< 2 Mbiri 29 >

1 Hezekiya anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 29. Dzina la amayi ake linali Abiya mwana wa Zekariya.
Ézéchias commença donc à régner à l’âge de vingt-cinq ans, et il en régna vingt-neuf dans Jérusalem; le nom de sa mère était Abia, fille de Zacharie.
2 Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Davide abambo ake.
Et il fit ce qui était agréable en la présence du Seigneur, selon tout ce qu’avait fait David son père.
3 Pa chaka choyamba cha ulamuliro wake, iye anatsekula zitseko za Nyumba ya Yehova ndipo anazikonza.
C’est lui qui, au premier mois de la première année de son règne, ouvrit les battants des portes de la maison du Seigneur, et les rétablit;
4 Iye analowetsamo ansembe ndi Alevi ndipo anawasonkhanitsa ku bwalo lakummawa
Et il fit venir les prêtres et les Lévites, et les assembla sur la place orientale.
5 ndipo anati: “Mverani, inu Alevi! Dziyeretseni tsopano ndiponso muyeretse Nyumba ya Yehova Mulungu wa makolo anu. Muchotse zodetsa zonse ku malo opatulika.
Et il leur dit: Ecoutez-moi, Lévites; sanctifiez-vous, purifiez la maison du Seigneur Dieu de vos pères, et ôtez toute impureté du sanctuaire.
6 Makolo athu anali osakhulupirika ndipo anachita zoyipa pa maso pa Yehova Mulungu wathu ndi kumusiya Yehovayo. Iwo anatembenuka ndi kusiya malo okhalako Yehova ndi kumufulatira.
Nos pères ont péché, et ils ont fait le mal en la présence du Seigneur notre Dieu, en l’abandonnant: ils ont détourné leurs faces du tabernacle du Seigneur, et ils ont montré le dos.
7 Iwowo anatsekanso zitseko zapakhonde ndi kuzimitsa nyale. Sanafukize lubani kapena kupereka nsembe zopsereza ku malo opatulika a Mulungu wa Israeli.
Ils ont fermé les portes qui étaient dans le portique, et ont éteint les lampes; ils n’ont pas brûlé d’encens, et n’ont pas offert d’holocaustes dans le sanctuaire au Dieu d’Israël.
8 Kotero, Yehova anakwiyira Yuda ndi Yerusalemu. Iye anawasandutsa chinthu chochititsa mantha, choopsa ndiponso chonyozedwa monga momwe mukuonera ndi maso anuwa lero lino.
C’est pourquoi la fureur du Seigneur a été excitée contre Juda et Jérusalem; il les a livrés à la commotion, à la mort et au sifflement, comme vous-mêmes le voyez de vos yeux.
9 Ichi nʼchifukwa chake makolo athu anaperekedwa ku lupanga ndipo nʼchifukwa chake ana athu aamuna ndi aakazi ndi akazi athu ali ku ukapolo.
Voilà que nos pères sont tombés sous le glaive, que nos fils, nos filles et nos femmes ont été emmenés captifs à cause de ce crime.
10 Tsono ine ndikuganiza zochita pangano ndi Yehova Mulungu wa Israeli, kuti mkwiyo wake woopsawu utichokere.
Il me plaît donc maintenant que nous contractions alliance avec le Seigneur Dieu d’Israël, et il détournera de nous la fureur de sa colère.
11 Ana anga, musanyalanyaze tsopano, pakuti Yehova wakusankhani kuti muziyima pamaso pake ndi kumutumikira Iye, kugwira ntchito pamaso pake ndi kufukiza lubani.”
Mes enfants, ne soyez point négligents: le Seigneur vous a choisis pour vous tenir devant lui, le servir, l’adorer et brûler pour lui de l’encens.
