< 2 Mbiri 32 >
1 Zitatha zonse zimene Hezekiya anachita mokhulupirika, Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anabwera ndi kuthira nkhondo dziko la Yuda. Iye anazinga mizinda yotetezedwa ya Yuda, kuganiza kuti ayigonjetsa.
Après ces événements et ces preuves de zèle, Sennachérib, roi d’Assyrie, vint envahir Juda, assiégea les villes fortes et prétendit les forcer pour s’en emparer.
2 Pamene Hezekiya anaona kuti Senakeribu wabwera ndipo wakonzeka kuchita nkhondo ndi Yerusalemu,
Ezéchias, voyant que Sennachérib était venu avec l’intention d’attaquer Jérusalem,
3 iye anakambirana ndi akuluakulu ake pamodzi ndi atsogoleri a gulu lankhondo za kutseka akasupe ochoka ku kasupe amene anali kunja kwa mzinda, ndipo iwo anamuthandiza.
consulta ses chefs et ses héros sur l’idée de boucher les sources d’eau qui se trouvaient en dehors de la ville, et ils l’appuyèrent.
4 Gulu lalikulu la anthu linasonkhana, ndipo anatseka akasupe onse pamodzi ndi mtsinje umene umayenda mʼkati mwa nthakamo. Iwo ankanena kuti, “Nʼchifukwa chiyani mafumu a Asiriya akabwera kuno adzapeze madzi ambiri?”
Alors ils se rassemblèrent en grand nombre et bouchèrent toutes les sources, ainsi que le torrent qui coulait dans le pays, en disant: "Pourquoi les rois d’Assyrie trouveraient-ils à leur arrivée quantité d’eau?"
5 Kenaka iye anagwira ntchito molimbika kukonza madera ogumuka a khoma ndi kumangapo msanja. Anamanganso mpanda wina kunja kwa mpanda winawo ndipo anamanga zolimbitsa Milo ku mzinda wa Davide.
Il s’enhardit et rebâtit toutes les brèches de la muraille; il suréleva les tours et l’autre muraille extérieure; il fortifia le Millo dans la cité de David et fabriqua un grand nombre d’armes de trait et des boucliers.
6 Iye anasankha atsogoleri a ankhondo olamulira anthu ndipo anawasonkhanitsa pamaso pake pa bwalo la chipata cha mzinda ndi kuwalimbikitsa ndi mawu awa:
Il établit des chefs militaires à la tête du peuple, les assembla autour de lui sur la place à la porte de la ville et les encouragea en ces termes:
7 “Khalani amphamvu ndi olimba mtima. Musachite mantha kapena kutaya mtima chifukwa cha mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lalikulu lankhondo limene ali nalo, pakuti ife tili ndi mphamvu yayikulu kuposa imene ili ndi iye.
"Soyez forts et courageux, n’ayez crainte et ne vous laissez point effrayer par le roi d’Assyrie et toute la foule qui raccompagne, car il y a avec nous quelqu’un de plus grand qu’avec lui.
8 Iye ali ndi mphamvu ya anthu basi, koma ife tili ndi Yehova Mulungu wathu kutithandiza ndi kuchita nkhondo zathu.” Ndipo anthu anapeza chilimbikitso kuchokera pa zimene Hezekiya mfumu ya Yuda ananena.
Avec lui est un bras de chair; avec nous est l’Eternel, notre Dieu, pour nous assister et combattre nos combats", et le peuple s’en rapporta aux paroles d’Ezéchias, roi de Juda.
9 Nthawi ina, pamene Senakeribu mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lake lonse lankhondo anali atazinga Lakisi, iye anatumiza atsogoleri ake ankhondo ku Yerusalemu ndi uthenga uwu kwa Hezekiya mfumu ya Yuda ndi anthu onse a ku Yuda amene anali kumeneko:
Après cela Sennachérib, roi d’Assyrie, envoya ses serviteurs à Jérusalem, tandis qu’il était lui-même devant Lakhich avec toutes ses forces, vers Ezéchias, roi de Juda, et vers tous ceux de Juda qui se trouvaient à Jérusalem pour leur dire:
10 “Senakeribu mfumu ya ku Asiriya akuti: Kodi inu mukukhulupirira chiyani, kuti mukukhalabe mu Yerusalemu mutazingidwa?
"Ainsi parle Sennachérib, roi d’Assyrie: En quoi mettez-vous votre confiance pour rester ainsi bloqués dans Jérusalem?
11 Pamene Hezekiya akunena kuti ‘Yehova Mulungu wathu adzatipulumutsa kuchoka mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya,’ iye akukusocheretsani, kuti mufe ndi njala ndi ludzu.
Ne voyez-vous pas qu’Ezéchias vous abuse pour vous livrer à la mort par la famine et par la soif, quand il vous dit: L’Eternel, notre Dieu, nous sauvera de la main du roi d’Assyrie?
