< 2 Mbiri 24 >
1 Yowasi anali wa zaka zisanu ndi ziwiri pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka makumi anayi. Dzina la amayi ake linali Zibiya wa ku Beeriseba.
Agtawen ni Joas iti pito idi nangrugi isuna a nagturay; nagturay isuna iti 40 a tawen idiay Jerusalem. Ti nagan ti inana ket Zibia a taga-Beerseba.
2 Yowasi anachita zolungama pamaso pa Yehova nthawi yonse ya moyo wa wansembe Yehoyada.
Inaramid ni Joas ti umno iti imatang ni Yahweh iti amin nga al-aldaw ni Jehoyada a padi.
3 Yehoyada anamupezera iye akazi awiri, ndipo anabereka ana aamuna ndi aakazi.
Nangpili ni Jehoyada iti dua nga assawa a para kenni Joas, ket naaddaan ni Joas kadagiti annak a lallaki ken babbai.
4 Patapita nthawi Yowasi anatsimikiza zokonzanso Nyumba ya Yehova.
Napasamak a kalpasan daytoy, nga inkeddeng ni Joas a patarimaan ti balay ni Yahweh.
5 Iye anayitanitsa pamodzi ansembe ndi Alevi ndipo anawawuza kuti, “Pitani ku mizinda ya Yuda ndi kukasonkhetsa ndalama za pa chaka kwa Aisraeli onse zokonzera Nyumba ya Mulungu wanu. Chitani zimenezi tsopano.” Koma Alevi sanachite zimenezi mwachangu.
Inummongna dagiti papadi ken dagiti Levita ket kinunana kadakuada, “Tinawen a mapankayo kadagiti siudad ti Juda ket urnongenyo ti kuarta manipud iti entero nga Israel a tinawen nga ibayad dagiti tattao tapno mapatarimaan ti balay ti Diosyo. Siguradoenyo nga irugiyo a dagus.” Ngem saan nga inaramid a dagus dagiti Levita.
6 Choncho mfumu inayitanitsa Yehoyada, mkulu wa ansembe ndipo inati kwa iye, “Kodi nʼchifukwa chiyani simunawuze Alevi kuti asonkhetse ndalama ku Yuda ndi Yerusalemu, msonkho umene anakhazikitsa Mose mtumiki wa Yehova ndiponso gulu lonse la Aisraeli mu tenti yaumboni?”
Isu a pinaayaban ti ari ni Jehoyada, a kangatoan a padi ket kinunana kenkuana, “Apay a saanmo a binagaan dagiti Levita nga iyegda manipud iti Juda ken iti Jerusalem ti buis nga imbilin ni Moises nga adipen ni Yahweh, ken ti agtaud iti gimong ti Israel nga agpaay iti tolda ti Dios?”
7 Ana a mkazi woyipa, Ataliya, anathyola chitseko cha Nyumba ya Mulungu ndipo anagwiritsa ntchito zinthu zopatulika popembedza Baala.
Ta dinadael dagiti annak a lallaki ni Atalia a nadangkes a babai ti balay ti Dios ket impanda kadagiti Baal dagiti amin a nasantoan a banbanag iti balay ni Yahweh.
8 Mfumu italamulira, bokosi linapangidwa ndipo linayikidwa panja pa chipata cha Nyumba ya Yehova.
Isu a nagbilin ti ari, ket nangaramidda iti kahon sada inkabil daytoy iti ruar iti pagserkan ti balay ni Yahweh.
9 Ndipo analengeza kwa anthu a mu Yuda ndi mu Yerusalemu kuti abweretse kwa Yehova msonkho umene Mose mtumiki wa Mulungu analamulira Aisraeli mʼchipululu.
Ket pinaiwaragawagda iti Juda ken Jerusalem nga iyeg dagiti tattao kenni Yahweh ti buis nga imbilin ni Moises nga adipen ti Dios iti Israel idiay let-ang.
10 Akuluakulu onse ndi anthu onse anabweretsa zopereka zawo mokondwera ndipo anaziponya mʼbokosi mpaka linadzaza.
Naragsakan dagiti amin a mangidadaulo ken amin a tattao ket nangiyegda iti kuarta sada inkabil daytoy iti kahon, agingga a napunnoda daytoy.
11 Nthawi ina iliyonse imene Alevi abweretsa bokosilo kwa akuluakulu a mfumu ndipo akaona kuti muli ndalama zambiri, mlembi waufumu ndi nduna yayikulu ya mkulu wa ansembe amabwera ndi kuchotsa ndalama mʼbokosi muja ndipo amalitenga kukaliyika pamalo pake. Iwo amachita izi nthawi ndi nthawi ndipo anapeza ndalama zambiri.
