< 2 Mbiri 31 >

1 Zonse zitatha, Aisraeli onse amene anali kumeneko anapita ku mizinda ya ku Yuda, nakaphwanya miyala yachipembedzo ndi kudula mitengo ya mafano a Asera. Iwo anakawononga malo achipembedzo ndi maguwa ansembe amene anali mʼdziko lonse la Yuda, Benjamini, Efereimu ndi Manase. Atawononga zonsezi, Aisraeli anabwerera ku mizinda yawo ndi ku malo awo.
Now when all this was finished, all the people of Israel who were there went out to the cities of Judah and broke to pieces the stone pillars and they cut down the Asherah poles, and they broke down the high places and the altars in all of Judah and Benjamin, and in Ephraim and Manasseh, until they had destroyed them all. Then all the people of Israel returned, every one to his own possession and his own city.
2 Hezekiya anakhazikitsa magulu a ansembe ndi Alevi, gulu lililonse monga mwa ntchito zawo ngati ansembe kapena Alevi, kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano, kutumikira, kuyamikira ndi kuyimba matamando pa zipata za ku malo okhala Yehova.
Hezekiah assigned the divisions of the priests and the Levites organized by their divisions, each man assigned to his work, both the priests and the Levites. He assigned them to make the burnt offerings and fellowship offerings, to serve, to give thanks, and to praise at the gates of Yahweh's temple.
3 Kuchokera pa chuma chake, mfumu inapereka nsembe zopsereza za mmawa ndi madzulo ndiponso nsembe zopsereza za pa Chikondwerero cha Masabata, Chikondwerero cha Mwezi Watsopano ndipo inakhazikitsa zikondwerero monga zinalembedwera mʼmalamulo a Yehova.
He also assigned the king's portion for the burnt offerings from his own possessions, that is, for the morning and evening burnt offerings, and the burnt offerings for the Sabbath days, the new moons, and the fixed festivals, as it was written in the law of Yahweh.
4 Iyo inalamula anthu amene amakhala mu Yerusalemu kupereka gawo lawo kwa ansembe ndi Alevi kuti iwowo adzipereke ku malamulo a Yehova.
Moreover, he commanded the people who lived in Jerusalem to give the portion for the priests and the Levites, so that they might concentrate on obeying the law of Yahweh.
5 Lamuloli atangolilengeza, Aisraeli anapereka mowolowamanja zipatso zoyamba kucha za tirigu, vinyo watsopano, mafuta ndi uchi ndi zonse zomwe nthaka yawo inabereka. Anabweretsa zochuluka kwambiri, chakhumi cha chilichonse.
As soon as the command was sent out, the people of Israel generously gave the firstfruits of grain, new wine, oil, honey, and from all their harvest of the field. They brought in a tithe of everything, which was a great quantity.
6 Aisraeli ndi Ayuda amene amakhala mʼmizinda ya Yuda anabweretsanso chakhumi cha ngʼombe zawo ndi nkhosa ndi chakhumi cha zinthu zoyera zoperekedwa kwa Yehova Mulungu wawo, ndipo anaziyika mʼmilumilu.
The people of Israel and Judah who lived in the cities of Judah also brought in the tithe of cattle and sheep, and the tithe of the holy things that were set apart to Yahweh their God, and they piled them up in heaps.
7 Anayamba kuchita izi mwezi wachitatu ndipo anatsiriza mwezi wachisanu ndi chiwiri.
It was in the third month when they began piling up their contribution in heaps, and they finished in the seventh month.
8 Hezekiya ndi akuluakulu ake atabwera ndi kuona miluyo, anatamanda Yehova ndi kudalitsa anthu ake, Aisraeli.
When Hezekiah and the leaders came and saw the heaps, they blessed Yahweh and his people Israel.
9 Hezekiya anafunsa ansembe ndi Alevi za miluyi;
Then Hezekiah questioned the priests and the Levites about the heaps.
10 ndipo Azariya, mkulu wa ansembe, ochokera ku banja la Zadoki anayankha kuti, “Kuyambira pamene anthu anayamba kubweretsa zopereka zawo ku Nyumba ya Yehova ife takhala ndi zokwanira kudya ndi zina zambiri zosunga, chifukwa Yehova wadalitsa anthu ake, ndipo mulu umenewu ndiye zotsala.”
Azariah, the chief priest, of the house of Zadok, answered him and said, “Since the people began to bring the offerings into the house of Yahweh, we have eaten and had enough, and have plenty left over, for Yahweh has blessed his people. What was left over is this large amount here.”
