< 2 Mbiri 33 >

1 Manase anali wa zaka khumi ndi ziwiri pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 55.
Manasseh te a manghai vaengah kum hlai nit lo ca pueng tih Jerusalem ah sawmnga neh kum nga manghai.
2 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, potsatira machitidwe a mitundu imene Yehova anayithamangitsa pamaso pa Aisraeli.
BOEIPA loh Israel ca mikhmuh lamkah a haek tangtae namtom kah tueilaehkoi bangla BOEIPA mik ah boethae a saii.
3 Iyeyo anamanganso malo opembedzerapo mafano amene Hezekiya abambo ake anawaphwasula; anamanganso maguwa ansembe a Baala ndi kupanga mafano a Asera. Iye amagwadira zolengedwa zonse zamlengalenga ndi kumazipembedza.
Mael tih a napa Hezekiah loh a palet tangtae hmuensang te a thoh. Baal hamla hmueihtuk a suem tih Asherah a saii. Vaan caempuei boeih taengah bakop tih te rhoek taengah tho a thueng.
4 Manase anamanga maguwa mʼNyumba ya Yehova, mʼmene Yehova ananena kuti, “Ine ndidzakhala mu Yerusalemu mpaka muyaya.”
BOEIPA loh, “Ka ming he Jerusalem ah kumhal duela om ni,” a ti lalah BOEIPA im khuiah hmueihtuk a suem.
5 Mʼmabwalo onse awiri a Nyumba ya Yehova anamangamo maguwa ansembe a zolengedwa zonse zamlengalenga.
BOEIPA im vongup rhoi ah vaan caempuei cungkuem ham hmueihtuk a suem.
6 Iye ankakapereka ana ake aamuna ngati nsembe yopsereza ku chigwa cha Hinomu, ankachita zamatsenga, kuwombeza ndi ufiti, ankakafunsira kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa. Iye anachita zoyipa zambiri pamaso pa Yehova, kumukwiyitsa Iyeyo.
Anih loh a ca rhoek te kolrhawk kah hmai khuila a kat sak. Kutyaek a sawt, lung a sawt, hlang a bi, rhaitonghma neh hnam a saii. Amah veet hamla BOEIPA mik ah boethae a saii khaw khawk.
7 Manase anatenga fano losema limene anapanga ndi kuliyika mʼNyumba ya Mulungu, zimene Mulungu ananena kwa Davide ndi kwa mwana wake Solomoni kuti, “Mʼnyumba ya Mulungu muno, mu Yerusalemu muno, malo amene ndawasankha pakati pa mafuko onse a Israeli, ndidzakhalamo mpaka muyaya.
Mueimae mueithuk a saii te Pathen im ah a khueh. Te te Pathen loh David taeng neh a capa Solomon taengah khaw, “Israel koca boeih lamloh ka coelh, he im khui neh Jerusalem khuiah tah kumhal duela ka ming te ka khueh eh.
8 Ine sindidzachotsanso phazi la Aisraeli kuchoka mʼdziko limene ndawapatsa makolo ako, ngatitu iwowa adzasamalira kuchita chilichonse chimene ndinawalamulira za malamulo onse, malangizo ndi miyambo imene inapatsidwa kudzera mwa Mose.”
Tedae Israel kah kho te na pa rhoek taengah ka thoh khohmuen dong lamloh nong sak ham ka khoep mahpawh. Moses kut lamloh amih ka uen bangla olkhueng neh oltlueh neh laitloeknah boeih te a cungkuem la vai ham a ngaithuen mak atah,” a ti.
9 Koma Manase anasocheretsa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu, kotero anachita zoyipa zambiri kupambana mitundu imene Yehova anayiwononga pamaso pa Aisraeli.
Tedae Manasseh loh namtom rhoek lakah boethae saii ham Judah neh Jerusalem khosa rhoek te kho a hmang sak. Te rhoek te BOEIPA loh Israel ca rhoek mikhmuh lamkah a mitmoeng sak coeng dae ta.
10 Yehova anayankhula kwa Manase ndi anthu ake, koma iwo sanasamaleko.
BOEIPA loh Manasseh taeng neh a pilnam taengah a thui dae hnatung uh pawh.
11 Kotero Yehova anawatumizira atsogoleri a ankhondo a ku Asiriya amene anagwira Manase ukapolo, anayika ngowe mʼmphuno mwake, namumanga ndi zingwe zamkuwa ndi kupita naye ku Babuloni.
Te dongah BOEIPA loh Assyria manghai kah caempuei mangpa rhoek te amih taengla a thak. Manasseh te mutlo hling neh a tuuk uh tih rhohum neh a khih uh phoeiah Babylon la a khuen uh.
12 Ali pa mavuto akewo anafunafuna kuti Yehova Mulungu wake amukomere mtima ndipo anadzichepetsa kwakukulu pamaso pa Mulungu wa makolo ake.
A taengah puen a cak vaengah tah a Pathen BOEIPA mikhmuh ah nue coeng tih a napa rhoek kah Pathen mikhmuh ah muep kunyun.
13 Ndipo atapemphera, Yehova anakhudzidwa ndi kupempha kwakeko ndipo anamvera madandawulo ake. Kotero anamubweretsanso ku Yerusalemu ndi ku ufumu wake. Ndipo Manase anadziwa kuti Yehova ndi Mulungu.