Napasamak a tunggal ipan dagiti Levita ti kahon kadagiti opisial ti ari, ken tunggal makitada nga adun ti kuarta a naikabil iti daytoy, ket umay dagiti eskriba ti ari ken ti opisial ti kangatoan a padi, ibukbokda ti linaon ti kahon sada alaen daytoy ket isublida manen iti sigud nga ayanna. Inaldaw a kastoy ti ar-aramidenda ket nakaurnongda iti dakkel a gatad ti kuarta.
12 Mfumu pamodzi ndi Yehoyada anapereka ndalamazo kwa anthu oyangʼanira ntchito ku Nyumba ya Yehova. Analemba ntchito amisiri a miyala ndi a matabwa kuti akonzenso Nyumba ya Yehova. Analembanso ntchito amisiri a zitsulo ndi mkuwa kuti akonze Nyumba ya Mulungu.
Ited ti ari ken Jehoyada ti kuarta kadagiti mangimaton iti pannakatarimaan ti balay ni Yahweh. Nangtangdan dagitoy a lallaki kadagiti kumakabite, karpintero ken mammanday a mangtarimaan iti balay ni Yahweh.
13 Anthu amene ankagwira ntchito anali odziwa bwino, ndipo ntchitoyo inagwiridwa bwino ndi manja awo. Iwo anamanganso Nyumba ya Mulungu motsatira mapangidwe ake oyamba ndipo anayilimbitsa.
Impasnek ngarud dagiti trabahador ti nagtrabaho, ken nagtultuloy ti panangtarimaanda; binangonda manen ti balay ti Dios kas iti sigud a langana ken pinalagdada daytoy.
14 Atamaliza, iwo anabweretsa ndalama zotsala kwa mfumu ndi Yehoyada, ndipo anazigwiritsira ntchito popangira zida za mʼNyumba ya Yehova: ziwiya zogwiritsa ntchito potumikira ndi popereka nsembe zopsereza, komanso mbale ndi ziwiya zagolide ndi siliva. Nthawi yonse ya moyo wa Yehoyada, nsembe zopsereza zinkaperekedwa mosalekeza mʼNyumba ya Yehova.
Idi nalpasdan, impanda ti nabati a kuarta iti ari ken kenni Jehoyada. Nausar daytoy a kuarta iti panagaramid kadagiti alikamen para iti balay ni Yahweh, a maus-usar iti panagserbi ken panangidaton-dagiti kutsara ken al-alikamen a balitok ken pirak. Nagtultuloy ti panangidatonda kadagiti daton a mapuoran iti balay ni Yahweh iti amin nga aldaw ni Jehoyada.
15 Tsono Yehoyada anakalamba ndipo anali ndi zaka zambiri. Pambuyo pake iye anamwalira ali ndi zaka 130.
Limmakay unay ni Jehoyada, ket natay; 130 ti tawenna idi natay isuna.
16 Iyeyo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi mafumu mu mzinda wa Davide chifukwa cha zabwino zimene anachita mu Israeli, kuchitira Mulungu ndi Nyumba yake.
Intanemda isuna iti siudad ni David a pakaitantaneman dagiti ar-ari, gapu ta naimbag ti inaramidna iti Israel, iti imatang ti Dios ken iti balay ti Dios.
17 Atamwalira Yehoyada, akuluakulu a Yuda anabwera kudzapereka ulemu kwa mfumu, ndipo mfumu inawamvera.
Ita, kalpasan iti ipapatay ni Jehoyada, immay dagiti mangidadaulo ti Juda ket sinugsuganda ti ari. Ket impangag ti ari ida.
18 Iwo anasiya Nyumba ya Yehova, Mulungu wa makolo awo ndipo anapembedza Asera ndi mafano. Chifukwa cha kulakwa kwawo, mkwiyo wa Yehova unabwera pa Yuda ndi Yerusalemu.
Binaybay-anda ti balay ni Yahweh a Dios dagiti kapuonanda, ket nagdaydayawda kadagiti diosa nga Asera ken kadagiti didiosen. Nakapungtot ti Dios iti Juda ken Jerusalem gapu iti daytoy a dakes nga inaramidda.
19 Ngakhale Yehova anatumiza aneneri kwa anthuwo kuti awabweze kwa Iye, ngakhale aneneri ananenera mowatsutsa, anthuwo sanamvere.
Ngem nangibaon latta isuna kadagiti profeta a mangisubli kadakuada kenkuana, ni Yahweh; binallaagan dagiti profeta dagiti tattao ngem saanda nga impangag ida.
