< 2 Mbiri 29 >

1 Hezekiya anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 29. Dzina la amayi ake linali Abiya mwana wa Zekariya.
Ezechiáš kralovati počal, když byl v pětmecítma letech, a dvadceti devět let kraloval v Jeruzalémě. Jméno matky jeho bylo Abia dcera Zachariášova.
2 Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Davide abambo ake.
A činil to, což pravého bylo před očima Hospodinovýma, podlé všech věcí, kteréž činil David otec jeho.
3 Pa chaka choyamba cha ulamuliro wake, iye anatsekula zitseko za Nyumba ya Yehova ndipo anazikonza.
On prvního léta kralování svého měsíce prvního otevřel dvéře domu Hospodinova, a opravil je.
4 Iye analowetsamo ansembe ndi Alevi ndipo anawasonkhanitsa ku bwalo lakummawa
Uvedl také kněží a Levíty, shromáždiv je do ulice východní,
5 ndipo anati: “Mverani, inu Alevi! Dziyeretseni tsopano ndiponso muyeretse Nyumba ya Yehova Mulungu wa makolo anu. Muchotse zodetsa zonse ku malo opatulika.
A řekl jim: Slyšte mne, Levítové. Nyní posvěťte se, posvěťte také i domu Hospodina Boha otců vašich, a vyneste nečistotu z svatyně.
6 Makolo athu anali osakhulupirika ndipo anachita zoyipa pa maso pa Yehova Mulungu wathu ndi kumusiya Yehovayo. Iwo anatembenuka ndi kusiya malo okhalako Yehova ndi kumufulatira.
Neboť zhřešili otcové naši, a činili zlé věci před očima Hospodina Boha našeho, opouštějíce jej, a odvracujíce tvář svou od stánku Hospodinova, obracejíce se hřbetem k němu.
7 Iwowo anatsekanso zitseko zapakhonde ndi kuzimitsa nyale. Sanafukize lubani kapena kupereka nsembe zopsereza ku malo opatulika a Mulungu wa Israeli.
Zavřeli také dvéře síně, a zhasili lampy, a kadidlem nekadili, aniž zápalu obětovali v svatyni Bohu Izraelskému.
8 Kotero, Yehova anakwiyira Yuda ndi Yerusalemu. Iye anawasandutsa chinthu chochititsa mantha, choopsa ndiponso chonyozedwa monga momwe mukuonera ndi maso anuwa lero lino.
Protož rozhněval se Hospodin na Judu a na Jeruzalém, a vydal je v posmýkání, zpuštění a ku podivení, jakož sami očima svýma vidíte.
9 Ichi nʼchifukwa chake makolo athu anaperekedwa ku lupanga ndipo nʼchifukwa chake ana athu aamuna ndi aakazi ndi akazi athu ali ku ukapolo.
A aj, padli otcové naši od meče, a synové naši i dcery naše a manželky naše zajaty jsou pro tu příčinu.
10 Tsono ine ndikuganiza zochita pangano ndi Yehova Mulungu wa Israeli, kuti mkwiyo wake woopsawu utichokere.
Nyní tedy umínil jsem učiniti smlouvu s Hospodinem Bohem Izraelským, aby odvrátil od nás hněv prchlivosti své.
11 Ana anga, musanyalanyaze tsopano, pakuti Yehova wakusankhani kuti muziyima pamaso pake ndi kumutumikira Iye, kugwira ntchito pamaso pake ndi kufukiza lubani.”
Synové moji, nebluďtež již. Vásť jest zajisté vyvolil Hospodin, abyste stojíce před ním, sloužili jemu, a byli služebníci jeho, a kadili.
12 Ndipo Alevi awa anakonzeka kugwira ntchito: Kuchokera ku banja la Kohati, Mahati mwana wa Amasai ndi Yoweli mwana wa Azariya; kuchokera ku banja la Merari, Kisi mwana wa Abidi ndi Azariya mwana wa Yehaleleli; kuchokera ku banja la Geresoni, Yowa mwana wa Zima ndi Edeni mwana wa Yowa;
Tedy povstali Levítové tito: Machat syn Amazai, a Joel syn Azariášův z synů Kahat; z synů pak Merari: Cis syn Abdi, a Azariáš syn Jehalleelův; a z Gersonitských: Joach syn Zimma, a Eden syn Joachův;
13 kuchokera kwa zidzukulu za Elizafani, Simiri ndi Yeiyeli; kuchokera kwa zidzukulu za Asafu, Zekariya ndi Mataniya;
Též z synů Elizafanových: Simri a Jehiel; z synů pak Azafových: Zachariáš a Mataniáš;
14 kuchokera kwa zidzukulu za Hemani, Yehieli ndi Simei; kuchokera kwa zidzukulu za Yedutuni, Semaya ndi Uzieli.
A z synů Hémanových: Jechiel a Simei; z synů pak Jedutunových: Semaiáš a Uziel.
