< 2 Mbiri 24 >

1 Yowasi anali wa zaka zisanu ndi ziwiri pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka makumi anayi. Dzina la amayi ake linali Zibiya wa ku Beeriseba.
E HIKU makahiki o Ioasa i kona wa i alii ai, a noho alii iho la oia i na makahiki hookahi kanaha ma Ierusalema; a o ka inoa o kona makuwahine o Zibia no Beereseba.
2 Yowasi anachita zolungama pamaso pa Yehova nthawi yonse ya moyo wa wansembe Yehoyada.
A hana pololei o Ioasa imua o Iehova i na la a pau o Iehoiada ke kahuna.
3 Yehoyada anamupezera iye akazi awiri, ndipo anabereka ana aamuna ndi aakazi.
A haawi aku o Iehoiada i mau wahine elua nana, a hanau mai la nana he mau keikikane a he mau kaikamahine.
4 Patapita nthawi Yowasi anatsimikiza zokonzanso Nyumba ya Yehova.
Mahope iho, komo iho la iloko o ka naau o Ioasa e hoomaikai hou i ka hale o Iehova.
5 Iye anayitanitsa pamodzi ansembe ndi Alevi ndipo anawawuza kuti, “Pitani ku mizinda ya Yuda ndi kukasonkhetsa ndalama za pa chaka kwa Aisraeli onse zokonzera Nyumba ya Mulungu wanu. Chitani zimenezi tsopano.” Koma Alevi sanachite zimenezi mwachangu.
Hoakoakoa ae la oia i ka poe kahuna, a me na Levi, a olelo aku la ia lakou, E hele oukou i na kulanakauhale o Iuda, a e houluulu i kahi kala a ka Iseraela a pau i mea e hoomaikai hou ai i ka hale o ko oukou Akua, i kela makahiki keia makahiki; e wikiwiki oukou i keia hana. Aka, aole i hana wawe na Levi.
6 Choncho mfumu inayitanitsa Yehoyada, mkulu wa ansembe ndipo inati kwa iye, “Kodi nʼchifukwa chiyani simunawuze Alevi kuti asonkhetse ndalama ku Yuda ndi Yerusalemu, msonkho umene anakhazikitsa Mose mtumiki wa Yehova ndiponso gulu lonse la Aisraeli mu tenti yaumboni?”
Kahea aku la ke alii ia Iehoiada ka luna, a olelo aku la ia ia, No ke aha la i hoeueu ole aku ai oe i na Levi e lawe mai, mailoko mai o Iuda a me Ierusalema i ka auhau a Mose ke kauwa a Iehova i kau aku ai maluna o ka ahakanaka o ka Iseraela, no ka halelewa o ke kanawai?
7 Ana a mkazi woyipa, Ataliya, anathyola chitseko cha Nyumba ya Mulungu ndipo anagwiritsa ntchito zinthu zopatulika popembedza Baala.
No ka mea, o Atalia, ua wahine ino la, a o kana mau keiki kekahi, wawahi iho la lakou i ka hale o ke Akua, a hoolilo lakou i na mea laa a pau o ka bale o Iehova na Baala.
8 Mfumu italamulira, bokosi linapangidwa ndipo linayikidwa panja pa chipata cha Nyumba ya Yehova.
Olelo ke alii, a hana lakou i pahu, a waiho iho la ia mea mawaho ma ka puka o ka hale o Iehova.
9 Ndipo analengeza kwa anthu a mu Yuda ndi mu Yerusalemu kuti abweretse kwa Yehova msonkho umene Mose mtumiki wa Mulungu analamulira Aisraeli mʼchipululu.
A kukala aku la lakou ma Iuda, a ma Ierusalema, E lawe mai na Iehova i ka auhau a Mose, ke kauwa a ke Akua i kau aku ai maluna o ka Iseraela ma ka waonahele.
10 Akuluakulu onse ndi anthu onse anabweretsa zopereka zawo mokondwera ndipo anaziponya mʼbokosi mpaka linadzaza.
A hauoli iho la na kaukaualii a pau a me na kanaka a pau, a lawe mai lakou, a hahao iloko o ka pahu, a hoopau ae la.
11 Nthawi ina iliyonse imene Alevi abweretsa bokosilo kwa akuluakulu a mfumu ndipo akaona kuti muli ndalama zambiri, mlembi waufumu ndi nduna yayikulu ya mkulu wa ansembe amabwera ndi kuchotsa ndalama mʼbokosi muja ndipo amalitenga kukaliyika pamalo pake. Iwo amachita izi nthawi ndi nthawi ndipo anapeza ndalama zambiri.
