< 2 Mbiri 29 >

1 Hezekiya anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 29. Dzina la amayi ake linali Abiya mwana wa Zekariya.
UHezekhiya wayeleminyaka engamatshumi amabili lemihlanu ubudala ethatha ubukhosi, njalo wabusa eJerusalema okweminyaka engamatshumi amabili lasificamunwemunye. Ibizo likanina lalingu-Abhija indodakazi kaZakhariya.
2 Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Davide abambo ake.
Wenza okulungileyo phambi kukaThixo, njengalokho okwakwenziwe nguyise uDavida.
3 Pa chaka choyamba cha ulamuliro wake, iye anatsekula zitseko za Nyumba ya Yehova ndipo anazikonza.
Ngenyanga yakuqala ngomnyaka wakuqala wokubusa kwakhe, wavula iminyango yethempeli likaThixo wayilungisa.
4 Iye analowetsamo ansembe ndi Alevi ndipo anawasonkhanitsa ku bwalo lakummawa
Wamema abaphristi kanye labaLevi, wababuthanisa egumeni eliseceleni langempumalanga
5 ndipo anati: “Mverani, inu Alevi! Dziyeretseni tsopano ndiponso muyeretse Nyumba ya Yehova Mulungu wa makolo anu. Muchotse zodetsa zonse ku malo opatulika.
wathi: “Lalelani kimi, lina baLevi! Zihlambululeni khathesi njalo lihlambulule lethempeli likaThixo, uNkulunkulu waboyihlo. Lisuse amanyala endaweni engcwele.
6 Makolo athu anali osakhulupirika ndipo anachita zoyipa pa maso pa Yehova Mulungu wathu ndi kumusiya Yehovayo. Iwo anatembenuka ndi kusiya malo okhalako Yehova ndi kumufulatira.
Obaba babengathembekanga; benza okubi emehlweni kaThixo uNkulunkulu wethu bamdela. Indawo kaThixo bayincitsha ubuso bakhangela eceleni njalo bamfulathela uThixo.
7 Iwowo anatsekanso zitseko zapakhonde ndi kuzimitsa nyale. Sanafukize lubani kapena kupereka nsembe zopsereza ku malo opatulika a Mulungu wa Israeli.
Bavala njalo izivalo zomphempe bacitsha izibane. Abazange batshise impepha njalo kabalethanga iminikelo yokutshiswa endaweni engcwele kaNkulunkulu ka-Israyeli.
8 Kotero, Yehova anakwiyira Yuda ndi Yerusalemu. Iye anawasandutsa chinthu chochititsa mantha, choopsa ndiponso chonyozedwa monga momwe mukuonera ndi maso anuwa lero lino.
Ngakho ulaka lukaThixo selwehlele phezu kwabakoJuda laphezu kwabaseJerusalema; uThixo usebenze besabeka, bathuthumelisa baba yinto yokweyiswa, njengoba lizibonela ngawenu amehlo.
9 Ichi nʼchifukwa chake makolo athu anaperekedwa ku lupanga ndipo nʼchifukwa chake ana athu aamuna ndi aakazi ndi akazi athu ali ku ukapolo.
Lokhu sekubangele ukubulawa kwabo ngenkemba njalo lokuthi amadodana lamadodakazi labomkethu babe sekuthunjweni.
10 Tsono ine ndikuganiza zochita pangano ndi Yehova Mulungu wa Israeli, kuti mkwiyo wake woopsawu utichokere.
Khathesi ngifuna ukwenza isivumelwano loThixo, uNkulunkulu ka-Israyeli, ukuze ulaka lwakhe oluvuthayo lusidedele.
11 Ana anga, musanyalanyaze tsopano, pakuti Yehova wakusankhani kuti muziyima pamaso pake ndi kumutumikira Iye, kugwira ntchito pamaso pake ndi kufukiza lubani.”
Madodana ami, kalingabi ngabangananziyo ngoba uThixo uselikhethile lina ukuma phambi kwakhe limkhonze, limsebenzele lokutshisa impepha.”
