< 2 Mbiri 27 >

1 Yotamu anakhala mfumu ali ndi zaka 25 ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 16. Dzina la amayi ake linali Yerusa mwana wa Zadoki.
Jotham var fem och tjugu åra gammal, då han Konung vardt, och regerade i sexton år i Jerusalem; hans moder het Jerusa, Zadoks dotter.
2 Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, monga anachitira Uziya abambo ake, kupatula kuti iyeyo sanalowe mʼNyumba ya Yehova. Komabe anthu anapitirira kuchita zoyipa.
Och han gjorde det Herranom väl behagade, såsom hans fader Ussia gjort hade; undantagno, att han icke gick i Herrans tempel. Och folket bar sig ännu illa åt.
3 Yotamu anamanganso chipata chakumtunda cha Nyumba ya Yehova ndipo anagwira ntchito yayikulu yomanga khoma la ku phiri la Ofeli.
Han byggde den höga porten i Herrans hus, och uppå muren Ophel byggde han mycket;
4 Iye anamanga mizinda mʼmapiri a ku Yuda ndipo anamanganso malinga ndi nsanja mʼmadera a ku nkhalango.
Och byggde städer på Juda berg, och i skogomen byggde han slott och torn.
5 Yotamu anachita nkhondo ndi mfumu ya Aamoni ndipo anawagonjetsa. Chaka chimenecho Aamoni anapereka makilogalamu 3,400, matani 1,000 a tirigu ndiponso matani 1,000 a barele. Aamoni anabweretsa zinthu zomwezi chaka chachiwiri ndi chachitatu.
Och han stridde med Ammons barnas Konung; och han vardt dem öfvermägtig; så att Ammons barn gåfvo honom i de samma årena hundrade centen er silfver, tio tusend corar hvete, och tiotusend corar bjugg; så mycket gåfvo ock Ammons barn honom i de andra och tredje årena.
6 Yotamu anakula mphamvu chifukwa anayenda molungama pamaso pa Yehova Mulungu wake.
Alltså vardt Jotham mägtig; ty han skickade sina vägar för Herranom sinom Gud.
7 Zina ndi zina zokhudza ulamuliro wa Yotamu, kuphatikizapo nkhondo zake zonse ndi zinthu zina zimene anachita, zinalembedwa mʼbuku la mafumu a Israeli ndi Yuda.
Hvad nu mer af Jotham sägande är, och alla hans strider, och hans vägar, si, det är skrifvet i Israels och Juda Konungars bok.
8 Iye anakhala mfumu ali ndi zaka 25 ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 16.
Fem och tjugu åra gammal var han, då han Konung vardt; och regerade i sexton år i Jerusalem.
9 Yotamu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu Mzinda wa Davide. Ndipo Ahazi mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Och Jotham afsomnade med sina fader; och de begrofvo honom i Davids stad. Och hans son Ahas vardt Konung i hans stad.

< 2 Mbiri 27 >