< 2 Mbiri 33 >

1 Manase anali wa zaka khumi ndi ziwiri pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 55.
UManase waba yinkosi eleminyaka elitshumi lambili ubudala njalo wabusa eJerusalema okweminyaka engamatshumi amahlanu lanhlanu.
2 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, potsatira machitidwe a mitundu imene Yehova anayithamangitsa pamaso pa Aisraeli.
Wenza ububi emehlweni kaThixo, elandela imikhuba eyenyanyekayo yezizwe uThixo ayezixotshile phambi kuka-Israyeli.
3 Iyeyo anamanganso malo opembedzerapo mafano amene Hezekiya abambo ake anawaphwasula; anamanganso maguwa ansembe a Baala ndi kupanga mafano a Asera. Iye amagwadira zolengedwa zonse zamlengalenga ndi kumazipembedza.
Wavuselela izindawo zokukhonzela ezazibhidlizwe nguyise uHezekhiya; waphinda wakhela oBhali ama-alithare kanye lezinsika zika-Ashera. Wakhothamela zonke izinkanyezi zezulu wazikhonza.
4 Manase anamanga maguwa mʼNyumba ya Yehova, mʼmene Yehova ananena kuti, “Ine ndidzakhala mu Yerusalemu mpaka muyaya.”
Wakha ama-alithare ethempelini likaThixo, lona uThixo ayekhulume ngalo wathi: “IBizo lami lizahlala eJerusalema kuze kube nininini.”
5 Mʼmabwalo onse awiri a Nyumba ya Yehova anamangamo maguwa ansembe a zolengedwa zonse zamlengalenga.
Emagumeni womabili ethempeli likaThixo wakhela izinkanyezi zezulu ama-alithare.
6 Iye ankakapereka ana ake aamuna ngati nsembe yopsereza ku chigwa cha Hinomu, ankachita zamatsenga, kuwombeza ndi ufiti, ankakafunsira kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa. Iye anachita zoyipa zambiri pamaso pa Yehova, kumukwiyitsa Iyeyo.
Wanikela amadodana akhe emlilweni eSigodini saseBheni-Hinomu, wenza imilingo, ukuvumisa, lokuthakatha njalo wayahlahlula lakwabalamadlozi. Wenza okubi kakhulu phambi kukaThixo, wamthukuthelisa.
7 Manase anatenga fano losema limene anapanga ndi kuliyika mʼNyumba ya Mulungu, zimene Mulungu ananena kwa Davide ndi kwa mwana wake Solomoni kuti, “Mʼnyumba ya Mulungu muno, mu Yerusalemu muno, malo amene ndawasankha pakati pa mafuko onse a Israeli, ndidzakhalamo mpaka muyaya.
Wathatha isithombe ayesibazile wasibeka ethempelini likaNkulunkulu, lelo uNkulunkulu ayethe kuDavida lasendodaneni yakhe uSolomoni, “Kulelithempeli kanye laseJerusalema, engilikhethileyo ezizwaneni zako-Israyeli, ngizafaka iBizo lami kuze kube nininini.
8 Ine sindidzachotsanso phazi la Aisraeli kuchoka mʼdziko limene ndawapatsa makolo ako, ngatitu iwowa adzasamalira kuchita chilichonse chimene ndinawalamulira za malamulo onse, malangizo ndi miyambo imene inapatsidwa kudzera mwa Mose.”
Angiyikuyekela inyawo zabako-Israyeli zisuke kulelilizwe engalabela okhokho babo, nxa bezananzelela benze konke engabalaya ngakho okwemithetho, izimiso leziqondiso ezaphiwa uMosi.”
9 Koma Manase anasocheretsa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu, kotero anachita zoyipa zambiri kupambana mitundu imene Yehova anayiwononga pamaso pa Aisraeli.
Kodwa uManase wakhokhelela abakoJuda labaseJerusalema ekulahlekeni, benza ububi okwedlula izizwe uThixo azibhubhisa mandulo kokufika kwabako-Israyeli.
10 Yehova anayankhula kwa Manase ndi anthu ake, koma iwo sanasamaleko.
UThixo wakhuluma kuManase labantu bakhe, kodwa kabalalelanga.
11 Kotero Yehova anawatumizira atsogoleri a ankhondo a ku Asiriya amene anagwira Manase ukapolo, anayika ngowe mʼmphuno mwake, namumanga ndi zingwe zamkuwa ndi kupita naye ku Babuloni.
Ngakho uThixo wabehlisela abalawuli bamabutho enkosi yase-Asiriya, abathumba uManase, bamfaka umkhala emakhaleni, bambopha ngamaketane ethusi bamusa eBhabhiloni.
12 Ali pa mavuto akewo anafunafuna kuti Yehova Mulungu wake amukomere mtima ndipo anadzichepetsa kwakukulu pamaso pa Mulungu wa makolo ake.
Ekuhlulukelweni kwakhe wacela umusa kaThixo uNkulunkulu waboyise.
13 Ndipo atapemphera, Yehova anakhudzidwa ndi kupempha kwakeko ndipo anamvera madandawulo ake. Kotero anamubweretsanso ku Yerusalemu ndi ku ufumu wake. Ndipo Manase anadziwa kuti Yehova ndi Mulungu.
