< 2 Mbiri 31 >

1 Zonse zitatha, Aisraeli onse amene anali kumeneko anapita ku mizinda ya ku Yuda, nakaphwanya miyala yachipembedzo ndi kudula mitengo ya mafano a Asera. Iwo anakawononga malo achipembedzo ndi maguwa ansembe amene anali mʼdziko lonse la Yuda, Benjamini, Efereimu ndi Manase. Atawononga zonsezi, Aisraeli anabwerera ku mizinda yawo ndi ku malo awo.
A gdy to wszystko się zakończyło, cały lud Izraela, który tam się znajdował, wyruszył do miast Judy i potłukł posągi, wyciął gaje, i zburzył do szczętu wyżyny oraz ołtarze w całej Judzie i Beniaminie, w Efraimie i Manassesie. Potem wszyscy synowie Izraela wrócili, każdy do swojej posiadłości [i] do swego miasta.
2 Hezekiya anakhazikitsa magulu a ansembe ndi Alevi, gulu lililonse monga mwa ntchito zawo ngati ansembe kapena Alevi, kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano, kutumikira, kuyamikira ndi kuyimba matamando pa zipata za ku malo okhala Yehova.
I Ezechiasz ustanowił zmiany kapłanów i Lewitów według ich podziałów, każdego według jego służby, kapłanów i Lewitów do [składania] całopaleń i ofiar pojednawczych, aby służyli i dziękowali PANU, a także wysławiali go w bramach [jego] obozu.
3 Kuchokera pa chuma chake, mfumu inapereka nsembe zopsereza za mmawa ndi madzulo ndiponso nsembe zopsereza za pa Chikondwerero cha Masabata, Chikondwerero cha Mwezi Watsopano ndipo inakhazikitsa zikondwerero monga zinalembedwera mʼmalamulo a Yehova.
Przeznaczył także część z majątku królewskiego na całopalenia poranne i wieczorne, na całopalenia w szabaty, nów księżyca i w uroczyste święta, jak to napisane jest w Prawie PANA.
4 Iyo inalamula anthu amene amakhala mu Yerusalemu kupereka gawo lawo kwa ansembe ndi Alevi kuti iwowo adzipereke ku malamulo a Yehova.
Rozkazał też ludowi mieszkającemu w Jerozolimie, aby oddawał należny dział kapłanom i Lewitom, aby mogli wytrwać w prawie PANA.
5 Lamuloli atangolilengeza, Aisraeli anapereka mowolowamanja zipatso zoyamba kucha za tirigu, vinyo watsopano, mafuta ndi uchi ndi zonse zomwe nthaka yawo inabereka. Anabweretsa zochuluka kwambiri, chakhumi cha chilichonse.
A gdy ten rozkaz rozszedł się, synowie Izraela przynieśli pod dostatkiem pierwocin zboża, moszczu, oliwy, miodu oraz wszelkich płodów rolnych, przynieśli także obfite dziesięciny ze wszystkiego.
6 Aisraeli ndi Ayuda amene amakhala mʼmizinda ya Yuda anabweretsanso chakhumi cha ngʼombe zawo ndi nkhosa ndi chakhumi cha zinthu zoyera zoperekedwa kwa Yehova Mulungu wawo, ndipo anaziyika mʼmilumilu.
Ponadto synowie Izraela i Judy, którzy mieszkali w miastach Judy, również przynieśli dziesięcinę z wołów i owiec oraz dziesięcinę z rzeczy świętych poświęconych PANU, ich Bogu, i składali to wszystko na stosy.
7 Anayamba kuchita izi mwezi wachitatu ndipo anatsiriza mwezi wachisanu ndi chiwiri.
W trzecim miesiącu rozpoczęli układać te stosy, a w siódmym miesiącu zakończyli.
8 Hezekiya ndi akuluakulu ake atabwera ndi kuona miluyo, anatamanda Yehova ndi kudalitsa anthu ake, Aisraeli.
Kiedy przyszedł Ezechiasz wraz z książętami i zobaczyli te stosy, błogosławili PANU i jego ludowi Izraelowi.
9 Hezekiya anafunsa ansembe ndi Alevi za miluyi;
Wtedy Ezechiasz wypytywał kapłanów i Lewitów o te stosy.
10 ndipo Azariya, mkulu wa ansembe, ochokera ku banja la Zadoki anayankha kuti, “Kuyambira pamene anthu anayamba kubweretsa zopereka zawo ku Nyumba ya Yehova ife takhala ndi zokwanira kudya ndi zina zambiri zosunga, chifukwa Yehova wadalitsa anthu ake, ndipo mulu umenewu ndiye zotsala.”
Odpowiedział mu Azariasz, najwyższy kapłan z domu Sadoka: Kiedy zaczęto przynosić te ofiary do domu PANA, jedliśmy i nasyciliśmy się, a jeszcze wiele pozostało, gdyż PAN błogosławił swojemu ludowi, a pozostało tego wiele.
