< 2 Mbiri 33 >

1 Manase anali wa zaka khumi ndi ziwiri pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 55.
Manasse var tolv År gammel, da han blev Konge, og han herskede fem og halvtredsindstyve År i Jerusalem.
2 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, potsatira machitidwe a mitundu imene Yehova anayithamangitsa pamaso pa Aisraeli.
Han gjorde, hvad der var ondt i HERRENs Øjne, og efterlignede de Folkeslags Vederstyggeligheder, som HERREN havde drevet bort foran Israeliterne.
3 Iyeyo anamanganso malo opembedzerapo mafano amene Hezekiya abambo ake anawaphwasula; anamanganso maguwa ansembe a Baala ndi kupanga mafano a Asera. Iye amagwadira zolengedwa zonse zamlengalenga ndi kumazipembedza.
Han byggede atter de Offerhøje, som hans Fader Ezekias havde nedrevet, rejste Altre for Ba'alerne, lavede Asjerastøtter og tilbad hele Himmelens Hær og dyrkede dem.
4 Manase anamanga maguwa mʼNyumba ya Yehova, mʼmene Yehova ananena kuti, “Ine ndidzakhala mu Yerusalemu mpaka muyaya.”
Og han byggede Altre i HERRENs Hus, om hvilket HERREN havde sagt: "I Jerusalem skal mit Navn være til evig Tid."
5 Mʼmabwalo onse awiri a Nyumba ya Yehova anamangamo maguwa ansembe a zolengedwa zonse zamlengalenga.
Og han byggede Altre for hele Himmelens Hær i begge HERRENs Hus's Forgårde.
6 Iye ankakapereka ana ake aamuna ngati nsembe yopsereza ku chigwa cha Hinomu, ankachita zamatsenga, kuwombeza ndi ufiti, ankakafunsira kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa. Iye anachita zoyipa zambiri pamaso pa Yehova, kumukwiyitsa Iyeyo.
Han lod sine Sønner gå igennem Ilden i Hinnoms Søns Dal, drev Trolddom og tog Varsler, drev hemmelige Kunster og ansatte Dødemanere og Sandsigere; han gjorde meget, som var ondt i HERRENs Øjne, og krænkede ham.
7 Manase anatenga fano losema limene anapanga ndi kuliyika mʼNyumba ya Mulungu, zimene Mulungu ananena kwa Davide ndi kwa mwana wake Solomoni kuti, “Mʼnyumba ya Mulungu muno, mu Yerusalemu muno, malo amene ndawasankha pakati pa mafuko onse a Israeli, ndidzakhalamo mpaka muyaya.
Det Gudebillede, han lod lave, opstillede han i Guds Hus, om hvilket Gud havde sagt til David og hans Søn Salomo: "I dette Hus og i Jerusalem, som jeg har udvalgt af alle Israels Stammer, vil jeg stedfæste mit Navn til evig Tid;
8 Ine sindidzachotsanso phazi la Aisraeli kuchoka mʼdziko limene ndawapatsa makolo ako, ngatitu iwowa adzasamalira kuchita chilichonse chimene ndinawalamulira za malamulo onse, malangizo ndi miyambo imene inapatsidwa kudzera mwa Mose.”
og jeg vil ikke mere fjerne Israels Fod fra det Land, jeg gav deres Fædre, dog kun på det Vilkår, at de omhyggeligt overholder alt, hvad jeg har pålagt dem, hele Loven, Anordningerne og Lovbudene, som de fik ved Moses,"
9 Koma Manase anasocheretsa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu, kotero anachita zoyipa zambiri kupambana mitundu imene Yehova anayiwononga pamaso pa Aisraeli.
Men Manasse forførte Juda og Jerusalems Indbyggere til at handle værre end de Folkeslag, HERREN havde udryddet for Israeliterne.
10 Yehova anayankhula kwa Manase ndi anthu ake, koma iwo sanasamaleko.
Da talede HERREN Manasse og hans Folk til, men de ænsede det ikke.
11 Kotero Yehova anawatumizira atsogoleri a ankhondo a ku Asiriya amene anagwira Manase ukapolo, anayika ngowe mʼmphuno mwake, namumanga ndi zingwe zamkuwa ndi kupita naye ku Babuloni.
Så førte HERREN Assyrerkongens Hærførere mod dem, og de fangede Manasse med Kroge, lagde ham i Kobberlænker og førte ham til Babel.
12 Ali pa mavuto akewo anafunafuna kuti Yehova Mulungu wake amukomere mtima ndipo anadzichepetsa kwakukulu pamaso pa Mulungu wa makolo ake.
Men da han var i Nød, bad han HERREN sin Gud om Nåde og ydmygede sig dybt for sine Fædres Gud.
13 Ndipo atapemphera, Yehova anakhudzidwa ndi kupempha kwakeko ndipo anamvera madandawulo ake. Kotero anamubweretsanso ku Yerusalemu ndi ku ufumu wake. Ndipo Manase anadziwa kuti Yehova ndi Mulungu.
