< 2 Mbiri 29 >

1 Hezekiya anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 29. Dzina la amayi ake linali Abiya mwana wa Zekariya.
And so Hezekiah began to reign when he was twenty-five years old. And he reigned for twenty-nine years in Jerusalem. The name of his mother was Abijah, the daughter of Zechariah.
2 Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Davide abambo ake.
And he did what was pleasing in the sight of the Lord, in accord with all that his father David had done.
3 Pa chaka choyamba cha ulamuliro wake, iye anatsekula zitseko za Nyumba ya Yehova ndipo anazikonza.
In the first year and month of his reign, he opened the double doors of the house of the Lord, and he repaired them.
4 Iye analowetsamo ansembe ndi Alevi ndipo anawasonkhanitsa ku bwalo lakummawa
And he brought together the priests and Levites. And he gathered them in the wide eastern street.
5 ndipo anati: “Mverani, inu Alevi! Dziyeretseni tsopano ndiponso muyeretse Nyumba ya Yehova Mulungu wa makolo anu. Muchotse zodetsa zonse ku malo opatulika.
And he said to them: “Listen to me, O Levites, and be sanctified. Cleanse the house of the Lord, the God of your fathers, and take away every uncleanness from the sanctuary.
6 Makolo athu anali osakhulupirika ndipo anachita zoyipa pa maso pa Yehova Mulungu wathu ndi kumusiya Yehovayo. Iwo anatembenuka ndi kusiya malo okhalako Yehova ndi kumufulatira.
Our fathers sinned and did evil in the sight of the Lord our God, abandoning him. They turned their faces away from the tabernacle of the Lord, and they presented their backs.
7 Iwowo anatsekanso zitseko zapakhonde ndi kuzimitsa nyale. Sanafukize lubani kapena kupereka nsembe zopsereza ku malo opatulika a Mulungu wa Israeli.
They closed up the doors which were in the portico, and they extinguished the lamps. And they did not burn incense, and they did not offer holocausts, in the sanctuary of the God of Israel.
8 Kotero, Yehova anakwiyira Yuda ndi Yerusalemu. Iye anawasandutsa chinthu chochititsa mantha, choopsa ndiponso chonyozedwa monga momwe mukuonera ndi maso anuwa lero lino.
And so the fury of the Lord was stirred up against Judah and Jerusalem, and he handed them over to turmoil, and to destruction, and to hissing, just as you discern with your own eyes.
9 Ichi nʼchifukwa chake makolo athu anaperekedwa ku lupanga ndipo nʼchifukwa chake ana athu aamuna ndi aakazi ndi akazi athu ali ku ukapolo.
Lo, our fathers have fallen by the sword. Our sons, and our daughters and wives have been led away as captives because of this wickedness.
10 Tsono ine ndikuganiza zochita pangano ndi Yehova Mulungu wa Israeli, kuti mkwiyo wake woopsawu utichokere.
Now therefore, it is pleasing to me that we should enter into a covenant with the Lord, the God of Israel. And he will turn away the fury of his indignation from us.
11 Ana anga, musanyalanyaze tsopano, pakuti Yehova wakusankhani kuti muziyima pamaso pake ndi kumutumikira Iye, kugwira ntchito pamaso pake ndi kufukiza lubani.”
My sons, do not choose to be negligent. The Lord has chosen you so that you would stand before him, and minister to him, and worship him, and burn incense to him.”
12 Ndipo Alevi awa anakonzeka kugwira ntchito: Kuchokera ku banja la Kohati, Mahati mwana wa Amasai ndi Yoweli mwana wa Azariya; kuchokera ku banja la Merari, Kisi mwana wa Abidi ndi Azariya mwana wa Yehaleleli; kuchokera ku banja la Geresoni, Yowa mwana wa Zima ndi Edeni mwana wa Yowa;
Therefore, the Levites rose up, Mahath, the son of Amasai, and Joel, the son of Azariah, from the sons of Kohath; then, from the sons of Merari, Kish, the son of Abdi, and Azariah, the son of Jehallelel; and from the sons of Gershon, Joah, the son of Zimmah, and Eden, the son of Joah;
13 kuchokera kwa zidzukulu za Elizafani, Simiri ndi Yeiyeli; kuchokera kwa zidzukulu za Asafu, Zekariya ndi Mataniya;
and truly, from the sons of Elizaphan, Shimri and Jeuel; also, from the sons of Asaph, Zechariah and Mattaniah;
14 kuchokera kwa zidzukulu za Hemani, Yehieli ndi Simei; kuchokera kwa zidzukulu za Yedutuni, Semaya ndi Uzieli.
indeed also, from the sons of Heman, Jehuel and Shimei; then too, from the sons of Jeduthun, Shemaiah and Uzziel.
