< 2 Mbiri 27 >

1 Yotamu anakhala mfumu ali ndi zaka 25 ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 16. Dzina la amayi ake linali Yerusa mwana wa Zadoki.
son: aged twenty and five year Jotham in/on/with to reign he and six ten year to reign in/on/with Jerusalem and name mother his Jerusha daughter Zadok
2 Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, monga anachitira Uziya abambo ake, kupatula kuti iyeyo sanalowe mʼNyumba ya Yehova. Komabe anthu anapitirira kuchita zoyipa.
and to make: do [the] upright in/on/with eye: appearance LORD like/as all which to make: do Uzziah father his except not to come (in): come to(wards) temple LORD and still [the] people to ruin
3 Yotamu anamanganso chipata chakumtunda cha Nyumba ya Yehova ndipo anagwira ntchito yayikulu yomanga khoma la ku phiri la Ofeli.
he/she/it to build [obj] gate house: temple LORD [the] high and in/on/with wall [the] Ophel to build to/for abundance
4 Iye anamanga mizinda mʼmapiri a ku Yuda ndipo anamanganso malinga ndi nsanja mʼmadera a ku nkhalango.
and city to build in/on/with mountain: hill country Judah and in/on/with wood to build fortress and tower
5 Yotamu anachita nkhondo ndi mfumu ya Aamoni ndipo anawagonjetsa. Chaka chimenecho Aamoni anapereka makilogalamu 3,400, matani 1,000 a tirigu ndiponso matani 1,000 a barele. Aamoni anabweretsa zinthu zomwezi chaka chachiwiri ndi chachitatu.
and he/she/it to fight with king son: descendant/people Ammon and to strengthen: prevail over upon them and to give: give to/for him son: descendant/people Ammon in/on/with year [the] he/she/it hundred talent silver: money and ten thousand kor wheat and barley ten thousand this to return: pay to/for him son: descendant/people (Ammon *LBH(a)*) and in/on/with year [the] second and [the] third
6 Yotamu anakula mphamvu chifukwa anayenda molungama pamaso pa Yehova Mulungu wake.
and to strengthen: strengthen Jotham for to establish: commit way: conduct his to/for face: before LORD God his
7 Zina ndi zina zokhudza ulamuliro wa Yotamu, kuphatikizapo nkhondo zake zonse ndi zinthu zina zimene anachita, zinalembedwa mʼbuku la mafumu a Israeli ndi Yuda.
and remainder word: deed Jotham and all battle his and way: conduct his look! they to write upon scroll: book king Israel and Judah
8 Iye anakhala mfumu ali ndi zaka 25 ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 16.
son: aged twenty and five year to be in/on/with to reign he and six ten year to reign in/on/with Jerusalem
9 Yotamu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu Mzinda wa Davide. Ndipo Ahazi mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
and to lie down: be dead Jotham with father his and to bury [obj] him in/on/with city David and to reign Ahaz son: child his underneath: instead him

< 2 Mbiri 27 >