< 2 Mbiri 28 >

1 Ahazi anali ndi zaka makumi awiri pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 16. Iye sanachite zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Davide kholo lake.
Achaz avait vingt ans à son avènement et il régna seize ans à Jérusalem; il ne fit pas ce qui est droit aux yeux de l’Eternel comme David, son aïeul.
2 Iye anayenda mʼnjira za mafumu a Israeli ndipo anawumbanso mafano a chipembedzo cha Abaala.
Au contraire, il suivit l’exemple des rois d’Israël et fit même des idoles de fonte en l’honneur des Bealim.
3 Iye amapsereza nsembe ku chigwa cha Hinomu, ndipo anaperekanso ana ake aamuna ngati nsembe yopsereza kutsatira njira zonyansa za mitundu imene Yehova anayithamangitsa pamaso pa Aisraeli.
Il offrit de l’encens dans la vallée de Ben-Hinnom, fit brûler ses fils dans le feu, imitant les abominations des peuples que l’Eternel avait dépossédés au profit des enfants d’Israël.
4 Iyeyo ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani pa malo opembedzerapo mafano, pamwamba pa mapiri ndi pansi pa mtengo uliwonse waukulu.
Il offrit des sacrifices et de l’encens sur les hauts lieux et les collines et sous tous les arbres verdoyants.
5 Nʼchifukwa chake Yehova Mulungu wake anamupereka mʼmanja mwa mfumu ya Aramu. Aaramu anamugonjetsa ndipo anagwira ukapolo anthu ake ambiri napita nawo ku Damasiko. Yehova anamuperekanso mʼmanja mwa mfumu ya Israeli, imene inamuzunza ndi kumuphera anthu ake ambiri.
Alors l’Eternel, son Dieu, le livra au pouvoir du roi des Syriens, qui le battirent, lui prirent un grand nombre de captifs, qu’ils emmenèrent à Damas. Il fut livré aussi au roi d’Israël, qui lui infligea une grande défaite.
6 Pa tsiku limodzi, Peka mwana wa Remaliya anapha asilikali 120,000 mu Yuda chifukwa Yuda anasiya Yehova, Mulungu wa makolo awo.
Pékah, fils de Remaliahou, tua en Juda cent vingt mille hommes en un jour, tous de vaillants guerriers, parce qu’ils avaient abandonné l’Eternel, le Dieu de leurs pères.
7 Zikiri msilikali wa ku Efereimu, anapha Maaseya mwana wa mfumu, Azirikamu woyangʼanira nyumba yaufumu, ndi Elikana wachiwiri kwa mfumu.
Zikhri, un guerrier d’Ephraïm, tua Maassêyahou, fils du roi, Azrikam, intendant du palais, et Elkana, le vice-roi.
8 Aisraeli anagwira ukapolo abale awo, akazi, ana aamuna ndi ana aakazi okwanira 200,000. Iwo anafunkhanso katundu wambiri amene anapita naye ku Samariya.
Les enfants d’Israël capturèrent d’entre leurs frères deux cent mille âmes, femmes, fils et filles et ils leur prirent, en outre, un butin abondant, qu’ils emportèrent à Samarie.
9 Koma kumeneko kunali mneneri wa Yehova dzina lake Odedi, ndipo anapita kukakumana ndi gulu lankhondo pamene linabwerera ku Samariya. Iye anawawuza kuti, “Chifukwa Yehova, Mulungu wa makolo anu anakwiyira Ayuda, Iye anawapereka mʼdzanja lanu. Koma inu mwawapha mwaukali, ukali wake wofika mpaka kumwamba.
Là se trouvait un prophète de l’Eternel, nommé Oded. Il sortit à la rencontre de l’armée revenant à Samarie et leur dit: "Voyez! C’Est dans sa colère contre Juda que l’Eternel, Dieu de vos pères, les a livrés entre vos mains; mais vous en avez fait un carnage féroce qui s’est amoncelé jusqu’au ciel.
10 Ndipo tsopano mukufuna kuti amuna ndi akazi a ku Yuda ndi ku Yerusalemu akhale akapolo anu.
Et maintenant, ces enfants de Juda et de Jérusalem, vous parlez de les réduire à la condition d’esclaves et de servantes. N’Est-ce pas vous rendre coupables vous-mêmes à l’égard de l’Eternel, votre Dieu?
11 Tsono mvereni! Abwezeni abale anu amene mwawagwira ukapolo, pakuti mkwiyo wa Yehova uli pa inu.”
Or donc, écoutez-moi et restituez ces captifs que vous avez faits d’entre vos frères, car la colère de l’Eternel s’enflamme contre vous."
12 Tsono atsogoleri ena a ku Efereimu, Azariya mwana wa Yehohanani, Berekiya mwana wa Mesilemoti, Yehizikiya mwana wa Salumu, ndi Amasa mwana wa Hadilayi anatsutsana nawo amene ankachokera ku nkhondo kuja.
Alors quelques hommes d’entre les chefs des Ephraïmites, Azariahou, fils de Yehohanan, Bérékhiahou, fils de Mechillêmôt, Yéhizkiyahou, fils de Challoum, et Amassa, fils de Hadlaï, s’élevèrent contre ceux qui revenaient de l’expédition.
13 Iwo anati, “Musabweretse akapolowo kuno, pakuti ife tidzakhala olakwa pamaso pa Yehova. Kodi mukufuna kuwonjezera pa machimo athu ndi kulakwa kwathu? Pakuti zolakwa zathu ndi zambiri kale ndipo mkwiyo wake woopsa uli pa Israeli.”
Ils leur dirent: "N’Amenez pas ces captifs ici, ce serait nous charger d’un crime envers l’Eternel: vous voudriez ajouter à nos péchés et à notre crime; notre faute est déjà grande et le courroux divin s’est enflammé contre Israël."
