< 2 Mbiri 25 >
1 Amaziya anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 29. Dzina la amayi ake linali Yehoyadini wa ku Yerusalemu.
A son of twenty and five year[s] he became king Amaziah and twenty and nine year[s] he reigned in Jerusalem and [the] name of mother his [was] Jehoaddan from Jerusalem.
2 Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, koma osati ndi mtima wonse.
And he did the right in [the] eyes of Yahweh only not with a heart complete.
3 Pamene mphamvu zonse zaufumu zinali mʼmanja mwake, iye anapha akuluakulu amene anapha abambo ake, mfumu ija.
And it was just when it was secure the kingdom on him and he killed servants his who had struck down the king father his.
4 Komabe iye sanaphe ana awo koma anatsatira zolembedwa mʼbuku la Mose, mʼmene Yehova analamula kuti, “Makolo sadzaphedwa chifukwa cha ana awo kapena ana kuphedwa chifukwa cha makolo awo. Aliyense adzafera machimo ake.”
And children their not he put to death for according to [what] is written in the law in [the] book of Moses which he commanded Yahweh saying not they will die parents on children and children not they will die on parents for each for own sin his they will die.
5 Amaziya anasonkhanitsa anthu a ku Yuda ndipo anawapatsa zochita molingana ndi mabanja awo kukhala anthu olamulira 1,000, ndi olamulira 100 pa Ayuda onse ndi Benjamini. Ndipo iye anawerenga amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo napeza kuti analipo amuna 300,000 okonzeka kugwira ntchito ya usilikali, okhoza kugwiritsa ntchito mkondo ndi chishango.
And he assembled Amaziah Judah and he appointed them to [the] house of ancestors to [the] commanders of the thousands and to [the] commanders of the hundreds for all Judah and Benjamin and he enrolled them from a son of twenty year[s] and up-wards and he found them three hundred thousand chosen [man] [one who] goes forth warfare [one who] holds spear and body shield.
6 Iye analembanso ntchito anthu odziwa nkhondo 100,000 ochokera ku Israeli pa mtengo wa makilogalamu 3,400 a siliva.
And he hired from Israel one hundred thousand mighty [man] of strength for one hundred talent[s] of silver.
7 Koma munthu wa Mulungu anabwera kwa iye ndipo anati, “Inu mfumu, asilikali awa ochokera ku Israeli asapite ndi inu, pakuti Yehova sali ndi Israeli kapena ndi aliyense wa anthu a Efereimu.
And [the] man of God he came to him saying O king may not it go with you [the] army of Israel for not Yahweh [is] with Israel all [the] descendants of Ephraim.
8 Ngakhale mupite ndi kuchita nkhondo molimba mtima, Mulungu adzakugonjetsani pamaso pa adani anu, pakuti Mulungu ali ndi mphamvu yothandiza kapena kugonjetsa.”
That except go you act be strong for the battle he will overthrow you God before [the] enemy for there [is] strength in God to help and to overthrow.
9 Amaziya anafunsa munthu wa Mulungu kuti, “Koma nanga za makilogalamu aja a siliva amene ndapereka kwa asilikali a Israeli?” Munthu wa Mulungu anayankha kuti, “Yehova atha kukupatsani zambiri kuposa zimenezo.”
And he said Amaziah to [the] man of God and what? [is] to do to [the] one hundred the talent[s] which I paid to [the] troop[s] of Israel and he said [the] man of God there [belongs] to Yahweh to give to you much more than this.
10 Choncho Amaziya anachotsa asilikali amene anabwera kwa iye kuchokera ku Efereimu ndipo anawatumiza kwawo. Iwo anakwiyira anthu a ku Yuda ndipo anapita kwawo atapsa mtima kwambiri.
And he separated them Amaziah the troop[s] which it had come to him from Ephraim to go to place their and it burned anger their exceedingly on Judah and they returned to place their in [the] heat of anger.
11 Ndipo Amaziya analimba mtima ndipo anatsogolera gulu lake lankhondo ku Chigwa cha Mchere, kumene anapha anthu 10,000 a ku Seiri.
And Amaziah he strengthened himself and he led out people his and he went [the] Valley of Salt and he struck down [the] people of Seir ten thousand.
12 Gulu la ankhondo la Yuda linagwiranso anthu amoyo 10,000, napita nawo pamwamba pa thanthwe ndipo anawaponya pansi kotero kuti onse ananyenyeka.
And ten thousand alive they took captive [the] people of Judah and they brought them to [the] top of the cliff and they threw them from [the] top of cliff and all of them they were split open.
13 Pa nthawi imeneyi asilikali amene Amaziya anawabweza ndipo sanawalole kuti achite nawo nkhondo, anakathira nkhondo mizinda ya Yuda kuyambira ku Samariya mpaka ku Beti-Horoni. Iwo anapha anthu 3,000 ndipo anafunkha katundu wambiri.
And [the] sons of the troop which he had turned back Amaziah from going with him to the battle and they made a raid on [the] cities of Judah from Samaria and to Beth Horon and they struck down of them three thousand and they plundered plunder much.
14 Amaziya atabwerera kuja anakapha Aedomu, anabweretsa milungu ya anthu a ku Seiri. Ndipo anayika kuti ikhale milungu yake, ankayipembedza ndi kupereka nsembe zopsereza.
And it was after came Amaziah from defeating [the] Edomites and he brought [the] gods of [the] people of Seir and he set up them for himself to gods and before them he bowed down and to them he made smoke.
15 Yehova anakwiyira Amaziya, ndipo anamutumizira mneneri amene anati, “Nʼchifukwa chiyani mukupembedza milungu ya anthu awa, imene sinathe kupulumutsa anthu ake mʼdzanja lanu?”