12 Ndipo Alevi awa anakonzeka kugwira ntchito: Kuchokera ku banja la Kohati, Mahati mwana wa Amasai ndi Yoweli mwana wa Azariya; kuchokera ku banja la Merari, Kisi mwana wa Abidi ndi Azariya mwana wa Yehaleleli; kuchokera ku banja la Geresoni, Yowa mwana wa Zima ndi Edeni mwana wa Yowa;
Ngakho laba abaLevi bahle baqalisa umsebenzi: KwabakaKhohathi, uMahathi indodana ka-Amasayi loJoweli indodana ka-Azariya; kwabakaMerari, uKhishi indodana ka-Abhidi lo-Azariya indodana kaJehaleleli; kwabakaGeshoni, uJowa indodana kaZima lo-Edeni indodana kaJowa;
13 kuchokera kwa zidzukulu za Elizafani, Simiri ndi Yeiyeli; kuchokera kwa zidzukulu za Asafu, Zekariya ndi Mataniya;
kwabosendo luka-Elizafani, kunguShimiri loJeyiyeli; kwabosendo luka-Asafi, kunguZakhariya loMathaniya;
14 kuchokera kwa zidzukulu za Hemani, Yehieli ndi Simei; kuchokera kwa zidzukulu za Yedutuni, Semaya ndi Uzieli.
kwabosendo lukaHemani, kunguJehiyeli loShimeyi; kwabosendo lukaJeduthuni, kunguShemaya lo-Uziyeli.
15 Atasonkhanitsa abale awo ndi kudziyeretsa, iwo anapita kukayeretsa Nyumba ya Yehova, monga inalamulira mfumu, potsatira mawu a Yehova.
Bathi sebebuthanise abafowabo bazihlambulula bona, bangena ukuyahlambulula ithempeli likaThixo, njengokuqondisa kwenkosi, eyayilandela ilizwi likaThixo.
16 Ansembe analowa ku malo opatulika a Yehova kukayeretsako. Anatulutsira ku bwalo la Nyumba ya Yehova chilichonse chodetsedwa chimene anachipeza mʼNyumba ya Yehova. Alevi anatenga zimenezo ndi kupita nazo ku chigwa cha Kidroni.
Abaphristi bangena endaweni engcwele kaThixo ukuba bayeyihlambulula. Konke okwakungcolile ethempelini likaThixo bakukhuphela egumeni lethempeli likaThixo. AbaLevi bakuthwala baya lakho eSigodini saseKhidironi.
17 Iwo anayamba mwambo woyeretsawu tsiku loyamba la mwezi woyamba ndipo pa tsiku lachisanu ndi chitatu la mweziwo anafika pa khonde la nyumba ya Yehova. Tsono anachita mwambo woyeretsa Nyumba ya Yehova ija masiku asanu ndi atatu, ndipo anamaliza pa tsiku la 16 mwezi woyamba.
Baqalisa ukwahlukanisela ngosuku lwakuqala lwenyanga yakuqala, kwathi ngosuku lwesificaminwembili lwenyanga bafika emphempeni kaThixo. Ngezinsuku ezilandelayo ezificaminwembili bangcwelisa ithempeli likaThixo uqobo, baze baqeda ngosuku lwetshumi lesithupha lwenyanga yakuqala.
18 Ndipo anapita kwa mfumu Hezekiya ndi kukafotokoza kuti, “Ife tayeretsa Nyumba ya Mulungu yonse, guwa lansembe zopsereza ndi ziwiya zake zonse, ndiponso tebulo limene timayikapo buledi wopatulika pamodzi ndi zinthu zake zonse.
Basebengena enkosini uHezekhiya ukuba bayembikela bathi: “Sesilihlambulule lonke ithempeli likaThixo, le-alithari lomnikelo wokutshiswa lezitsha zalo zonke, kanye lethala lokwendlalela isinkwa esingcwelisiweyo kanye lazozonke impahla zakhona.
19 Takonza ndi kuyeretsa zinthu zonse zimene mfumu Ahazi anazichotsa mwa kusakhulupirika kwake pamene anali mfumu. Taziyika kutsogolo kwa guwa la Yehova.”
Sesilungise sangcwelisa zonke izitsha ezasuswa yinkosi u-Ahazi ngokungathembeki kwakhe eseseyinkosi. Khathesi seziphambi kwe-alithari likaThixo.”
20 Mmamawa tsiku linalo, mfumu Hezekiya inasonkhanitsa pamodzi akuluakulu a mu mzindawo ndipo inapita ku Nyumba ya Yehova.