14 Kotero asilikali aja anawasiya akapolowo pamodzi ndi katundu amene analanda ku nkhondo pamaso pa akuluakulu ndi gulu lonse la anthu.
Alors l’armée abandonna la capture et le butin aux chefs et à toute la foule.
15 Anthu amene atchulidwa mayina aja anatenga akapolowo, ndipo kuchokera pa zolanda ku nkhondo, anawaveka onse amene anali maliseche. Anawapatsa zovala ndi nsapato, chakudya ndi chakumwa ndi mankhwala. Onse amene anali ofowoka anawakweza pa abulu. Choncho anabwera nawo kwa abale awo ku Yeriko, Mzinda wa Migwalangwa, ndipo kenaka anawabweza ku Samariya.
Les hommes désignés nominativement se levèrent, se saisirent des captifs; tous ceux qui étaient nus, ils les vêtirent d’habits pris du butin, les habillèrent, les chaussèrent, leur donnèrent à manger et à boire, les frictionnèrent, conduisirent à âne tous ceux qui trébuchaient, les menèrent à Jéricho, la ville des palmiers, auprès de leurs frères et revinrent à Samarie.
16 Pa nthawi imeneyo mfumu Ahazi inatumiza mawu kwa mfumu ya ku Asiriya kupempha chithandizo.
En ce temps-là, le roi Achaz envoya demander aux rois d’Assyrie de lui venir en aide.
17 Ankhondo a ku Edomu anabweranso ndi kuthira nkhondo Yuda ndi kugwira akapolo.
Des Iduméens vinrent aussi, remportèrent une victoire en Juda et emmenèrent des prisonniers.
18 Pamenepo nʼkuti Afilisti atathira nkhondo mizinda ya mʼmbali mwa phiri ndi ku Negevi ku Yuda. Iwo analanda mizindayo nakhala ku Beti-Semesi, Ayaloni ndi Gederoti, komanso Soko, Timna ndi Gimizo pamodzi ndi midzi yawo yozungulira.
De plus, des Philistins envahirent les villes de la Basse-Terre et du Sud de Juda, conquirent Beth-Chémech, Ayyalôn, Ghedèrôt, Sokho avec ses dépendances, Timna avec ses dépendances et Ghimzo avec ses dépendances, et s’y établirent.
19 Yehova anapeputsa Yuda chifukwa cha mfumu Ahazi ya Israeli, pakuti analimbikitsa zoyipa ku Yuda ndipo anali munthu wosakhulupirika kwambiri pamaso pa Yehova.
Car l’Eternel avait humilié Juda à cause d’Achaz, roi d’Israël, qui s’était déréglé en Juda et montré rebelle à l’Eternel.
20 Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya anabwera kwa iye, ndipo anabweretsa mavuto mʼmalo momuthandiza.
Tilgat-Pilneécer, roi d’Assyrie, marcha contre lui et l’assiégea au lieu de l’assister.
21 Ahazi anatenga zinthu zochokera mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba yaufumu ndi kwa atsogoleri ndipo anazipereka kwa mfumu ya ku Asiriya, koma zimenezo sizinamuthandize.
Car Achaz avait dépouillé la maison de l’Eternel, le palais du roi et les chefs pour tout donner au roi d’Assyrie, mais cela ne lui servit de rien.
22 Pa nthawi yake yamavutoyi mfumu Ahazi inapitirira kukhalabe yosakhulupirika pamaso pa Yehova.
Et dans le temps de sa détresse, il continua ses infidélités à l’Eternel, lui, le roi Achaz.
23 Ahazi ankapereka nsembe kwa milungu ya ku Damasiko, imene inamugonjetsa. Iye ankaganiza kuti, “Popeza milungu ya mafumu a Aaramu yawathandiza, ine ndidzapereka nsembe kwa iyo kuti indithandize.” Koma iyoyo inakhala kugwa kwake ndi kugwa kwa Aisraeli onse.
Il sacrifia aux dieux de Damas qui l’avaient battu et dit: "Ce sont les dieux des rois de Syrie qui les ont secourus, je vais leur sacrifier et ils me secourront." Mais ce furent eux qui causèrent sa chute et celle de tout Israël.
24 Ahazi anasonkhanitsa pamodzi zinthu zonse kuchokera mʼNyumba ya Mulungu ndipo anazitenga. Iye anatseka zitseko za Nyumba ya Yehova ndipo anayimika maguwa ansembe pa ngodya iliyonse ya msewu mu Yerusalemu.
Achaz réunit les vases du temple de Dieu et les brisa. Il ferma les portes du temple de l’Eternel et se fit des autels dans tous les coins de Jérusalem.
25 Mu mzinda uliwonse wa Yuda anamangamo malo achipembedzo, operekerapo nsembe zopsereza kwa milungu ina ndipo anaputa mkwiyo wa Yehova, Mulungu wa makolo ake.
Et dans chaque ville de Juda il érigea des hauts lieux pour encenser les dieux étrangers, irritant ainsi l’Eternel, le Dieu de ses pères.
26 Zochitika zina pa ulamuliro wake ndi machitidwe ake onse, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli.
Le reste de ses faits et gestes et toutes ses actions, des premières aux dernières, se trouvent consignés dans le livre des Rois de Juda et d’Israël.
27 Ahazi anamwalira ndipo anayikidwa mu mzinda wa Yerusalemu, koma sanamuyike mʼmanda a mafumu a Israeli. Ndipo Hezekiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Achaz s’endormit avec ses pères et fut enterré dans la ville, à Jérusalem, car on ne le plaça point dans le sépulcre des rois d’Israël. Son fils Ezéchias lui succéda.

< 2 Mbiri 28 >