< 2 Mbiri 26 >

1 Kenaka anthu onse a ku Yuda anatenga Uziya amene anali wa zaka 16, namuyika kukhala mfumu mʼmalo mwa Amaziya abambo ake.
Då tog hele Juda folk Ussia, som var sexton åra gammal, och gjorde honom till Konung i hans faders Amazia stad.
2 Iye anamanganso mzinda wa Eloti ndi kuwubwezeranso ku Yuda abambo ake atamwalira.
Han byggde Eloth, och lät det igenkomma till Juda, sedan Konungen afsomnad var med sina fäder.
3 Uziya anali wa zaka 16 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 70. Dzina la amayi ake linali Yekoliya wa ku Yerusalemu.
Sexton åra gammal var Ussia, då han Konung vardt, och regerade tu och femtio år i Jerusalem; hans moder het Jecholia af Jerusalem.
4 Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Amaziya abambo ake.
Och han gjorde det Herranom väl behagade, såsom hans fader Amazia gjort hade.
5 Iye anapembedza Mulungu nthawi ya Zekariya, amene ankamulangiza za kuopa Mulungu amene anamupatsa chipambano.
Och han sökte Gud, så länge Zacharia lefde, den läraren i Guds syner; och så länge han sökte Herren, lät honom Gud väl gå.
6 Iyeyo anapita kukachita nkhondo ndi Afilisti ndipo anagwetsa makoma a Gati, Yabine ndi Asidodi. Ndipo kenaka anamanganso mizinda ya pafupi ndi Asidodi ndi malo ena pafupi ndi Afilisti.
Ty han drog ut, och stridde emot de Philisteer, och bröt neder murarna i Gath, och murarna i Jabne, och murarna i Asdod, och ibland de Philisteer.
7 Mulungu anamuthandiza polimbana ndi Afilisti ndi Aarabu amene amakhala ku Guri-Baala ndiponso polimbana ndi Ameuni.
Ty Gud halp honom emot de Philisteer, emot de Araber, dem i Gurbaal, och emot de Menniter.
8 Aamoni ankabweretsa msonkho kwa Uziya ndipo mbiri yake inamveka mpaka ku malire a dziko la Igupto chifukwa anali wamphamvu kwambiri.
Och de Ammoniter gåfvo Ussia skänker, och han vardt namnkunnig allt intill der man kommer in i Egypten; ty han vardt ju starkare och starkare.
9 Uziya anamanga nsanja ku Yerusalemu ku Chipata Chapangodya, ku Chigwa cha Chipata ndi pokhotera mpanda, ndipo anayikamo chitetezo.
Och Ussia byggde torn i Jerusalem på hörnportenom, och på dalportenom, och på annor hörn, och befäste dem.
10 Iye anamanganso nsanja ku chipululu ndi kukumbanso zitsime zambiri chifukwa anali ndi ziweto zambiri mʼmbali mwa phiri ndi ku zigwa. Iye anali ndi anthu amene ankagwira ntchito mʼminda yake ndiponso mʼminda yake ya mphesa mʼphiri ndi malo achonde, pakuti ankakonda nthaka.
Han byggde ock slott i öknene, och grof många brunnar; ty han hade mycken boskap, både i dalar och slättmark, desslikes åkermän och vingårdsmän på bergen, och på Carmel; förty han hade lust till åkerverk.
11 Uziya anali ndi gulu lankhondo lophunzitsidwa bwino, lokonzekera kupita ku nkhondo mʼmagulu monga mwa chiwerengero chawo chimene mlembi Yeiyeli ndi Maaseya anasonkhanitsa motsogozedwa ndi Hananiya mmodzi mwa akuluakulu a mfumu.
Och Ussia hade en magt till strid, af krigsmän som i här drogo, i tal räknade under Jegiels skrifvarens hand, och Maaseja befallningsmansens, under Hanania hand, den af Konungens öfverstar var.
12 Chiwerengero chonse cha atsogoleri a mʼmabanja oyangʼanira anthu ochita nkhondo chinali 2,600.
Och talet på de yppersta fäder af de starka örligsmän var tutusend och sexhundrad.
13 Pansi pa ulamuliro wawo panali asilikali 307,500 ophunzitsidwa nkhondo, gulu lamphamvu lothandiza mfumu kulimbana ndi adani ake.
Och under deras hand härsmagten trehundradtusend, och sjutusend och femhundrad, skickelige till strid i härskraft, till att hjelpa Konungenom emot fienderna.
14 Uziya anawapangira asilikaliwo zishango, mikondo, zipewa zankhondo, malaya ankhondo achitsulo, mauta ndi miyala yogendera.