20 Kenaka Mzimu wa Mulungu unabwera pa Zekariya mwana wa wansembe Yehoyada. Iye anayimirira pamaso pa anthu ndipo anati, “Zimene Mulungu akunena ndi Izi: ‘Chifukwa chiyani simukumvera Malamulo a Yehova? Simudzapindula. Chifukwa mwasiya Yehova, Iyenso wakusiyani.’”
Immay ti Espiritu ti Dios kenni Zacarias a putot a lalaki ni Jehoyada, a padi; nagtakder ni Zacarias iti nangato a disso iti sangoanan dagiti tattao ket kinuna kadakuada, “Kastoy ti kuna ti Dios; 'Apay a salsalungasingenyo dagiti bilbilin ni Yahweh, nga isu a saankayo a dumur-as? Agsipud ta tinallikudanyo ni Yahweh, tinallikudannakayo met.'”
21 Koma anthuwo anamuchitira chiwembu molamulidwa ndi mfumu ndipo anamugenda miyala ndi kumupha mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu.
Ngem nagpanggepda iti maibusor kenkuana ket iti bilin ti ari, inuborda isuna idiay paraangan ti balay ni Yahweh.
22 Mfumu Yowasi sinakumbukire zabwino zimene Yehoyada abambo ake a Zekariya anamuchitira, koma anapha mwana wake. Pamene amafa, iye ananena kuti, “Yehova aone zimenezi ndipo abwezere chilango.”
Iti kastoy a wagas ket saan a linagip ni Joas nga ari ti kinaimbag nga inaramid kenkuana ni Jehoyada nga ama ni Zacarias. Ngem ketdi, pinapatayna ti putot a lalaki ni Jehoyada. Idi matmatayen ni Zacarias, kinunana, “Makita koma ni Yahweh daytoy ket balsennaka.”
23 Pakutha kwa chaka, gulu lankhondo la Aramu linadzamenyana ndi Yowasi. Linalowa mu Yuda ndi mu Yerusalemu ndi kupha atsogoleri onse a anthu. Zonse zimene analanda anazitumiza kwa mfumu ya ku Damasiko.
Ket napasamak nga iti pagleppasan ti tawen, rinaut ti armada ti Aram ni Joas. Napanda iti Juda ken Jerusalem; pinapatayda dagiti amin a mangidadaulo kadagiti tattao ket impatulodda iti ari ti Damasco dagiti amin a sinamsamda kadakuada.
24 Ngakhale kuti gulu lankhondo la Aramu linabwera ndi anthu ochepa okha, Yehova anapereka mʼmanja mwawo gulu lalikulu lankhondo. Chifukwa Yuda anasiya Yehova Mulungu wa makolo awo, chiweruzo chinachitika pa Yowasi.
Immay ti Aram a bassitda laeng nga armada, ngem pinagballigi ida ni Yahweh a maibusor iti nakadakdakkel nga armada gapu ta tinallikudan ti Juda ni Yahweh a Dios dagiti kapuonanda. Iti kastoy a wagas, inyeg dagiti taga-Aram ti pannakadusa ni Joas.
25 Pamene Aaramu amachoka, anasiya Yowasi atavulazidwa kwambiri. Akuluakulu ake anamuchitira chiwembu chifukwa anapha mwana wa wansembe Yehoyada, ndipo anamupha ali pa bedi pake. Choncho anafa ndipo anayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide, koma osati manda a mafumu.
Iti tiempo a nakapanawen dagiti taga-Aram, nasugatan iti nakaro ni Joas. Naggandat dagiti adipenna iti maibusor kenkuana gapu iti pannakatay dagiti annak ni Jehoyada a padi. Pinapatayda isuna iti pagiddaanna ket natay; intanemda isuna iti siudad ni David ngem saan a kadagiti pakaitantaneman dagiti ar-ari.
26 Iwo amene anamuchitira chiwembu anali Zabadi mwana wa Simeati, mkazi wa ku Amoni, ndi Yehozabadi mwana wa Simiriti, mkazi wa ku Mowabu.
Dagitoy dagiti tattao a naggandat iti maibusor kenkuana: ni Zabad nga anak a lalaki ni Simat nga Ammonita; ken ni Josabad nga anak a lalaki ni Simrit a Moabita.
27 Za ana ake aamuna, uneneri wonena za iye, mbiri ya kumanganso Nyumba ya Mulungu, zalembedwa mʼbuku lofotokoza za mafumu. Ndipo Amaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Ita, ti pakasaritaan maipapan kadagiti annakna, dagiti napapateg a padto maipanggep kenkuana, ken ti pannakatarimaan ti balay ti Dios, adtoy, naisurat dagitoy iti Komentario iti Libro dagiti Ar-ari. Ket ni Amazias nga anakna ti simmukat kenkuana a kas ari.