< 2 Mbiri 25 >

1 Amaziya anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 29. Dzina la amayi ake linali Yehoyadini wa ku Yerusalemu.
U-Amaziya wayeleminyaka engamatshumi amabili lanhlanu ubudala ekubekweni kwakhe ukuba yinkosi, njalo wabusa eJerusalema okweminyaka engamatshumi amabili lasificamunwemunye. Ibizo likanina linguJehowadani evela eJerusalema.
2 Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, koma osati ndi mtima wonse.
Wenza okulungileyo emehlweni kaThixo, kodwa kakwenzanga ngenhliziyo yakhe yonke.
3 Pamene mphamvu zonse zaufumu zinali mʼmanja mwake, iye anapha akuluakulu amene anapha abambo ake, mfumu ija.
Kwathi umbuso wakhe usuqinile, wabulala izikhulu zakhe ezazibulele inkosi uyise.
4 Komabe iye sanaphe ana awo koma anatsatira zolembedwa mʼbuku la Mose, mʼmene Yehova analamula kuti, “Makolo sadzaphedwa chifukwa cha ana awo kapena ana kuphedwa chifukwa cha makolo awo. Aliyense adzafera machimo ake.”
Kodwa amadodana azo kawabulalanga, wenza okuseMthethweni, eNcwadini kaMosi, lapho uThixo wapha umlayo wathi: “Oyise kabayikubulawa ngenxa yabantwababo, labantwababo kabayikubulawa ngenxa yaboyise; ngulowo lalowo uzafela izono zakhe.”
5 Amaziya anasonkhanitsa anthu a ku Yuda ndipo anawapatsa zochita molingana ndi mabanja awo kukhala anthu olamulira 1,000, ndi olamulira 100 pa Ayuda onse ndi Benjamini. Ndipo iye anawerenga amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo napeza kuti analipo amuna 300,000 okonzeka kugwira ntchito ya usilikali, okhoza kugwiritsa ntchito mkondo ndi chishango.
U-Amaziya wabuthanisa abantu bakoJuda wabamisa ngezindlu zabo bephethwe yizinduna zezinkulungwane lezamakhulu kwelakoJuda lelakoBhenjamini. Wasebutha kusukela kwabaleminyaka engamatshumi amabili kusiya phezulu, wathola bezinkulungwane ezingamakhulu amathathu, amadoda akhethiweyo, angaphuma impi, angahloma ngemikhonto langezihlangu.
6 Iye analembanso ntchito anthu odziwa nkhondo 100,000 ochokera ku Israeli pa mtengo wa makilogalamu 3,400 a siliva.
Wabuya waqhatsha ko-Israyeli amaqhawe alamandla azinkulungwane ezilikhulu ngamathalenta esiliva alikhulu.
7 Koma munthu wa Mulungu anabwera kwa iye ndipo anati, “Inu mfumu, asilikali awa ochokera ku Israeli asapite ndi inu, pakuti Yehova sali ndi Israeli kapena ndi aliyense wa anthu a Efereimu.
Kodwa kwafika kuye inceku kaNkulunkulu yathi: “Nkosi yami, amabutho ako-Israyeli la akufanelanga aphume impi kanye lawe ngoba uThixo kakho kwabako-Israyeli, kakho lakubani ebantwini bako-Efrayimi.
8 Ngakhale mupite ndi kuchita nkhondo molimba mtima, Mulungu adzakugonjetsani pamaso pa adani anu, pakuti Mulungu ali ndi mphamvu yothandiza kapena kugonjetsa.”
Loba ungaze uhambe uyekulwa ngesibindi empini, uNkulunkulu uzakuchitha phambi kwesitha ngoba uNkulunkulu ulamandla okukusiza loba ukukuchitha.”
9 Amaziya anafunsa munthu wa Mulungu kuti, “Koma nanga za makilogalamu aja a siliva amene ndapereka kwa asilikali a Israeli?” Munthu wa Mulungu anayankha kuti, “Yehova atha kukupatsani zambiri kuposa zimenezo.”
U-Amaziya wasebuza inceku kaNkulunkulu wathi, “Pho ngizakuthini ngamathalenta alikhulu engiwabhadalele amabutho ako-Israyeli?” Inceku kaNkulunkulu yaphendula yathi, “UThixo angakunika okunengi kakhulu kulalokho.”
10 Choncho Amaziya anachotsa asilikali amene anabwera kwa iye kuchokera ku Efereimu ndipo anawatumiza kwawo. Iwo anakwiyira anthu a ku Yuda ndipo anapita kwawo atapsa mtima kwambiri.