12 Ndipo Alevi awa anakonzeka kugwira ntchito: Kuchokera ku banja la Kohati, Mahati mwana wa Amasai ndi Yoweli mwana wa Azariya; kuchokera ku banja la Merari, Kisi mwana wa Abidi ndi Azariya mwana wa Yehaleleli; kuchokera ku banja la Geresoni, Yowa mwana wa Zima ndi Edeni mwana wa Yowa;
Ainsi se levèrent les Lévites, Mahath, fils d’Amasaï, et Joël, fils d’Azarias, d’entre les descendants de Caath; mais d’entre les descendants de Mérari, Cis, fils d’Abdi, et Azarias, fils de Jalaléel; et d’entre les descendants de Gersom, Joab, fils de Zemma, et Eden, fils de Joab;
13 kuchokera kwa zidzukulu za Elizafani, Simiri ndi Yeiyeli; kuchokera kwa zidzukulu za Asafu, Zekariya ndi Mataniya;
Mais d’entre les descendants d’Elisaphan, Samri et Jahiel; comme aussi les descendants d’Asaph, Zacharie et Mathanie;
14 kuchokera kwa zidzukulu za Hemani, Yehieli ndi Simei; kuchokera kwa zidzukulu za Yedutuni, Semaya ndi Uzieli.
Et d’entre les descendants d’Héman, Jahiel et Séméi; mais aussi les descendants d’Idithun, Séméias et Oziel.
15 Atasonkhanitsa abale awo ndi kudziyeretsa, iwo anapita kukayeretsa Nyumba ya Yehova, monga inalamulira mfumu, potsatira mawu a Yehova.
Et ils assemblèrent leurs frères, puis ils se sanctifièrent et entrèrent, suivant l’ordre du roi et le commandement du Seigneur, pour purifier la maison de Dieu.
16 Ansembe analowa ku malo opatulika a Yehova kukayeretsako. Anatulutsira ku bwalo la Nyumba ya Yehova chilichonse chodetsedwa chimene anachipeza mʼNyumba ya Yehova. Alevi anatenga zimenezo ndi kupita nazo ku chigwa cha Kidroni.
Les prêtres aussi entrèrent dans le temple du Seigneur pour le sanctifier, et ils ôtèrent toute impureté qu’ils trouvèrent au dedans, dans le vestibule de la maison du Seigneur, et que les Lévites enlevèrent et emportèrent dans le torrent de Cédron.
17 Iwo anayamba mwambo woyeretsawu tsiku loyamba la mwezi woyamba ndipo pa tsiku lachisanu ndi chitatu la mweziwo anafika pa khonde la nyumba ya Yehova. Tsono anachita mwambo woyeretsa Nyumba ya Yehova ija masiku asanu ndi atatu, ndipo anamaliza pa tsiku la 16 mwezi woyamba.
Or ils commencèrent au premier jour du premier mois à purifier, et au huitième jour du même mois ils entrèrent dans le portique du temple du Seigneur: ils purifièrent le temple durant huit jours; et, au seizième jour du même mois, ils achevèrent ce qu’ils avaient commencé.
18 Ndipo anapita kwa mfumu Hezekiya ndi kukafotokoza kuti, “Ife tayeretsa Nyumba ya Mulungu yonse, guwa lansembe zopsereza ndi ziwiya zake zonse, ndiponso tebulo limene timayikapo buledi wopatulika pamodzi ndi zinthu zake zonse.
ils entrèrent aussi auprès du roi Ezéchias, et lui dirent: Nous avons sanctifié toute la maison du Seigneur, l’autel de l’holocauste, et ses vases, et même la table de proposition avec tous ses vases,
19 Takonza ndi kuyeretsa zinthu zonse zimene mfumu Ahazi anazichotsa mwa kusakhulupirika kwake pamene anali mfumu. Taziyika kutsogolo kwa guwa la Yehova.”
Et tous les meubles du temple, qu’avait souillés le roi Achaz, durant son règne, après qu’il eut prévariqué; et voilà que tout a été posé devant l’autel du Seigneur.
