< 2 Mbiri 31 >
1 Zonse zitatha, Aisraeli onse amene anali kumeneko anapita ku mizinda ya ku Yuda, nakaphwanya miyala yachipembedzo ndi kudula mitengo ya mafano a Asera. Iwo anakawononga malo achipembedzo ndi maguwa ansembe amene anali mʼdziko lonse la Yuda, Benjamini, Efereimu ndi Manase. Atawononga zonsezi, Aisraeli anabwerera ku mizinda yawo ndi ku malo awo.
Lolo nasu dagoloba, Isala: ili fi dunu huluane da Yuda moilai bai bagade huluane amoga asili, ogogosu ‘gode’ma nodoma: ne duni bugi, ogogosu uda ‘gode’ Asila agoai loboga hamoi liligi, ogogosu ‘gode’ nodoma: ne oloda amola sogebi, amo huluane gugunufinisi dagoi. Ilia amo hou defele, Yuda soge, Bediamini, Ifala: ime amola Ma: na: se, amo soge huluane ganodini agoane hamonanu, ilia diasuga buhagi.
2 Hezekiya anakhazikitsa magulu a ansembe ndi Alevi, gulu lililonse monga mwa ntchito zawo ngati ansembe kapena Alevi, kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano, kutumikira, kuyamikira ndi kuyimba matamando pa zipata za ku malo okhala Yehova.
Hina bagade Hesigaia da gobele salasu dunu amola Lifai dunu ilia hawa: hamosu ilegesu, amo bu hahamoi. Ilia hawa: hamosu da Wadela: i Hou Dabe Ima: ne gobele salasu ouligisu hou amola Debolo Diasu ganodini Hina Godema nodone sia: ne gadosu ouligisu hou.
3 Kuchokera pa chuma chake, mfumu inapereka nsembe zopsereza za mmawa ndi madzulo ndiponso nsembe zopsereza za pa Chikondwerero cha Masabata, Chikondwerero cha Mwezi Watsopano ndipo inakhazikitsa zikondwerero monga zinalembedwera mʼmalamulo a Yehova.
Hesigaia da hina: fofoi ohe fi amoga ohe hahabe amola daeya gobele salimusa: , gobele salasu ilia Sa: bade eso hamosu, Oubi Gaheabolo Lolo Nasu gobele salasu amola Lolo Nasu eno amo da Hina Gode Ea Sema ganodini dedei, amo huluane hamomusa: e da i.
4 Iyo inalamula anthu amene amakhala mu Yerusalemu kupereka gawo lawo kwa ansembe ndi Alevi kuti iwowo adzipereke ku malamulo a Yehova.
Amola, hina bagade da sia: beba: le, Yelusaleme fi dunu da hahawane dogolegele iasu, amo ilia da gobele salasu dunu amola Lifai fi dunuma ima: ne ilegei, amo ilima i. Bai amo da Lifai fi amola gobele salasu dunu ilia osobo bagade liligi mae dawa: le, Hina Gode Ea Sema dedei hou, amo fawane dawa: le hamomusa: logo doasi.
5 Lamuloli atangolilengeza, Aisraeli anapereka mowolowamanja zipatso zoyamba kucha za tirigu, vinyo watsopano, mafuta ndi uchi ndi zonse zomwe nthaka yawo inabereka. Anabweretsa zochuluka kwambiri, chakhumi cha chilichonse.
Hina bagade da amo hamoma: ne sia: beba: le, Isala: ili fi dunu da ilia gala: ine noga: idafa, waini hano, olife susuligi, agime hano, ifabia dadami amola fage amola ilia liligi huluanedafa nabuane mogi afae, amo huluane gaguli misi.
6 Aisraeli ndi Ayuda amene amakhala mʼmizinda ya Yuda anabweretsanso chakhumi cha ngʼombe zawo ndi nkhosa ndi chakhumi cha zinthu zoyera zoperekedwa kwa Yehova Mulungu wawo, ndipo anaziyika mʼmilumilu.
Dunu huluane ilia da Yuda moilai bai bagade ganodini esalu, ilia da ilia bulamagau amola sibi nabuane mogi, afae gaguli misi. Amola hahawane dogolegele iasu liligi, ilia Hina Godema modale ligiagale imunusa: gaguli misi.
7 Anayamba kuchita izi mwezi wachitatu ndipo anatsiriza mwezi wachisanu ndi chiwiri.
Ilia da oubi osodaga hahawane dogolegele iasu hemone, amola oubi ageyadu eno amoga liligi bagadedafa iasu.
8 Hezekiya ndi akuluakulu ake atabwera ndi kuona miluyo, anatamanda Yehova ndi kudalitsa anthu ake, Aisraeli.
Hina bagade Hesigaia amola eagene ouligisu dunu da amo bagadedafa iasu ba: beba: le, Hina Godema amola Ea Isala: ili dunuma nodoi.
9 Hezekiya anafunsa ansembe ndi Alevi za miluyi;
Hina bagade da gobele salasu dunu amola Lifai fi dunu, ilima amo hahawane iasu hou gilisili sia: dasu.
10 ndipo Azariya, mkulu wa ansembe, ochokera ku banja la Zadoki anayankha kuti, “Kuyambira pamene anthu anayamba kubweretsa zopereka zawo ku Nyumba ya Yehova ife takhala ndi zokwanira kudya ndi zina zambiri zosunga, chifukwa Yehova wadalitsa anthu ake, ndipo mulu umenewu ndiye zotsala.”
Gobele salasu dunu ilia ouligisu dunu A: salaia (Sa: idoge egaga fi dunu) da ema amane sia: i, “Dunu da hahawane dogolegele iasu Debolo Diasuga muni gaguli misi amogainini wali, ninia da ha: i moma: ne defele ba: i dagoi. Amola eno hame mai bagade diala. Hina Gode da ninima hahawane dogolegele hamoiba: le, ninia da amo hou ba: sa.”
11 Hezekiya analamula kuti akonze zipinda zosungiramo za mʼNyumba ya Yehova, ndipo izi zinachitika.
Hina bagade da hamoma: ne sia: beba: le, ilia da liligi ligisisu sesei Debolo Diasu sogebiga momagei.
12 Ndipo iwo mokhulupirika anabweretsa zopereka, chakhumi ndi mphatso zopatulika. Konaniya Mlevi ndiye amayangʼanira zinthu zimenezi ndipo mʼbale wake Simei ndiye anali wachiwiri wake.
Ilia da amo ganodini, hahawane dogolegele iasu liligi amola liligi nabuane mogili afae iasu, amo huluane lidili legei. Ilia da Lifai fi dunu ea dio Gononaia amo sesei ouligima: ne ilegei. Amola e bagia fidima: ne, ea eya Simiai ilegei.
13 Yehieli, Azaziya, Nahati, Asaheli, Yerimoti, Yozabadi, Elieli, Isimakiya, Mahati ndi Benaya anali oyangʼanira motsogozedwa ndi Konaniya ndi Simei, mʼbale wake. Iwowa anasankhidwa ndi mfumu Hezekiya ndi Azariya mkulu woyangʼanira Nyumba ya Mulungu.
Elaha hawa: hamoma: ne, ilia da Lifai fi dunu nabuane ilegei. Ilia dio da Yihaiele, A:isasaia, Na: iha: de, A:sahele, Yelimode, Yosaba: de, Ilaiele, Isimagaia, Ma: iha: de amola Bina: ia. Hina bagade Hesigaia amola gobele salasu ouligisu A: salaia, ela hamoma: ne sia: beba: le, amo hou huluane hamosu.
14 Kore mwana wa Imuna Mlevi, mlonda wa Chipata Chakummawa, amayangʼanira zopereka zaufulu kwa Mulungu, ankagawa zopereka za kwa Yehova ndiponso mphatso zopatulika.
Ilia da Gouli (Imina egefe) amo Hina Godema hahawane dogolegele iamabe amo ouligima: ne ilegei. Gouli da Debolo Diasu gusudili logo ga: su sosodo aligisu dunu ilia bisilua esalu, amola e da amo iasu liligi lidili legei, amola eno dunuma bu iasu.
15 Edeni, Miniyamini, Yesuwa, Semaya, Amariya, Sekaniya amamuthandiza mokhulupirika mʼmizinda yonse a ansembe kugawira kwa ansembe anzawo monga mwa magulu awo, aakulu ndi aangʼono omwe.
Moilai bai bagade oda amo ganodini gobele salasu dunu esalebe ba: i, amoga Lifai dunu eno da Gouli noga: le fidisu. Ilia dio da Idini, Miniamine, Yesua, Siema: ia, A:malaia amola Sieganaia. Ilia da ha: i manu i, amo momogili, ilia na: iyado Lifai fi dunuma (fi mae dawa: le) ilia hawa: hamosu defele, ilima iasu.
16 Kuwonjezera apa, amagawira ana aamuna a zaka zitatu kapena kupitirira amene mayina awo anali mʼmbiri ya mibado yawo, amene adzalowe mʼNyumba ya Yehova kugwira ntchito za tsiku ndi tsiku za magulu awo, molingana ndi udindo ndi magulu awo.
Ilia da dunu amo da lalelegele, ode30 esalu amola amo baligi, ilia eso huluane Debolo Diasu ganodini hawa: hamonanebe defele, ha: i manu ilima i.
17 Ndipo anazigawa kwa ansembe amene analembetsa mayina awo mwa mbiri ya mabanja awo, chimodzimodzinso Alevi amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirira molingana ndi udindo wawo ndi magulu awo.
Ilia da gobele salasu dunu, ilia sosogo fi afae afae amo defele, ilima hawa: hamosu ilegei. Amola Lifai fi dunu amo da lalelegele, ode20esalu amola amo baligi, ilia da amo dunu hawa: hamosu gilisisu afae afae amoma ili ilegele, hawa: hamosu ilegei.
18 Iwo anaphatikizanso ana onse aangʼono, akazi ndiponso ana aamuna ndi ana aakazi a gulu lonse amene analembedwa mʼmbiri ya mibado yawo iyi, pakuti anakhulupirika pa kudzipatula okha.
Ili huluane amola ilia uda amola mano amola fofoi mano, idili dedei dagoi ba: i. Bai ilia da Debolo Diasu ganodini gasia o yoga udigili sema hawa: hamomusa: momagele ouesalumusa: ilegei.
19 Kunena za ansembe, zidzukulu za Aaroni, amene amakhala mʼminda yozungulira mizinda yawo kapena mzinda wina uliwonse, anthu anasankhidwa mowatchula mayina kuti azipereka magawo kwa munthu wamwamuna aliyense pakati pawo ndiponso kwa onse amene analembedwa mʼmbiri ya mibado ya Alevi.
Gobele salasu dunu amo da Elane egaga fi ilia moilai bai bagade ganodini esalu o ohe fofole nasu soge amo gadenene dialu amoga esalu, amo moloi dunu mogili da gobele salasu dunumusu amola Lifai fi dunu amo da fi idisu meloaga dedei, ilima ha: i manu sagosu.
20 Izi ndi zimene Hezekiya anachita mu Yuda monse, kuchita zabwino, zolungama ndi zokhulupirika pamaso pa Yehova Mulungu wake.
Yuda soge huluane ganodini, hina bagade Hesigaia da ea Hina Gode hahawane ba: ma: ne fawane hamosu.
21 Pa chilichonse chimene anachita pa ntchito ya Nyumba ya Mulungu ndi pa kumvera malangizo ndi malamulo, iye anafunafuna Mulungu wake ndipo anagwira ntchito ndi mtima wake wonse. Ndipo zinthu zimamuyendera bwino.
E da ea hawa: hamosu huluane didi hamosu. Bai ea da molole Debolo hawa: hamosu amola Gode Ea Sema amoma fa: no bobogebeba: le, e da ea Hina Godema madelagiwane amola asigiwane hamosu.