< 2 Mbiri 26 >
1 Kenaka anthu onse a ku Yuda anatenga Uziya amene anali wa zaka 16, namuyika kukhala mfumu mʼmalo mwa Amaziya abambo ake.
Entonces toda la gente de Judá tomó a Uzías, que tenía dieciséis años, y lo hizo rey en lugar de su padre Amasías.
2 Iye anamanganso mzinda wa Eloti ndi kuwubwezeranso ku Yuda abambo ake atamwalira.
Fue él que reconstruyó Elat, que regresó para Judá después de la muerte del rey.
3 Uziya anali wa zaka 16 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 70. Dzina la amayi ake linali Yekoliya wa ku Yerusalemu.
Uzías tenía dieciséis años cuando comenzó a reinar, y reinó en Jerusalén durante cincuenta y dos años; el nombre de su madre era Jecolias de Jerusalén.
4 Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Amaziya abambo ake.
Hizo lo correcto ante los ojos del Señor, como lo había hecho su padre Amasías.
5 Iye anapembedza Mulungu nthawi ya Zekariya, amene ankamulangiza za kuopa Mulungu amene anamupatsa chipambano.
Se dedicó a buscar a Dios en los días de Zacarías, que hizo sabios a los hombres en el temor de Dios; y mientras fue fiel al Señor, Dios lo prosperó.
6 Iyeyo anapita kukachita nkhondo ndi Afilisti ndipo anagwetsa makoma a Gati, Yabine ndi Asidodi. Ndipo kenaka anamanganso mizinda ya pafupi ndi Asidodi ndi malo ena pafupi ndi Afilisti.
Salió e hizo la guerra contra los filisteos, derribando los muros de Gat y Jabnia y Asdod, y construyendo ciudades en el campo alrededor de Asdod entre los filisteos.
7 Mulungu anamuthandiza polimbana ndi Afilisti ndi Aarabu amene amakhala ku Guri-Baala ndiponso polimbana ndi Ameuni.
Y Dios le dio ayuda contra los filisteos, y contra los árabes que viven en Gur-baal, y contra los de meunim.
8 Aamoni ankabweretsa msonkho kwa Uziya ndipo mbiri yake inamveka mpaka ku malire a dziko la Igupto chifukwa anali wamphamvu kwambiri.
Los amonitas hicieron ofrendas a Uzías; y noticias de él llegaron hasta el límite de Egipto; porque se hizo muy grande en poder.
9 Uziya anamanga nsanja ku Yerusalemu ku Chipata Chapangodya, ku Chigwa cha Chipata ndi pokhotera mpanda, ndipo anayikamo chitetezo.
Uzías hizo torres en Jerusalén, en la puerta de la esquina, en la puerta en el valle y en el giro de la esquina, los fortificó.
10 Iye anamanganso nsanja ku chipululu ndi kukumbanso zitsime zambiri chifukwa anali ndi ziweto zambiri mʼmbali mwa phiri ndi ku zigwa. Iye anali ndi anthu amene ankagwira ntchito mʼminda yake ndiponso mʼminda yake ya mphesa mʼphiri ndi malo achonde, pakuti ankakonda nthaka.
Y él levantó torres en el desierto e hizo pozos para almacenar agua, porque tenía mucho ganado, en las llanuras y en las mesetas; y tenía granjeros y viticultores en las montañas y en la tierra fértil, porque era un amante de la agricultura.
11 Uziya anali ndi gulu lankhondo lophunzitsidwa bwino, lokonzekera kupita ku nkhondo mʼmagulu monga mwa chiwerengero chawo chimene mlembi Yeiyeli ndi Maaseya anasonkhanitsa motsogozedwa ndi Hananiya mmodzi mwa akuluakulu a mfumu.
Además, Uzías tenía un ejército de guerreros que salían a la guerra en bandas, como habían sido listados por Jeiel el escriba y Maasias, el gobernante, bajo la autoridad de Hananías, uno de los capitanes del rey.
12 Chiwerengero chonse cha atsogoleri a mʼmabanja oyangʼanira anthu ochita nkhondo chinali 2,600.
Los jefes de familia, los hombres de guerra fuertes, eran dos mil seiscientos.
13 Pansi pa ulamuliro wawo panali asilikali 307,500 ophunzitsidwa nkhondo, gulu lamphamvu lothandiza mfumu kulimbana ndi adani ake.
Y bajo sus órdenes había un ejército entrenado de trescientos siete mil quinientos, guerreros valientes ayudando al rey contra cualquiera que viniera contra él.
14 Uziya anawapangira asilikaliwo zishango, mikondo, zipewa zankhondo, malaya ankhondo achitsulo, mauta ndi miyala yogendera.