15 Atasonkhanitsa abale awo ndi kudziyeretsa, iwo anapita kukayeretsa Nyumba ya Yehova, monga inalamulira mfumu, potsatira mawu a Yehova.
And they gathered together their brothers. And they were sanctified. And they entered in accord with the command of the king and the order of the Lord, so that they might expiate the house of God.
16 Ansembe analowa ku malo opatulika a Yehova kukayeretsako. Anatulutsira ku bwalo la Nyumba ya Yehova chilichonse chodetsedwa chimene anachipeza mʼNyumba ya Yehova. Alevi anatenga zimenezo ndi kupita nazo ku chigwa cha Kidroni.
And the priests, entering the temple of the Lord so that they might sanctify it, took every uncleanness, which they had found inside, out to the vestibule of the house of the Lord; and the Levites took it away and transported it outside, to the torrent Kidron.
17 Iwo anayamba mwambo woyeretsawu tsiku loyamba la mwezi woyamba ndipo pa tsiku lachisanu ndi chitatu la mweziwo anafika pa khonde la nyumba ya Yehova. Tsono anachita mwambo woyeretsa Nyumba ya Yehova ija masiku asanu ndi atatu, ndipo anamaliza pa tsiku la 16 mwezi woyamba.
Now they began to cleanse on the first day of the first month. And on the eighth day of the same month, they entered the portico of the temple of the Lord. And then they expiated the temple over eight days. And on the sixteenth day of the same month, they finished what they had begun.
18 Ndipo anapita kwa mfumu Hezekiya ndi kukafotokoza kuti, “Ife tayeretsa Nyumba ya Mulungu yonse, guwa lansembe zopsereza ndi ziwiya zake zonse, ndiponso tebulo limene timayikapo buledi wopatulika pamodzi ndi zinthu zake zonse.
Also, they entered to king Hezekiah, and they said to him: “We have sanctified the entire house of the Lord, and the altar of holocaust, and its vessels, indeed also the table of the presence, with all its vessels,
19 Takonza ndi kuyeretsa zinthu zonse zimene mfumu Ahazi anazichotsa mwa kusakhulupirika kwake pamene anali mfumu. Taziyika kutsogolo kwa guwa la Yehova.”
and all the equipment of the temple, which king Ahaz, during his reign, had polluted after his transgression. And behold, these have all been set forth before the altar of the Lord.”
20 Mmamawa tsiku linalo, mfumu Hezekiya inasonkhanitsa pamodzi akuluakulu a mu mzindawo ndipo inapita ku Nyumba ya Yehova.
And rising up at first light, king Hezekiah joined as one all the leaders of the city, and they ascended to the house of the Lord.
21 Iwo anabweretsa ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ziwiri monga nsembe zoperekedwa chifukwa cha tchimo la ufumu, la malo opatulika ndi Yuda. Tsono mfumu inalamula ansembe, zidzukulu za Aaroni, kuti apereke zimenezi pa guwa lansembe la Yehova.
And together they offered seven bulls and seven rams, seven lambs and seven he-goats, for sin, for the kingdom, for the Sanctuary, for Judah. And he spoke to the priests, the sons of Aaron, so that they would offer these upon the altar of the Lord.
22 Choncho anthuwo anapha ngʼombe zazimunazo ndipo ansembe anatenga magazi ake ndi kuwawaza pa guwa lansembe, kenaka anapha nkhosa zazimuna zija ndipo anawaza magazi ake pa guwa lansembe; anaphanso ana ankhosa aja ndipo anawaza magazi ake pa guwa lansembe.
And so they slaughtered the bulls. And the priests took up the blood, and they poured it upon the altar. Then they also slaughtered the rams, and they poured their blood upon the altar. And they immolated the lambs, and they poured the blood upon the altar.
23 Mbuzi zoperekedwa chifukwa cha tchimo zija zinabweretsedwa pamaso pa mfumu ndi anthu onse, ndipo anasanjika manja awo pa izo.
They brought the he-goats for sin before the king and the entire multitude. And they laid their hands upon them.
24 Kenaka ansembe anapha mbuzizo ndipo anapereka magazi ake pa guwa, kuti ukhale mwambo wofafanizira machimo a Aisraeli onse, pakuti mfumu inalamula kuti nsembe yopsereza ndi yopepesera machimo zichitike chifukwa cha Aisraeli onse.
And the priests immolated them, and they sprinkled their blood before the altar, for the expiation of all Israel. For certainly the king had instructed that the holocaust and the sin offering should be made on behalf of all Israel.