11 Hezekiya analamula kuti akonze zipinda zosungiramo za mʼNyumba ya Yehova, ndipo izi zinachitika.
Then Hezekiah commanded storerooms to be prepared in the house of Yahweh, and they prepared them.
12 Ndipo iwo mokhulupirika anabweretsa zopereka, chakhumi ndi mphatso zopatulika. Konaniya Mlevi ndiye amayangʼanira zinthu zimenezi ndipo mʼbale wake Simei ndiye anali wachiwiri wake.
Then they faithfully brought in the offerings, the tithes and the things that belonged to Yahweh. Konaniah the Levite was the manager in charge of them, and his brother Shimei was second to him.
13 Yehieli, Azaziya, Nahati, Asaheli, Yerimoti, Yozabadi, Elieli, Isimakiya, Mahati ndi Benaya anali oyangʼanira motsogozedwa ndi Konaniya ndi Simei, mʼbale wake. Iwowa anasankhidwa ndi mfumu Hezekiya ndi Azariya mkulu woyangʼanira Nyumba ya Mulungu.
Jehiel, Azaziah, Nahath, Asahel, Jerimoth, Jozabad, Eliel, Ismakiah, Mahath, and Benaiah were managers under the hand of Konaniah and Shimei his brother, by appointment of Hezekiah, the king, and Azariah, the official over the house of God.
14 Kore mwana wa Imuna Mlevi, mlonda wa Chipata Chakummawa, amayangʼanira zopereka zaufulu kwa Mulungu, ankagawa zopereka za kwa Yehova ndiponso mphatso zopatulika.
Kore son of Imnah the Levite, the porter at the east gate, was over the free will offerings of God, in charge of distributing the offerings to Yahweh and the most holy offerings.
15 Edeni, Miniyamini, Yesuwa, Semaya, Amariya, Sekaniya amamuthandiza mokhulupirika mʼmizinda yonse a ansembe kugawira kwa ansembe anzawo monga mwa magulu awo, aakulu ndi aangʼono omwe.
Under him were Eden, Miniamin, Jeshua, Shemaiah, Amariah, and Shecaniah, in the cities of the priests. They filled offices of trust, in order to give these offerings to their brothers division by division, to both the important and the unimportant.
16 Kuwonjezera apa, amagawira ana aamuna a zaka zitatu kapena kupitirira amene mayina awo anali mʼmbiri ya mibado yawo, amene adzalowe mʼNyumba ya Yehova kugwira ntchito za tsiku ndi tsiku za magulu awo, molingana ndi udindo ndi magulu awo.
They also gave to those males three years old and up, who were listed in the records of their ancestors who entered the house of Yahweh, as required by the daily schedule, to do the work in their offices and their divisions.
17 Ndipo anazigawa kwa ansembe amene analembetsa mayina awo mwa mbiri ya mabanja awo, chimodzimodzinso Alevi amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirira molingana ndi udindo wawo ndi magulu awo.
They distributed to the priests according to the records of their ancestors, and the same to the Levites twenty years old and more, according to their offices and their divisions.
18 Iwo anaphatikizanso ana onse aangʼono, akazi ndiponso ana aamuna ndi ana aakazi a gulu lonse amene analembedwa mʼmbiri ya mibado yawo iyi, pakuti anakhulupirika pa kudzipatula okha.
They included all their little ones, their wives, their sons, and their daughters, through the whole community, for they were faithful in keeping themselves holy.
19 Kunena za ansembe, zidzukulu za Aaroni, amene amakhala mʼminda yozungulira mizinda yawo kapena mzinda wina uliwonse, anthu anasankhidwa mowatchula mayina kuti azipereka magawo kwa munthu wamwamuna aliyense pakati pawo ndiponso kwa onse amene analembedwa mʼmbiri ya mibado ya Alevi.
For the priests, the descendants of Aaron, who were in the fields of the villages belonging to their cities, or in every city, there were men assigned by name to give portions to all the males among the priests, and to all who were listed in the records of their ancestors as being among the Levites.
20 Izi ndi zimene Hezekiya anachita mu Yuda monse, kuchita zabwino, zolungama ndi zokhulupirika pamaso pa Yehova Mulungu wake.
Hezekiah did this throughout all Judah. He accomplished what was good, right, and faithful before Yahweh, his God.
21 Pa chilichonse chimene anachita pa ntchito ya Nyumba ya Mulungu ndi pa kumvera malangizo ndi malamulo, iye anafunafuna Mulungu wake ndipo anagwira ntchito ndi mtima wake wonse. Ndipo zinthu zimamuyendera bwino.
In every project that he began in the service of the house of God, the law, and the commandments, to seek his God, he performed it with all his heart, and he succeeded.

< 2 Mbiri 31 >