< 2 Mbiri 3 >

1 Pamenepo Solomoni anayamba kumanga Nyumba ya Yehova mu Yerusalemu pa Phiri la Moriya, pamene Yehova anaonekera Davide abambo ake. Panali pabwalo lopunthirapo tirigu la Arauna Myebusi, malo amene anapereka Davide.
USolomoni waseqala ukwakha indlu yeNkosi eJerusalema entabeni yeMoriya lapho eyabonakala khona kuDavida uyise, endaweni uDavida ayilungisayo ebaleni lokubhulela likaOrinani umJebusi.
2 Iye anayamba kumanga pa tsiku lachiwiri la mwezi wachiwiri mʼchaka chachinayi cha ulamuliro wake.
Waseqalisa ukwakha ngenyanga yesibili ngolwesibili ngomnyaka wesine wokubusa kwakhe.
3 Maziko amene Solomoni anayika pomanga Nyumba ya Mulungu ndi awa: Mulitali munali mamita 27, mulifupi munali mamita asanu ndi anayi (potsata miyeso yakale).
Lalezi yizisekelo zikaSolomoni zokwakha indlu kaNkulunkulu. Ubude ngezingalo ngesilinganiso esidala babuzingalo ezingamatshumi ayisithupha, lobubanzi buzingalo ezingamatshumi amabili.
4 Chipinda cha polowera mulitali mwake chinali mamita asanu ndi anayi ofanana ndi mulifupi mwake mwa nyumbayo. Msinkhu wake unali mamita 54. Iye anakuta nyumbayo mʼkati mwake ndi golide woyengeka bwino.
Lekhulusi elaliphambili, ubude njengobubanzi bendlu babuzingalo ezingamatshumi amabili, lokuphakama kwakuzingalo ezilikhulu lamatshumi amabili. Wayihuqa ngaphakathi ngegolide elicwengekileyo.
5 Chipinda chachikulu, khoma lake anakhomera matabwa a payini ndipo analikutira ndi golide wabwino ndi kulikongoletsa ndi zithunzi za kanjedza ndi maunyolo.
Lendlu enkulu wayembesa ngezigodo zefiri, wayihuqa ngegolide elihle, wamisa phezu kwayo amalala lamaketane.
6 Iye anakongoletsa Nyumba ya Mulunguyo ndi miyala yokongola. Ndipo golide amene anagwiritsa ntchito anali golide wa ku Paravaimu.
Wayembesela ubuhle indlu ngamatshe aligugu; njalo igolide laliligolide leParivayimi.
7 Iye anakutira ndi golide mitanda ya ku denga, maferemu a zitseko, makoma ndi zitseko za Nyumba ya Mulungu, ndipo anajambula Akerubi mʼmakoma mwake.
Waseyihuqa indlu, imijabo, imigubazi, lemiduli yayo, leminyango yayo ngegolide, wabaza ngokugubha amakherubhi emidulwini.
8 Iye anamanga Malo Opatulika Kwambiri ndipo mulitali mwake munali mofanana ndi mulifupi mwa Nyumba mamita asanu ndi anayi. Anakuta mʼkati mwake ndi golide wosalala wolemera matani makumi awiri.
Wasesenza indlu yengcwele yezingcwele; ubude bayo njengobubanzi bendlu babuzingalo ezingamatshumi amabili, lobubanzi bayo buzingalo ezingamatshumi amabili; wayihuqa ngegolide elihle kwaze kwaba ngamathalenta angamakhulu ayisithupha.
9 Misomali yagolide imalemera magalamu 570. Anakutanso ndi golide zipinda zapamwamba.
Lesisindo sezipikili saze saba ngamashekeli egolide angamatshumi amahlanu. Wawahuqa amakamelo aphezulu ngegolide.
10 Ku Malo Opatulika Kwambiri iye anapangako Akerubi awiri achitsulo ndipo anawakuta ndi golide.
Wasesenza endlini yengcwele yezingcwele amakherubhi amabili ngomsebenzi obaziweyo, wawahuqa ngegolide.
11 Kutalika kwa mapiko onse a Akerubi kunali mamita asanu ndi anayi. Phiko la Kerubi woyamba linali loposerapo mamita awiri ndipo limakhudza khoma la Nyumba ya Mulungu, pamene phiko linalo, lotalikanso koposerapo mamita awiri, limakhudza phiko la Kerubi winayo.
Lempiko zamakherubhi, ubude bazo babuzingalo ezingamatshumi amabili. Uphiko lwelilodwa lwaluzingalo ezinhlanu lufinyelela emdulini wendlu, lolunye uphiko lwaluzingalo ezinhlanu lufinyelela ophikweni lwelinye ikherubhi.
12 Chimodzimodzinso phiko la Kerubi wachiwiri linali loposerapo mamita awiri ndipo limakhudza mbali ina ya khoma la Nyumba ya Mulungu, ndipo linalo limene linalinso loposera mamita awiri, limakhudza phiko la Kerubi woyamba uja.
Ngokunjalo uphiko lwelinye ikherubhi lwaluzingalo ezinhlanu lufinyelela emdulini wendlu; lolunye uphiko lwaluzingalo ezinhlanu lunamathele ephikweni lwelinye ikherubhi.
13 Mapiko a Akerubiwa akawatambasula amatalika mamita asanu ndi anayi. Akerubiwa anayimirira pa mapazi awo, kuyangʼana chipinda chachikulu.
Impiko zalamakherubhi zeluleka ingalo ezingamatshumi amabili; njalo ema ngenyawo zawo, lobuso bawo bukhangele ngasendlini.
14 Solomoni anapanga nsalu zotchingira zobiriwira, zapepo ndi zofiira ndi nsalu zofewa zosalala, atajambulapo Akerubi.
Wasesenza iveyili ngokuluhlaza okwesibhakabhaka lokuyibubende lokubomvu langelembu elicolekileyo kakhulu, wabeka kulo amakherubhi.
15 Kutsogolo kwa Nyumba ya Mulungu anamangako zipilala ziwiri, zimene zonse pamodzi zinali zotalika mamita khumi ndi asanu ndi theka; chipilala chilichonse chinali ndi mutu woposera mamita awiri.
Wasesenza phambi kwendlu insika ezimbili, ubude babuzingalo ezingamatshumi amathathu lanhlanu, lesiduku phezu kwengqonga yayo buzingalo ezinhlanu.
16 Iye anapanga maunyolo olumikizanalumikizana ndipo anawayika pamwamba pa zipilalazo. Anapanganso makangadza 100 ndipo anawalumikiza ku maunyolo aja.
Wasesenza amaketane njengendaweni yelizwi, wawafaka esihlokweni sezinsika; wenza lamapomegranati alikhulu, wawafaka emaketaneni.
17 Solomoni anayimika nsanamirazo kutsogolo kwa Nyumba ya Mulungu, imodzi mbali ya kummwera ndi inayo mbali ya kumpoto. Nsanamira ya kummwera anayitcha Yakini ndipo ya kumpoto anayitcha Bowazi.
Wasemisa izinsika ngaphambi kwethempeli, enye ngakwesokunene, lenye ngakwesokhohlo; wasebiza ibizo lengakwesokunene uJakini, lebizo lengakwesokhohlo uBhowazi.

< 2 Mbiri 3 >