< 2 Mbiri 3 >

1 Pamenepo Solomoni anayamba kumanga Nyumba ya Yehova mu Yerusalemu pa Phiri la Moriya, pamene Yehova anaonekera Davide abambo ake. Panali pabwalo lopunthirapo tirigu la Arauna Myebusi, malo amene anapereka Davide.
USolomoni waseqalisa ukwakha ithempeli likaThixo eJerusalema eNtabeni yaseMoriya, lapho uThixo wayeke waziveza khona phambi kukayise uDavida. Kwakusesizeni sokubhulela amabele sika-Onani umJebusi, indawo eyayilungiselelwe nguDavida.
2 Iye anayamba kumanga pa tsiku lachiwiri la mwezi wachiwiri mʼchaka chachinayi cha ulamuliro wake.
Waqalisa ukwakha ngosuku lwesibili lwenyanga yesibili ngomnyaka wesine wokubusa kwakhe.
3 Maziko amene Solomoni anayika pomanga Nyumba ya Mulungu ndi awa: Mulitali munali mamita 27, mulifupi munali mamita asanu ndi anayi (potsata miyeso yakale).
Isisekelo sesakhiwo sethempeli likaNkulunkulu esasimiswe nguSolomoni sasizingalo ezingamatshumi ayisithupha ubude baso njalo sibanzi okwezingalo ezingamatshumi amabili (kuyisilinganiso sezingalo zakudala).
4 Chipinda cha polowera mulitali mwake chinali mamita asanu ndi anayi ofanana ndi mulifupi mwake mwa nyumbayo. Msinkhu wake unali mamita 54. Iye anakuta nyumbayo mʼkati mwake ndi golide woyengeka bwino.
Umkhandlwana owawuphambi kwethempeli wawubanzi okwezingalo ezingamatshumi amabili ulingana lowethempeli njalo umude ukuyaphezulu lakho kuzingalo ezingamatshumi amabili. Ngaphakathi wagudula ngegolide elihle.
5 Chipinda chachikulu, khoma lake anakhomera matabwa a payini ndipo analikutira ndi golide wabwino ndi kulikongoletsa ndi zithunzi za kanjedza ndi maunyolo.
Wabethela indlu yalo enkulu ngamapulanka ephayini wasehuqa ngegolide elicengekileyo wacecisa ngokucomba amalala lemiceco yamaketane.
6 Iye anakongoletsa Nyumba ya Mulunguyo ndi miyala yokongola. Ndipo golide amene anagwiritsa ntchito anali golide wa ku Paravaimu.
Wagqizisa ithempeli ngamatshe aligugu. Igolide alisebenzisayo kwakuligolide lePharivayimu.
7 Iye anakutira ndi golide mitanda ya ku denga, maferemu a zitseko, makoma ndi zitseko za Nyumba ya Mulungu, ndipo anajambula Akerubi mʼmakoma mwake.
Wasegudula ingaphakathi yophahla lemijabo yakhona, imigubazi, imiduli lezivalo zethempeli ngegolide, njalo wabazela amakherubhi emidulini.
8 Iye anamanga Malo Opatulika Kwambiri ndipo mulitali mwake munali mofanana ndi mulifupi mwa Nyumba mamita asanu ndi anayi. Anakuta mʼkati mwake ndi golide wosalala wolemera matani makumi awiri.
Wakha iNdawo eNgcwelengcwele, ubude bayo bulingana lobubanzi bethempeli, izingalo ezingamatshumi amabili ubude njalo ezingamatshumi amabili ububanzi bayo. Wagudula ngaphakathi ngamathalenta angamakhulu ayisithupha egolide elicengekileyo.
9 Misomali yagolide imalemera magalamu 570. Anakutanso ndi golide zipinda zapamwamba.
Izipikili zegolide zilesisindo samashekeli angamatshumi amahlanu. Wabuye wagudula ngegolide izindawo ezingaphezulu.
10 Ku Malo Opatulika Kwambiri iye anapangako Akerubi awiri achitsulo ndipo anawakuta ndi golide.
ENdaweni eNgcwelengcwele wenza amakherubhi abaziweyo wawahuqa ngegolide.
11 Kutalika kwa mapiko onse a Akerubi kunali mamita asanu ndi anayi. Phiko la Kerubi woyamba linali loposerapo mamita awiri ndipo limakhudza khoma la Nyumba ya Mulungu, pamene phiko linalo, lotalikanso koposerapo mamita awiri, limakhudza phiko la Kerubi winayo.
Amaphiko amakherubhi nxa evulekile eyizingalo ezingamatshumi amabili. Uphiko olulodwa lwekherubhi lakuqala lwaluzingalo ezinhlanu ubude balo njalo luthinta umduli wethempeli, kusithi olunye uphiko, lalo luzingalo ezinhlanu, luthinta uphiko lwelinye ikherubhi.
12 Chimodzimodzinso phiko la Kerubi wachiwiri linali loposerapo mamita awiri ndipo limakhudza mbali ina ya khoma la Nyumba ya Mulungu, ndipo linalo limene linalinso loposera mamita awiri, limakhudza phiko la Kerubi woyamba uja.
Ngokufananayo uphiko lwekherubhi lesibili lwaluzingalo ezinhlanu ubude balo lalo luthinta omunye umduli wethempeli, njalo kusithi olunye uphiko lalo oluzingalo ezinhlanu ubude balo, luthinta uphiko lwekherubhi lakuqala.
13 Mapiko a Akerubiwa akawatambasula amatalika mamita asanu ndi anayi. Akerubiwa anayimirira pa mapazi awo, kuyangʼana chipinda chachikulu.
Amaphiko amakherubhi ayechaye okuzingalo ezingamatshumi amabili. Ayemi ngezinyawo zawo, ekhangele indlu enkulu.
14 Solomoni anapanga nsalu zotchingira zobiriwira, zapepo ndi zofiira ndi nsalu zofewa zosalala, atajambulapo Akerubi.
Wenza ikhetheni ngelembu eliluhlaza, leliyibubende lelibomvu, langelineni elicolekileyo, welukela imifanekiso yamakherubhi kilo.
15 Kutsogolo kwa Nyumba ya Mulungu anamangako zipilala ziwiri, zimene zonse pamodzi zinali zotalika mamita khumi ndi asanu ndi theka; chipilala chilichonse chinali ndi mutu woposera mamita awiri.
Ngapha ngaphambi kwethempeli wamisa insika ezimbili, zona zombili zazizinde okwezingalo ezingamatshumi amathathu lanhlanu, ngalinye lilesiduku phezulu esilingana izingalo ezinhlanu.
16 Iye anapanga maunyolo olumikizanalumikizana ndipo anawayika pamwamba pa zipilalazo. Anapanganso makangadza 100 ndipo anawalumikiza ku maunyolo aja.
Wenza amaketane aphotheneyo wawabeka phezu kwezinsika. Njalo wenza amaphomegranathi alikhulu wawanamathisela emaketaneni.
17 Solomoni anayimika nsanamirazo kutsogolo kwa Nyumba ya Mulungu, imodzi mbali ya kummwera ndi inayo mbali ya kumpoto. Nsanamira ya kummwera anayitcha Yakini ndipo ya kumpoto anayitcha Bowazi.
Wasesakha izinsika zaphansi kwethempeli, eyinye ngezansi eyinye layo ngenyakatho. Insika engezansi wayibiza ngokuthi Jakhini kwathi eyenyakatho wayibiza ngokuthi Bhowazi.

< 2 Mbiri 3 >