12 Kodi si Hezekiya amene anachotsa malo opembedzerapo Mulungu ameneyu ndi maguwa ansembe ndi kunena kwa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu kuti, ‘Muzipembedza pa guwa lansembe limodzi ndi kupserezapo nsembe?’
N’Est-ce pas lui, Ezéchias, qui a fait disparaître ses hauts lieux et ses autels et qui a parlé en ces termes à Juda et à Jérusalem: Devant un seul autel vous vous prosternerez et ferez fumer l’encens?
13 “Kodi inu simukudziwa zimene ine ndi makolo anga tachita kwa anthu a mitundu ina? Kodi milungu ya mitundu imeneyi inatha kupulumutsa dziko lawo kuchoka mʼdzanja langa?
Ne savez-vous pas ce que j’ai fait, moi et mes pères, à tous les peuples des diverses contrées? Est-ce que les dieux des nations de ces contrées ont jamais pu soustraire leur pays à mon pouvoir?
14 Kodi ndi milungu iti mwa milungu ya mitundu ina ya anthuwo, imene makolo anga anayiwononga kotheratu, inatha kupulumutsa anthu ake mʼdzanja langa? Nanga tsono Mulungu wanuyo adzakupulumutsani mʼdzanja langa motani?
De tous les dieux de ces nations qu’ont anéanties mes pères, quel est celui qui a pu soustraire son peuple à mon pouvoir? Et votre Dieu pourrait vous arracher à ma domination!
15 Choncho inu musalole kuti Hezekiya akunamizeni ndi kukusocheretsani motere. Musamukhulupirire, pakuti palibe mulungu wa mtundu wina uliwonse kapena ufumu wina uliwonse umene unatha kupulumutsa anthu ake kuchoka mʼdzanja langa kapena mʼdzanja la makolo anga. Nanga bwanji Mulungu wanuyo, sadzatha kukupulumutsani kuchoka mʼdzanja langa!”
Et maintenant, ne vous laissez pas abuser par Ezéchias ni séduire ainsi, ne croyez pas en lui, car aucun dieu d’aucune nation et royaume ne pourra soustraire son peuple à ma domination et à celle de mes pères, à plus forte raison votre Dieu ne pourra-t-il vous soustraire à mon pouvoir."
16 Atsogoleri a ankhondo a Senakeribu anapitiriza kuyankhula zotsutsana ndi Yehova Mulungu ndi mtumiki wake Hezekiya.
Ses serviteurs continuèrent à déblatérer contre le Seigneur Dieu et contre Ezéchias, son serviteur.
17 Mfumunso inalemba makalata onyoza Yehova, Mulungu wa Israeli, ndipo inanena zotsutsana naye izi: “Monga momwe milungu ya anthu a mayiko ena sinathe kuwapulumutsa kuchoka mʼdzanja langa, chonchonso Mulungu wa Hezekiya sadzapulumutsa anthu ake kuchoka mʼdzanja langa.”
Il avait écrit aussi des libelles injurieux pour l’Eternel, Dieu d’Israël, et s’exprimait sur lui en ces termes: "Tels les dieux des contrées qui n’ont pu soustraire leur peuple à mon pouvoir, ainsi le Dieu d’Ezéchias ne soustraira point son peuple à mon pouvoir."
18 Kenaka iwo anafuwula mu Chihebri kwa anthu a mu Yerusalemu amene anali pa khoma, kuwaopseza ndi kuwachititsa mantha ndi cholinga choti alande mzindawo.
Ils s’adressaient à haute voix en judéen au peuple de Jérusalem qui était sur le rempart pour les effrayer et les troubler afin de s’emparer de la ville.
19 Iwo anayankhula za Mulungu wa Yerusalemu monga anayankhulira za milungu ya anthu ena a pa dziko lapansi, ntchito ya manja a anthu.
Ils parlaient du Dieu de Jérusalem comme des dieux des nations de la terre, œuvre des mains de l’homme.
20 Mfumu Hezekiya ndi mneneri Yesaya mwana wa Amozi anafuwulira kumwamba mʼpemphero chifukwa cha zimenezi.
Alors le roi Ezéchias et le prophète Isaïe, fils d’Amoç, se mirent à prier à ce sujet et ils implorèrent le Ciel.
21 Ndipo Yehova anatumiza mngelo amene anadzapha anthu onse odziwa nkhondo ndi atsogoleri ndiponso oyangʼanira misasa ya mfumu ya ku Asiriya. Choncho Senakeribu anabwerera kwawo wamanyazi. Ndipo atalowa mʼnyumba ya mulungu wake, ena mwa ana ake anamupha ndi lupanga.
L’Eternel envoya un ange, qui extermina tous les guerriers, princes et chefs, dans le camp du roi d’Assyrie, lequel s’en revint, plein de confusion, dans son pays. Il entra dans le temple de son dieu et là, il tomba sous le glaive de sa propre progéniture.
22 Kotero Yehova anapulumutsa Hezekiya ndi anthu a ku Yerusalemu kuchoka mʼdzanja la Senakeribu mfumu ya ku Asiriya ndi mʼdzanja la anthu ena. Yehova anawateteza ku mbali zonse.
