< 2 Mbiri 33 >

1 Manase anali wa zaka khumi ndi ziwiri pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 55.
Manassé avait douze ans quand il commença à régner, et il régna cinquante-cinq ans à Jérusalem.
2 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, potsatira machitidwe a mitundu imene Yehova anayithamangitsa pamaso pa Aisraeli.
Or il fit le mal devant le Seigneur, suivant les abominations des nations que le Seigneur avait détruites devant les enfants d’Israël.
3 Iyeyo anamanganso malo opembedzerapo mafano amene Hezekiya abambo ake anawaphwasula; anamanganso maguwa ansembe a Baala ndi kupanga mafano a Asera. Iye amagwadira zolengedwa zonse zamlengalenga ndi kumazipembedza.
Et il en revint à restaurer les hauts lieux qu’avait démolis Ezéchias, son père; il construisit des autels aux Baalim, il fit des bois sacrés, et il adora toute la milice du ciel, et la servit.
4 Manase anamanga maguwa mʼNyumba ya Yehova, mʼmene Yehova ananena kuti, “Ine ndidzakhala mu Yerusalemu mpaka muyaya.”
Il bâtit aussi des autels dans la maison du Seigneur, de laquelle le Seigneur avait dit: C’est dans Jérusalem que sera mon nom éternellement.
5 Mʼmabwalo onse awiri a Nyumba ya Yehova anamangamo maguwa ansembe a zolengedwa zonse zamlengalenga.
Or il les bâtit à toute l’armée du ciel, dans les deux parvis du temple du Seigneur.
6 Iye ankakapereka ana ake aamuna ngati nsembe yopsereza ku chigwa cha Hinomu, ankachita zamatsenga, kuwombeza ndi ufiti, ankakafunsira kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa. Iye anachita zoyipa zambiri pamaso pa Yehova, kumukwiyitsa Iyeyo.
Et il fit passer ses fils par le feu dans la vallée de Bénennom: il observait les songes, il suivait les augures, il s’adonnait à l’art magique, il avait avec lui des magiciens et des enchanteurs, et il commit de grand maux devant le Seigneur, jusqu’à l’irriter.
7 Manase anatenga fano losema limene anapanga ndi kuliyika mʼNyumba ya Mulungu, zimene Mulungu ananena kwa Davide ndi kwa mwana wake Solomoni kuti, “Mʼnyumba ya Mulungu muno, mu Yerusalemu muno, malo amene ndawasankha pakati pa mafuko onse a Israeli, ndidzakhalamo mpaka muyaya.
Il mit aussi une image taillée au ciseau et une statue de fonte dans la maison du Seigneur, de laquelle Dieu avait dit à David et à Salomon, son fils: C’est dans cette maison et dans Jérusalem, que j’ai choisie d’entre toutes les tribus d’Israël, que j’établirai mon nom pour jamais.
8 Ine sindidzachotsanso phazi la Aisraeli kuchoka mʼdziko limene ndawapatsa makolo ako, ngatitu iwowa adzasamalira kuchita chilichonse chimene ndinawalamulira za malamulo onse, malangizo ndi miyambo imene inapatsidwa kudzera mwa Mose.”
Et je ne ferai pas mouvoir le pied d’Israël de la terre que j’ai livrée à leurs pères, pourvu seulement qu’ils aient soin d’accomplir ce que je leur ai ordonné, toute la loi, les cérémonies et les ordonnances, que je leur ai données par l’entremise de Moïse.
9 Koma Manase anasocheretsa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu, kotero anachita zoyipa zambiri kupambana mitundu imene Yehova anayiwononga pamaso pa Aisraeli.
Manassé séduisit donc Juda et les habitants de Jérusalem, en sorte qu’ils firent plus de mal que toutes les autres nations que le Seigneur avait exterminées de la face des enfants d’Israël.
10 Yehova anayankhula kwa Manase ndi anthu ake, koma iwo sanasamaleko.
Et Dieu lui parla, à lui et à son peuple, et ils ne voulurent point faire attention.
11 Kotero Yehova anawatumizira atsogoleri a ankhondo a ku Asiriya amene anagwira Manase ukapolo, anayika ngowe mʼmphuno mwake, namumanga ndi zingwe zamkuwa ndi kupita naye ku Babuloni.
C’est pourquoi Dieu amena sur eux les princes de l’armée du roi des Assyriens; ils prirent donc Manassé, et après l’avoir lié de chaînes et lui avoir mis des entraves, ils l’emmenèrent à Babylone.
12 Ali pa mavuto akewo anafunafuna kuti Yehova Mulungu wake amukomere mtima ndipo anadzichepetsa kwakukulu pamaso pa Mulungu wa makolo ake.
Lorsque Manassé se trouva dans cette détresse, il pria le Seigneur son Dieu, et fit beaucoup pénitence devant le Dieu de ses pères.
