< 2 Mbiri 30 >
1 Hezekiya anatumiza uthenga mʼdziko lonse la Israeli ndi ku Yuda ndiponso analemba makalata ku Efereimu ndi Manase, oyitana anthu kuti abwere ku Nyumba ya Yehova ku Yerusalemu kudzakondwerera Paska wa Yehova, Mulungu wa Israeli.
І послав Єзекія по всьому Ізраїлю та по Юдеї, а також написав листи́ до країв Єфрема та Манасії, щоб прийшли до Господнього дому в Єрусалимі, щоб спра́вити Пасху для Господа, Ізраїлевого Бога.
2 Mfumu ndi akuluakulu ake pamodzi ndi anthu onse a mu Yerusalemu anagwirizana kuti akondwerere Paska pa mwezi wachiwiri.
І радився цар і зверхники його та ввесь збір в Єрусалимі, щоб справити Пасху другого місяця.
3 Iwo sanathe kukondwerera pa nthawi yake chifukwa si ansembe ambiri amene anadziyeretsa ndiponso anthu anali asanasonkhane mu Yerusalemu.
Бо не могли справити її того ча́су, бо священики не освятилися в потрі́бному числі, а наро́д не зібрався до Єрусалиму.
4 Chikonzerochi chinaoneka kuti chinali chabwino kwa mfumu pamodzi ndi anthu onse.
І була вгодна та річ в оча́х царевих та в оча́х усього збору.
5 Iwo anagwirizana zoti alengeze mu Israeli monse kuyambira ku Beeriseba mpaka ku Dani, kuyitana anthu kuti abwere ku Yerusalemu ndi kudzakondwerera Paska wa Yehova, Mulungu wa Israeli. Si ambiri amene ankachita chikondwererochi monga momwe kunalembedwera.
І вони постанови́ли оголоси́ти по всьому Ізраїлю від Беер-Шеви й аж до Дана, щоб прихо́дили справити Пасху для Господа, Ізраїлевого Бога, в Єрусалим, бо не часто робили її так, як написано.
6 Molamulidwa ndi mfumu, amithenga anapita mu Israeli yense ndi Yuda ndi makalata ochokera kwa mfumu ndi kwa akuluakulu ake, olembedwa kuti, “Aisraeli bwererani kwa Yehova, Mulungu wa Abrahamu, Isake ndi Israeli, kuti abwerere kwa inu amene mwatsala, amene mwapulumuka mʼdzanja la mafumu a ku Asiriya.
І пішли бігуни́ з листа́ми від царя та його зверхників по всьому Ізраїлі та Юдеї, та за нака́зом царя говорили: „Ізра́їлеві сини, верніться до Господа, Бога Авраамового, Ісакового та Ізраїлевого, — і Він пове́рнеться до останку, позосталого вам із руки асирійських царів.
7 Musakhale ngati makolo anu ndi abale anu, amene anali osakhulupirika kwa Yehova Mulungu wa makolo awo kotero kuti anawachititsa kuti akhale chinthu chochititsa mantha, monga mukuoneramu.
І не будьте такі, як ваші батьки та як ваші брати, що спроневі́рилися Господе́ві, Богові їхніх батьків, — і Він дав їх на спусто́шення, як ви бачите.
8 Musawumitse khosi monga anachitira makolo anu, Gonjerani Yehova. Bwerani ku malo opatulika, amene anawapatula kwamuyaya. Tumikirani Yehova Mulungu wanu kuti mkwiyo wake ukuchokereni.
Тепер не будьте твердоши́ї, як ваші батьки. Покоріться Господе́ві, і ввійдіть до святині Його, яку Він освятив навіки, і служіть Господе́ві, Богові вашому, і Він відве́рне від вас жар гніву Свого.
9 Ngati inu mubwerera kwa Yehova, pamenepo abale anu ndi ana anu adzachitiridwa chifundo ndi amene anawagwira ukapolo ndipo adzabwereranso ku dziko lino pakuti Yehova, Mulungu wanu ndi wokoma mtima ndi wachifundo. Iye sadzakufulatirani ngati inuyo mubwerera kwa Iye.”
Бо як ви наве́рнетесь до Господа, то брати́ ваші та ваші сини зна́йдуть милосердя в своїх поневі́льників, і зможуть вернутися до цього Кра́ю, — бо милости́вий і милосердний Господь, Бог ваш, і Він не відве́рне лиця від вас, якщо ви наве́рнетеся до Нього“.
10 Amithenga aja anapita mzinda ndi mzinda wa ku Efereimu ndi Manase mpaka ku Zebuloni, koma anthu anawanyoza ndi kuwachita chipongwe.
І сторожі́ все перехо́дили з міста до міста по кра́ю Єфремовому та Манасіїному й аж до Завуло́на. Та люди глузува́ли з них, і висміювали їх.
11 Komabe anthu ena a ku Aseri, Manase ndi Zebuloni anadzichepetsa ndipo anapita ku Yerusalemu.
Тільки люди з Асира, і Манасії та з Завулона впокори́лися, і поприхо́дили до Єрусалиму.
12 Dzanja la Mulungu linalinso pa anthu a ku Yuda, kuwapatsa mtima umodzi wochita zimene mfumu ndi akuluakulu ake analamula potsata mawu a Yehova.
Також в Юдеї була Божа рука, щоб дати їм одне серце для ви́конання наказу царя та зверхників за Господнім словом.
13 Gulu lalikulu la anthu linasonkhana mu Yerusalemu kudzachita chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti pa mwezi wachiwiri.
I зібрався до Єрусалиму числе́нний народ, щоб справити свято Опрі́сноків другого місяця, збір дуже числе́нний.
