< 2 Mbiri 32 >

1 Zitatha zonse zimene Hezekiya anachita mokhulupirika, Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anabwera ndi kuthira nkhondo dziko la Yuda. Iye anazinga mizinda yotetezedwa ya Yuda, kuganiza kuti ayigonjetsa.
После тих ствари и пошто се оне утврдише, дође Сенахирим цар асирски, и уђе у земљу Јудину, и опколи тврде градове, и мишљаше их освојити.
2 Pamene Hezekiya anaona kuti Senakeribu wabwera ndipo wakonzeka kuchita nkhondo ndi Yerusalemu,
А кад виде Језекија где дође Сенахирим и где се окрену да удари на Јерусалим,
3 iye anakambirana ndi akuluakulu ake pamodzi ndi atsogoleri a gulu lankhondo za kutseka akasupe ochoka ku kasupe amene anali kunja kwa mzinda, ndipo iwo anamuthandiza.
Учини веће с кнезовима својим и с јунацима својим да зарони изворе водене, који беху иза града, и помогоше му.
4 Gulu lalikulu la anthu linasonkhana, ndipo anatseka akasupe onse pamodzi ndi mtsinje umene umayenda mʼkati mwa nthakamo. Iwo ankanena kuti, “Nʼchifukwa chiyani mafumu a Asiriya akabwera kuno adzapeze madzi ambiri?”
Јер се сабра мноштво народа, те заронише све изворе и поток који тече посред земље говорећи: Зашто кад дођу цареви асирски да нађу толико воде?
5 Kenaka iye anagwira ntchito molimbika kukonza madera ogumuka a khoma ndi kumangapo msanja. Anamanganso mpanda wina kunja kwa mpanda winawo ndipo anamanga zolimbitsa Milo ku mzinda wa Davide.
И охрабри се, те озида вас зид оборени, и подиже куле, и споља озида још један зид; и утврди Милон у граду Давидовом, и начини много оружја и штитова.
6 Iye anasankha atsogoleri a ankhondo olamulira anthu ndipo anawasonkhanitsa pamaso pake pa bwalo la chipata cha mzinda ndi kuwalimbikitsa ndi mawu awa:
И постави војводе над народом, и сабра их к себи на улицу код врата градских, и говори им љубазно и рече:
7 “Khalani amphamvu ndi olimba mtima. Musachite mantha kapena kutaya mtima chifukwa cha mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lalikulu lankhondo limene ali nalo, pakuti ife tili ndi mphamvu yayikulu kuposa imene ili ndi iye.
Будите слободни и храбри, не бојте се и не плашите се цара асирског ни свега мноштва што је с њим, јер је с нама већи него с њим.
8 Iye ali ndi mphamvu ya anthu basi, koma ife tili ndi Yehova Mulungu wathu kutithandiza ndi kuchita nkhondo zathu.” Ndipo anthu anapeza chilimbikitso kuchokera pa zimene Hezekiya mfumu ya Yuda ananena.
С њим је мишица телесна а с нама је Господ Бог наш да нам помогне и да бије наше бојеве. И народ се ослони на речи Језекије цара Јудиног.
9 Nthawi ina, pamene Senakeribu mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lake lonse lankhondo anali atazinga Lakisi, iye anatumiza atsogoleri ake ankhondo ku Yerusalemu ndi uthenga uwu kwa Hezekiya mfumu ya Yuda ndi anthu onse a ku Yuda amene anali kumeneko:
Потом Сенахирим цар асирски док беше на Лахису са свом силом својом, посла слуге своје у Јерусалим к Језекији цару Јудином и ка свему народу Јудином који беше у Јерусалиму, и поручи:
10 “Senakeribu mfumu ya ku Asiriya akuti: Kodi inu mukukhulupirira chiyani, kuti mukukhalabe mu Yerusalemu mutazingidwa?
Овако вели Сенахирим цар асирски: У шта се уздате, те стојите у Јерусалиму затворени?
11 Pamene Hezekiya akunena kuti ‘Yehova Mulungu wathu adzatipulumutsa kuchoka mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya,’ iye akukusocheretsani, kuti mufe ndi njala ndi ludzu.
Не наговара ли вас Језекија да вас помори глађу и жеђу говорећи: Господ Бог наш избавиће нас из руке цара асирског?
12 Kodi si Hezekiya amene anachotsa malo opembedzerapo Mulungu ameneyu ndi maguwa ansembe ndi kunena kwa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu kuti, ‘Muzipembedza pa guwa lansembe limodzi ndi kupserezapo nsembe?’