13 Ndipo atapemphera, Yehova anakhudzidwa ndi kupempha kwakeko ndipo anamvera madandawulo ake. Kotero anamubweretsanso ku Yerusalemu ndi ku ufumu wake. Ndipo Manase anadziwa kuti Yehova ndi Mulungu.
Et il l’implora, et le supplia avec instance; et le Seigneur exauça sa prière, et le ramena à Jérusalem dans son royaume; et Manassé reconnut que le Seigneur était le vrai Dieu.
14 Zitapita izi iye anamanga khoma la kunja kwa Mzinda wa Davide kumadzulo kwa kasupe wa Gihoni ku chigwa mpaka polowera ku Chipata cha Nsomba kuzungulira phiri la Ofeli. Iyeyo anakweza kwambiri khomalo. Anayikanso atsogoleri a nkhondo ku mizinda yonse yotetezedwa ya Yuda.
Après cela, il bâtit un mur hors de la cité de David, à l’occident de Gihon, dans la vallée, depuis l’entrée de la porte des Poissons, à travers l’enceinte, jusqu’à Ophel, et il l’éleva très haut: il établit aussi des princes de l’armée dans toutes les villes de Juda fortifiées;
15 Iye anachotsa milungu yonse yachilendo ndi fano mʼNyumba ya Yehova komanso maguwa ansembe onse amene anamanga pa phiri la Nyumba ya Mulungu ndi mu Yerusalemu, nazitayira kunja kwa mzinda.
Et il enleva les dieux étrangers et le simulacre de la maison du Seigneur, comme aussi les autels qu’il avait faits sur la montagne de la maison du Seigneur et dans Jérusalem, et il jeta tout hors de la ville.
16 Kenaka anabwezeretsa guwa lansembe la Yehova ndi kupereka zopereka zachiyanjano ndiponso zopereka zamatamando ndipo anawuza Yuda kuti atumikire Yehova Mulungu wa Israeli.
De plus il restaura l’autel du Seigneur, et il immola dessus des victimes et des hosties pacifiques et de louange; et il ordonna à Juda de servir le Seigneur Dieu d’Israël.
17 Komabe anthu anapitiriza kupereka nsembe ku malo achipembedzo, koma kwa Yehova, Mulungu wawo yekha.
Cependant le peuple immolait encore sur les hauts lieux au Seigneur son Dieu.
18 Zina ndi zina zokhudza ulamuliro wa Manase, kuphatikiza mapemphero ake kwa Mulungu wake ndi mawu amene alosi anayankhula kwa iye mʼdzina la Yehova Mulungu wa Israeli, zalembedwa mʼmabuku a mafumu a Israeli.
Mais le reste des faits de Manassé, sa supplication à son Dieu, et les paroles des Voyants qui lui parlaient au nom du Seigneur Dieu d’Israël, sont contenus dans le Livre des actions des rois d’Israël;
19 Pemphero lake ndi momwe Mulungu anakhudzidwira ndi kupempha kwakeko, pamodzinso ndi machimo ake onse ndi kusakhulupirika kwake, ndiponso malo onse amene anamanga, malo azipembedzo ndi mafano a Asera ndi mafano asanadzichepetse, zonse zalembedwa mʼmbiri ya alosi.
De plus, sa prière à Dieu, et la manière dont il fut exaucé, tous ses péchés, le mépris de Dieu, comme aussi les endroits dans lesquels il bâtit des hauts lieux, et fit des bois sacrés et des statues, avant qu’il fît pénitence, sont écrits parmi les paroles d’Hozaï.
20 Manase anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mʼnyumba yake yaufumu. Ndipo Amoni mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Manassé dormit donc avec ses pères, et on l’ensevelit dans sa maison; et son fils Amon régna en sa place.
21 Amoni anali wa zaka 22 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka ziwiri.
Amon avait vingt-deux ans lorsqu’il commença à régner, et il régna deux ans dans Jérusalem.
22 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga anachitira Manase abambo ake. Amoni analambira ndi kupereka nsembe kwa mafano onse amene anapanga Manase.
Et il fit le mal en la présence du Seigneur, comme avait fait Manassé son père, et il sacrifia à toutes les idoles que Manassé avait fabriquées, et il les servit.
23 Koma kusiyana ndi abambo ake Manase, iye sanadzichepetse pamaso pa Yehova. Amoni anawonjeza kulakwa kwake.
Et il ne révéra point la face du Seigneur, comme la révéra Manassé son père, et il commit des crimes beaucoup plus grands.
24 Akuluakulu a Amoni anamuchita chiwembu ndipo anamupha mʼnyumba yake yaufumu.
Or ses serviteurs, ayant conspiré contre lui, le tuèrent dans sa maison.
25 Koma anthu a mʼdzikomo anapha onse amene anakonzera chiwembu mfumu Amoni, ndipo anayika mwana wake Yosiya kukhala mfumu mʼmalo mwake.
Mais le reste du peuple, après avoir taillé en pièces ceux qui avaient tué Amon, établit roi Josias, son fils, en sa place.

< 2 Mbiri 33 >