Ekuseni ngosuku olulandelayo inkosi uHezekhiya wabuthanisa izikhulu zedolobho ndawonye wasesiya ethempelini likaThixo.
21 Iwo anabweretsa ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ziwiri monga nsembe zoperekedwa chifukwa cha tchimo la ufumu, la malo opatulika ndi Yuda. Tsono mfumu inalamula ansembe, zidzukulu za Aaroni, kuti apereke zimenezi pa guwa lansembe la Yehova.
Baletha inkunzi eziyisikhombisa, lenqama eziyisikhombisa, lamazinyane ezimvu amaduna ayisikhombisa kanye lempongo eziyisikhombisa kungumnikelo wesono sombuso, lesendlu yokukhonzela kanye lesikaJuda. Inkosi yalaya abaphristi, abenzalo ka-Aroni, ukunikela ngalokho e-alithareni likaThixo.
22 Choncho anthuwo anapha ngʼombe zazimunazo ndipo ansembe anatenga magazi ake ndi kuwawaza pa guwa lansembe, kenaka anapha nkhosa zazimuna zija ndipo anawaza magazi ake pa guwa lansembe; anaphanso ana ankhosa aja ndipo anawaza magazi ake pa guwa lansembe.
Ngakho babulala inkunzi, abaphristi bathatha igazi bachela ngalo e-alithareni; kwalandela inqama abazibulala bachela igazi lazo e-alithareni; basebebulala amazinyane ezimvu bachela igazi lawo e-alithareni.
23 Mbuzi zoperekedwa chifukwa cha tchimo zija zinabweretsedwa pamaso pa mfumu ndi anthu onse, ndipo anasanjika manja awo pa izo.
Impongo zomnikelo wesono zalethwa phambi kwenkosi laphambi kwebandla, babeka izandla zabo phezu kwazo.
24 Kenaka ansembe anapha mbuzizo ndipo anapereka magazi ake pa guwa, kuti ukhale mwambo wofafanizira machimo a Aisraeli onse, pakuti mfumu inalamula kuti nsembe yopsereza ndi yopepesera machimo zichitike chifukwa cha Aisraeli onse.
Abaphristi basebebulala impongo baletha igazi lazo e-alithareni kungumnikelo wesono ukuze kwenzelwe wonke u-Israyeli indlela yokubuyisana, ngoba inkosi yayilaye ukuthi kube lomnikelo wokutshiswa lomnikelo wesono kunikelelwa wonke u-Israyeli.
25 Iye anayika Alevi mʼNyumba ya Yehova ali ndi ziwaya za malipenga, azeze ndi apangwe potsata lamulo la Davide, Gadi mlosi wa mfumu ndi mneneri Natani. Pakuti Yehova ndiye analamula zimenezi kudzera mwa aneneri.
AbaLevi yababeka phakathi kwethempeli likaThixo belezigubhu, lamachacho lemihubhe njengalokho okwakumiswe nguDavida loGadi umboni wenkosi loNathani umphrofethi; lokhu kwakungumlayo kaThixo oweza ngabaphrofethi bakhe.
26 Kotero Alevi anayima okonzekera atanyamula zoyimbira za Davide ndiponso ansembe atanyamula malipenga awo.
Ngakho abaLevi balinda belamachacho kaDavida, abaphristi belamacilongo.
27 Hezekiya analamulira kuti apereke nsembe zopsereza pa guwa. Pamene amayamba kupereka nsembezo, kuyimbira Yehova kunayambikanso, pamodzi ndi malipenga ndi zipangizo zoyimbira za Davide mfumu ya Israeli.
UHezekhiya wakhupha isiqondiso sokuba kwenziwe umnikelo wokutshiswa e-alithareni. Kuthe kuqalisa umnikelo, ukuhlabelela uThixo lakho kwaqalisa, kwahamba kanyekanye lamacilongo kanye lamachacho kaDavida inkosi yako-Israyeli.
28 Anthu onse anawerama pansi ndi kulambira, pamene oyimba amayimba ndi malipenga. Izi zonse zinapitirira mpaka pa mapeto pa nsembe zopsereza.
