< 2 Mbiri 33 >

1 Manase anali wa zaka khumi ndi ziwiri pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 55.
Manasseh leng ahung chanchun kum 12 bep anahin aman Jerusalem mah kum 55 geijin vai ana hommin ahi
2 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, potsatira machitidwe a mitundu imene Yehova anayithamangitsa pamaso pa Aisraeli.
Amahin Pakaiyin Israel chate masanga anano doh namdangho chonna kidah umtah ho chonna chu anache pi in Pakai mitmun thilse ngen abollin ahi
3 Iyeyo anamanganso malo opembedzerapo mafano amene Hezekiya abambo ake anawaphwasula; anamanganso maguwa ansembe a Baala ndi kupanga mafano a Asera. Iye amagwadira zolengedwa zonse zamlengalenga ndi kumazipembedza.
Amahin apa Hezekiah in ana vohlhuh munsang hochu anasapha kitnin, Baal doihouna anatung doh kitnin pathen lim semthu Asherah doi hochu ana tungdoh kitnin ahi
4 Manase anamanga maguwa mʼNyumba ya Yehova, mʼmene Yehova ananena kuti, “Ine ndidzakhala mu Yerusalemu mpaka muyaya.”
Aman Pakai houinmai leh amiten ama ahin houna ding mun atiova chun semthu pathen houna maicham atungdoh kitnin ahi
5 Mʼmabwalo onse awiri a Nyumba ya Yehova anamangamo maguwa ansembe a zolengedwa zonse zamlengalenga.
Pakai houin na hongcha teni a chun ahsi ho houna maicham anatung doh in ahi
6 Iye ankakapereka ana ake aamuna ngati nsembe yopsereza ku chigwa cha Hinomu, ankachita zamatsenga, kuwombeza ndi ufiti, ankakafunsira kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa. Iye anachita zoyipa zambiri pamaso pa Yehova, kumukwiyitsa Iyeyo.
Hinnom phaicham mah achate pumgo thilto in anakatdoh in ahi. Themka pou anadongin, ailhimjong jong, phunsan jong anachepin, thillha gaochang mijong ana tahsannin mitphel doithem hojong anamangin. Hiti hin Pakai mitmun thet um tahtah anabol doh in Pathen ana phin lung hangin ahi
7 Manase anatenga fano losema limene anapanga ndi kuliyika mʼNyumba ya Mulungu, zimene Mulungu ananena kwa Davide ndi kwa mwana wake Solomoni kuti, “Mʼnyumba ya Mulungu muno, mu Yerusalemu muno, malo amene ndawasankha pakati pa mafuko onse a Israeli, ndidzakhalamo mpaka muyaya.
Hiti in Manasseh hin milim doihou najong Pathen houin sungah anatungdoh in ahi hiche houin chung changa Pathennin David le achapa Solomon jah a anasei, “Hiche houin sung le keiman Israel phung hijat laha kalhen dohsa Jerusalem khopi sunga hi a itihchan na jong keima eiki houjing nading munna kalhen doh ahi
8 Ine sindidzachotsanso phazi la Aisraeli kuchoka mʼdziko limene ndawapatsa makolo ako, ngatitu iwowa adzasamalira kuchita chilichonse chimene ndinawalamulira za malamulo onse, malangizo ndi miyambo imene inapatsidwa kudzera mwa Mose.”
“Chuleh Israel mipiten kathupeh hi ajuijuva chuleh kalhacha pa Mosen anapeh u daanchu anit uva ahileh apu apateo kanapeh gam ma konna koima kakaidoh sah louhelding ahi”
9 Koma Manase anasocheretsa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu, kotero anachita zoyipa zambiri kupambana mitundu imene Yehova anayiwononga pamaso pa Aisraeli.
Manasseh in Judah mipi te achonset sah hi keiman kamite ahung kitolluva kana nodoh peh namdang ho chonset sangin agimnei jon ahi.
10 Yehova anayankhula kwa Manase ndi anthu ake, koma iwo sanasamaleko.
Pakaiyin Manasseh leh amipi te anagih vang'in amahon ana nahsah pouvin ahi
11 Kotero Yehova anawatumizira atsogoleri a ankhondo a ku Asiriya amene anagwira Manase ukapolo, anayika ngowe mʼmphuno mwake, namumanga ndi zingwe zamkuwa ndi kupita naye ku Babuloni.
Hijeh chun Pakaiyin Assyria sepaite atildoh in Judahte chungah gal abolsah in, amahon Manasseh chu aman nun thihkol toh abutaovin thih khaovin akan nun Babylon nah akailut nun ahi
12 Ali pa mavuto akewo anafunafuna kuti Yehova Mulungu wake amukomere mtima ndipo anadzichepetsa kwakukulu pamaso pa Mulungu wa makolo ake.
Ahahsat phatnin ahung kineosah in a Pakai a Pathen nah ahung kiheilut nin kithopi athummin ahi
13 Ndipo atapemphera, Yehova anakhudzidwa ndi kupempha kwakeko ndipo anamvera madandawulo ake. Kotero anamubweretsanso ku Yerusalemu ndi ku ufumu wake. Ndipo Manase anadziwa kuti Yehova ndi Mulungu.