15 Atasonkhanitsa abale awo ndi kudziyeretsa, iwo anapita kukayeretsa Nyumba ya Yehova, monga inalamulira mfumu, potsatira mawu a Yehova.
I shromáždili bratří své, kteříž posvětivše se, přišli podlé rozkázaní králova a slov Hospodinových, aby vyčistili dům Hospodinův.
16 Ansembe analowa ku malo opatulika a Yehova kukayeretsako. Anatulutsira ku bwalo la Nyumba ya Yehova chilichonse chodetsedwa chimene anachipeza mʼNyumba ya Yehova. Alevi anatenga zimenezo ndi kupita nazo ku chigwa cha Kidroni.
A všedše kněží do domu Hospodinova, aby jej vyčistili, vynesli všelikou nečistotu, kterouž našli v chrámě Hospodinově, do síně domu Hospodinova. Levítové pak probravše to, vynesli ven ku potoku Cedron.
17 Iwo anayamba mwambo woyeretsawu tsiku loyamba la mwezi woyamba ndipo pa tsiku lachisanu ndi chitatu la mweziwo anafika pa khonde la nyumba ya Yehova. Tsono anachita mwambo woyeretsa Nyumba ya Yehova ija masiku asanu ndi atatu, ndipo anamaliza pa tsiku la 16 mwezi woyamba.
Začali pak prvního dne měsíce prvního posvěcovati, a dne osmého téhož měsíce vešli do síně Hospodinovy, a posvěcovali domu Hospodinova za osm dní, a dne šestnáctého měsíce prvního dokonali.
18 Ndipo anapita kwa mfumu Hezekiya ndi kukafotokoza kuti, “Ife tayeretsa Nyumba ya Mulungu yonse, guwa lansembe zopsereza ndi ziwiya zake zonse, ndiponso tebulo limene timayikapo buledi wopatulika pamodzi ndi zinthu zake zonse.
Tedy vešli k Ezechiášovi králi, a řekli: Vyčistili jsme všecken dům Hospodinův, i oltář zápalu, i všecky nádoby jeho, i stůl předložení a všecky nádoby jeho.
19 Takonza ndi kuyeretsa zinthu zonse zimene mfumu Ahazi anazichotsa mwa kusakhulupirika kwake pamene anali mfumu. Taziyika kutsogolo kwa guwa la Yehova.”
Všecky také nádoby, kteréž byl zavrhl král Achas za kralování svého, když převráceně činil, připravili jsme a posvětili, a aj, jsou před oltářem Hospodinovým.
20 Mmamawa tsiku linalo, mfumu Hezekiya inasonkhanitsa pamodzi akuluakulu a mu mzindawo ndipo inapita ku Nyumba ya Yehova.
Potom vstav ráno Ezechiáš král, shromáždil úředníky města, a vstoupil do domu Hospodinova.
21 Iwo anabweretsa ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ziwiri monga nsembe zoperekedwa chifukwa cha tchimo la ufumu, la malo opatulika ndi Yuda. Tsono mfumu inalamula ansembe, zidzukulu za Aaroni, kuti apereke zimenezi pa guwa lansembe la Yehova.
A přivedli volků sedm, a skopců sedm, a beránků sedm, a kozlů sedm za hřích, za království, a za svatyni, a za Judu; a rozkázal synům Aronovým kněžím, aby obětovali na oltáři Hospodinovu.
22 Choncho anthuwo anapha ngʼombe zazimunazo ndipo ansembe anatenga magazi ake ndi kuwawaza pa guwa lansembe, kenaka anapha nkhosa zazimuna zija ndipo anawaza magazi ake pa guwa lansembe; anaphanso ana ankhosa aja ndipo anawaza magazi ake pa guwa lansembe.
Takž zbili voly ty, a kněží berouce krev jejich, kropili na oltář. Zbili též i skopce a pokropovali krví jejich oltáře; zbili také i beránky, a krví jejich kropili na oltář.
23 Mbuzi zoperekedwa chifukwa cha tchimo zija zinabweretsedwa pamaso pa mfumu ndi anthu onse, ndipo anasanjika manja awo pa izo.
Přivedli i kozly k oběti za hřích před krále i shromáždění, kteřížto vložili ruce své na ně.
24 Kenaka ansembe anapha mbuzizo ndipo anapereka magazi ake pa guwa, kuti ukhale mwambo wofafanizira machimo a Aisraeli onse, pakuti mfumu inalamula kuti nsembe yopsereza ndi yopepesera machimo zichitike chifukwa cha Aisraeli onse.
I zbili je kněží a vyčistili krví jejich oltář k očištění všeho Izraele; nebo za všecken lid Izraelský rozkázal král obětovati zápal a oběti za hřích.
25 Iye anayika Alevi mʼNyumba ya Yehova ali ndi ziwaya za malipenga, azeze ndi apangwe potsata lamulo la Davide, Gadi mlosi wa mfumu ndi mneneri Natani. Pakuti Yehova ndiye analamula zimenezi kudzera mwa aneneri.