20 Mmamawa tsiku linalo, mfumu Hezekiya inasonkhanitsa pamodzi akuluakulu a mu mzindawo ndipo inapita ku Nyumba ya Yehova.
Et le roi Ezéchias, se levant au point du jour, réunit tous les princes de la ville, et monta à la maison du Seigneur;
21 Iwo anabweretsa ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ziwiri monga nsembe zoperekedwa chifukwa cha tchimo la ufumu, la malo opatulika ndi Yuda. Tsono mfumu inalamula ansembe, zidzukulu za Aaroni, kuti apereke zimenezi pa guwa lansembe la Yehova.
Et ils offrirent ensemble sept taureaux et sept béliers, sept agneaux et sept boucs, pour le péché, pour le royaume, pour le sanctuaire, pour Juda, et il dit aux prêtres descendants d’Aaron d’offrir ces victimes sur l’autel du Seigneur.
22 Choncho anthuwo anapha ngʼombe zazimunazo ndipo ansembe anatenga magazi ake ndi kuwawaza pa guwa lansembe, kenaka anapha nkhosa zazimuna zija ndipo anawaza magazi ake pa guwa lansembe; anaphanso ana ankhosa aja ndipo anawaza magazi ake pa guwa lansembe.
Ils tuèrent donc les taureaux, et les prêtres prirent le sang et le répandirent sur l’autel; ils tuèrent aussi les béliers, et ils en répandirent le sang sur l’autel; ils immolèrent aussi les agneaux, et ils répandirent sur l’autel le sang.
23 Mbuzi zoperekedwa chifukwa cha tchimo zija zinabweretsedwa pamaso pa mfumu ndi anthu onse, ndipo anasanjika manja awo pa izo.
Ils firent avancer les boucs pour le péché, devant le roi et toute la multitude, et ils posèrent leurs mains sur eux;
24 Kenaka ansembe anapha mbuzizo ndipo anapereka magazi ake pa guwa, kuti ukhale mwambo wofafanizira machimo a Aisraeli onse, pakuti mfumu inalamula kuti nsembe yopsereza ndi yopepesera machimo zichitike chifukwa cha Aisraeli onse.
Et les prêtres les immolèrent, et en répandirent le sang devant l’autel pour l’expiation de tout Israël; car c’est pour tout Israël que le roi avait commandé que l’holocauste se fît, et pour le péché.
25 Iye anayika Alevi mʼNyumba ya Yehova ali ndi ziwaya za malipenga, azeze ndi apangwe potsata lamulo la Davide, Gadi mlosi wa mfumu ndi mneneri Natani. Pakuti Yehova ndiye analamula zimenezi kudzera mwa aneneri.
Il établit aussi les Lévites dans la maison du Seigneur, avec des cymbales, des psaltérions et des harpes, selon les prescriptions du roi David, de Gad, le Voyant, et de Nathan, le prophète; attendu que c’était un ordre du Seigneur par l’entremise de ses prophètes.
26 Kotero Alevi anayima okonzekera atanyamula zoyimbira za Davide ndiponso ansembe atanyamula malipenga awo.
Ainsi les Lévites s’y trouvèrent, tenant les instruments de David, et les prêtres les trompettes.
27 Hezekiya analamulira kuti apereke nsembe zopsereza pa guwa. Pamene amayamba kupereka nsembezo, kuyimbira Yehova kunayambikanso, pamodzi ndi malipenga ndi zipangizo zoyimbira za Davide mfumu ya Israeli.
Et Ezéchias commanda qu’on offrît les holocaustes sur l’autel; et, lorsque l’on offrait les holocaustes, ils commencèrent à chanter des louanges au Seigneur, à sonner des trompettes, et à faire retentir divers instruments que David, roi d’Israël, avait préparés.
28 Anthu onse anawerama pansi ndi kulambira, pamene oyimba amayimba ndi malipenga. Izi zonse zinapitirira mpaka pa mapeto pa nsembe zopsereza.
