< 2 Mbiri 28 >
1 Ahazi anali ndi zaka makumi awiri pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 16. Iye sanachite zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Davide kholo lake.
UAhazi wayeleminyaka engamatshumi amabili esiba yinkosi; wabusa iminyaka elitshumi lesithupha eJerusalema. Kodwa kenzanga okuqondileyo emehlweni eNkosi, njengoDavida uyise.
2 Iye anayenda mʼnjira za mafumu a Israeli ndipo anawumbanso mafano a chipembedzo cha Abaala.
Ngoba wahamba ezindleleni zamakhosi akoIsrayeli, wasesenzela oBhali izithombe ezibunjwe ngokuncibilikisa.
3 Iye amapsereza nsembe ku chigwa cha Hinomu, ndipo anaperekanso ana ake aamuna ngati nsembe yopsereza kutsatira njira zonyansa za mitundu imene Yehova anayithamangitsa pamaso pa Aisraeli.
Yena watshisa impepha esihotsheni sendodana kaHinomu, watshisa lamadodana akhe emlilweni, njengokwamanyala ezizwe iNkosi eyazixotsha elifeni phambi kwabantwana bakoIsrayeli.
4 Iyeyo ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani pa malo opembedzerapo mafano, pamwamba pa mapiri ndi pansi pa mtengo uliwonse waukulu.
Wanikela imihlatshelo watshisa impepha endaweni eziphakemeyo laphezu kwamaqaqa langaphansi kwaso sonke isihlahla esiluhlaza.
5 Nʼchifukwa chake Yehova Mulungu wake anamupereka mʼmanja mwa mfumu ya Aramu. Aaramu anamugonjetsa ndipo anagwira ukapolo anthu ake ambiri napita nawo ku Damasiko. Yehova anamuperekanso mʼmanja mwa mfumu ya Israeli, imene inamuzunza ndi kumuphera anthu ake ambiri.
Ngakho iNkosi uNkulunkulu wakhe yamnikela esandleni senkosi yeSiriya; asemtshaya, athumba kuye abathunjiweyo abanengi, abasa eDamaseko. Futhi wanikelwa esandleni senkosi yakoIsrayeli eyamtshaya ngokutshaya okukhulu.
6 Pa tsiku limodzi, Peka mwana wa Remaliya anapha asilikali 120,000 mu Yuda chifukwa Yuda anasiya Yehova, Mulungu wa makolo awo.
Ngoba uPheka indodana kaRemaliya wabulala koJuda abazinkulungwane ezilikhulu lamatshumi amabili ngasuku lunye, bonke bengamadoda alamandla, ngoba babeyidelile iNkosi uNkulunkulu waboyise.
7 Zikiri msilikali wa ku Efereimu, anapha Maaseya mwana wa mfumu, Azirikamu woyangʼanira nyumba yaufumu, ndi Elikana wachiwiri kwa mfumu.
UZikiri iqhawe lakoEfrayimi wasebulala uMahaseya indodana yenkosi loAzirikamu umphathi wendlu loElkana owesibili enkosini.
8 Aisraeli anagwira ukapolo abale awo, akazi, ana aamuna ndi ana aakazi okwanira 200,000. Iwo anafunkhanso katundu wambiri amene anapita naye ku Samariya.
Abantwana bakoIsrayeli basebethumba kubafowabo abazinkulungwane ezingamakhulu amabili, abesifazana, amadodana, lamadodakazi; baphanga lempango enengi kibo, bayiletha impango eSamariya.
9 Koma kumeneko kunali mneneri wa Yehova dzina lake Odedi, ndipo anapita kukakumana ndi gulu lankhondo pamene linabwerera ku Samariya. Iye anawawuza kuti, “Chifukwa Yehova, Mulungu wa makolo anu anakwiyira Ayuda, Iye anawapereka mʼdzanja lanu. Koma inu mwawapha mwaukali, ukali wake wofika mpaka kumwamba.
Kodwa kwakukhona lapho umprofethi weNkosi obizo lakhe lalinguOdedi; wasephuma phambi kwebutho elalisiza eSamariya, wathi kibo: Khangelani, ngenxa yolaka lweNkosi uNkulunkulu waboyihlo phezu kukaJuda, ibanikele esandleni senu; libabulele-ke ngolaka olufinyelele emazulwini.
