< 2 Mbiri 25 >

1 Amaziya anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 29. Dzina la amayi ake linali Yehoyadini wa ku Yerusalemu.
Amaziah was fiue and twentie yere old when he began to reigne, and he reigned nine and twentie yeere in Ierusalem: and his mothers name was Iehoaddan, of Ierusalem.
2 Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, koma osati ndi mtima wonse.
And he did vprightly in the eyes of the Lord, but not with a perfite heart.
3 Pamene mphamvu zonse zaufumu zinali mʼmanja mwake, iye anapha akuluakulu amene anapha abambo ake, mfumu ija.
And when the kingdome was established vnto him, he slewe his seruants, that had slaine the King his father.
4 Komabe iye sanaphe ana awo koma anatsatira zolembedwa mʼbuku la Mose, mʼmene Yehova analamula kuti, “Makolo sadzaphedwa chifukwa cha ana awo kapena ana kuphedwa chifukwa cha makolo awo. Aliyense adzafera machimo ake.”
But he slewe not their children, but did as it is written in the Lawe, and in the booke of Moses, where the Lord commanded, saying, The fathers shall not dye for the children, neyther shall the children die for the fathers, but euery man shall dye for his owne sinne.
5 Amaziya anasonkhanitsa anthu a ku Yuda ndipo anawapatsa zochita molingana ndi mabanja awo kukhala anthu olamulira 1,000, ndi olamulira 100 pa Ayuda onse ndi Benjamini. Ndipo iye anawerenga amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo napeza kuti analipo amuna 300,000 okonzeka kugwira ntchito ya usilikali, okhoza kugwiritsa ntchito mkondo ndi chishango.
And Amaziah assembled Iudah, and made them captaines ouer thousandes, and captaines ouer hundreths, according to the houses of their fathers, thorowout all Iudah and Beniamin: and he nombred them from twentie yeere olde and aboue, and founde among them three hundreth thousand chosen men, to goe foorth to the warre, and to handle speare and shield.
6 Iye analembanso ntchito anthu odziwa nkhondo 100,000 ochokera ku Israeli pa mtengo wa makilogalamu 3,400 a siliva.
He hyred also an hundreth thousand valiant men out of Israel for an hundreth talents of siluer.
7 Koma munthu wa Mulungu anabwera kwa iye ndipo anati, “Inu mfumu, asilikali awa ochokera ku Israeli asapite ndi inu, pakuti Yehova sali ndi Israeli kapena ndi aliyense wa anthu a Efereimu.
But a man of God came to him, saying, O King, let not the armie of Israel goe with thee: for the Lord is not with Israel, neither with all the house of Ephraim.
8 Ngakhale mupite ndi kuchita nkhondo molimba mtima, Mulungu adzakugonjetsani pamaso pa adani anu, pakuti Mulungu ali ndi mphamvu yothandiza kapena kugonjetsa.”
If not, goe thou on, doe it, make thy selfe strong to the battel, but God shall make thee fall before the enemie: for God hath power to helpe, and to cast downe.
9 Amaziya anafunsa munthu wa Mulungu kuti, “Koma nanga za makilogalamu aja a siliva amene ndapereka kwa asilikali a Israeli?” Munthu wa Mulungu anayankha kuti, “Yehova atha kukupatsani zambiri kuposa zimenezo.”
And Amaziah sayde to the man of God, What shall we doe then for the hundreth talents, which I haue giuen to the hoste of Israel? Then the man of God answered, The Lord is able to giue thee more then this.
10 Choncho Amaziya anachotsa asilikali amene anabwera kwa iye kuchokera ku Efereimu ndipo anawatumiza kwawo. Iwo anakwiyira anthu a ku Yuda ndipo anapita kwawo atapsa mtima kwambiri.
So Amaziah separated them, to wit, the armie that was come to him out of Ephraim, to returne to their place: wherefore their wrath was kindled greatly against Iudah, and they returned to their places with great anger.
11 Ndipo Amaziya analimba mtima ndipo anatsogolera gulu lake lankhondo ku Chigwa cha Mchere, kumene anapha anthu 10,000 a ku Seiri.
Then Amaziah was encouraged, and led forth his people, and went to the salt valley, and smote of the children of Seir, ten thousand.
12 Gulu la ankhondo la Yuda linagwiranso anthu amoyo 10,000, napita nawo pamwamba pa thanthwe ndipo anawaponya pansi kotero kuti onse ananyenyeka.
And other ten thousand did the children of Iudah take aliue, and caryed them to the top of a rocke, and cast them downe from the top of the rocke, and they all burst to pieces.
13 Pa nthawi imeneyi asilikali amene Amaziya anawabweza ndipo sanawalole kuti achite nawo nkhondo, anakathira nkhondo mizinda ya Yuda kuyambira ku Samariya mpaka ku Beti-Horoni. Iwo anapha anthu 3,000 ndipo anafunkha katundu wambiri.
But the men of the armie, which Amaziah sent away, that they should not goe with his people to battell, fell vpon the cities of Iudah from Samaria vnto Beth-horon, and smote three thousand of them, and tooke much spoyle.
14 Amaziya atabwerera kuja anakapha Aedomu, anabweretsa milungu ya anthu a ku Seiri. Ndipo anayika kuti ikhale milungu yake, ankayipembedza ndi kupereka nsembe zopsereza.
Now after that Amaziah was come from the slaughter of the Edomites, he brought the gods of the children of Seir, and set them vp to be his gods, and worshipped them, and burned incense vnto them.
15 Yehova anakwiyira Amaziya, ndipo anamutumizira mneneri amene anati, “Nʼchifukwa chiyani mukupembedza milungu ya anthu awa, imene sinathe kupulumutsa anthu ake mʼdzanja lanu?”
