< 2 Mbiri 26 >

1 Kenaka anthu onse a ku Yuda anatenga Uziya amene anali wa zaka 16, namuyika kukhala mfumu mʼmalo mwa Amaziya abambo ake.
Tedy wszystek lud Judzki wzięli Uzyjasza, który miał szesnaście lat, i postanowili go królem miasto ojca jego Amazyjasza.
2 Iye anamanganso mzinda wa Eloti ndi kuwubwezeranso ku Yuda abambo ake atamwalira.
Ten pobudował Elat, a przywrócił je do Judy, gdy zasnął król z ojcami swymi.
3 Uziya anali wa zaka 16 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 70. Dzina la amayi ake linali Yekoliya wa ku Yerusalemu.
Szesnaście lat było Uzyjaszowi, gdy królować począł, a pięćdziesiąt i dwa lata królował w Jeruzalemie; a imię matki jego Jechalija z Jeruzalemu.
4 Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Amaziya abambo ake.
Ten czynił, co było dobrego w oczach Pańskich według wszystkiego, jako czynił Amazyjasz, ojciec jego.
5 Iye anapembedza Mulungu nthawi ya Zekariya, amene ankamulangiza za kuopa Mulungu amene anamupatsa chipambano.
I szukał Boga za dnia Zacharyjasza, rozumiejącego widzenia Boże; a po wszystkie one dni, których szukał Pana, szczęścił go Bóg.
6 Iyeyo anapita kukachita nkhondo ndi Afilisti ndipo anagwetsa makoma a Gati, Yabine ndi Asidodi. Ndipo kenaka anamanganso mizinda ya pafupi ndi Asidodi ndi malo ena pafupi ndi Afilisti.
Bo ruszywszy się, walczył z Filistynami, i poburzył mury w Get, i mury w Jabnie, i mury w Azocie, a pobudował miasta w Azocie i w ziemi Filistyńskiej.
7 Mulungu anamuthandiza polimbana ndi Afilisti ndi Aarabu amene amakhala ku Guri-Baala ndiponso polimbana ndi Ameuni.
Albowiem pomagał mu Bóg przeciw Filistynom, i przeciw Arabczykom, którzy mieszkali w Gurbaalu, i przeciw Mahunitom.
8 Aamoni ankabweretsa msonkho kwa Uziya ndipo mbiri yake inamveka mpaka ku malire a dziko la Igupto chifukwa anali wamphamvu kwambiri.
I dawali Ammonitowie Uzyjaszowi dary, a rozniosło się imię jego aż do samego Egiptu; bo się był zmocnił nader bardzo.
9 Uziya anamanga nsanja ku Yerusalemu ku Chipata Chapangodya, ku Chigwa cha Chipata ndi pokhotera mpanda, ndipo anayikamo chitetezo.
I budował Uzyjasz wieże w Jeruzalemie nad bramą narożną, i nad bramą doliny, i nad Mikzoa, i umocnił je.
10 Iye anamanganso nsanja ku chipululu ndi kukumbanso zitsime zambiri chifukwa anali ndi ziweto zambiri mʼmbali mwa phiri ndi ku zigwa. Iye anali ndi anthu amene ankagwira ntchito mʼminda yake ndiponso mʼminda yake ya mphesa mʼphiri ndi malo achonde, pakuti ankakonda nthaka.
Pobudował też wieże na puszczy, i pokopał wiele studzien; bo miał bardzo wiele stad, tak w dolinach, jako i w równinach, i rolników, i winiarzy po górach, i na Karmelu: albowiem się kochał w uprawianiu ról.
11 Uziya anali ndi gulu lankhondo lophunzitsidwa bwino, lokonzekera kupita ku nkhondo mʼmagulu monga mwa chiwerengero chawo chimene mlembi Yeiyeli ndi Maaseya anasonkhanitsa motsogozedwa ndi Hananiya mmodzi mwa akuluakulu a mfumu.
Miał też Uzyjasz wojsko gotowe do bitwy, które wychodziło na wojnę w pocztach swych według liczby, jako byli obliczeni przez Jechijela kanclerza, i Maasajasza kapłana, pod sprawą Hananijasza, książęcia królewskiego.
12 Chiwerengero chonse cha atsogoleri a mʼmabanja oyangʼanira anthu ochita nkhondo chinali 2,600.
Wszystka liczba przedniejszych z domów ojcowskich, ludzi rycerskich, dwa tysiące i sześć set.
13 Pansi pa ulamuliro wawo panali asilikali 307,500 ophunzitsidwa nkhondo, gulu lamphamvu lothandiza mfumu kulimbana ndi adani ake.
A pod sprawą ich ludu walecznego trzy kroć i sto tysięcy, i siedm tysięcy i pięć set, ludu sposobnego do wojny, na pomoc królowi przeciw nieprzyjacielowi.