10 Ndipo tsopano mukufuna kuti amuna ndi akazi a ku Yuda ndi ku Yerusalemu akhale akapolo anu.
Khathesi-ke lina lithi lehlisela ngaphansi kwenu abantwana bakoJuda labeJerusalema babe yizigqili lezigqilikazi. Kodwa lina kakulamacala yini kini amelene leNkosi uNkulunkulu wenu?
11 Tsono mvereni! Abwezeni abale anu amene mwawagwira ukapolo, pakuti mkwiyo wa Yehova uli pa inu.”
Ngakho-ke ngilalelani; libuyisele abathunjiweyo elibathumbe kubafowenu, ngoba ukuvutha kolaka lweNkosi kuphezu kwenu.
12 Tsono atsogoleri ena a ku Efereimu, Azariya mwana wa Yehohanani, Berekiya mwana wa Mesilemoti, Yehizikiya mwana wa Salumu, ndi Amasa mwana wa Hadilayi anatsutsana nawo amene ankachokera ku nkhondo kuja.
Kwasekusukuma amadoda kunhloko zabantwana bakoEfrayimi, oAzariya indodana kaJohanani, uBerekiya indodana kaMeshilemothi, loJehizikiya indodana kaShaluma, loAmasa indodana kaHadilayi, bamelana lalabo ababengena bevela ebuthweni.
13 Iwo anati, “Musabweretse akapolowo kuno, pakuti ife tidzakhala olakwa pamaso pa Yehova. Kodi mukufuna kuwonjezera pa machimo athu ndi kulakwa kwathu? Pakuti zolakwa zathu ndi zambiri kale ndipo mkwiyo wake woopsa uli pa Israeli.”
Basebesithi kibo: Kaliyikungenisa abathunjiweyo lapha kube licala eNkosini limelene lathi; ngoba lina lithi lizakwengeza ezonweni zethu lemacaleni ethu, ngoba isiphambeko sethu sikhulu, lokuvutha kolaka kuphezu kukaIsrayeli.
14 Kotero asilikali aja anawasiya akapolowo pamodzi ndi katundu amene analanda ku nkhondo pamaso pa akuluakulu ndi gulu lonse la anthu.
Ngakho abahlomileyo batshiya abathunjiweyo lempango phambi kweziphathamandla lebandla lonke.
15 Anthu amene atchulidwa mayina aja anatenga akapolowo, ndipo kuchokera pa zolanda ku nkhondo, anawaveka onse amene anali maliseche. Anawapatsa zovala ndi nsapato, chakudya ndi chakumwa ndi mankhwala. Onse amene anali ofowoka anawakweza pa abulu. Choncho anabwera nawo kwa abale awo ku Yeriko, Mzinda wa Migwalangwa, ndipo kenaka anawabweza ku Samariya.
Lamadoda abizwa ngamabizo asukuma, abamba abathunjiweyo, agqokisa bonke ababenqunu babo ngokuvela empangweni; yebo abagqokisa, abafaka amanyathela, abanika ukudla, abanathisa, abagcoba, athwala bonke ababuthakathaka ngabobabhemi, abasa eJeriko, umuzi wamalala, duze labafowabo; basebebuyela eSamariya.
16 Pa nthawi imeneyo mfumu Ahazi inatumiza mawu kwa mfumu ya ku Asiriya kupempha chithandizo.
Ngalesosikhathi inkosi uAhazi yathuma emakhosini eAsiriya ukumncedisa.
17 Ankhondo a ku Edomu anabweranso ndi kuthira nkhondo Yuda ndi kugwira akapolo.
Ngoba amaEdoma ayesebuye atshaya uJuda, athumba abathunjwa.
18 Pamenepo nʼkuti Afilisti atathira nkhondo mizinda ya mʼmbali mwa phiri ndi ku Negevi ku Yuda. Iwo analanda mizindayo nakhala ku Beti-Semesi, Ayaloni ndi Gederoti, komanso Soko, Timna ndi Gimizo pamodzi ndi midzi yawo yozungulira.