Postavil zase i Levíty v domě Hospodinově s cymbály, loutnami a harfami podlé rozkázaní Davidova, a Gáda proroka královského, a Nátana proroka; nebo od Hospodina bylo to přikázáno skrze proroky jeho.
26 Kotero Alevi anayima okonzekera atanyamula zoyimbira za Davide ndiponso ansembe atanyamula malipenga awo.
A tak stáli Levítové s nástroji Davidovými a kněží s trubami.
27 Hezekiya analamulira kuti apereke nsembe zopsereza pa guwa. Pamene amayamba kupereka nsembezo, kuyimbira Yehova kunayambikanso, pamodzi ndi malipenga ndi zipangizo zoyimbira za Davide mfumu ya Israeli.
I rozkázal Ezechiáš, aby obětovali zápal na oltáři. A když se začala obět zápalná, začal se zpěv Hospodinův a troubení i zpěvové na nástroje Davida, krále Izraelského.
28 Anthu onse anawerama pansi ndi kulambira, pamene oyimba amayimba ndi malipenga. Izi zonse zinapitirira mpaka pa mapeto pa nsembe zopsereza.
Všecko pak shromáždění klanělo se, když zpěváci zpívali, a trubači troubili, a to vše, až se dokonal zápal.
29 Zopereka zitatha, mfumu ndi wina aliyense amene anali naye anagwada pansi ndi kulambira.
A když dokonali obětování zápalu, sklonili se král a všickni, kteříž byli s ním, a poklonu učinili.
30 Mfumu Hezekiya ndi akuluakulu ake analamulira Alevi kuti atamande Yehova potsata mawu a Davide ndi mlosi Asafu. Kotero anayimba nyimbo zamatamando mokondwera ndipo anaweramitsa mitu yawo ndi kulambira.
Tedy přikázal Ezechiáš král i knížata Levítům, aby chválili Hospodina slovy Davidovými a Azafa proroka. I chválili s velikým veselím, a sklánějíce se, poklonu činili.
31 Kenaka Hezekiya anati, “Inu mwadzipereka tsopano kwa Yehova. Bwerani ndipo mufike ndi nsembe ndi zopereka zachiyamiko ku Nyumba ya Yehova.” Choncho anthu onse anabweretsa nsembe ndi zopereka zachiyamiko, ndipo anthu onse amene anali ofuna mu mtima mwawo anabweretsa nsembe zopsereza.
Potom mluvil Ezechiáš, řka: Nyní jste posvětili rukou svých Hospodinu. Přistupte, a přiveďte oběti vítězné a oběti chvály do domu Hospodinova. Protož přivodilo shromáždění to oběti vítězné a oběti chvály, ano i každý z srdce ochotného k zápalným obětem,
32 Chiwerengero cha nsembe zopsereza chimene anthu onse anabweretsa chinali ngʼombe zazimuna makumi asanu ndi awiri, nkhosa zazimuna 100, ana ankhosa aamuna 200 ndipo zonsezi zinali za nsembe yopsereza kwa Yehova.
Tak že počet obětí zápalných, kteréž přivedlo shromáždění to, byl volů sedmdesáte, skopců sto, beránků dvě stě, všecko to na obět zápalnou Hospodinu.
33 Ziweto zimene zinapatulidwa kukhala nsembe zinalipo ngʼombe zazimuna 600, nkhosa ndi mbuzi 3,000.
Jiných pak věcí posvěcených bylo volů šest set, a ovec tři tisíce.
34 Koma ansembe anali ochepa kuti asende zonse zopsereza. Choncho abale awo Alevi anawathandiza mpaka ntchito yonse inatha ndipo mpaka ansembe ena atadziyeretsa, pakuti Alevi anachita changu kudziyeretsa kulekana ndi momwe anachitira ansembe.
Kněží však bylo málo, tak že nemohli postačiti vytahovati z koží všech obětí zápalných. Pročež pomáhali jim bratří jejich Levítové, až i dokonali dílo to, a dokudž se neposvětili jiní kněží; nebo Levítové byli hotovější ku posvěcení se, nežli kněží.
35 Panali nsembe zopsereza zochuluka, pamodzi ndi mafuta a nsembe yachiyanjano ndi nsembe yachakumwa imene imachitika pamodzi ndi nsembe yopsereza. Kotero ntchito ya mʼNyumba ya Mulungu inakhazikitsidwanso.
K tomu k zápalům bylo množství veliké tuků z obětí pokojných a obětí mokrých, kromě jiných zápalů. A tak vykonána byla služba domu Hospodinova.
36 Hezekiya ndi anthu onse anakondwera pa zimene Mulungu anachitira anthu ake, chifukwa zinachita mwamsangamsanga.
A veselil se Ezechiáš i všecken lid, že Bůh byl nastrojil lid, tak aby se ta věc rychle spravila.

< 2 Mbiri 29 >