And it burned [the] anger of Yahweh on Amaziah and he sent to him a prophet and he said to him why? have you sought [the] gods of the people which not they delivered own people their from hand your.
16 Iye ali kuyankhula, mfumu inati, “Kodi ife takusankha iwe kuti ukhale mlangizi wa mfumu? Khala chete! Ufuna kuphedweranji?” Choncho mneneriyo analeka koma anati, “Ine ndikudziwa kuti Mulungu watsimikiza kukuwonongani chifukwa mwachita izi ndipo simunamvere uphungu wanga.”
And it was - when was speaking he to him and he said to him ¿ into a counselor of the king have we made you cease yourself why? will people strike down you and he ceased the prophet and he said I know that he has planned God to destroy you for you have done this and not you have listened to counsel my.
17 Amaziya mfumu ya ku Yuda, atafunsa alangizi ake, anatumiza mawu awa kwa Yowasi mwana wa Yehowahazi mwana wa Yehu, mfumu ya Israeli: “Bwera udzakumane nane maso ndi maso.”
And he took counsel Amaziah [the] king of Judah and he sent to Joash [the] son of Jehoahaz [the] son of Jehu [the] king of Israel saying (come! *Q(K)*) let us look at one another faces.
18 Koma Yowasi mfumu ya Israeli inayankha Amaziya mfumu ya Yuda kuti, “Nthawi ina kamtengo kaminga ka ku Lebanoni kanatumiza mawu kwa mkungudza wa ku Lebanoni kuti, ‘Pereka mwana wako wamkazi kwa mwana wanga kuti amukwatire!’ Koma chirombo cha ku Lebanoni chinabwera ndi kupondaponda mtengo wa minga uja.
And he sent Joash [the] king of Israel to Amaziah [the] king of Judah saying the thornbush which [was] in Lebanon it sent to the cedar which [was] in Lebanon saying give! daughter your to son my to a wife and it passed by [the] animal of the field which [was] in Lebanon and it trampled the thornbush.
19 Iwe ukuti wagonjetsa Edomu, ndipo tsopano ukudzikuza ndi kudzitamandira, koma khala kwanu komweko! Nʼchifukwa chiyani ukufuna mavuto ndi kudzichititsa kuti ugwe pamodzinso ndi Yuda?”
You have said here! you have struck down Edom and it has lifted you heart your to become heavy now remain! in house your why? will you engage in strife with harm and you will fall you and Judah with you.
20 Komabe Amaziya sanamvere pakuti ndi Mulungu amene anakonzeratu kuti awapereke kwa Yehowasi, chifukwa iwo amapembedza milungu ya ku Edomu.
And not he listened Amaziah for [was] from God it so as to give them in a hand for they had sought [the] gods of Edom.
21 Kotero Yowasi mfumu ya Israeli inakamuthira nkhondo. Iye ndi Amaziya anayangʼanana maso ndi maso ku Beti-Semesi ku Yuda.
And he went up Joash [the] king of Israel and they looked at one another faces he and Amaziah [the] king of Judah at Beth Shemesh which [belonged] to Judah.
22 Yuda anagonjetsedwa ndi Israeli ndipo munthu aliyense anathawira kwawo.
And it was defeated Judah before Israel and they fled each to tents his.
23 Yehowahazi mfumu ya Israeli inagwira Amaziya mfumu ya Yuda, mwana wa Yowasi, mwana wa Ahaziya ku Beti-Semesi. Yehowasi anabwera naye ku Yerusalemu ndipo anagwetsa khoma la Yerusalemu kuyambira pa Chipata cha Efereimu mpaka ku Chipata Chapangodya, khoma lotalika mamita 180.
And Amaziah [the] king of Judah [the] son of Joash [the] son of Jehoahaz he caught Joash [the] king of Israel at Beth Shemesh and he brought him Jerusalem and he made a breach in [the] wall of Jerusalem from [the] gate of Ephraim to [the] gate of the Corner four hundred cubit[s].
24 Iye anatenga golide ndi siliva yense ndi zida zonse zimene zimapezeka mʼNyumba ya Mulungu zimene ankazisamalira Obedi-Edomu, pamodzinso ndi chuma cha mʼnyumba yaufumu ndipo anatenga anthu ngati chikole.
And all the gold and the silver and all the articles which were found in [the] house of God with Obed-Edom and [the] treasures of [the] house of the king and [the] sons of the pledges and he returned Samaria.
25 Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anakhala ndi moyo kwa zaka khumi ndi zisanu atamwalira Yehowasi mwana wa Yehowahazi mfumu ya Israeli.
And he lived Amaziah [the] son of Joash [the] king of Judah after [the] death of Joash [the] son of Jehoahaz [the] king of Israel fif-teen year[s].
26 Ntchito zina za mfumu Amaziya, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli?
And [the] rest of [the] matters of Amaziah former and latter ¿ not there! [are] they written on [the] scroll of [the] kings of Judah and Israel.
27 Kuyambira nthawi imene Amaziya analeka kutsatira Yehova anthu anamukonzera chiwembu mu Yerusalemu ndipo anathawira ku Lakisi, koma adaniwo anatumiza anthu ku Lakisiko ndipo anamupha komweko.
And from [the] time when he turned aside Amaziah from after Yahweh and people conspired on him a conspiracy in Jerusalem and he fled Lachish towards and they sent after him Lachish towards and they put to death him there.
28 Iwo anabwera naye ali pa kavalo ndipo anayikidwa mʼmanda ndi makolo ake mu mzinda wa Yuda.
And they carried him on horses and they buried him with ancestors his in [the] city of Judah.