Og da han bad til ham, bønhørte han ham; han hørte hans Bøn og bragte ham tilbage til Jerusalem til hans Kongedømme; da indså Manasse, at HERREN er Gud.
14 Zitapita izi iye anamanga khoma la kunja kwa Mzinda wa Davide kumadzulo kwa kasupe wa Gihoni ku chigwa mpaka polowera ku Chipata cha Nsomba kuzungulira phiri la Ofeli. Iyeyo anakweza kwambiri khomalo. Anayikanso atsogoleri a nkhondo ku mizinda yonse yotetezedwa ya Yuda.
Senere byggede han en ydre Mur ved Davidsbyen vesten for Gihon i Dalen og hen imod Fiskeporten, så at den omsluttede Ofel; og han byggede den meget høj. I alle de befæstede Byer i Juda ansatte han Hærførere.
15 Iye anachotsa milungu yonse yachilendo ndi fano mʼNyumba ya Yehova komanso maguwa ansembe onse amene anamanga pa phiri la Nyumba ya Mulungu ndi mu Yerusalemu, nazitayira kunja kwa mzinda.
Han fjernede de fremmede Guder og Gudebilledet fra HERRENs Hus og alle de Altre, han havde bygget på Tempelbjerget og i Jerusalem, og kastede dem uden for Byen.
16 Kenaka anabwezeretsa guwa lansembe la Yehova ndi kupereka zopereka zachiyanjano ndiponso zopereka zamatamando ndipo anawuza Yuda kuti atumikire Yehova Mulungu wa Israeli.
Og han istandsatte HERRENs Alter og ofrede Tak- og Lovprisningsofre derpå; og han bød Juda at dyrke HERREN, Israels Gud.
17 Komabe anthu anapitiriza kupereka nsembe ku malo achipembedzo, koma kwa Yehova, Mulungu wawo yekha.
Men Folket vedblev at ofre på Offerhøjene, dog kun til HERREN deres Gutd.
18 Zina ndi zina zokhudza ulamuliro wa Manase, kuphatikiza mapemphero ake kwa Mulungu wake ndi mawu amene alosi anayankhula kwa iye mʼdzina la Yehova Mulungu wa Israeli, zalembedwa mʼmabuku a mafumu a Israeli.
Hvad der ellers er at fortælle om Manasse, hans Bøn til sin Gud og de Seeres Ord, som talte til ham i HERRENs, Israels Guds, Navn, står jo optegnet i Israels Kongers Krønike;
19 Pemphero lake ndi momwe Mulungu anakhudzidwira ndi kupempha kwakeko, pamodzinso ndi machimo ake onse ndi kusakhulupirika kwake, ndiponso malo onse amene anamanga, malo azipembedzo ndi mafano a Asera ndi mafano asanadzichepetse, zonse zalembedwa mʼmbiri ya alosi.
hans Bøn og Bønhørelse, al hans Synd og Troløshed og de Steder, hvor han opførte Offerhøje og opstillede Asjerastøtter og Gudebilleder, før han ydmygede sig, står jo optegnet i Seernes Krønike.
20 Manase anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mʼnyumba yake yaufumu. Ndipo Amoni mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Så lagde Manasse sig til Hvile hos sine Fædre, og man jordede ham i Haven ved hans Hus; og hans Søn Amon blev Konge i hans Sted.
21 Amoni anali wa zaka 22 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka ziwiri.
Amon var to og tyve År gammel, da han blev Konge, og han hersltede to År i Jerusalem.
22 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga anachitira Manase abambo ake. Amoni analambira ndi kupereka nsembe kwa mafano onse amene anapanga Manase.
Han gjorde, hvad der var ondt i HERRENs Øjne, ligesom hans Fader Manasse, og Amon ofrede til alle de Gudebilleder, hans Fader Manasse havde ladet lave, og dyrkede dem.
23 Koma kusiyana ndi abambo ake Manase, iye sanadzichepetse pamaso pa Yehova. Amoni anawonjeza kulakwa kwake.
Han ydmygede sig ikke for HERRENs Åsyn, som hans Fader Manasse havde gjort, men Amon dyngede Skyld på Skyld.
24 Akuluakulu a Amoni anamuchita chiwembu ndipo anamupha mʼnyumba yake yaufumu.
Hans Tjenere sammensvor sig imod ham og dræbte ham i hans Hus;
25 Koma anthu a mʼdzikomo anapha onse amene anakonzera chiwembu mfumu Amoni, ndipo anayika mwana wake Yosiya kukhala mfumu mʼmalo mwake.
men Folket fra Landet dræbte alle dem, der havde sammensvoret sig imod Kong Amon, og gjorde hans Søn Josias til Konge i hans Sted.

< 2 Mbiri 33 >