Tedae a taengla a thangthui vaengah tah anih te a rhoi tih a lungmacil te a hnatun pah. Te dongah amah khaw a ram te Jerusalem la mael. Te vaengah Manasseh loh Yahweh amah he Pathen ni tila a ming.
14 Zitapita izi iye anamanga khoma la kunja kwa Mzinda wa Davide kumadzulo kwa kasupe wa Gihoni ku chigwa mpaka polowera ku Chipata cha Nsomba kuzungulira phiri la Ofeli. Iyeyo anakweza kwambiri khomalo. Anayikanso atsogoleri a nkhondo ku mizinda yonse yotetezedwa ya Yuda.
A hnukah tah David khopuei rhamvoel kah vongtung te khotlak kah Gihon soklong ah a sak tih nga vongka a pha. Ophel te a tuung tih muep a sang sak. Judah kah vong cak khopuei boeih ah tatthai mangpa rhoek a khueh.
15 Iye anachotsa milungu yonse yachilendo ndi fano mʼNyumba ya Yehova komanso maguwa ansembe onse amene anamanga pa phiri la Nyumba ya Mulungu ndi mu Yerusalemu, nazitayira kunja kwa mzinda.
Kholong pathen rhoek neh a mueimae te khaw BOEIPA im lamloh a khoe tih, BOEIPA im tlang neh Jerusalem kah a sak hmueihtuk boeih khaw khopuei rhamvoel la a voeih.
16 Kenaka anabwezeretsa guwa lansembe la Yehova ndi kupereka zopereka zachiyanjano ndiponso zopereka zamatamando ndipo anawuza Yuda kuti atumikire Yehova Mulungu wa Israeli.
BOEIPA kah hmueihtuk te cikngae la a sak bal tih a soah rhoepnah neh uemonah hmueih te a nawn. Judah taengah khaw Israel Pathen BOEIPA taengah thothueng hamla a thui pah.
17 Komabe anthu anapitiriza kupereka nsembe ku malo achipembedzo, koma kwa Yehova, Mulungu wawo yekha.
Tedae pilnam te hmuensang ah a nawn pueng tih a Pathen BOEIPA te khaw a bawkuh.
18 Zina ndi zina zokhudza ulamuliro wa Manase, kuphatikiza mapemphero ake kwa Mulungu wake ndi mawu amene alosi anayankhula kwa iye mʼdzina la Yehova Mulungu wa Israeli, zalembedwa mʼmabuku a mafumu a Israeli.
Manasseh kah ol noi khaw, a Pathen taengah a thangthuinah khaw, Israel Pathen BOEIPA ming neh anih taengah aka thui khohmu rhoek kah ol khaw, Israel manghai rhoek kah olka khuiah om coeng ke.
19 Pemphero lake ndi momwe Mulungu anakhudzidwira ndi kupempha kwakeko, pamodzinso ndi machimo ake onse ndi kusakhulupirika kwake, ndiponso malo onse amene anamanga, malo azipembedzo ndi mafano a Asera ndi mafano asanadzichepetse, zonse zalembedwa mʼmbiri ya alosi.
A thangthuinah neh a thangthui khaw, a tholhnah neh a boekoeknah boeih khaw, a soah hmuensang a sak nah hmuen te khaw, Asherah neh mueidaep a hol tih a hmai ah a kunyun khaw, Hozai kah olka khuiah a daek uh coeng ke.
20 Manase anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mʼnyumba yake yaufumu. Ndipo Amoni mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Manasseh te a napa rhoek taengla a khoem uh vaengah anih te amah im ah a up uh. Te phoeiah tah a capa Amon te anih yueng la manghai.
21 Amoni anali wa zaka 22 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka ziwiri.
Amon a manghai vaengah kum kul kum nit lo ca pueng tih Jerusalem ah kum nit manghai.
22 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga anachitira Manase abambo ake. Amoni analambira ndi kupereka nsembe kwa mafano onse amene anapanga Manase.
A napa Manasseh kah a saii bangla BOEIPA mik ah boethae a saii. A napa Manasseh kah a saii mueidaep cungkuem taengah Amon loh a nawn tih tho a thueng.
23 Koma kusiyana ndi abambo ake Manase, iye sanadzichepetse pamaso pa Yehova. Amoni anawonjeza kulakwa kwake.
A napa Manasseh kah a kunyun bangla BOEIPA mikhmuh ah a kunyun moenih. Amon amah lat loh dumlai a pung sak.
24 Akuluakulu a Amoni anamuchita chiwembu ndipo anamupha mʼnyumba yake yaufumu.
Te vaengah anih te a sal rhoek loh a taeng uh tih amah im ah a duek sakuh.
25 Koma anthu a mʼdzikomo anapha onse amene anakonzera chiwembu mfumu Amoni, ndipo anayika mwana wake Yosiya kukhala mfumu mʼmalo mwake.
Te dongah manghai Amon aka taeng boeih te khohmuen pilnam loh a ngawn. Te phoeiah tah khohmuen pilnam loh a capa Josiah te anih yueng la a manghai sak.

< 2 Mbiri 33 >