< 2 Mbiri 24 >

1 Yowasi anali wa zaka zisanu ndi ziwiri pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka makumi anayi. Dzina la amayi ake linali Zibiya wa ku Beeriseba.
Joas var syv Aar gammel, der han blev Konge, og regerede fyrretyve Aar i Jerusalem, og hans Moders Navn var Zibna fra Beersaba.
2 Yowasi anachita zolungama pamaso pa Yehova nthawi yonse ya moyo wa wansembe Yehoyada.
Og Joas gjorde det, som var ret for Herrens Øjne, i alle Præsten Jojadas Dage.
3 Yehoyada anamupezera iye akazi awiri, ndipo anabereka ana aamuna ndi aakazi.
Og Jojada tog ham to Hustruer, og han avlede Sønner og Døtre.
4 Patapita nthawi Yowasi anatsimikiza zokonzanso Nyumba ya Yehova.
Og det skete derefter, at det laa Joas paa Hjerte at forny Herrens Hus.
5 Iye anayitanitsa pamodzi ansembe ndi Alevi ndipo anawawuza kuti, “Pitani ku mizinda ya Yuda ndi kukasonkhetsa ndalama za pa chaka kwa Aisraeli onse zokonzera Nyumba ya Mulungu wanu. Chitani zimenezi tsopano.” Koma Alevi sanachite zimenezi mwachangu.
Og han samlede Præsterne og Leviterne og sagde til dem: Drager ud til Judas Stæder og samler Penge ind af al Israel til at udbedre eders Guds Hus Aar for Aar, og I skulle skynde eder med Gerningen; men Leviterne skyndte sig ikke.
6 Choncho mfumu inayitanitsa Yehoyada, mkulu wa ansembe ndipo inati kwa iye, “Kodi nʼchifukwa chiyani simunawuze Alevi kuti asonkhetse ndalama ku Yuda ndi Yerusalemu, msonkho umene anakhazikitsa Mose mtumiki wa Yehova ndiponso gulu lonse la Aisraeli mu tenti yaumboni?”
Da kaldte Kongen ad Jojada, den Ypperstepræst, og sagde til ham: Hvorfor giver du ikke Agt paa Leviterne, at de fra Juda og Jerusalem bringe det Paalæg, som Mose, Herrens Tjener, og Israels Menighed har bestemt, ind til Vidnesbyrdets Paulun?
7 Ana a mkazi woyipa, Ataliya, anathyola chitseko cha Nyumba ya Mulungu ndipo anagwiritsa ntchito zinthu zopatulika popembedza Baala.
Thi under den ugudelige Athalia havde hendes Sønner gjort Brud paa Guds Hus; ja endog alt det, som var helliget til Herrens Hus, havde de anvendt til Baalerne.
8 Mfumu italamulira, bokosi linapangidwa ndipo linayikidwa panja pa chipata cha Nyumba ya Yehova.
Da befalede Kongen, og de gjorde en Kiste, og de satte den udenfor i Herrens Hus's Port.
9 Ndipo analengeza kwa anthu a mu Yuda ndi mu Yerusalemu kuti abweretse kwa Yehova msonkho umene Mose mtumiki wa Mulungu analamulira Aisraeli mʼchipululu.
Og de lode udraabe i Juda og i Jerusalem, at de skulde bringe for Herren det Paalæg, som Mose, Guds Tjener, havde lagt paa Israel i Ørken.
10 Akuluakulu onse ndi anthu onse anabweretsa zopereka zawo mokondwera ndipo anaziponya mʼbokosi mpaka linadzaza.
Da bleve alle Øverster og alt Folket glade, og de bragte det ind og lagde det i Kisten, indtil alt var kommet ind.
11 Nthawi ina iliyonse imene Alevi abweretsa bokosilo kwa akuluakulu a mfumu ndipo akaona kuti muli ndalama zambiri, mlembi waufumu ndi nduna yayikulu ya mkulu wa ansembe amabwera ndi kuchotsa ndalama mʼbokosi muja ndipo amalitenga kukaliyika pamalo pake. Iwo amachita izi nthawi ndi nthawi ndipo anapeza ndalama zambiri.