Or, toute la multitude adorant le Seigneur, les chantres et ceux qui tenaient les trompettes étaient à leur devoir, jusqu’à ce que l’holocauste fût achevé.
29 Zopereka zitatha, mfumu ndi wina aliyense amene anali naye anagwada pansi ndi kulambira.
Et lorsque l’oblation fut finie, le roi s’inclina, et tous ceux qui étaient avec lui, et ils adorèrent.
30 Mfumu Hezekiya ndi akuluakulu ake analamulira Alevi kuti atamande Yehova potsata mawu a Davide ndi mlosi Asafu. Kotero anayimba nyimbo zamatamando mokondwera ndipo anaweramitsa mitu yawo ndi kulambira.
Et Ezéchias et les princes ordonnèrent aux Lévites de louer le Seigneur avec les paroles de David et d’Asaph, le Voyant; et ils le louèrent avec une grande joie, et, le genou courbé, ils adorèrent.
31 Kenaka Hezekiya anati, “Inu mwadzipereka tsopano kwa Yehova. Bwerani ndipo mufike ndi nsembe ndi zopereka zachiyamiko ku Nyumba ya Yehova.” Choncho anthu onse anabweretsa nsembe ndi zopereka zachiyamiko, ndipo anthu onse amene anali ofuna mu mtima mwawo anabweretsa nsembe zopsereza.
Mais Ezéchias ajouta encore ceci: Vous avez rempli vos mains pour le Seigneur; approchez, et offrez des victimes et des louanges dans la maison du Seigneur. Toute la multitude offrit donc des hosties, des louanges et des holocaustes avec un cœur dévoué.
32 Chiwerengero cha nsembe zopsereza chimene anthu onse anabweretsa chinali ngʼombe zazimuna makumi asanu ndi awiri, nkhosa zazimuna 100, ana ankhosa aamuna 200 ndipo zonsezi zinali za nsembe yopsereza kwa Yehova.
Quant au nombre des holocaustes qu’offrit la multitude, ce furent soixante-dix taureaux, cent béliers, et deux cents agneaux.
33 Ziweto zimene zinapatulidwa kukhala nsembe zinalipo ngʼombe zazimuna 600, nkhosa ndi mbuzi 3,000.
Et ils consacrèrent au Seigneur six cents bœufs et trois mille moutons.
34 Koma ansembe anali ochepa kuti asende zonse zopsereza. Choncho abale awo Alevi anawathandiza mpaka ntchito yonse inatha ndipo mpaka ansembe ena atadziyeretsa, pakuti Alevi anachita changu kudziyeretsa kulekana ndi momwe anachitira ansembe.
Or les prêtres étaient en petit nombre, et ils ne pouvaient suffire à enlever la peau des holocaustes: c’est pourquoi les Lévites, leurs frères, les aidèrent jusqu’à ce que l’ouvrage fût achevé et que les prêtres fussent sanctifiés; car les Lévites sont sanctifiés avec un rit plus facile que les prêtres.
35 Panali nsembe zopsereza zochuluka, pamodzi ndi mafuta a nsembe yachiyanjano ndi nsembe yachakumwa imene imachitika pamodzi ndi nsembe yopsereza. Kotero ntchito ya mʼNyumba ya Mulungu inakhazikitsidwanso.
On offrit donc un très grand nombre d’holocaustes, les graisses des hosties pacifiques, et les libations des holocaustes, et l’on rétablit entièrement le culte de la maison du Seigneur.
36 Hezekiya ndi anthu onse anakondwera pa zimene Mulungu anachitira anthu ake, chifukwa zinachita mwamsangamsanga.
Et Ezéchias se livra à l’allégresse, ainsi que tout le peuple, de ce que le service du Seigneur était entièrement rétabli; car il avait plu que cela se fît soudainement.

< 2 Mbiri 29 >