LamaFilisti ayehlasele imizi yesihotsha leningizimu yakoJuda, athumba iBeti-Shemeshi, leAjaloni, leGederothi, leSoko lemizana yayo, leTimina lemizana yayo, leGimizo lemizana yayo; ahlala khona.
19 Yehova anapeputsa Yuda chifukwa cha mfumu Ahazi ya Israeli, pakuti analimbikitsa zoyipa ku Yuda ndipo anali munthu wosakhulupirika kwambiri pamaso pa Yehova.
Ngoba iNkosi yamthobisa uJuda ngenxa kaAhazi inkosi yakoIsrayeli, ngoba wamenza ze uJuda, wasephambuka kakhulu eNkosini.
20 Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya anabwera kwa iye, ndipo anabweretsa mavuto mʼmalo momuthandiza.
Ngakho uTiligathi-Pileseri inkosi yeAsiriya wafika kuye, wamhlupha, kodwa kamqinisanga.
21 Ahazi anatenga zinthu zochokera mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba yaufumu ndi kwa atsogoleri ndipo anazipereka kwa mfumu ya ku Asiriya, koma zimenezo sizinamuthandize.
Ngoba uAhazi wathatha isabelo sendlu kaJehova lesendlu yenkosi leseziphathamandla, wasipha inkosi yeAsiriya; kodwa kayimsizanga.
22 Pa nthawi yake yamavutoyi mfumu Ahazi inapitirira kukhalabe yosakhulupirika pamaso pa Yehova.
Ngesikhathi sohlupho lwakhe wengeza-ke ekuphambekeni emelene loJehova. Le yinkosi uAhazi.
23 Ahazi ankapereka nsembe kwa milungu ya ku Damasiko, imene inamugonjetsa. Iye ankaganiza kuti, “Popeza milungu ya mafumu a Aaramu yawathandiza, ine ndidzapereka nsembe kwa iyo kuti indithandize.” Koma iyoyo inakhala kugwa kwake ndi kugwa kwa Aisraeli onse.
Ngoba wahlabela onkulunkulu beDamaseko ababemtshayile, wathi: Ngoba onkulunkulu bamakhosi eSiriya bayawasiza, ngizahlabela bona ukuze bangisize. Kodwa bona baba yimbangela yokuwa kwakhe, kuye lakuIsrayeli wonke.
24 Ahazi anasonkhanitsa pamodzi zinthu zonse kuchokera mʼNyumba ya Mulungu ndipo anazitenga. Iye anatseka zitseko za Nyumba ya Yehova ndipo anayimika maguwa ansembe pa ngodya iliyonse ya msewu mu Yerusalemu.
UAhazi waseqoqa izitsha zendlu kaNkulunkulu, waziquma iziqa izitsha zendlu kaNkulunkulu, wavala iminyango yendlu yeNkosi, wazenzela amalathi kuyo yonke ingonsi eJerusalema.
25 Mu mzinda uliwonse wa Yuda anamangamo malo achipembedzo, operekerapo nsembe zopsereza kwa milungu ina ndipo anaputa mkwiyo wa Yehova, Mulungu wa makolo ake.
Lakuwo wonke umuzi ngomuzi wakoJuda wenza indawo eziphakemeyo zokutshisela abanye onkulunkulu impepha, wayithukuthelisa iNkosi uNkulunkulu waboyise.
26 Zochitika zina pa ulamuliro wake ndi machitidwe ake onse, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli.
Ezinye-ke zezindaba zakhe lazo zonke indlela zakhe, ezokuqala lezokucina, khangela, zibhaliwe egwalweni lwamakhosi akoJuda lawakoIsrayeli.
27 Ahazi anamwalira ndipo anayikidwa mu mzinda wa Yerusalemu, koma sanamuyike mʼmanda a mafumu a Israeli. Ndipo Hezekiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
UAhazi waselala laboyise, basebemngcwabela emzini, eJerusalema; kodwa kabamlethanga emangcwabeni amakhosi akoIsrayeli. UHezekhiya indodana yakhe wasesiba yinkosi esikhundleni sakhe.