Ngakho uthe esekhuleka kuThixo, wezwa ukuncenga kwakhe walalela isicelo sakhe; wambuyisela eJerusalema ebukhosini bakhe. Ngalokho uManase wakwazi ukuthi uThixo unguNkulunkulu.
14 Zitapita izi iye anamanga khoma la kunja kwa Mzinda wa Davide kumadzulo kwa kasupe wa Gihoni ku chigwa mpaka polowera ku Chipata cha Nsomba kuzungulira phiri la Ofeli. Iyeyo anakweza kwambiri khomalo. Anayikanso atsogoleri a nkhondo ku mizinda yonse yotetezedwa ya Yuda.
Ngemva kwalokho wakha kutsha umduli wangaphandle owoMuzi kaDavida, entshonalanga kwentombo yesigodini seGihoni, kusiya emangenelweni eSango leNhlanzi kubhoda uqaqa lwe-Ofeli; njalo wawakha waba mude kulakuqala. Wafaka abalawuli bamabutho kuwo wonke amadolobho alezinqaba koJuda.
15 Iye anachotsa milungu yonse yachilendo ndi fano mʼNyumba ya Yehova komanso maguwa ansembe onse amene anamanga pa phiri la Nyumba ya Mulungu ndi mu Yerusalemu, nazitayira kunja kwa mzinda.
Wasusa bonke onkulunkulu bezizweni wasusa lesithombe ethempelini likaThixo, lawo wonke ama-alithare ayewakhele eqaqeni lwethempeli kanye laseJerusalema; konke lokhu wakulahlela ngaphandle kwedolobho.
16 Kenaka anabwezeretsa guwa lansembe la Yehova ndi kupereka zopereka zachiyanjano ndiponso zopereka zamatamando ndipo anawuza Yuda kuti atumikire Yehova Mulungu wa Israeli.
Wavuselela i-alithari likaThixo wenza iminikelo yobudlelwano leminikelo yokubonga phezu kwalo njalo watshela uJuda ukumkhonza uThixo, uNkulunkulu ka-Israyeli.
17 Komabe anthu anapitiriza kupereka nsembe ku malo achipembedzo, koma kwa Yehova, Mulungu wawo yekha.
Kodwa abantu baqhubeka benikela imihlatshelo ezindaweni zokukhonzela, kodwa benikela kuphela kuThixo uNkulunkulu wabo.
18 Zina ndi zina zokhudza ulamuliro wa Manase, kuphatikiza mapemphero ake kwa Mulungu wake ndi mawu amene alosi anayankhula kwa iye mʼdzina la Yehova Mulungu wa Israeli, zalembedwa mʼmabuku a mafumu a Israeli.
Ezinye izehlakalo ngombuso kaManase, kanye lomkhuleko wakhe kuNkulunkulu wakhe lamazwi akhulunywa ngababoni kuye ngebizo likaThixo, uNkulunkulu ka-Israyeli, kulotshiwe embalini yamakhosi ako-Israyeli.
19 Pemphero lake ndi momwe Mulungu anakhudzidwira ndi kupempha kwakeko, pamodzinso ndi machimo ake onse ndi kusakhulupirika kwake, ndiponso malo onse amene anamanga, malo azipembedzo ndi mafano a Asera ndi mafano asanadzichepetse, zonse zalembedwa mʼmbiri ya alosi.
Umkhuleko wakhe lokuthi uNkulunkulu wakwamukela njani ukuncenga kwakhe, lokona kwakhe konke, kanye lokungathembeki, lalezozindawo zokukhonzela ayezakhile lezinsika zika-Ashera lezithombe engakazehlisi ngokuzithoba, kulotshiwe konke emibhalweni yababoni.
20 Manase anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mʼnyumba yake yaufumu. Ndipo Amoni mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
UManase waphumula labokhokho bakhe wangcwatshwa esigodlweni sakhe. U-Amoni indodana yakhe yathatha isikhundla sakhe.
21 Amoni anali wa zaka 22 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka ziwiri.
U-Amoni wayeleminyaka engamatshumi amabili lambili ubudala esiba yinkosi, njalo wabusa eJerusalema okweminyaka emibili.
22 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga anachitira Manase abambo ake. Amoni analambira ndi kupereka nsembe kwa mafano onse amene anapanga Manase.
Wenza ububi phambi kukaThixo, njengalokhu okwakwenziwe nguyise uManase. U-Amoni wakhonza njalo wanikela imihlatshelo kuzozonke izithombe ezazenziwe nguManase.
23 Koma kusiyana ndi abambo ake Manase, iye sanadzichepetse pamaso pa Yehova. Amoni anawonjeza kulakwa kwake.
Kodwa kenzanga njengoyise uManase, ngoba yena kazehlisanga phansi kukaThixo; u-Amoni wenza amacala ngokuphindiweyo.
24 Akuluakulu a Amoni anamuchita chiwembu ndipo anamupha mʼnyumba yake yaufumu.
Izikhulu zika-Amoni zathama icebo zambulalela esigodlweni sakhe.
25 Koma anthu a mʼdzikomo anapha onse amene anakonzera chiwembu mfumu Amoni, ndipo anayika mwana wake Yosiya kukhala mfumu mʼmalo mwake.
Kodwa abantu belizwe babulala bonke labo ababethame amacebo ngenkosi u-Amoni, babeka uJosiya indodana yakhe wathatha ubukhosi.

< 2 Mbiri 33 >