Wherefore the Lord was wroth with Amaziah, and sent vnto him a Prophet, which sayd vnto him, Why hast thou sought the gods of the people, which were not able to deliuer their owne people out of thine hand?
16 Iye ali kuyankhula, mfumu inati, “Kodi ife takusankha iwe kuti ukhale mlangizi wa mfumu? Khala chete! Ufuna kuphedweranji?” Choncho mneneriyo analeka koma anati, “Ine ndikudziwa kuti Mulungu watsimikiza kukuwonongani chifukwa mwachita izi ndipo simunamvere uphungu wanga.”
And as he talked with him, he said vnto him, Haue they made thee the Kings counseler? cease thou: why should they smite thee? And the Prophet ceased, but said, I knowe that God hath determined to destroy thee, because thou hast done this, and hast not obeyed my counsell.
17 Amaziya mfumu ya ku Yuda, atafunsa alangizi ake, anatumiza mawu awa kwa Yowasi mwana wa Yehowahazi mwana wa Yehu, mfumu ya Israeli: “Bwera udzakumane nane maso ndi maso.”
Then Amaziah King of Iudah tooke counsell, and sent to Ioash the sonne of Iehoahaz, the sonne of Iehu King of Israel, saying, Come, let vs see one another in the face.
18 Koma Yowasi mfumu ya Israeli inayankha Amaziya mfumu ya Yuda kuti, “Nthawi ina kamtengo kaminga ka ku Lebanoni kanatumiza mawu kwa mkungudza wa ku Lebanoni kuti, ‘Pereka mwana wako wamkazi kwa mwana wanga kuti amukwatire!’ Koma chirombo cha ku Lebanoni chinabwera ndi kupondaponda mtengo wa minga uja.
But Ioash King of Israel sent to Amaziah King of Iudah, saying, The thistle that is in Lebanon, sent to the cedar that is in Lebanon, saying, Giue thy daughter to my sonne to wife: and the wilde beast that was in Lebanon went and trode downe the thistle.
19 Iwe ukuti wagonjetsa Edomu, ndipo tsopano ukudzikuza ndi kudzitamandira, koma khala kwanu komweko! Nʼchifukwa chiyani ukufuna mavuto ndi kudzichititsa kuti ugwe pamodzinso ndi Yuda?”
Thou thinkest: lo, thou hast smitten Edom, and thine heart lifteth thee vp to bragge: abide now at home: why doest thou prouoke to thine hurt, that thou shouldest fall, and Iudah with thee?
20 Komabe Amaziya sanamvere pakuti ndi Mulungu amene anakonzeratu kuti awapereke kwa Yehowasi, chifukwa iwo amapembedza milungu ya ku Edomu.
But Amaziah would not heare: for it was of God, that he might deliuer them into his had, because they had sought the gods of Edom.
21 Kotero Yowasi mfumu ya Israeli inakamuthira nkhondo. Iye ndi Amaziya anayangʼanana maso ndi maso ku Beti-Semesi ku Yuda.
So Ioash the King of Israel went vp: and he, and Amaziah King of Iudah saw one another in the face at Bethshemesh, which is in Iudah.
22 Yuda anagonjetsedwa ndi Israeli ndipo munthu aliyense anathawira kwawo.
And Iudah was put to the worse before Israel, and they fled euery man to his tents.
23 Yehowahazi mfumu ya Israeli inagwira Amaziya mfumu ya Yuda, mwana wa Yowasi, mwana wa Ahaziya ku Beti-Semesi. Yehowasi anabwera naye ku Yerusalemu ndipo anagwetsa khoma la Yerusalemu kuyambira pa Chipata cha Efereimu mpaka ku Chipata Chapangodya, khoma lotalika mamita 180.
But Ioash the King of Israel tooke Amaziah King of Iudah, the sonne of Ioash, the sonne of Iehoahaz in Bethshemesh, and brought him to Ierusalem, and brake downe the wall of Ierusalem, from the gate of Ephraim vnto the corner gate, foure hundreth cubites.
24 Iye anatenga golide ndi siliva yense ndi zida zonse zimene zimapezeka mʼNyumba ya Mulungu zimene ankazisamalira Obedi-Edomu, pamodzinso ndi chuma cha mʼnyumba yaufumu ndipo anatenga anthu ngati chikole.
And he tooke all the gold and the siluer, and all the vessels that were found in the house of God with Obed Edom, and in the treasures of the Kings house, and the children that were in hostage, and returned to Samaria.
25 Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anakhala ndi moyo kwa zaka khumi ndi zisanu atamwalira Yehowasi mwana wa Yehowahazi mfumu ya Israeli.
And Amaziah the sonne of Ioash King of Iudah liued after the death of Ioash sonne of Iehoahaz King of Israel, fifteene yeere.
26 Ntchito zina za mfumu Amaziya, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli?
Concerning the rest of the actes of Amaziah first and last, are they not written in the booke of the Kings of Iudah and Israel?
27 Kuyambira nthawi imene Amaziya analeka kutsatira Yehova anthu anamukonzera chiwembu mu Yerusalemu ndipo anathawira ku Lakisi, koma adaniwo anatumiza anthu ku Lakisiko ndipo anamupha komweko.
Nowe after the time that Amaziah did turne away from ye Lord, they wrought treason against him in Ierusalem: and when he was fled to Lachish, they sent to Lachish after him, and slewe him there.
28 Iwo anabwera naye ali pa kavalo ndipo anayikidwa mʼmanda ndi makolo ake mu mzinda wa Yuda.
And they brought him vpon horses, and buried him with his fathers in the citie of Iudah.

< 2 Mbiri 25 >