14 Anachotsa mu Yerusalemu maguwa ofukizira lubani ndipo anakawaponya mʼchigwa cha Kidroni.
І встали вони, і повикида́ли і́дольські же́ртівники, що були в Єрусалимі, і повикида́ли всі кадильниці, та й повкидали до долини Кедро́н.
15 Iwo anapha mwana wankhosa wa Paska pa tsiku la 14 la mwezi wachiwiri. Ansembe ndi Alevi anachita manyazi ndipo anadziyeretsa ndi kubweretsa nsembe zopsereza ku Nyumba ya Yehova.
І зарізали пасха́льне ягня чотирнадцятого дня другого місяця, а священики та Левити засоро́милися й освятилися, і прине́сли цілопа́лення до Господнього дому.
16 Ndipo anakhala mʼmalo awo a nthawi zonse potsatira zolembedwa mʼmalamulo a Mose munthu wa Mulungu. Ansembe anawaza magazi amene anawapatsa Alevi.
І постава́ли вони на своє́му місці за їхнім правом, за Зако́ном Мойсея, чоловіка Божого. Священики кропили кров, беручи́ з руки Левитів.
17 Popeza ambiri mʼgululo anali asanadziyeretse, Alevi anapha ana ankhosa a Paska a iwo amene, mwa mwambo, anali osayeretsedwa ndipo sakanatha kupereka ana ankhosa awo kwa Yehova.
Багато бо було в зборі, що не освятилися, тому Левити були для рі́зання пасха́льних ягнят за кожного нечистого, щоб посвятити для Господа.
18 Ngakhale kuti ambiri mwa anthu ochokera ku Efereimu, Manase, Isakara ndi Zebuloni sanadziyeretse okha, komabe anadya Paska motsutsana ndi zimene zinalembedwa. Koma Hezekiya anawapempherera, kunena kuti, “Yehova wabwino, khululukirani aliyense
Бо бе́зліч наро́ду, багато з Єфрема та Манасії, Іссахара та Завулона не очи́стилися, але їли Пасху, не так, як написано. Та Єзекія молився за них, говорячи: „Добрий Господь про́стить кожному,
19 amene wayika mtima wake kufunafuna Yehova, Mulungu wa makolo ake, ngakhale ali wosayeretsedwa molingana ndi malamulo a malo opatulika.”
хто все своє серце міцно встанови́в, щоб звертатися до Бога, Господа, Бога батьків своїх, хоч не зробив він за правилами чистости святині“.
20 Ndipo Yehova anamvera Hezekiya ndipo anachiritsa anthuwo.
І послухав Господь Єзекію, і прости́в народ.
21 Aisraeli amene anali mu Yerusalemu anachita chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti kwa masiku asanu ndi awiri akusangalala kwambiri, pamene Alevi ndi ansembe amayimbira Yehova tsiku lililonse, akuyimbira zida zamatamando za Yehova.
І справля́ли Ізраїлеві сини, що знахо́дилися в Єрусалимі, свято Опрісноків сім день з великою радістю, а Левити та священики день-у-день сла́вили Господа всією силою.
22 Hezekiya anayankhula molimbikitsa Alevi onse amene anaonetsa kumvetsa bwino za kutumikira Yehova. Kwa masiku asanu ndi awiri anadya gawo lawo ndi kupereka nsembe zachiyanjano ndi kutamanda Yehova, Mulungu wa makolo awo.
І промовляв Єзекія до серця всіх Левитів, що мали добре розуміння для Господа. І їли святко́ву жертву сім день, і прино́сили мирні жертви, і сповіда́лися Господе́ві, Богові батьків своїх.
23 Ndipo msonkhano wonse unagwirizana zopitiriza chikondwerero kwa masiku ena asanu ndi awiri. Kotero kwa masiku ena asanu ndi awiri anachita chikondwererocho mosangalala.
І ввесь збір нара́дився справити свято ще другі сім день, — і справля́ли сім день в радості.
24 Hezekiya mfumu ya Yuda anapereka ngʼombe zamphongo 1,000 ndi nkhosa ndi mbuzi 7,000 ku msonkhanoko ndipo akuluakulu ake anapereka ngʼombe zamphongo 1,000, nkhosa ndi mbuzi 10,000. Ansembe ambiri anadziyeretsa.
Бо Єзекія, цар Юдин, дав для збору тисячу биків і сім тисяч худоби дрібно́ї, а зверхники дали́ для збору тисячу биків і десять тисяч худоби дрібно́ї. І освятилося багато священиків.
25 Gulu lonse la ku Yuda linasangalala, pamodzi ndi ansembe ndi Alevi ndi onse amene anasonkhana ochokera ku Israeli, kuphatikizanso alendo amene anachokera ku Israeli ndi amene amakhala ku Yuda.
І радів увесь Юдин збір, і священики та Левити, і ввесь збір, що прийшов з Ізраїля, і прихо́дьки, що поприхо́дили з Ізраїлевого Краю, та ті, що сиділи в Юдеї.
26 Munali chikondwerero chachikulu mu Yerusalemu, pakuti kuyambira masiku a Solomoni mwana wa Davide mfumu ya Israeli sizinachitikepo zotere mu Yerusalemu.
І була велика радість в Єрусалимі, бо від днів Соломона, Давидового сина, Ізраїлевого царя, не було такого, як оце в Єрусалимі!
27 Ansembe ndi Alevi anayimirira kudalitsa anthu, ndipo Mulungu anawamvera pakuti pemphero lawo linafika kumwamba, malo ake oyera.
І встали священики та Левити, і поблагословили наро́д. І почутий був їхній голос, а їхня молитва дійшла до оселі святости Його́, — до небе́с!