< 2 Mbiri 29 >
1 Hezekiya anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 29. Dzina la amayi ake linali Abiya mwana wa Zekariya.
Ezéchias devint roi à l’âge de vingt cinq ans, et il régna vingt-neuf ans à Jérusalem. Sa mère s’appelait Abia, fille de Zacharias.
2 Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Davide abambo ake.
Il fit ce qui est droit aux yeux de Yahweh, selon tout ce qu’avait fait David, son père.
3 Pa chaka choyamba cha ulamuliro wake, iye anatsekula zitseko za Nyumba ya Yehova ndipo anazikonza.
La première année de son règne, le premier mois, il ouvrit les portes de la maison de Yahweh et il les répara.
4 Iye analowetsamo ansembe ndi Alevi ndipo anawasonkhanitsa ku bwalo lakummawa
Il fit venir les prêtres et les lévites et, les ayant réunis sur la place orientale,
5 ndipo anati: “Mverani, inu Alevi! Dziyeretseni tsopano ndiponso muyeretse Nyumba ya Yehova Mulungu wa makolo anu. Muchotse zodetsa zonse ku malo opatulika.
il leur dit: « Ecoutez-moi, lévites! Sanctifiez-vous maintenant, sanctifiez la maison de Yahweh, le Dieu de vos pères, et faites sortir du sanctuaire ce qui est impur.
6 Makolo athu anali osakhulupirika ndipo anachita zoyipa pa maso pa Yehova Mulungu wathu ndi kumusiya Yehovayo. Iwo anatembenuka ndi kusiya malo okhalako Yehova ndi kumufulatira.
Car nos pères ont péché, ils ont fait ce qui est mal aux yeux de Yahweh, notre Dieu, ils l’ont abandonné, ils ont détourné leur visage de la demeure de Yahweh et lui ont tourné le dos.
7 Iwowo anatsekanso zitseko zapakhonde ndi kuzimitsa nyale. Sanafukize lubani kapena kupereka nsembe zopsereza ku malo opatulika a Mulungu wa Israeli.
Ils ont même fermé les portes du portique et éteint les lampes, et ils n’ont pas fait brûler de parfums ni offert d’holocaustes dans le sanctuaire au Dieu d’Israël.
8 Kotero, Yehova anakwiyira Yuda ndi Yerusalemu. Iye anawasandutsa chinthu chochititsa mantha, choopsa ndiponso chonyozedwa monga momwe mukuonera ndi maso anuwa lero lino.
Et la colère de Yahweh a été sur Juda et Jérusalem, et il en a fait un objet de terreur, de stupeur et de moquerie, comme vous le voyez de vos yeux;
9 Ichi nʼchifukwa chake makolo athu anaperekedwa ku lupanga ndipo nʼchifukwa chake ana athu aamuna ndi aakazi ndi akazi athu ali ku ukapolo.
et voici qu’à cause de cela, nos pères sont tombés par l’épée, et nos fils, nos filles et nos femmes sont en captivité.
10 Tsono ine ndikuganiza zochita pangano ndi Yehova Mulungu wa Israeli, kuti mkwiyo wake woopsawu utichokere.
Maintenant, j’ai l’intention de faire alliance avec Yahweh, le Dieu d’Israël, pour que l’ardeur de sa colère se détourne de nous.
11 Ana anga, musanyalanyaze tsopano, pakuti Yehova wakusankhani kuti muziyima pamaso pake ndi kumutumikira Iye, kugwira ntchito pamaso pake ndi kufukiza lubani.”
Maintenant, mes enfants, ne soyez plus négligents; car c’est vous que Yahweh a choisis pour vous tenir devant lui à son service, pour être ses serviteurs et pour lui offrir des parfums. »
12 Ndipo Alevi awa anakonzeka kugwira ntchito: Kuchokera ku banja la Kohati, Mahati mwana wa Amasai ndi Yoweli mwana wa Azariya; kuchokera ku banja la Merari, Kisi mwana wa Abidi ndi Azariya mwana wa Yehaleleli; kuchokera ku banja la Geresoni, Yowa mwana wa Zima ndi Edeni mwana wa Yowa;
Alors les lévites se levèrent: Mahath, fils d’Amasaï, Joël, fils d’Azarias, des fils des Caathites; des fils de Mérari, Cis fils d’Abdi, Azarias, fils de Jalaléel; des Gersonites, Joah, fils de Zemma, Eden, fils de Joah;
13 kuchokera kwa zidzukulu za Elizafani, Simiri ndi Yeiyeli; kuchokera kwa zidzukulu za Asafu, Zekariya ndi Mataniya;
des fils d’Elisaphan, Samri et Jahiel; des fils d’Asaph, Zacharias et Mathanias;
14 kuchokera kwa zidzukulu za Hemani, Yehieli ndi Simei; kuchokera kwa zidzukulu za Yedutuni, Semaya ndi Uzieli.
des fils d’Héman, Jahiel et Seméï; et des fils d’Idithun, Séméïas et Oziel.