11 Hezekiya analamula kuti akonze zipinda zosungiramo za mʼNyumba ya Yehova, ndipo izi zinachitika.
Rozkazał więc Ezechiasz, aby przygotowano spichlerze w domu PANA. I przygotowano je;
12 Ndipo iwo mokhulupirika anabweretsa zopereka, chakhumi ndi mphatso zopatulika. Konaniya Mlevi ndiye amayangʼanira zinthu zimenezi ndipo mʼbale wake Simei ndiye anali wachiwiri wake.
I złożono tam wiernie ofiary, dziesięciny i rzeczy poświęcone. Przełożonym nad nimi był Konaniasz, Lewita, a jego brat Szimei [był] drugi.
13 Yehieli, Azaziya, Nahati, Asaheli, Yerimoti, Yozabadi, Elieli, Isimakiya, Mahati ndi Benaya anali oyangʼanira motsogozedwa ndi Konaniya ndi Simei, mʼbale wake. Iwowa anasankhidwa ndi mfumu Hezekiya ndi Azariya mkulu woyangʼanira Nyumba ya Mulungu.
A Jechiel, Azariasz, Nachat, Asahel, Jerimot, Jozabad, Eliel, Ismakiasz, Machat i Benajasz [byli] nadzorcami pod kierunkiem Konaniasza i jego brata Szimejego, zgodnie z rozkazem króla Ezechiasza i Azariasza, przełożonego domu Bożego.
14 Kore mwana wa Imuna Mlevi, mlonda wa Chipata Chakummawa, amayangʼanira zopereka zaufulu kwa Mulungu, ankagawa zopereka za kwa Yehova ndiponso mphatso zopatulika.
Kore, syn Jimny, Lewita, odźwierny [przy bramie] wschodniej, czuwał nad dobrowolnymi ofiarami dla Boga, rozdzielał ofiary PANA i rzeczy najświętsze.
15 Edeni, Miniyamini, Yesuwa, Semaya, Amariya, Sekaniya amamuthandiza mokhulupirika mʼmizinda yonse a ansembe kugawira kwa ansembe anzawo monga mwa magulu awo, aakulu ndi aangʼono omwe.
Jego pomocnikami [byli]: Eden, Miniamin, Jeszua, Szemejasz, Amariasz i Szekaniasz, w miastach kapłanów, aby wiernie rozdawać [zaopatrzenie] swoim braciom według ich zmian, zarówno wielkiemu, jak i małemu;
16 Kuwonjezera apa, amagawira ana aamuna a zaka zitatu kapena kupitirira amene mayina awo anali mʼmbiri ya mibado yawo, amene adzalowe mʼNyumba ya Yehova kugwira ntchito za tsiku ndi tsiku za magulu awo, molingana ndi udindo ndi magulu awo.
A także mężczyznom z ich rodowodu w wieku od trzech lat wzwyż, każdemu wchodzącemu do domu PANA, dzienny dział za ich służbę, według ich obowiązków i zmian;
17 Ndipo anazigawa kwa ansembe amene analembetsa mayina awo mwa mbiri ya mabanja awo, chimodzimodzinso Alevi amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirira molingana ndi udindo wawo ndi magulu awo.
Zarówno tym, którzy spośród rodowodu kapłańskiego byli policzeni według ich rodów, jak i Lewitom od dwudziestego roku życia wzwyż, według ich obowiązków i zmian;
18 Iwo anaphatikizanso ana onse aangʼono, akazi ndiponso ana aamuna ndi ana aakazi a gulu lonse amene analembedwa mʼmbiri ya mibado yawo iyi, pakuti anakhulupirika pa kudzipatula okha.
Oraz wszystkim dzieciom, żonom, synom i córkom z ich rodu, [wśród] całego zgromadzenia. Oni bowiem, pełniąc swój urząd, poświęcali się w świętości.
19 Kunena za ansembe, zidzukulu za Aaroni, amene amakhala mʼminda yozungulira mizinda yawo kapena mzinda wina uliwonse, anthu anasankhidwa mowatchula mayina kuti azipereka magawo kwa munthu wamwamuna aliyense pakati pawo ndiponso kwa onse amene analembedwa mʼmbiri ya mibado ya Alevi.
Także i synom Aarona, kapłanom [mieszkającym] na polach pastwisk ich miast, we wszystkich miastach, tym mężczyznom, wyznaczonym imiennie, aby oddano należny dział wszystkim mężczyznom spośród kapłanów oraz wszystkim spisanym według rodowodów spośród Lewitów.
20 Izi ndi zimene Hezekiya anachita mu Yuda monse, kuchita zabwino, zolungama ndi zokhulupirika pamaso pa Yehova Mulungu wake.
Tak Ezechiasz uczynił w całej Judzie i czynił [to, co] dobre i prawe, i prawdziwe przed PANEM, swoim Bogiem.
21 Pa chilichonse chimene anachita pa ntchito ya Nyumba ya Mulungu ndi pa kumvera malangizo ndi malamulo, iye anafunafuna Mulungu wake ndipo anagwira ntchito ndi mtima wake wonse. Ndipo zinthu zimamuyendera bwino.
W każdej sprawie, którą rozpoczął w służbie domu Bożego, w prawie i przykazaniach, by szukać swojego Boga, czynił [wszystko] z całego serca, i szczęściło mu się.

< 2 Mbiri 31 >