Pathen nin Manasseh taona asangin Jerusalemma ale sollin avaihom sahkitnin ahi. Hiche phat chun Manasseh in Pakai chu Pathen tahbeh ahi ahechen taan ahi
14 Zitapita izi iye anamanga khoma la kunja kwa Mzinda wa Davide kumadzulo kwa kasupe wa Gihoni ku chigwa mpaka polowera ku Chipata cha Nsomba kuzungulira phiri la Ofeli. Iyeyo anakweza kwambiri khomalo. Anayikanso atsogoleri a nkhondo ku mizinda yonse yotetezedwa ya Yuda.
Hiche jouhin Manasseh chun David khopi solang panga chun polang pal chu asesangin, nga kelkot sahleng Gihon twiphul kom phaicham ma kon in Ophel kiti khopi kom geijin pal chu asesangin ahi. Kul kiget khum Judah khopi ho khatcheh a chun sepai aloi loijin lamkai khatnoija akoiyin ahi
15 Iye anachotsa milungu yonse yachilendo ndi fano mʼNyumba ya Yehova komanso maguwa ansembe onse amene anamanga pa phiri la Nyumba ya Mulungu ndi mu Yerusalemu, nazitayira kunja kwa mzinda.
Houin na konchun gamdang pathen holeh milim semthu aman anakoi holeh, namdang maicham thinglhanga atundoh nao ahouin houleh Jerusalem mundang danga umho chu aladoh sohkeijin aga paimang jengin ahi
16 Kenaka anabwezeretsa guwa lansembe la Yehova ndi kupereka zopereka zachiyanjano ndiponso zopereka zamatamando ndipo anawuza Yuda kuti atumikire Yehova Mulungu wa Israeli.
Aman Pakai ahounao maicham jongchu asemphan ahi, hiche chunga chun chamna thilto leh thangvah na thilto abollin ahi, aman Judah mipi techu Israel Pathen Pakai chu nahou diu ahitin thu apen ahi
17 Komabe anthu anapitiriza kupereka nsembe ku malo achipembedzo, koma kwa Yehova, Mulungu wawo yekha.
Ahin lah mipi hochun munsang dunga pumgo thilto chu achepi jing nalaijun ahi, ahivangin Pakai Pathen komma bou abol taovin ahi
18 Zina ndi zina zokhudza ulamuliro wa Manase, kuphatikiza mapemphero ake kwa Mulungu wake ndi mawu amene alosi anayankhula kwa iye mʼdzina la Yehova Mulungu wa Israeli, zalembedwa mʼmabuku a mafumu a Israeli.
Manasseh in anabol jouse, Pathen henga ataona, themgao hon Pathen minna akom ma thu aseihou abonchan Israel lengte thusim bua abonchan akijhlut sohkei jin ahi
19 Pemphero lake ndi momwe Mulungu anakhudzidwira ndi kupempha kwakeko, pamodzinso ndi machimo ake onse ndi kusakhulupirika kwake, ndiponso malo onse amene anamanga, malo azipembedzo ndi mafano a Asera ndi mafano asanadzichepetse, zonse zalembedwa mʼmbiri ya alosi.
Lengpa taonaleh Pathennin adonbutna alung ahin hei masanga achonset na ho jouse le thilse abolho, namdnag pathen houna le adoihou munchom chomma atundoh ho jouse chu themgao ho thusim bua akijih lut nin ahi
20 Manase anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mʼnyumba yake yaufumu. Ndipo Amoni mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Manasseh athiphat nin khopi sungah avuijun achapa Amon nin lengmun alotan ahi
21 Amoni anali wa zaka 22 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka ziwiri.
Amon chu Juda gamma leng ahung chanchun kum 22 alhingtan ahi, amahin Jerusalema kum ni aleng chang ngin ahi
22 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga anachitira Manase abambo ake. Amoni analambira ndi kupereka nsembe kwa mafano onse amene anapanga Manase.
Ama apa Manasseh bangin Pakai dounan achonse tan ahi aman apan anahou doiho chu ana houvin ahi
23 Koma kusiyana ndi abambo ake Manase, iye sanadzichepetse pamaso pa Yehova. Amoni anawonjeza kulakwa kwake.
Ahinlah apa banhgin Pakai anga kisuhnem na anabol pon apa sangin chonset ana ha boljon ahi
24 Akuluakulu a Amoni anamuchita chiwembu ndipo anamupha mʼnyumba yake yaufumu.
Amon noija natong lamkai ho chu ana kihoutoh un leng inpi sunga chun ana that taovin ahi
25 Koma anthu a mʼdzikomo anapha onse amene anakonzera chiwembu mfumu Amoni, ndipo anayika mwana wake Yosiya kukhala mfumu mʼmalo mwake.
Judah mipiten Amon that hochu ana thatdoh un achapa Josiah chu leng anachan sah un ahi

< 2 Mbiri 33 >