14 Uziya anawapangira asilikaliwo zishango, mikondo, zipewa zankhondo, malaya ankhondo achitsulo, mauta ndi miyala yogendera.
I zgotował Uzyjasz wszystkiemu onemu wojsku tarcze i drzewce, i przyłbice, i pancerze, i łuki, i kamienie do proc.
15 Mu Yerusalemu anapanga makina okonzedwa ndi anthu aluso amene amagwiritsidwa ntchito pa malo otetezera a pa nsanja ndi pa ngodya kuponyera mivi ndi kugubuduzira miyala. Mbiri yake inamveka kutali ndi ponseponse pakuti anathandizidwa kwambiri mpaka anakhala wamphamvu kwambiri.
Naczynił też w Jeruzalemie sztuk wojennych bardzo misternych, aby były na wieżach, i na węgłach ku wypuszczaniu strzał, i kamienia wielkiego; i rozniosło się imię jego daleko, przeto, że miał dziwną pomoc, aż się zmocnił.
16 Koma pamene Uziya anakhala wamphamvu kwambiri, kunyada kwake kunamuwononga. Iye sanakhulupirike kwa Yehova Mulungu wake, ndipo analowa mʼNyumba ya Yehova kukafukiza lubani pa guwa lofukizira.
Ale gdy się zmocnił, podniosło się serce jego ku zginieniu jego, i wystąpił przeciw Panu, Bogu swemu, i wszedł do kościoła Pańskiego, aby kadził na ołtarzu kadzenia.
17 Wansembe Azariya pamodzi ndi ansembe a Yehova ena 80 olimba mtima anamutsatira.
I wszedł za nim Azaryjasz kapłan, a z nim kapłanów Pańskich ośmdziesiąt, mężów dużych.
18 Iwo anatsutsana naye ndipo anati, “Sibwino kuti inu mfumu muzifukiza lubani koma zidzukulu za Aaroni, zimene zinapatulidwa kuti zizifukiza lubani. Chokani pa malo opatulika ano, pakuti inu mwakhala osakhulupirika, ndipo simudzalemekezedwa ndi Yehova Mulungu.”
I stanęli przeciw Uzyjaszowi królowi, a mówili mu: Nie twoja to rzecz Uzyjaszu! kadzić Panu, ale kapłanów, synów Aaronowych, którzy są poświęceni, aby kadzili. Wynijdźże z świątnicy; albowiemeś wystąpił, a nie będzieć to ku sławie przed Panem Bogiem.
19 Uziya, amene anali ndi chofukizira mʼmanja mwake wokonzeka kuti afukize lubani, anapsa mtima. Iye anakwiyira ansembewo. Ndipo ansembe aja akuona patsogolo pa guwa lofukizira lubani mʼNyumba ya Mulungu, khate linayamba pamphumi pake.
Przetoż się rozgniewał Uzyjasz, mając w rękach swych kadzielnicę, aby kadził. A gdy się srożył przeciwko kapłanom, trąd wystąpił na czoło jego przed kapłanami w domu Pańskim u ołtarza kadzenia.
20 Azariya, mkulu wa ansembe pamodzi ndi ansembe ena onse atamuyangʼana anaona kuti anali ndi khate pamphumi pake, ndipo anamutulutsa mofulumira. Ndipo iye mwini anafulumira kutuluka, chifukwa Yehova anamulanga.
A wejrzawszy nań Azaryjasz, kapłan najwyższy, i wszyscy kapłani, a oto był trędowatym na czole swojem; przetoż prędko wygnali go stamtąd; owszem i sam pospieszał wynijść, przeto, iż go zaraził Pan.
21 Mfumu Uziya anali ndi khate mpaka tsiku limene anamwalira. Iye amakhala mʼnyumba ya yekha ngati wakhate, ndipo samalowa mʼNyumba ya Yehova. Yotamu mwana wake ndiye amayangʼanira nyumba yaufumu ndipo ankalamulira anthu a mʼdzikomo.
A tak był król Uzyjasz trędowatym aż do dnia śmierci swej, i mieszkał w domu osobnym, będąc trędowatym; albowiem był wyłączon z domu Pańskiego; międzytem Joatam, syn jego, był nad domem królewskim, sądząc lud ziemi.
22 Ntchito zina za mfumu Uziya, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zinalembedwa ndi mneneri Yesaya mwana wa Amozi.
A inne sprawy Uzyjaszowe, pierwsze i poślednie, opisał prorok Izajasz, syn Amosowy.
23 Uziya analondola makolo ake, ndipo anamuyika pamodzi ndi makolo ake ku malo a manda a mafumu, koma osati mʼmanda mwawomo poti anthu anati, “Iyeyu anali ndi khate.” Ndipo Yotamu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
I zasnął Uzyjasz z ojcami swymi, a pochowano go z ojcami jego na polu grobów królewskich; bo mówili: Trędowaty jest. A królował Joatam, syn jego, miasto niego.

< 2 Mbiri 26 >