Није ли тај Језекија оборио висине његове и олтаре његове, и заповедио Јуди и Јерусалимљанима говорећи: Клањајте се само пред једним олтаром и на њему кадите?
13 “Kodi inu simukudziwa zimene ine ndi makolo anga tachita kwa anthu a mitundu ina? Kodi milungu ya mitundu imeneyi inatha kupulumutsa dziko lawo kuchoka mʼdzanja langa?
Еда ли не знате шта сам учинио ја и моји стари од свих народа на земљи? Јесу ли богови народа земаљских могли избавити земљу своју из мојих руку?
14 Kodi ndi milungu iti mwa milungu ya mitundu ina ya anthuwo, imene makolo anga anayiwononga kotheratu, inatha kupulumutsa anthu ake mʼdzanja langa? Nanga tsono Mulungu wanuyo adzakupulumutsani mʼdzanja langa motani?
Који је између свих богова оних народа које затрше оци моји, могао избавити свој народ из мојих руку, да би могао ваш Бог вас избавити из моје руке?
15 Choncho inu musalole kuti Hezekiya akunamizeni ndi kukusocheretsani motere. Musamukhulupirire, pakuti palibe mulungu wa mtundu wina uliwonse kapena ufumu wina uliwonse umene unatha kupulumutsa anthu ake kuchoka mʼdzanja langa kapena mʼdzanja la makolo anga. Nanga bwanji Mulungu wanuyo, sadzatha kukupulumutsani kuchoka mʼdzanja langa!”
Немојте дакле да вас вара Језекија и да вас тако наговара, и не верујте му; јер ниједан бог ниједног народа или царства није могао избавити народ свој из мојих руку ни из руку мојих отаца, а камоли ће ваши богови избавити вас из мојих руку?
16 Atsogoleri a ankhondo a Senakeribu anapitiriza kuyankhula zotsutsana ndi Yehova Mulungu ndi mtumiki wake Hezekiya.
И још више говорише слуге његове на Господа Бога и на Језекију, слугу Његовог.
17 Mfumunso inalemba makalata onyoza Yehova, Mulungu wa Israeli, ndipo inanena zotsutsana naye izi: “Monga momwe milungu ya anthu a mayiko ena sinathe kuwapulumutsa kuchoka mʼdzanja langa, chonchonso Mulungu wa Hezekiya sadzapulumutsa anthu ake kuchoka mʼdzanja langa.”
А и књигу написа ружећи Господа Бога Израиљевог и говорећи на Њ речима: Као што богови народа земаљских нису избавили свој народ из мојих руку, тако неће ни Бог Језекијин избавити народ свој из мојих руку.
18 Kenaka iwo anafuwula mu Chihebri kwa anthu a mu Yerusalemu amene anali pa khoma, kuwaopseza ndi kuwachititsa mantha ndi cholinga choti alande mzindawo.
И викаху гласно јудејски народу јерусалимском који беше на зиду да их уплаше и смету да би узели град.
19 Iwo anayankhula za Mulungu wa Yerusalemu monga anayankhulira za milungu ya anthu ena a pa dziko lapansi, ntchito ya manja a anthu.
И говораху о Богу јерусалимском као о боговима народа земаљских, који су дело руку човечјих.
20 Mfumu Hezekiya ndi mneneri Yesaya mwana wa Amozi anafuwulira kumwamba mʼpemphero chifukwa cha zimenezi.
Тада се помоли тога ради цар Језекија и пророк Исаија син Амосов, и вапише к небу.
21 Ndipo Yehova anatumiza mngelo amene anadzapha anthu onse odziwa nkhondo ndi atsogoleri ndiponso oyangʼanira misasa ya mfumu ya ku Asiriya. Choncho Senakeribu anabwerera kwawo wamanyazi. Ndipo atalowa mʼnyumba ya mulungu wake, ena mwa ana ake anamupha ndi lupanga.
И посла Господ анђела, који поби све јунаке и војводе и кнезове у војсци цара асирског, те се врати са срамотом у своју земљу. И кад уђе у кућу свог бога, убише га онде мачем који изиђоше из бедара његових.
22 Kotero Yehova anapulumutsa Hezekiya ndi anthu a ku Yerusalemu kuchoka mʼdzanja la Senakeribu mfumu ya ku Asiriya ndi mʼdzanja la anthu ena. Yehova anawateteza ku mbali zonse.