C’Est ainsi que l’Eternel sauva Ezéchias et les habitants de Jérusalem de la main de Sennachérib, roi d’Assyrie, et de la main de tous leurs ennemis et les protégea tout alentour.
23 Anthu ambiri anabweretsa zopereka kwa Yehova ku Yerusalemu ndi mphatso zamtengowapatali kwa Hezekiya mfumu ya Yuda. Kuyambira nthawi imeneyo Hezekiya ankalemekezedwa kwambiri ndi mitundu ina yonse.
Puis, beaucoup apportèrent une offrande à l’Eternel à Jérusalem et des présents à Ezéchias, roi de Juda; et il fut élevé après cela aux yeux de tous les peuples.
24 Pa nthawi imeneyo Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Iye anapemphera kwa Yehova, amene anamuyankha ndi kumupatsa chizindikiro chodabwitsa.
En ce temps-là Ezéchias fut atteint d’une maladie mortelle. Il implora le Seigneur, qui lui parla et lui accorda un prodige.
25 Koma Hezekiya anali ndi mtima wonyada ndipo sanachite molingana ndi kukoma mtima kumene Mulungu anamuonetsera. Choncho mkwiyo wa Yehova unali pa iye ndi pa Yuda ndi Yerusalemu.
Mais Ezéchias n’agit pas comme il aurait dû en retour de cette faveur, car son cœur s’enorgueillit, et la colère divine fut excitée contre lui et contre Juda et Jérusalem.
26 Koma kenaka Hezekiya analapa za kunyada kwakeko, monga anachitanso anthu a mu Yerusalemu. Choncho mkwiyo wa Yehova sunafike pa iwo pa nthawi ya Hezekiya.
Mais Ezéchias s’humilia dans son cœur orgueilleux, lui et les habitants de Jérusalem, et la colère de l’Eternel ne les atteignit pas du temps d’Ezéchias.
27 Hezekiya anali ndi chuma ndi ulemu wambiri ndipo anamanga nyumba zosungiramo chuma cha siliva wake ndi golide ndi za miyala yokongola, zokometsera zakudya, zishango ndi mtundu uliwonse wa zinthu zamtengowapatali.
Ezéchias eut des richesses et des honneurs en grande abondance; il se fit des trésors pour l’argent, l’or et les pierres précieuses, pour les aromates, les boucliers et tous les objets de prix,
28 Iye anamanganso nyumba zosungiramo tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta a olivi, ndiponso anamanga nyumba zodyeramo ngʼombe zosiyanasiyana, ndi makola a nkhosa.
des magasins pour les récoltes de blé, pour le moût et l’huile, des étables pour tous les animaux domestiques et des troupeaux pour les étables.
29 Iyeyo anamanga midzi ndipo anali ndi nkhosa ndi ngʼombe zambiri, pakuti Mulungu anamupatsa chuma chambiri.
Il se bâtit des villes, s’acquit du menu et du gros bétail en quantité, car Dieu lui avait donné des richesses très considérables.
30 Ndi Hezekiya amene anatseka ku mtunda kwa kasupe wa Gihoni, ndi kumuwongolera kuti madzi ake apite mbali ya kumadzulo kwa Mzinda wa Davide. Iye ankachita bwino pa ntchito iliyonse imene ankagwira.
Ce fut Ezéchias qui boucha l’issue supérieure des eaux du Ghihôn et les dirigea par en bas du côté occidental vers la cité de David, et Ezéchias réussit dans toutes ses entreprises.
31 Koma pamene nthumwi zotumizidwa ndi atsogoleri a ku Babuloni zinabwera kudzamufunsa za chizindikiro chozizwitsa chimene chinachitika mʼdzikomo, Mulungu anamusiya yekha, kumuyesa kuti adziwe zonse zimene zinali mu mtima mwake.
Pourtant, dans l’affaire des conseillers des princes de Babylone qui lui avaient envoyé une ambassade pour s’informer du prodige qui avait eu lieu dans le pays, Dieu l’abandonna afin de le mettre à l’épreuve et connaître tous les sentiments de son cœur.
32 Zina ndi zina zokhudza ulamuliro wa Hezekiya ndi ntchito za kudzipereka kwake zalembedwa mʼmasomphenya a Yesaya mwana wa Amozi, mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli.
Pour les autres faits concernant Ezéchias et ses mérites, tout cela est consigné dans les prophéties d’Isaïe, fils d’Amoç et dans le livre des rois de Juda et d’Israël.
33 Hezekiya anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pa phiri pamene pali manda a zidzukulu za Davide. Ayuda onse ndi anthu a mu Yerusalemu anamulemekeza atamwalira. Ndipo Manase mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Ezéchias s’endormit avec ses pères; on l’ensevelit sur la montée des tombeaux de la famille de David, et des honneurs lui furent rendus à sa mort par tout Juda et par les habitants de Jérusalem. Il eut pour successeur son fils Manassé.