< 2 Mbiri 28 >
1 Ahazi anali ndi zaka makumi awiri pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 16. Iye sanachite zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Davide kholo lake.
Akaz var tyve Aar gammel da han blev Konge, og han herskede seksten Aar i Jerusalem. Han gjorde ikke, hvad der var ret i HERRENS Øjne, som hans Fader David,
2 Iye anayenda mʼnjira za mafumu a Israeli ndipo anawumbanso mafano a chipembedzo cha Abaala.
men vandrede i Israels Kongers Spor Ja, han lod lave støbte Billeder til Ba'alerne;
3 Iye amapsereza nsembe ku chigwa cha Hinomu, ndipo anaperekanso ana ake aamuna ngati nsembe yopsereza kutsatira njira zonyansa za mitundu imene Yehova anayithamangitsa pamaso pa Aisraeli.
han tændte selv Offerild i Hinnoms Søns Dal og lod sine Sønner gaa igennem Ilden efter de Folks vederstyggelige Skik, som HERREN havde drevet bort foran Israeliterne.
4 Iyeyo ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani pa malo opembedzerapo mafano, pamwamba pa mapiri ndi pansi pa mtengo uliwonse waukulu.
Han ofrede og tændte Offerild paa Offerhøjene og de høje Steder og under alle grønne Træer.
5 Nʼchifukwa chake Yehova Mulungu wake anamupereka mʼmanja mwa mfumu ya Aramu. Aaramu anamugonjetsa ndipo anagwira ukapolo anthu ake ambiri napita nawo ku Damasiko. Yehova anamuperekanso mʼmanja mwa mfumu ya Israeli, imene inamuzunza ndi kumuphera anthu ake ambiri.
Derfor gav HERREN hans Gud ham i Arams Konges Haand, og de slog ham og tog mange af hans Folk til Fange og førte dem til Darmaskus. Ligeledes blev han givet i Israels Konges Haand, og denne tilføjede ham et stort Nederlag.
6 Pa tsiku limodzi, Peka mwana wa Remaliya anapha asilikali 120,000 mu Yuda chifukwa Yuda anasiya Yehova, Mulungu wa makolo awo.
Peka, Remaljas Søn, dræbte i Juda 120 000 Mennesker paa een Dag, lutter dygtige Krigsfolk, fordi de havde forladt HERREN, deres Fædres Gud.
7 Zikiri msilikali wa ku Efereimu, anapha Maaseya mwana wa mfumu, Azirikamu woyangʼanira nyumba yaufumu, ndi Elikana wachiwiri kwa mfumu.
Den efraimitiske Helt Zikri dræbte Kongesønnen Ma'aseja, Paladsøversten Azrikam og Elkana, den ypperste næst Kongen.
8 Aisraeli anagwira ukapolo abale awo, akazi, ana aamuna ndi ana aakazi okwanira 200,000. Iwo anafunkhanso katundu wambiri amene anapita naye ku Samariya.
Israeliterne bortførte fra deres Brødre 200 000 Hustruer, Sønner og Døtre som Fanger og fratog dem et stort Bytte, som de førte til Samaria.
9 Koma kumeneko kunali mneneri wa Yehova dzina lake Odedi, ndipo anapita kukakumana ndi gulu lankhondo pamene linabwerera ku Samariya. Iye anawawuza kuti, “Chifukwa Yehova, Mulungu wa makolo anu anakwiyira Ayuda, Iye anawapereka mʼdzanja lanu. Koma inu mwawapha mwaukali, ukali wake wofika mpaka kumwamba.
Her boede en HERRENS Profet ved Navn Oded; han gik Hæren i Møde, da den kom til Samaria, og sagde til dem: »Fordi HERREN, eders Fædres Gud, var vred paa Juda, gav han dem i eders Haand; men I har anrettet et Blodbad iblandt dem med et Raseri, der naar til Himmelen!
10 Ndipo tsopano mukufuna kuti amuna ndi akazi a ku Yuda ndi ku Yerusalemu akhale akapolo anu.
Og nu tænker I paa at faa Magten over Folkene fra Juda og Jerusalem og gøre dem til eders Trælle og Trælkvinder! Har I da ikke ogsaa selv nok paa Samvittigheden over for HERREN eders Gud!
11 Tsono mvereni! Abwezeni abale anu amene mwawagwira ukapolo, pakuti mkwiyo wa Yehova uli pa inu.”
Lyd derfor mig og send de Fanger tilbage, som I har gjort blandt eders Brødre, thi HERRENS glødende Vrede er over eder!«
12 Tsono atsogoleri ena a ku Efereimu, Azariya mwana wa Yehohanani, Berekiya mwana wa Mesilemoti, Yehizikiya mwana wa Salumu, ndi Amasa mwana wa Hadilayi anatsutsana nawo amene ankachokera ku nkhondo kuja.
Da traadte nogle af Efraimiternes Overhoveder, Azarja, Johanans Søn, Berekja, Mesjillemots Søn, Hizkija, Sjallums Søn, og Amasa, Hadlajs Søn, frem for de hjemvendte Krigere
13 Iwo anati, “Musabweretse akapolowo kuno, pakuti ife tidzakhala olakwa pamaso pa Yehova. Kodi mukufuna kuwonjezera pa machimo athu ndi kulakwa kwathu? Pakuti zolakwa zathu ndi zambiri kale ndipo mkwiyo wake woopsa uli pa Israeli.”
og sagde til dem: »I maa ikke bringe Fangerne herhen! Thi I har i Sinde at øge vore Synder og vor Skyld ud over den Skyld, vi har over for HERREN; thi stor er vor Skyld, og glødende Vrede er over Israel!«
14 Kotero asilikali aja anawasiya akapolowo pamodzi ndi katundu amene analanda ku nkhondo pamaso pa akuluakulu ndi gulu lonse la anthu.