Og det skete, naar man ved Leviterne bragte Kisten ind efter Kongens Befaling, og man da saa, at der var mange Penge i den, da kom Kongens Skriver og Ypperstepræstens Befalingsmand, og de tømte Kisten og bare den hen og satte den igen paa sit Sted; saa gjorde de Dag for Dag og samlede Penge i Mangfoldighed.
12 Mfumu pamodzi ndi Yehoyada anapereka ndalamazo kwa anthu oyangʼanira ntchito ku Nyumba ya Yehova. Analemba ntchito amisiri a miyala ndi a matabwa kuti akonzenso Nyumba ya Yehova. Analembanso ntchito amisiri a zitsulo ndi mkuwa kuti akonze Nyumba ya Mulungu.
Og Kongen og Jojada gav dem til den, som havde at gøre med Gerningen i Herrens Hus's Tjeneste, og de lejede Stenhuggere og Tømmermænd til at fornye Herrens Hus, saa og Mestre til at arbejde i Jern og Kobber, til at udbedre Herrens Hus.
13 Anthu amene ankagwira ntchito anali odziwa bwino, ndipo ntchitoyo inagwiridwa bwino ndi manja awo. Iwo anamanganso Nyumba ya Mulungu motsatira mapangidwe ake oyamba ndipo anayilimbitsa.
Saa arbejdede Folkene, og Udbedringen af det, der arbejdedes paa, gik frem ved deres Haand; og de satte Guds Hus i Stand efter dets Maal og gjorde det stærkt.
14 Atamaliza, iwo anabweretsa ndalama zotsala kwa mfumu ndi Yehoyada, ndipo anazigwiritsira ntchito popangira zida za mʼNyumba ya Yehova: ziwiya zogwiritsa ntchito potumikira ndi popereka nsembe zopsereza, komanso mbale ndi ziwiya zagolide ndi siliva. Nthawi yonse ya moyo wa Yehoyada, nsembe zopsereza zinkaperekedwa mosalekeza mʼNyumba ya Yehova.
Og der de havde fuldendt det, bragte de de øvrige Penge frem for Kongens og Jojadas Ansigt, og for disse gjorde man Redskaber til Herrens Hus, Redskaber til Tjenesten og til at ofre, Røgelseskaaler og Guldkar og Sølvkar; og de ofrede stedse Brændofre i Herrens Hus alle Jojadas Dage.
15 Tsono Yehoyada anakalamba ndipo anali ndi zaka zambiri. Pambuyo pake iye anamwalira ali ndi zaka 130.
Og Jojada blev gammel og mæt af Dage og døde; han var hundrede og tredive Aar gammel, der han døde.
16 Iyeyo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi mafumu mu mzinda wa Davide chifukwa cha zabwino zimene anachita mu Israeli, kuchitira Mulungu ndi Nyumba yake.
Og de begrove ham i Davids Stad iblandt Kongerne, fordi han havde gjort godt i Israel og imod Gud og hans Hus.
17 Atamwalira Yehoyada, akuluakulu a Yuda anabwera kudzapereka ulemu kwa mfumu, ndipo mfumu inawamvera.
Men efter Jojadas Død kom de Øverste af Juda og nedbøjede sig for Kongen; da føjede Kongen dem.
18 Iwo anasiya Nyumba ya Yehova, Mulungu wa makolo awo ndipo anapembedza Asera ndi mafano. Chifukwa cha kulakwa kwawo, mkwiyo wa Yehova unabwera pa Yuda ndi Yerusalemu.
Saa forlode de Herrens, deres Fædres Guds, Hus og tjente Astartebillederne og Afguderne; og der kom en Vrede over Juda og Jerusalem for denne deres Syndeskyld.