Y Uzías tenía todas estas fuerzas armaduras y lanzas y cabezas protectoras y escudos, arcos y piedras para enviar desde bandas de cuero.
15 Mu Yerusalemu anapanga makina okonzedwa ndi anthu aluso amene amagwiritsidwa ntchito pa malo otetezera a pa nsanja ndi pa ngodya kuponyera mivi ndi kugubuduzira miyala. Mbiri yake inamveka kutali ndi ponseponse pakuti anathandizidwa kwambiri mpaka anakhala wamphamvu kwambiri.
Y en Jerusalén hizo máquinas, la invención de hombres expertos, para colocarlas en las torres y los ángulos de las paredes para enviar flechas y piedras grandes. Y su nombre fue honrado por todas partes; porque fue ayudado grandemente hasta que fue fuerte.
16 Koma pamene Uziya anakhala wamphamvu kwambiri, kunyada kwake kunamuwononga. Iye sanakhulupirike kwa Yehova Mulungu wake, ndipo analowa mʼNyumba ya Yehova kukafukiza lubani pa guwa lofukizira.
Pero cuando se hizo fuerte, su corazón se enorgulleció, causando su destrucción; e hizo lo malo contra el SEÑOR su Dios; porque entró al Templo del Señor con el propósito de quemar incienso en el altar del incienso.
17 Wansembe Azariya pamodzi ndi ansembe a Yehova ena 80 olimba mtima anamutsatira.
Luego entró el sacerdote Azarías con él, con ochenta sacerdotes del Señor, que eran hombres valientes;
18 Iwo anatsutsana naye ndipo anati, “Sibwino kuti inu mfumu muzifukiza lubani koma zidzukulu za Aaroni, zimene zinapatulidwa kuti zizifukiza lubani. Chokani pa malo opatulika ano, pakuti inu mwakhala osakhulupirika, ndipo simudzalemekezedwa ndi Yehova Mulungu.”
E hicieron protestas al rey Uzías, y le dijeron: Él ofrecer incienso, Rey Uzías, no es asunto tuyo, sino de los sacerdotes, los hijos de Aarón, que han sido consagrados para este trabajo: Sal del lugar santo, porque has hecho mal, y no será para tu honor delante de Dios.
19 Uziya, amene anali ndi chofukizira mʼmanja mwake wokonzeka kuti afukize lubani, anapsa mtima. Iye anakwiyira ansembewo. Ndipo ansembe aja akuona patsogolo pa guwa lofukizira lubani mʼNyumba ya Mulungu, khate linayamba pamphumi pake.
Entonces Uzías se enojó; y tenía en su mano un recipiente para quemar incienso; y mientras su ira era amarga contra los sacerdotes, la marca de la enfermedad del leproso apareció en su frente, ante los ojos de los sacerdotes en la casa del Señor por el altar de los inciensos.
20 Azariya, mkulu wa ansembe pamodzi ndi ansembe ena onse atamuyangʼana anaona kuti anali ndi khate pamphumi pake, ndipo anamutulutsa mofulumira. Ndipo iye mwini anafulumira kutuluka, chifukwa Yehova anamulanga.
Y Azarías, el principal sacerdote, y todos los sacerdotes, mirándolo, vieron la marca del leproso en su frente, lo enviaron rápidamente y él mismo salió de inmediato, porque el castigo del Señor había venido sobre él.
21 Mfumu Uziya anali ndi khate mpaka tsiku limene anamwalira. Iye amakhala mʼnyumba ya yekha ngati wakhate, ndipo samalowa mʼNyumba ya Yehova. Yotamu mwana wake ndiye amayangʼanira nyumba yaufumu ndipo ankalamulira anthu a mʼdzikomo.
Así que el rey Uzías fue un leproso hasta el día de su muerte, viviendo separado en su casa particular; porque fue cortado de la casa de Dios; y Jotam su hijo estaba gobernando su casa, juzgando a la gente de la tierra.
22 Ntchito zina za mfumu Uziya, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zinalembedwa ndi mneneri Yesaya mwana wa Amozi.
Ahora, el resto de los hechos de Uzías, desde él principio a fin, fueron registrados por el profeta Isaías, el hijo de Amoz.
23 Uziya analondola makolo ake, ndipo anamuyika pamodzi ndi makolo ake ku malo a manda a mafumu, koma osati mʼmanda mwawomo poti anthu anati, “Iyeyu anali ndi khate.” Ndipo Yotamu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Y Uzías murió; y lo enterraron en el campo del cementerio real usado para los reyes, porque dijeron: Es un leproso, y Jotam su hijo se convirtió en rey en su lugar.