A i ka wa i laweia mai ai ka pahu imua o na luna o ke alii e na Levi, a ike lakou ua nui ke kala, alaila hele mai ka lunakakau o ke alii, a me ka luna o ke kahuna nui, a hoohuli lakou i ka pahu, a lawe ae ia mea, a hoihoi aku i kona wahi; pela lakou i hana'i i kela la i keia la, a hoiliili lakou i ke kala he nui loa.
12 Mfumu pamodzi ndi Yehoyada anapereka ndalamazo kwa anthu oyangʼanira ntchito ku Nyumba ya Yehova. Analemba ntchito amisiri a miyala ndi a matabwa kuti akonzenso Nyumba ya Yehova. Analembanso ntchito amisiri a zitsulo ndi mkuwa kuti akonze Nyumba ya Mulungu.
A o ke alii a me Iehoiada, haawi laua i keia mea i ka poe ia lakou ka hana ma ka hale o Iehova, a hoolimalima lakou i poe kalai pohaku, a i ka poe kamana, e hoomaikai hou i ka hale o Iehova, a i poe kui hao a me ke keleawe, e hoopaa hou i ka hale o Iehova.
13 Anthu amene ankagwira ntchito anali odziwa bwino, ndipo ntchitoyo inagwiridwa bwino ndi manja awo. Iwo anamanganso Nyumba ya Mulungu motsatira mapangidwe ake oyamba ndipo anayilimbitsa.
A hana iho la ka poe paahana, a paa ia hana ia lakou, a kukulu lakou i ka hale o ke Akua, e like me kona ano mamua, hana hoi lakou a paa.
14 Atamaliza, iwo anabweretsa ndalama zotsala kwa mfumu ndi Yehoyada, ndipo anazigwiritsira ntchito popangira zida za mʼNyumba ya Yehova: ziwiya zogwiritsa ntchito potumikira ndi popereka nsembe zopsereza, komanso mbale ndi ziwiya zagolide ndi siliva. Nthawi yonse ya moyo wa Yehoyada, nsembe zopsereza zinkaperekedwa mosalekeza mʼNyumba ya Yehova.
A paa ia hana, lawe mai lakou imua o ke alii a me Iehoiada i ke koena o ke kala, a hana lakou i na kiaha no ka hale o Iehova, i na kiaha e lawelawe ai, a e mohai aku ai, a me na puna a me na kiaha gula a me ke kala. A mohai mau aku lakou i na mohai iloko o ka hale o Iehova i na la a pau o Iehoiada.
15 Tsono Yehoyada anakalamba ndipo anali ndi zaka zambiri. Pambuyo pake iye anamwalira ali ndi zaka 130.
A elemakule iho la o Iehoiada, a nui loa kona mau la, a make iho la ia. Hookahi haneri kona mau makahiki a me kanakolu, i kona make ana.
16 Iyeyo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi mafumu mu mzinda wa Davide chifukwa cha zabwino zimene anachita mu Israeli, kuchitira Mulungu ndi Nyumba yake.
A kanu lakou ia ia iloko o ke kulanakauhale o Davida me na alii, no ka mea, ua hana pono ia iloko o ka Iseraela, i ke Akua kekahi, a i kona hale iho no hoi.
17 Atamwalira Yehoyada, akuluakulu a Yuda anabwera kudzapereka ulemu kwa mfumu, ndipo mfumu inawamvera.
A mahope o ka make ana o Iehoiada, hele mai na kaukaualii o luda, a kulou imua o ke alii; alaila, hoolohe ke alii ia lakou.
18 Iwo anasiya Nyumba ya Yehova, Mulungu wa makolo awo ndipo anapembedza Asera ndi mafano. Chifukwa cha kulakwa kwawo, mkwiyo wa Yehova unabwera pa Yuda ndi Yerusalemu.
A haalele lakou i ka hale o Iehova, ke Akua o ko lakou poe kupuna, a hookauwa lakou na Asetarota a me na kii; a hiki mai ka huhu maluna o Iuda, a me Ierusalema no keia hewa o lakou.
19 Ngakhale Yehova anatumiza aneneri kwa anthuwo kuti awabweze kwa Iye, ngakhale aneneri ananenera mowatsutsa, anthuwo sanamvere.
Hoouna mai no nae oia io lakou la i na kaula e hoohuli ia lakou ia Iehova, a e ao pinepine ia lakou, aka, aole lakou i hoolohe.