19 Ngakhale Yehova anatumiza aneneri kwa anthuwo kuti awabweze kwa Iye, ngakhale aneneri ananenera mowatsutsa, anthuwo sanamvere.
Og han sendte Profeter til dem at omvende dem til Herren; og disse vidnede for dem, men de vilde ikke høre dem.
20 Kenaka Mzimu wa Mulungu unabwera pa Zekariya mwana wa wansembe Yehoyada. Iye anayimirira pamaso pa anthu ndipo anati, “Zimene Mulungu akunena ndi Izi: ‘Chifukwa chiyani simukumvera Malamulo a Yehova? Simudzapindula. Chifukwa mwasiya Yehova, Iyenso wakusiyani.’”
Og Guds Aand iførte sig Sakaria, Præsten Jojadas Søn, og han stod oven over Folket og sagde til dem: Saa sagde Gud: Hvorfor overtræde I Herrens Bud? derfor skulle I ikke være lykkelige, thi I have forladt Herren, og han har forladt eder.
21 Koma anthuwo anamuchitira chiwembu molamulidwa ndi mfumu ndipo anamugenda miyala ndi kumupha mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu.
Men de sammensvore sig imod ham og stenede ham med Stene, efter Kongens Bud, i Forgaarden til Herrens Hus.
22 Mfumu Yowasi sinakumbukire zabwino zimene Yehoyada abambo ake a Zekariya anamuchitira, koma anapha mwana wake. Pamene amafa, iye ananena kuti, “Yehova aone zimenezi ndipo abwezere chilango.”
Og Kong Joas kom ikke den Miskundhed i Hu, som Jojada, hans Fader, havde gjort imod ham, men slog hans Søn ihjel; og der denne døde, sagde han: Herren skal se og hjemsøge det.
23 Pakutha kwa chaka, gulu lankhondo la Aramu linadzamenyana ndi Yowasi. Linalowa mu Yuda ndi mu Yerusalemu ndi kupha atsogoleri onse a anthu. Zonse zimene analanda anazitumiza kwa mfumu ya ku Damasiko.
Og det skete, der Aaret var omme, drog Syrernes Hær op imod ham, og de kom til Juda og Jerusalem og udryddede af Folket alle Folkets Øverster, og de sendte alt deres Rov til Kongen af Damaskus.
24 Ngakhale kuti gulu lankhondo la Aramu linabwera ndi anthu ochepa okha, Yehova anapereka mʼmanja mwawo gulu lalikulu lankhondo. Chifukwa Yuda anasiya Yehova Mulungu wa makolo awo, chiweruzo chinachitika pa Yowasi.
Skønt Syrernes Hær kom med faa Mænd, gav Herren dog en saare stor Hær i deres Haand, fordi den havde forladt Herren, sine Fædres Gud; og de udførte Straffedommene over Joas.
25 Pamene Aaramu amachoka, anasiya Yowasi atavulazidwa kwambiri. Akuluakulu ake anamuchitira chiwembu chifukwa anapha mwana wa wansembe Yehoyada, ndipo anamupha ali pa bedi pake. Choncho anafa ndipo anayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide, koma osati manda a mafumu.
Og der de vare dragne fra ham, hvem de forlode i en svar Sygdom, indgik hans Tjenere et Forbund imod ham for Præsten Jojadas Sønners Blods Skyld, og de sloge ham ihjel paa hans Seng, og han døde; og de begrove ham i Davids Stad; men de begrove ham ikke i Kongernes Grave.
26 Iwo amene anamuchitira chiwembu anali Zabadi mwana wa Simeati, mkazi wa ku Amoni, ndi Yehozabadi mwana wa Simiriti, mkazi wa ku Mowabu.
Og de, som indgik Forbund imod ham, vare: Sabad, Simeaths den ammonitiske Kvindes Søn, og Josabad, Simriths den moabitiske Kvindes Søn.
27 Za ana ake aamuna, uneneri wonena za iye, mbiri ya kumanganso Nyumba ya Mulungu, zalembedwa mʼbuku lofotokoza za mafumu. