< 2 Mbiri 33 >

1 Manase anali wa zaka khumi ndi ziwiri pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 55.
We dwunastym roku był Manases, gdy królować począł; a pięćdziesiąt i pięć lat królował w Jeruzalemie.
2 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, potsatira machitidwe a mitundu imene Yehova anayithamangitsa pamaso pa Aisraeli.
Ten czynił złe przed oczyma Pańskiemi według obrzydłości onych narodów, które wygnał Pan przed obliczem synów Izraelskich.
3 Iyeyo anamanganso malo opembedzerapo mafano amene Hezekiya abambo ake anawaphwasula; anamanganso maguwa ansembe a Baala ndi kupanga mafano a Asera. Iye amagwadira zolengedwa zonse zamlengalenga ndi kumazipembedza.
Albowiem znowu pobudował wyżyny, które był poburzył Ezechyjasz, ojciec jego; wystawił też i ołtarze Baalom, a nasadził gajów, i kłaniał się wszystkiemu wojsku niebieskiemu, a służył mu,
4 Manase anamanga maguwa mʼNyumba ya Yehova, mʼmene Yehova ananena kuti, “Ine ndidzakhala mu Yerusalemu mpaka muyaya.”
Pobudował też ołtarze w domu Pańskim, o którym powiedział był Pan: W Jeruzalemie będzie imię moje na wieki.
5 Mʼmabwalo onse awiri a Nyumba ya Yehova anamangamo maguwa ansembe a zolengedwa zonse zamlengalenga.
Nadto nabudował ołtarze wszystkiemu wojsku niebieskiemu we dwóch sieniach domu Pańskiego.
6 Iye ankakapereka ana ake aamuna ngati nsembe yopsereza ku chigwa cha Hinomu, ankachita zamatsenga, kuwombeza ndi ufiti, ankakafunsira kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa. Iye anachita zoyipa zambiri pamaso pa Yehova, kumukwiyitsa Iyeyo.
I przewodził synów swych przez ogień w dolinie synów Hennomowych; nadto czasów przestrzegał, i bawił się wieszczbą i czarnoksięstwem, a ustawił czarnoksiężników i guślarzy, i bardzo wiele złego czynił przed oczyma Pańskiemi, draźniąc go.
7 Manase anatenga fano losema limene anapanga ndi kuliyika mʼNyumba ya Mulungu, zimene Mulungu ananena kwa Davide ndi kwa mwana wake Solomoni kuti, “Mʼnyumba ya Mulungu muno, mu Yerusalemu muno, malo amene ndawasankha pakati pa mafuko onse a Israeli, ndidzakhalamo mpaka muyaya.
Postawił także bałwana rytego, którego był uczynił w domu Bożym, o którym był rzekł Bóg do Dawida i do Salomona, syna jego: W domu tym i w Jeruzalemie, którem obrał ze wszystkich pokoleń Izraelskich, położę imię moje na wieki;
8 Ine sindidzachotsanso phazi la Aisraeli kuchoka mʼdziko limene ndawapatsa makolo ako, ngatitu iwowa adzasamalira kuchita chilichonse chimene ndinawalamulira za malamulo onse, malangizo ndi miyambo imene inapatsidwa kudzera mwa Mose.”
A nie dopuszczę się więcej ruszyć nodze Izraela z ziemi, którąm naznaczył ojcom waszym, by jedno strzegli i sprawowali się według wszystkiego, com i rozkazał, według wszystkiego zakonu, i ustaw, i sądów wydanych przez Mojżesza.
9 Koma Manase anasocheretsa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu, kotero anachita zoyipa zambiri kupambana mitundu imene Yehova anayiwononga pamaso pa Aisraeli.
Ale Manases zwiódł Judę i obywateli Jeruzalemskich, tak iż się gorzej sprawowali niż narody, które Pan wygładził przed obliczem synów Izraelskich.
10 Yehova anayankhula kwa Manase ndi anthu ake, koma iwo sanasamaleko.
Bo choć mówił Pan do Manasesa, i do ludu jego, przecież oni nie słuchali.
11 Kotero Yehova anawatumizira atsogoleri a ankhondo a ku Asiriya amene anagwira Manase ukapolo, anayika ngowe mʼmphuno mwake, namumanga ndi zingwe zamkuwa ndi kupita naye ku Babuloni.
Przetoż Pan nawiódł na nich hetmanów wojska króla Assyryjskiego, którzy pojmawszy Manasesa w cierniu, i związawszy go dwoma łańcuchami, zawiedli go do Babilonu.
12 Ali pa mavuto akewo anafunafuna kuti Yehova Mulungu wake amukomere mtima ndipo anadzichepetsa kwakukulu pamaso pa Mulungu wa makolo ake.
Który będąc uciśniony, modlił się Panu, Bogu swemu, i upokorzył się bardzo przed obliczem Boga ojców swoich,
13 Ndipo atapemphera, Yehova anakhudzidwa ndi kupempha kwakeko ndipo anamvera madandawulo ake. Kotero anamubweretsanso ku Yerusalemu ndi ku ufumu wake. Ndipo Manase anadziwa kuti Yehova ndi Mulungu.
I prosił go; a dał mu się uprosić, i wysłuchał modlitwę jego, a przywrócił go do Jeruzalemu na królestwo jego. Tedy poznał Manases, iż sam Pan jest Bogiem.
14 Zitapita izi iye anamanga khoma la kunja kwa Mzinda wa Davide kumadzulo kwa kasupe wa Gihoni ku chigwa mpaka polowera ku Chipata cha Nsomba kuzungulira phiri la Ofeli. Iyeyo anakweza kwambiri khomalo. Anayikanso atsogoleri a nkhondo ku mizinda yonse yotetezedwa ya Yuda.
Potem budował mur około miasta Dawidowego ku zachodniej stronie Gichonu potoku aż do wejścia do bramy rybnej, i otoczył murem Ofel, i wywiódł go bardzo wysoko; postanowił też hetmanów po wszystkich miastach obronnych w Judzie.
15 Iye anachotsa milungu yonse yachilendo ndi fano mʼNyumba ya Yehova komanso maguwa ansembe onse amene anamanga pa phiri la Nyumba ya Mulungu ndi mu Yerusalemu, nazitayira kunja kwa mzinda.
Zniósł też bogów cudzych, i bałwana z domu Pańskiego, i wszystkie ołtarze, które był pobudował na górze domu Pańskiego, i w Jeruzalemie, i wyrzucił za miasto.
16 Kenaka anabwezeretsa guwa lansembe la Yehova ndi kupereka zopereka zachiyanjano ndiponso zopereka zamatamando ndipo anawuza Yuda kuti atumikire Yehova Mulungu wa Israeli.
Zatem naprawił ołtarz Pański, i sprawował na nim ofiary spokojne, i dziękczynienia, a przykazał Judzie, aby służyli Panu, Bogu Izraelskiemu.
17 Komabe anthu anapitiriza kupereka nsembe ku malo achipembedzo, koma kwa Yehova, Mulungu wawo yekha.
Wszakże jeszcze lud ofiarował na wyżynach, lecz tylko Panu, Bogu swemu.
18 Zina ndi zina zokhudza ulamuliro wa Manase, kuphatikiza mapemphero ake kwa Mulungu wake ndi mawu amene alosi anayankhula kwa iye mʼdzina la Yehova Mulungu wa Israeli, zalembedwa mʼmabuku a mafumu a Israeli.
Ale inne sprawy Manasesowe, i modlitwa jego do Boga jego, i słowa widzących, którzy mawiali do niego w imię Pana, Boga Izraelskiego, są w księgach spraw królów Izraelskich.
19 Pemphero lake ndi momwe Mulungu anakhudzidwira ndi kupempha kwakeko, pamodzinso ndi machimo ake onse ndi kusakhulupirika kwake, ndiponso malo onse amene anamanga, malo azipembedzo ndi mafano a Asera ndi mafano asanadzichepetse, zonse zalembedwa mʼmbiri ya alosi.
Modlitwa zaś jego, i jako jest wysłuchany, i każdy grzech jego, i przestępstwo jego, i miejsca, na których był pobudował wyżyny, i wystawił gaje święcone, i bałwany, przedtem niż się był upokorzył, zapisane w księgach Chozaja.
20 Manase anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mʼnyumba yake yaufumu. Ndipo Amoni mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Potem zasnął Manases z ojcami swymi, i pochowali go w domu jego; a Amon, syn jego, królował miasto niego.
21 Amoni anali wa zaka 22 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka ziwiri.
We dwudziestu i dwóch latach był Amon, gdy królować począł, a dwa lata królował w Jeruzalemie.
22 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga anachitira Manase abambo ake. Amoni analambira ndi kupereka nsembe kwa mafano onse amene anapanga Manase.
I czynił złe przed oczyma Pańskiemi, jako czynił Manases, ojciec jego; albowiem wszystkim bałwanom, których był naczynił Manases, ojciec jego, ofiarował Amon, i służył im.
23 Koma kusiyana ndi abambo ake Manase, iye sanadzichepetse pamaso pa Yehova. Amoni anawonjeza kulakwa kwake.
A nie upokorzył się przed obliczem Pańskiem, jako się upokorzył Manases, ojciec jego; owszem ten Amon daleko więcej grzeszył.
24 Akuluakulu a Amoni anamuchita chiwembu ndipo anamupha mʼnyumba yake yaufumu.
I sprzysięgli się przeciw niemu słudzy jego, i zabili go w domu jego.
25 Koma anthu a mʼdzikomo anapha onse amene anakonzera chiwembu mfumu Amoni, ndipo anayika mwana wake Yosiya kukhala mfumu mʼmalo mwake.
Ale lud onej ziemi pobił wszystkich, co się byli sprzysięgli przeciw królowi Amonowi; a postanowił lud ziemi królem Jozjasza, syna jego, miasto niego.

< 2 Mbiri 33 >