U-Amaziya wawakhulula amabutho ayevela ko-Efrayimi wathi kawabuyele kibo. Lokhu amabutho abazondela abakoJuda abuyela kibo ngokufuthelana okukhulu.
11 Ndipo Amaziya analimba mtima ndipo anatsogolera gulu lake lankhondo ku Chigwa cha Mchere, kumene anapha anthu 10,000 a ku Seiri.
U-Amaziya wasequnga isibindi, waphuma lamabutho akhe, waya eSigodini seTswayi, lapho abulala khona amadoda aseSeyiri azinkulungwane ezilitshumi.
12 Gulu la ankhondo la Yuda linagwiranso anthu amoyo 10,000, napita nawo pamwamba pa thanthwe ndipo anawaponya pansi kotero kuti onse ananyenyeka.
Ibutho lakoJuda lathumba amadoda azinkulungwane ezilitshumi ephila, lawaqhuba layawafikisa engqongeni yeliwa lapho awaphosela khona phansi aphahlazeka wonke aba yizicucu.
13 Pa nthawi imeneyi asilikali amene Amaziya anawabweza ndipo sanawalole kuti achite nawo nkhondo, anakathira nkhondo mizinda ya Yuda kuyambira ku Samariya mpaka ku Beti-Horoni. Iwo anapha anthu 3,000 ndipo anafunkha katundu wambiri.
Kwathi amabutho ayebuyiselwe emuva ngu-Amaziya ngoba engasafuni ukuthi amlwele impi, ahamba ehlasela imizi yaseSamariya laseBhethi-Horoni kwelakoJuda. Abulala abantu abazinkulungwane ezintathu njalo athutha impango enengi kakhulu.
14 Amaziya atabwerera kuja anakapha Aedomu, anabweretsa milungu ya anthu a ku Seiri. Ndipo anayika kuti ikhale milungu yake, ankayipembedza ndi kupereka nsembe zopsereza.
U-Amaziya wathi esevela bulala ama-Edomi wabuya ethwele onkulunkulu babantu baseSeyiri. Wabamisa baba ngonkulunkulu bakhe wakhothama kubo wanikela iminikelo yokutshiswa.
15 Yehova anakwiyira Amaziya, ndipo anamutumizira mneneri amene anati, “Nʼchifukwa chiyani mukupembedza milungu ya anthu awa, imene sinathe kupulumutsa anthu ake mʼdzanja lanu?”
Ulaka lukaThixo lwavutha wathukuthelela u-Amaziya, wasethuma umphrofethi owafika wambuza wathi, “Kungani udinga uncedo kubonkulunkulu balababantu na, abehluleka ukuvikela abantu babo ekubahlaseleni kwakho?”
16 Iye ali kuyankhula, mfumu inati, “Kodi ife takusankha iwe kuti ukhale mlangizi wa mfumu? Khala chete! Ufuna kuphedweranji?” Choncho mneneriyo analeka koma anati, “Ine ndikudziwa kuti Mulungu watsimikiza kukuwonongani chifukwa mwachita izi ndipo simunamvere uphungu wanga.”
Wathi esakhuluma, inkosi yathi kuye, “Sikubekile yini ukuba ngumcebisi wenkosi na? Thula! Kungani udinga ukubulawa na?” Ngakho umphrofethi wema kodwa wasesithi, “Ngiyakwazi ukuthi uNkulunkulu uzimisele ukuthi akubhubhise, ngoba lokhu akwenzileyo kutsho ukuthi awuzange ulalele ukucebisa kwami.”
17 Amaziya mfumu ya ku Yuda, atafunsa alangizi ake, anatumiza mawu awa kwa Yowasi mwana wa Yehowahazi mwana wa Yehu, mfumu ya Israeli: “Bwera udzakumane nane maso ndi maso.”
Ngemva kokuba u-Amaziya inkosi yakoJuda eseke wabuza abacebisi bakhe, wathumela ilizwi kuJowashi indodana kaJehowahazi, indodana kaJehu, inkosi yako-Israyeli wathi: “Woza, siqondane ubuso ngobuso.”
18 Koma Yowasi mfumu ya Israeli inayankha Amaziya mfumu ya Yuda kuti, “Nthawi ina kamtengo kaminga ka ku Lebanoni kanatumiza mawu kwa mkungudza wa ku Lebanoni kuti, ‘Pereka mwana wako wamkazi kwa mwana wanga kuti amukwatire!’ Koma chirombo cha ku Lebanoni chinabwera ndi kupondaponda mtengo wa minga uja.