Тако сачува Господ Језекију и народ јерусалимски од руку Сенахирима цара асирског и од руку свих других, и чува их на све стране.
23 Anthu ambiri anabweretsa zopereka kwa Yehova ku Yerusalemu ndi mphatso zamtengowapatali kwa Hezekiya mfumu ya Yuda. Kuyambira nthawi imeneyo Hezekiya ankalemekezedwa kwambiri ndi mitundu ina yonse.
И многи доношаху даре Господу у Јерусалим и закладе Језекији цару Јудином; и од тада се узвиси пред свим народима.
24 Pa nthawi imeneyo Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Iye anapemphera kwa Yehova, amene anamuyankha ndi kumupatsa chizindikiro chodabwitsa.
У то време разболи се Језекија на смрт, и помоли се Господу, који му проговори и учини му чудо.
25 Koma Hezekiya anali ndi mtima wonyada ndipo sanachite molingana ndi kukoma mtima kumene Mulungu anamuonetsera. Choncho mkwiyo wa Yehova unali pa iye ndi pa Yuda ndi Yerusalemu.
Али Језекија не поступи према добру које му се учини, јер се понесе срце његово; зато се подиже на њ гнев и на Јуду и на Јерусалим.
26 Koma kenaka Hezekiya analapa za kunyada kwakeko, monga anachitanso anthu a mu Yerusalemu. Choncho mkwiyo wa Yehova sunafike pa iwo pa nthawi ya Hezekiya.
Али се понизи Језекија зато што се беше понело срце његово, и он и Јерусалимљани, те не дође на њих гнев Господњи за живота Језекијиног.
27 Hezekiya anali ndi chuma ndi ulemu wambiri ndipo anamanga nyumba zosungiramo chuma cha siliva wake ndi golide ndi za miyala yokongola, zokometsera zakudya, zishango ndi mtundu uliwonse wa zinthu zamtengowapatali.
А имаше Језекија врло велико благо и славу; и начини себи ризнице за сребро и злато и за драго камење и за мирисе и за штитове и за свакојаке закладе,
28 Iye anamanganso nyumba zosungiramo tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta a olivi, ndiponso anamanga nyumba zodyeramo ngʼombe zosiyanasiyana, ndi makola a nkhosa.
И стаје за доходе од жита и од вина и од уља, и стаје за свакојаку стоку, и торове за овце.
29 Iyeyo anamanga midzi ndipo anali ndi nkhosa ndi ngʼombe zambiri, pakuti Mulungu anamupatsa chuma chambiri.
И градове сазида себи, и имаше много стоке, и оваца и говеда, јер му Бог даде веома велико благо.
30 Ndi Hezekiya amene anatseka ku mtunda kwa kasupe wa Gihoni, ndi kumuwongolera kuti madzi ake apite mbali ya kumadzulo kwa Mzinda wa Davide. Iye ankachita bwino pa ntchito iliyonse imene ankagwira.
Исти Језекија загради горњи извор воде Гиона, и право је сведе доле на западну страну града Давидовог; и беше срећан Језекија у сваком послу свом.
31 Koma pamene nthumwi zotumizidwa ndi atsogoleri a ku Babuloni zinabwera kudzamufunsa za chizindikiro chozizwitsa chimene chinachitika mʼdzikomo, Mulungu anamusiya yekha, kumuyesa kuti adziwe zonse zimene zinali mu mtima mwake.
Само кад дођоше посланици кнезова вавилонских, који послаше к њему да распитају за чудо које би у земљи, остави га Бог да би га искушао, да би се знало све што му је у срцу.
32 Zina ndi zina zokhudza ulamuliro wa Hezekiya ndi ntchito za kudzipereka kwake zalembedwa mʼmasomphenya a Yesaya mwana wa Amozi, mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli.
А остала дела Језекијина и милости његове, ето, то је записано у утвари пророка Исаије, сина Амосовог и у књизи о царевима Јудиним и Израиљевим.
33 Hezekiya anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pa phiri pamene pali manda a zidzukulu za Davide. Ayuda onse ndi anthu a mu Yerusalemu anamulemekeza atamwalira. Ndipo Manase mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
И почину Језекија код отаца својих, и погребоше га изнад гробова синова Давидових; и учинише му на смрти част сви Јудејци и Јерусалимљани. А на његово се место зацари Манасија, син његов.

< 2 Mbiri 32 >