Och Ussia fick dem till hela hären sköldar, spjut, hjelmar, pansar, bågar, och slungor till att kasta sten med;
15 Mu Yerusalemu anapanga makina okonzedwa ndi anthu aluso amene amagwiritsidwa ntchito pa malo otetezera a pa nsanja ndi pa ngodya kuponyera mivi ndi kugubuduzira miyala. Mbiri yake inamveka kutali ndi ponseponse pakuti anathandizidwa kwambiri mpaka anakhala wamphamvu kwambiri.
Och gjorde i Jerusalem bröstvärn konsteliga, som skulle vara på tornen och hörnen, till att der utskjuta med pil och stora stenar. Och hans rykte kom vidt ut, derföre, att honom besynnerliga hulpet vardt, tilldess han mägtig blef.
16 Koma pamene Uziya anakhala wamphamvu kwambiri, kunyada kwake kunamuwononga. Iye sanakhulupirike kwa Yehova Mulungu wake, ndipo analowa mʼNyumba ya Yehova kukafukiza lubani pa guwa lofukizira.
Och då han var mägtig vorden, hof hans hjerta sig upp till hans förderf; ty han förtog sig på Herranom sinom Gud, och gick in i Herrans tempel, till att röka på rökaltaret.
17 Wansembe Azariya pamodzi ndi ansembe a Yehova ena 80 olimba mtima anamutsatira.
Men Asaria Presten gick efter honom, och åttatio Herrans Prester med honom, starke män;
18 Iwo anatsutsana naye ndipo anati, “Sibwino kuti inu mfumu muzifukiza lubani koma zidzukulu za Aaroni, zimene zinapatulidwa kuti zizifukiza lubani. Chokani pa malo opatulika ano, pakuti inu mwakhala osakhulupirika, ndipo simudzalemekezedwa ndi Yehova Mulungu.”
Och stodo emot Konung Ussia, och sade till honom: Det hörer icke dig till, Ussia, att röka för Herranom; utan Prestomen, Aarons barnom, som till att röka helgade äro. Gack härutu helgedomenom; ty du förtager dig, och det kommer dig till ingen äro för Herranom Gud.
19 Uziya, amene anali ndi chofukizira mʼmanja mwake wokonzeka kuti afukize lubani, anapsa mtima. Iye anakwiyira ansembewo. Ndipo ansembe aja akuona patsogolo pa guwa lofukizira lubani mʼNyumba ya Mulungu, khate linayamba pamphumi pake.
Men Ussia vardt vred, och hade ett rökelsekar i handene; och som han trätte med Presterna, gick spitelska ut i hans änne, för Presterna i Herrans hus, inför rökaltaret.
20 Azariya, mkulu wa ansembe pamodzi ndi ansembe ena onse atamuyangʼana anaona kuti anali ndi khate pamphumi pake, ndipo anamutulutsa mofulumira. Ndipo iye mwini anafulumira kutuluka, chifukwa Yehova anamulanga.
Och Asaria öfverste Presten vände sig till honom, och alle Presterna; och si, då var han spitelsk i hans änne; och de drefvo honom dädan. Skyndade han sig ock sjelf ut; ty hans plåga var af Herranom.
21 Mfumu Uziya anali ndi khate mpaka tsiku limene anamwalira. Iye amakhala mʼnyumba ya yekha ngati wakhate, ndipo samalowa mʼNyumba ya Yehova. Yotamu mwana wake ndiye amayangʼanira nyumba yaufumu ndipo ankalamulira anthu a mʼdzikomo.
Alltså var Konung Ussia spitelsk allt intill sin död, och bodde uti ett fritt hus spitelsk; ty han vardt utdrifven af Herrans hus. Men Jotham hans son stod Konungshuset före, och dömde folket i landena.
22 Ntchito zina za mfumu Uziya, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zinalembedwa ndi mneneri Yesaya mwana wa Amozi.
Hvad nu mer af Ussia sägande är, både det första och det sista, hafver den Propheten Esaia, Amos son, skrifvit.
23 Uziya analondola makolo ake, ndipo anamuyika pamodzi ndi makolo ake ku malo a manda a mafumu, koma osati mʼmanda mwawomo poti anthu anati, “Iyeyu anali ndi khate.” Ndipo Yotamu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Och Ussia afsomnade med sina fäder, och de begrofvo honom med sina fäder i åkrenom när Konungagrafvarna; ty de sade: Han är spitelsk. Och Jotham hans son vardt Konung i hans stad.

< 2 Mbiri 26 >