15 Atasonkhanitsa abale awo ndi kudziyeretsa, iwo anapita kukayeretsa Nyumba ya Yehova, monga inalamulira mfumu, potsatira mawu a Yehova.
Ils réunirent leurs frères et, après s’être sanctifiés, ils vinrent, selon l’ordre du roi, d’après les paroles de Yahweh, pour purifier la maison de Yahweh.
16 Ansembe analowa ku malo opatulika a Yehova kukayeretsako. Anatulutsira ku bwalo la Nyumba ya Yehova chilichonse chodetsedwa chimene anachipeza mʼNyumba ya Yehova. Alevi anatenga zimenezo ndi kupita nazo ku chigwa cha Kidroni.
Les prêtres entrèrent dans l’intérieur de la maison de Yahweh pour la purifier; ils firent sortir dans le parvis de la maison de Yahweh toutes les impuretés qu’ils trouvèrent dans le temple de Yahweh, et de là les lévites les prirent pour les emporter dehors à la vallée de Cédron.
17 Iwo anayamba mwambo woyeretsawu tsiku loyamba la mwezi woyamba ndipo pa tsiku lachisanu ndi chitatu la mweziwo anafika pa khonde la nyumba ya Yehova. Tsono anachita mwambo woyeretsa Nyumba ya Yehova ija masiku asanu ndi atatu, ndipo anamaliza pa tsiku la 16 mwezi woyamba.
Ils commencèrent à purifier le premier jour du premier mois; le huitième jour du mois, ils entrèrent dans le portique de Yahweh, et ils mirent huit jours à purifier la maison de Yahweh; le seizième jour du premier mois, ils avaient achevé.
18 Ndipo anapita kwa mfumu Hezekiya ndi kukafotokoza kuti, “Ife tayeretsa Nyumba ya Mulungu yonse, guwa lansembe zopsereza ndi ziwiya zake zonse, ndiponso tebulo limene timayikapo buledi wopatulika pamodzi ndi zinthu zake zonse.
Ils se rendirent ensuite chez le roi Ezéchias et dirent: « Nous avons purifié toute la maison de Yahweh, l’autel des holocaustes et tous ses ustensiles, et la table de proposition et tous ses ustensiles.
19 Takonza ndi kuyeretsa zinthu zonse zimene mfumu Ahazi anazichotsa mwa kusakhulupirika kwake pamene anali mfumu. Taziyika kutsogolo kwa guwa la Yehova.”
Et tous les ustensiles que le roi Achaz avait profanés pendant son règne, lors de ses transgressions, nous les avons remis en état et purifiés; ils sont devant l’autel de Yahweh. »
20 Mmamawa tsiku linalo, mfumu Hezekiya inasonkhanitsa pamodzi akuluakulu a mu mzindawo ndipo inapita ku Nyumba ya Yehova.
Le roi Ezéchias, s’étant levé de bon matin, assembla les chefs de la ville et monta à la maison de Yahweh.
21 Iwo anabweretsa ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ziwiri monga nsembe zoperekedwa chifukwa cha tchimo la ufumu, la malo opatulika ndi Yuda. Tsono mfumu inalamula ansembe, zidzukulu za Aaroni, kuti apereke zimenezi pa guwa lansembe la Yehova.
Ils présentèrent sept taureaux, sept béliers, sept agneaux et sept boucs, en sacrifice pour le péché, pour le royaume, pour le sanctuaire et pour Juda. Le roi dit aux prêtres, fils d’Aaron, de les offrir sur l’autel de Yahweh.
22 Choncho anthuwo anapha ngʼombe zazimunazo ndipo ansembe anatenga magazi ake ndi kuwawaza pa guwa lansembe, kenaka anapha nkhosa zazimuna zija ndipo anawaza magazi ake pa guwa lansembe; anaphanso ana ankhosa aja ndipo anawaza magazi ake pa guwa lansembe.
Ils immolèrent les bœufs, et les prêtres recueillirent le sang, qu’ils répandirent sur l’autel; ils immolèrent les béliers, et répandirent le sang sur l’autel; ils immolèrent les agneaux, et répandirent le sang sur l’autel.
23 Mbuzi zoperekedwa chifukwa cha tchimo zija zinabweretsedwa pamaso pa mfumu ndi anthu onse, ndipo anasanjika manja awo pa izo.
Puis ils firent approcher les boucs pour le péché devant le roi et l’assemblée, et tous posèrent la main sur eux.
24 Kenaka ansembe anapha mbuzizo ndipo anapereka magazi ake pa guwa, kuti ukhale mwambo wofafanizira machimo a Aisraeli onse, pakuti mfumu inalamula kuti nsembe yopsereza ndi yopepesera machimo zichitike chifukwa cha Aisraeli onse.
Les prêtres les égorgèrent et avec leur sang ils firent l’expiation à l’autel, faisant l’expiation pour tout Israël; car c’était pour tout Israël que le roi avait ordonné l’holocauste et le sacrifice pour le péché.
25 Iye anayika Alevi mʼNyumba ya Yehova ali ndi ziwaya za malipenga, azeze ndi apangwe potsata lamulo la Davide, Gadi mlosi wa mfumu ndi mneneri Natani. Pakuti Yehova ndiye analamula zimenezi kudzera mwa aneneri.