25 Iye anayika Alevi mʼNyumba ya Yehova ali ndi ziwaya za malipenga, azeze ndi apangwe potsata lamulo la Davide, Gadi mlosi wa mfumu ndi mneneri Natani. Pakuti Yehova ndiye analamula zimenezi kudzera mwa aneneri.
Also, he situated the Levites in the house of the Lord, with cymbals, and psalteries, and harps, according to the disposition of king David, and of the seer Gad, and of the prophet Nathan. For indeed, this was the precept of the Lord, by the hand of his prophets.
26 Kotero Alevi anayima okonzekera atanyamula zoyimbira za Davide ndiponso ansembe atanyamula malipenga awo.
And the Levites stood, holding the musical instruments of David, and the priests held the trumpets.
27 Hezekiya analamulira kuti apereke nsembe zopsereza pa guwa. Pamene amayamba kupereka nsembezo, kuyimbira Yehova kunayambikanso, pamodzi ndi malipenga ndi zipangizo zoyimbira za Davide mfumu ya Israeli.
And Hezekiah ordered that they should offer holocausts upon the altar. And when the holocausts were being offered, they began to sing praises to the Lord, and to sound the trumpets, and to play various musical instruments, which David, the king of Israel, had prepared.
28 Anthu onse anawerama pansi ndi kulambira, pamene oyimba amayimba ndi malipenga. Izi zonse zinapitirira mpaka pa mapeto pa nsembe zopsereza.
Then the entire crowd was adoring, and the singers and those who were holding the trumpeters were exercising their office, until the holocaust was completed.
29 Zopereka zitatha, mfumu ndi wina aliyense amene anali naye anagwada pansi ndi kulambira.
And when the oblation was finished, the king, and all who were with him, bowed down and adored.
30 Mfumu Hezekiya ndi akuluakulu ake analamulira Alevi kuti atamande Yehova potsata mawu a Davide ndi mlosi Asafu. Kotero anayimba nyimbo zamatamando mokondwera ndipo anaweramitsa mitu yawo ndi kulambira.
And Hezekiah and the rulers instructed the Levites to praise the Lord with the words of David, and of Asaph, the seer. And they praised him with great joy, and kneeling down, they adored.
31 Kenaka Hezekiya anati, “Inu mwadzipereka tsopano kwa Yehova. Bwerani ndipo mufike ndi nsembe ndi zopereka zachiyamiko ku Nyumba ya Yehova.” Choncho anthu onse anabweretsa nsembe ndi zopereka zachiyamiko, ndipo anthu onse amene anali ofuna mu mtima mwawo anabweretsa nsembe zopsereza.
And now Hezekiah also added: “You have filled your hands for the Lord. Draw near, and offer victims and praises in the house of the Lord.” Therefore, the entire multitude offered victims and praises and holocausts, with devout intention.
32 Chiwerengero cha nsembe zopsereza chimene anthu onse anabweretsa chinali ngʼombe zazimuna makumi asanu ndi awiri, nkhosa zazimuna 100, ana ankhosa aamuna 200 ndipo zonsezi zinali za nsembe yopsereza kwa Yehova.
Now the number of the holocausts that the multitude offered was seventy bulls, one hundred rams, two hundred lambs.
33 Ziweto zimene zinapatulidwa kukhala nsembe zinalipo ngʼombe zazimuna 600, nkhosa ndi mbuzi 3,000.
And they sanctified to the Lord six hundred oxen and three thousand sheep.
34 Koma ansembe anali ochepa kuti asende zonse zopsereza. Choncho abale awo Alevi anawathandiza mpaka ntchito yonse inatha ndipo mpaka ansembe ena atadziyeretsa, pakuti Alevi anachita changu kudziyeretsa kulekana ndi momwe anachitira ansembe.
Truly, the priests were few; neither were they sufficient to remove the pelts from the holocausts. Therefore, the Levites, their brothers, also assisted them, until the work was completed, and the priests, who were of higher rank, were sanctified. For indeed, the Levites are sanctified with an easier ritual than the priests.
35 Panali nsembe zopsereza zochuluka, pamodzi ndi mafuta a nsembe yachiyanjano ndi nsembe yachakumwa imene imachitika pamodzi ndi nsembe yopsereza. Kotero ntchito ya mʼNyumba ya Mulungu inakhazikitsidwanso.
Thus, there were very numerous holocausts, with the fat of the peace offerings and the libations of the holocausts. And the service of the house of the Lord was completed.
36 Hezekiya ndi anthu onse anakondwera pa zimene Mulungu anachitira anthu ake, chifukwa zinachita mwamsangamsanga.
And Hezekiah and all the people were joyful because the ministry of the Lord was accomplished. For certainly, it had pleased them to do this suddenly.

< 2 Mbiri 29 >