Ibandla lonke lakhothama lakhonza, abahlabeleli behlabela labamacilongo bewavuthela. Konke lokhu kwaqhubeka kwaze kwaphela umnikelo wokutshiswa.
29 Zopereka zitatha, mfumu ndi wina aliyense amene anali naye anagwada pansi ndi kulambira.
Ngemva kokuphela kweminikelo inkosi labo bonke ababekhona baguqa bakhonza.
30 Mfumu Hezekiya ndi akuluakulu ake analamulira Alevi kuti atamande Yehova potsata mawu a Davide ndi mlosi Asafu. Kotero anayimba nyimbo zamatamando mokondwera ndipo anaweramitsa mitu yawo ndi kulambira.
Inkosi uHezekhiya lezikhulu zayo yatshela abaLevi ukuba badumise uThixo ngamazwi kaDavida kanye laka-Asafi umboni. Ngakho badumisa ngokuhlabelela ngenjabulo bakhothamisa amakhanda abo bakhonza.
31 Kenaka Hezekiya anati, “Inu mwadzipereka tsopano kwa Yehova. Bwerani ndipo mufike ndi nsembe ndi zopereka zachiyamiko ku Nyumba ya Yehova.” Choncho anthu onse anabweretsa nsembe ndi zopereka zachiyamiko, ndipo anthu onse amene anali ofuna mu mtima mwawo anabweretsa nsembe zopsereza.
UHezekhiya wasesithi, “Selizinikele kuThixo khathesi. Wozani lilethe imihlatshelo leminikelo yokubonga ethempelini likaThixo.” Ngakho ibandla laletha imihlatshelo leminikelo, yokubonga, njalo ababelenhliziyo ezivumayo baletha iminikelo yokutshiswa.
32 Chiwerengero cha nsembe zopsereza chimene anthu onse anabweretsa chinali ngʼombe zazimuna makumi asanu ndi awiri, nkhosa zazimuna 100, ana ankhosa aamuna 200 ndipo zonsezi zinali za nsembe yopsereza kwa Yehova.
Inani leminikelo yokutshiswa eyalethwa libandla kwakuzinkunzi ezingamatshumi ayisikhombisa, inqama ezilikhulu lamazinyane amaduna ezimvu angamakhulu amabili, konke kungokomnikelo wokutshiswa kuThixo.
33 Ziweto zimene zinapatulidwa kukhala nsembe zinalipo ngʼombe zazimuna 600, nkhosa ndi mbuzi 3,000.
Izifuyo ezahlukaniselwa ukuba ngumhlatshelo kwakuzinkunzi ezingamakhulu ayisithupha lezimvu lembuzi ezizinkulungwane ezintathu.
34 Koma ansembe anali ochepa kuti asende zonse zopsereza. Choncho abale awo Alevi anawathandiza mpaka ntchito yonse inatha ndipo mpaka ansembe ena atadziyeretsa, pakuti Alevi anachita changu kudziyeretsa kulekana ndi momwe anachitira ansembe.
Kodwa, abaphristi babebalutshwana kakhulu ekuhlinzeni ezomnikelo wokutshiswa; ngakho basebencediswa ngabafowabo abaLevi waze waphela umsebenzi njalo abanye abaphristi baze bangcweliswa ngoba abaLevi babekunanzelele kakhulu ukuzingcwelisa kulabaphristi.
35 Panali nsembe zopsereza zochuluka, pamodzi ndi mafuta a nsembe yachiyanjano ndi nsembe yachakumwa imene imachitika pamodzi ndi nsembe yopsereza. Kotero ntchito ya mʼNyumba ya Mulungu inakhazikitsidwanso.
Umnikelo wokutshiswa wawumnengi, kanye lamafutha omnikelo wobudlelwano kanye lomnikelo wokunathwayo okwakuhambelana lomnikelo wokutshiswa. Ngakho lokhu kwaba yikuvuselelwa kwenkonzo ethempelini likaThixo.
36 Hezekiya ndi anthu onse anakondwera pa zimene Mulungu anachitira anthu ake, chifukwa zinachita mwamsangamsanga.
UHezekhiya labo bonke abantu bajabula ngababekuphiwe nguNkulunkulu ekwenzela abantu bakhe, ngoba kwakwenzakale ngokuphangisa.

< 2 Mbiri 29 >