20 Kenaka Mzimu wa Mulungu unabwera pa Zekariya mwana wa wansembe Yehoyada. Iye anayimirira pamaso pa anthu ndipo anati, “Zimene Mulungu akunena ndi Izi: ‘Chifukwa chiyani simukumvera Malamulo a Yehova? Simudzapindula. Chifukwa mwasiya Yehova, Iyenso wakusiyani.’”
Alaila, kau mai la i ka Uhane o ke Akua maluna o Zekaria, ke keiki a Iehoiada, ke kahuna, a ku ae la ia imua o kanaka, olelo mai la ia lakou, Penei i olelo mai ai ke Akua. No ke aha la oukou i malama ole ai i na kanawai o Iehova, i pono ole ai oukou? No ka mea, ua haalele oukou ia Iehova, a ua haalele no hoi kela ia oukou.
21 Koma anthuwo anamuchitira chiwembu molamulidwa ndi mfumu ndipo anamugenda miyala ndi kumupha mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu.
Alaila, hui ku e lakou ia ia, hailuku lakou ia ia i ka pohaku, mamuli o ke kauoha a ke alii ma ka lanai o ka hale o Iehova.
22 Mfumu Yowasi sinakumbukire zabwino zimene Yehoyada abambo ake a Zekariya anamuchitira, koma anapha mwana wake. Pamene amafa, iye ananena kuti, “Yehova aone zimenezi ndipo abwezere chilango.”
Pela i hoomanao ole ai o Ioasa, ke alii, i ka lokomaikai a Iehoiada a kona makuakane i hana mai ai ia in, aka, pepehi ia i kana keiki: a i kona make ana, i mai la ia, E nana mai o Iehova, a e uku mai hoi.
23 Pakutha kwa chaka, gulu lankhondo la Aramu linadzamenyana ndi Yowasi. Linalowa mu Yuda ndi mu Yerusalemu ndi kupha atsogoleri onse a anthu. Zonse zimene analanda anazitumiza kwa mfumu ya ku Damasiko.
A i ka pau ana o ka makahiki, pii ku e mai la io na la ko Suria poe koa; a komo lakou iloko o Iuda, a me Ierusalema, a luku mai la lakou i na kaukaualii o na kanaka mailoko mai o ka poe kanaka, a hoouka aku la i ka waiwai pio a pau o lakou i ke alii ma Damaseko.
24 Ngakhale kuti gulu lankhondo la Aramu linabwera ndi anthu ochepa okha, Yehova anapereka mʼmanja mwawo gulu lalikulu lankhondo. Chifukwa Yuda anasiya Yehova Mulungu wa makolo awo, chiweruzo chinachitika pa Yowasi.
No ka mea, he poe uuku ko Suria poe i hele mai, aka, ua haawi mai o Iehova iloko o ko lakou lima i ka poe nui loa, no ka mea, ua haa. lele lakou nei ia Iehova ke Akua o ko lakou poe kupuna. Pela lakou i hoopai mai ai ia Ioasa.
25 Pamene Aaramu amachoka, anasiya Yowasi atavulazidwa kwambiri. Akuluakulu ake anamuchitira chiwembu chifukwa anapha mwana wa wansembe Yehoyada, ndipo anamupha ali pa bedi pake. Choncho anafa ndipo anayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide, koma osati manda a mafumu.
A i ko lakou hoi ana mai ona aku, (no ka mea, he mai nui kona i ko lakou hanlele ana ia ia, ) hui ku e kana poe kauwa ia ia, no ke koko o na keiki a Iehoiada, ke kahuna, a pepehi lakou ia ia maluna o kona wahi moe, a make iho la ia; a ua kanu lakou ia ia iloko o ke kulanakauhale o Davida, aole nae i kanu lakou ia ia iloko o ka ilina o na'lii.
26 Iwo amene anamuchitira chiwembu anali Zabadi mwana wa Simeati, mkazi wa ku Amoni, ndi Yehozabadi mwana wa Simiriti, mkazi wa ku Mowabu.
Eia na mea i hui ku e ia ia; o Zabada, ke keiki a Simeata, a kekahi wahine Amona, a o Iehozabada ke keiki a Simerita, a kekahi wahine Moaba.
27 Za ana ake aamuna, uneneri wonena za iye, mbiri ya kumanganso Nyumba ya Mulungu, zalembedwa mʼbuku lofotokoza za mafumu. Ndipo Amaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
A no kana poe keiki, a me na mea nui i kauia maluna ona, a no ka hoomaikai hou ana i ka hale o ke Akua, aia hoi. ua kakauia ia mau mea ma ka palapala o ka buke no ua'lii. A noho alii iho la o Amazia kana keiki mahope ona.

< 2 Mbiri 24 >