Kodwa uJowashi inkosi yako-Israyeli waphendula u-Amaziya inkosi yakoJuda wathi: “Isihlahla sameva saseLebhanoni sathumela umbiko kwesomsedari waseLebhanoni sathi: ‘Yendisela indodakazi yakho endodaneni yami ibe ngumkayo.’ Ngakho kwavela isilo saseLebhanoni sanyathela safohloza isihlahla sameva.
19 Iwe ukuti wagonjetsa Edomu, ndipo tsopano ukudzikuza ndi kudzitamandira, koma khala kwanu komweko! Nʼchifukwa chiyani ukufuna mavuto ndi kudzichititsa kuti ugwe pamodzinso ndi Yuda?”
Uzitshela ukuthi usuyinqobile i-Edomi, khathesi usuziqhenya. Kodwa hlala ekhaya! Kungani uzibangela uhlupho oluzakuchitha luze luchithe loJuda na?”
20 Komabe Amaziya sanamvere pakuti ndi Mulungu amene anakonzeratu kuti awapereke kwa Yehowasi, chifukwa iwo amapembedza milungu ya ku Edomu.
Kodwa u-Amaziya kazange alalele ngoba uNkulunkulu wayekumisile ukuthi uzabanikela kuJowashi, ngenxa yokukhonza kwabo onkulunkulu bama-Edomi.
21 Kotero Yowasi mfumu ya Israeli inakamuthira nkhondo. Iye ndi Amaziya anayangʼanana maso ndi maso ku Beti-Semesi ku Yuda.
Ngakho uJowashi inkosi yako-Israyeli wasehlasela. Yena kanye lo-Amaziya inkosi yakoJuda baqondana ubuso ngobuso eBhethi-Shemeshi koJuda.
22 Yuda anagonjetsedwa ndi Israeli ndipo munthu aliyense anathawira kwawo.
UJuda wachithwa ngu-Israyeli, kwathi amadoda wonke abalekela emizini yawo.
23 Yehowahazi mfumu ya Israeli inagwira Amaziya mfumu ya Yuda, mwana wa Yowasi, mwana wa Ahaziya ku Beti-Semesi. Yehowasi anabwera naye ku Yerusalemu ndipo anagwetsa khoma la Yerusalemu kuyambira pa Chipata cha Efereimu mpaka ku Chipata Chapangodya, khoma lotalika mamita 180.
UJowashi inkosi yako-Israyeli wathumba u-Amaziya inkosi yakoJuda, indodana kaJowashi indodana ka-Ahaziya, eBhethi-Shemeshi. Ngakho uJowashi waya laye eJerusalema njalo wadiliza umduli weJerusalema kusukela eSangweni lika-Efrayimi kusiya eSangweni laseJikweni isibanga esingaba ngamanyathelo angamakhulu ayisithupha ubude baso.
24 Iye anatenga golide ndi siliva yense ndi zida zonse zimene zimapezeka mʼNyumba ya Mulungu zimene ankazisamalira Obedi-Edomu, pamodzinso ndi chuma cha mʼnyumba yaufumu ndipo anatenga anthu ngati chikole.
Wasethatha lonke igolide lesiliva lazozonke impahla azithola ethempelini likaNkulunkulu ezazilindwe ngu-Obhedi-Edomi, kanye leziligugu zenotho yesigodlweni lezithunjwa, wasebuyela eSamariya.
25 Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anakhala ndi moyo kwa zaka khumi ndi zisanu atamwalira Yehowasi mwana wa Yehowahazi mfumu ya Israeli.
U-Amaziya indodana kaJowashi inkosi yakoJuda waphila okweminyaka elitshumi lemihlanu ngemva kokufa kukaJowashi indodana kaJehowahazi inkosi yako-Israyeli.
26 Ntchito zina za mfumu Amaziya, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli?
Ezinye izehlakalo ngombuso ka-Amaziya, kusukela ekuqaleni kuze kube sekupheleni, azilotshwanga yini egwalweni lwamakhosi akoJuda lako-Israyeli na?
27 Kuyambira nthawi imene Amaziya analeka kutsatira Yehova anthu anamukonzera chiwembu mu Yerusalemu ndipo anathawira ku Lakisi, koma adaniwo anatumiza anthu ku Lakisiko ndipo anamupha komweko.
Kusukela ekuphambukeni kuka-Amaziya engasalandeli uThixo, bamsongela eJerusalema wabalekela eLakhishi, kodwa bathumela amadoda amlandela eLakhishi ambulalela khonale.
28 Iwo anabwera naye ali pa kavalo ndipo anayikidwa mʼmanda ndi makolo ake mu mzinda wa Yuda.
Wabuyiswa esethwelwe ngebhiza wangcwatshwa labokhokho bakhe eMzini kaJuda.

< 2 Mbiri 25 >