Da gav de væbnede Slip paa Fangerne og Byttet i Øversternes og hele Forsamlingens Paasyn;
15 Anthu amene atchulidwa mayina aja anatenga akapolowo, ndipo kuchokera pa zolanda ku nkhondo, anawaveka onse amene anali maliseche. Anawapatsa zovala ndi nsapato, chakudya ndi chakumwa ndi mankhwala. Onse amene anali ofowoka anawakweza pa abulu. Choncho anabwera nawo kwa abale awo ku Yeriko, Mzinda wa Migwalangwa, ndipo kenaka anawabweza ku Samariya.
og de ovenfor nævnte Mænd stod op og tog sig af Fangerne, gav alle de nøgne iblandt dem Klæder af Byttet, forsynede dem med Klæder og Sko, gav dem Mad og Drikke, salvede dem, lod dem, der ikke kunde gaa, ride paa Æsler og bragte dem til Jeriko, Palmestaden, hen i Nærheden af deres Brødre; derpaa vendte de tilbage til Samaria.
16 Pa nthawi imeneyo mfumu Ahazi inatumiza mawu kwa mfumu ya ku Asiriya kupempha chithandizo.
Paa den Tid sendte Kong Akaz Assyrerkongen Bud om Hjælp.
17 Ankhondo a ku Edomu anabweranso ndi kuthira nkhondo Yuda ndi kugwira akapolo.
Tilmed trængte Edomiterne ind og slog Judæerne og slæbte Krigsfanger bort.
18 Pamenepo nʼkuti Afilisti atathira nkhondo mizinda ya mʼmbali mwa phiri ndi ku Negevi ku Yuda. Iwo analanda mizindayo nakhala ku Beti-Semesi, Ayaloni ndi Gederoti, komanso Soko, Timna ndi Gimizo pamodzi ndi midzi yawo yozungulira.
Og Filisterne faldt ind i Lavlandets Byer og den judæiske Del af Sydlandet og indtog Bet-Sjemesj, Ajjalon, Gederot, Soko med Smaabyer, Timna med Smaabyer og Gimzo med Smaabyer og bosatte sig der.
19 Yehova anapeputsa Yuda chifukwa cha mfumu Ahazi ya Israeli, pakuti analimbikitsa zoyipa ku Yuda ndipo anali munthu wosakhulupirika kwambiri pamaso pa Yehova.
Thi HERREN ydmygede Juda for Kong Akaz af Judas Skyld, fordi han havde ladet Tøjlesløshed opkomme i Juda og været troløs mod HERREN.
20 Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya anabwera kwa iye, ndipo anabweretsa mavuto mʼmalo momuthandiza.
Men Assyrerkongen Tillegat-Pilneser drog imod ham og bragte ham i Nød i Stedet for at hjælpe ham;
21 Ahazi anatenga zinthu zochokera mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba yaufumu ndi kwa atsogoleri ndipo anazipereka kwa mfumu ya ku Asiriya, koma zimenezo sizinamuthandize.
thi Akaz plyndrede HERRENS Hus, og Kongens Palads og Øversternes Palads og gav det til Assyrerkongen, men det hjalp ham intet.
22 Pa nthawi yake yamavutoyi mfumu Ahazi inapitirira kukhalabe yosakhulupirika pamaso pa Yehova.
Og selv da Assyrerkongen bragte ham i Nød, var Kong Akaz paa ny troløs mod HERREN;
23 Ahazi ankapereka nsembe kwa milungu ya ku Damasiko, imene inamugonjetsa. Iye ankaganiza kuti, “Popeza milungu ya mafumu a Aaramu yawathandiza, ine ndidzapereka nsembe kwa iyo kuti indithandize.” Koma iyoyo inakhala kugwa kwake ndi kugwa kwa Aisraeli onse.
han ofrede til Darmaskus's Guder, som havde slaaet ham, idet han sagde: »Aramæerkongernes Guder har jo hjulpet dem; til dem vil jeg ofre, at de ogsaa maa hjælpe mig!« Men de blev ham og hele Israel til Fald.
24 Ahazi anasonkhanitsa pamodzi zinthu zonse kuchokera mʼNyumba ya Mulungu ndipo anazitenga. Iye anatseka zitseko za Nyumba ya Yehova ndipo anayimika maguwa ansembe pa ngodya iliyonse ya msewu mu Yerusalemu.
Ogsaa samlede Akaz Karrene i Guds Hus og slog dem i Stykker; og han lukkede HERRENS Hus's Porte og lavede sig Altre ved hvert et Hjørne i Jerusalem;
25 Mu mzinda uliwonse wa Yuda anamangamo malo achipembedzo, operekerapo nsembe zopsereza kwa milungu ina ndipo anaputa mkwiyo wa Yehova, Mulungu wa makolo ake.
og i hver eneste By i Juda indrettede han Offerhøje for at tænde Offerild for fremmede Guder; saaledes krænkede han HERREN, sine Fædres Gud.
26 Zochitika zina pa ulamuliro wake ndi machitidwe ake onse, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli.
Hvad der ellers er at fortælle om ham og hele hans Færd fra først til sidst, staar jo optegnet i Bogen om Judas og Israels Konger.
27 Ahazi anamwalira ndipo anayikidwa mu mzinda wa Yerusalemu, koma sanamuyike mʼmanda a mafumu a Israeli. Ndipo Hezekiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Saa lagde Akaz sig til Hvile hos sine Fædre, og man jordede ham i Jerusalem, inde i Byen, thi man vilde ikke jorde ham i Israels Kongegrave; og hans Søn Ezekias blev Konge i hans Sted.