariot, and took him back in his second chariot to Jerusalem, where he died. Josiah was buried in the tomb of his forefathers. All Judah and Jerusalem wept for him.
25 Yeremiya anapeka nyimbo za maliro chifukwa cha Yosiya, ndipo mpaka lero lino amuna ndi akazi onse oyimba amakumbukira Yosiya pa nyimbo zawo za maliro. Izi zinakhala mwambo mu Israeli ndipo zinalembedwa mʼNyimbo za Maliro.
Then Jeremiah wrote a lament over Josiah, and to this day male and female choirs sing sad songs about Josiah. They have become a part of what is regularly sung in Israel, and they are recorded in the Book of Laments.
26 Zochitika zina za ulamuliro wa Yosiya ndi ntchito za kudzipereka kwake, monga zinalembedwa mʼMalamulo a Yehova,
The rest of what Josiah did, along with his acts of loyalty following what is written in the Law of the Lord,
27 zochitika zonse, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la mafumu a Israeli ndi Yuda.
all his actions, from beginning to end, are recorded in the Book of the Kings of Israel and Judah.

< 2 Mbiri 35 >