Il fit placer les lévites dans la maison de Yahweh avec des cymbales, des cithares et des harpes, selon l’ordre de David, de Gad, le voyant du roi, et de Nathan le prophète; car cet ordre venait de Yahweh, par l’organe de ses prophètes.
26 Kotero Alevi anayima okonzekera atanyamula zoyimbira za Davide ndiponso ansembe atanyamula malipenga awo.
Les lévites prirent place avec les instruments de David, et les prêtres avec les trompettes.
27 Hezekiya analamulira kuti apereke nsembe zopsereza pa guwa. Pamene amayamba kupereka nsembezo, kuyimbira Yehova kunayambikanso, pamodzi ndi malipenga ndi zipangizo zoyimbira za Davide mfumu ya Israeli.
Et Ezéchias dit d’offrir l’holocauste, sur l’autel. Au moment où commença l’holocauste, commencèrent aussi le chant de Yahweh et le son des trompettes, accompagnés avec les instruments de David, roi d’Israël.
28 Anthu onse anawerama pansi ndi kulambira, pamene oyimba amayimba ndi malipenga. Izi zonse zinapitirira mpaka pa mapeto pa nsembe zopsereza.
Toute l’assemblée se prosterna, on chanta le cantique et l’on sonna des trompettes, le tout jusqu’à ce que l’holocauste fut achevé.
29 Zopereka zitatha, mfumu ndi wina aliyense amene anali naye anagwada pansi ndi kulambira.
Quand l’holocauste fut achevé, le roi et tous ceux qui étaient avec lui fléchirent le genou et adorèrent.
30 Mfumu Hezekiya ndi akuluakulu ake analamulira Alevi kuti atamande Yehova potsata mawu a Davide ndi mlosi Asafu. Kotero anayimba nyimbo zamatamando mokondwera ndipo anaweramitsa mitu yawo ndi kulambira.
Le roi Ezéchias et les chefs dirent aux lévites de célébrer Yahweh avec les paroles de David et d’Asaph le voyant, et ils célébrèrent avec joie, et, s’inclinant, ils adorèrent.
31 Kenaka Hezekiya anati, “Inu mwadzipereka tsopano kwa Yehova. Bwerani ndipo mufike ndi nsembe ndi zopereka zachiyamiko ku Nyumba ya Yehova.” Choncho anthu onse anabweretsa nsembe ndi zopereka zachiyamiko, ndipo anthu onse amene anali ofuna mu mtima mwawo anabweretsa nsembe zopsereza.
Alors Ezéchias prit la parole et dit: « Maintenant, vous vous êtes consacrés de nouveau à Yahweh, approchez-vous, présentez des sacrifices et des actions de grâce dans la maison de Yahweh. » Et l’assemblée présenta des sacrifices et des actions de grâces, et tous ceux dont le cœur était généreux offrirent des holocaustes.
32 Chiwerengero cha nsembe zopsereza chimene anthu onse anabweretsa chinali ngʼombe zazimuna makumi asanu ndi awiri, nkhosa zazimuna 100, ana ankhosa aamuna 200 ndipo zonsezi zinali za nsembe yopsereza kwa Yehova.
Le nombre des holocaustes qu’offrit l’assemblée fut de soixante dix bœufs, cent béliers et deux cents agneaux: tout cela pour un holocauste à Yahweh.
33 Ziweto zimene zinapatulidwa kukhala nsembe zinalipo ngʼombe zazimuna 600, nkhosa ndi mbuzi 3,000.
On consacra en outre six cents bœufs et trois mille brebis.
34 Koma ansembe anali ochepa kuti asende zonse zopsereza. Choncho abale awo Alevi anawathandiza mpaka ntchito yonse inatha ndipo mpaka ansembe ena atadziyeretsa, pakuti Alevi anachita changu kudziyeretsa kulekana ndi momwe anachitira ansembe.
Mais les prêtres, étant en petit nombre, ne purent dépouiller tous les holocaustes; leurs frères, les lévites, les aidèrent jusqu’à ce que l’ouvrage fut fini et jusqu’à ce que les autres prêtres se fussent sanctifiés, car les lévites avaient mis plus de sincérité de cœur que les prêtres à se sanctifier.
35 Panali nsembe zopsereza zochuluka, pamodzi ndi mafuta a nsembe yachiyanjano ndi nsembe yachakumwa imene imachitika pamodzi ndi nsembe yopsereza. Kotero ntchito ya mʼNyumba ya Mulungu inakhazikitsidwanso.
Il y avait d’ailleurs beaucoup d’holocaustes, outre les graisses des sacrifices pacifiques et les libations pour les holocaustes. Ainsi fut rétabli le service de la maison de Yahweh.
36 Hezekiya ndi anthu onse anakondwera pa zimene Mulungu anachitira anthu ake, chifukwa zinachita mwamsangamsanga.
Ezéchias et tout le peuple se réjouirent de ce que Dieu avait préparé pour le peuple, car la chose s’était faite subitement.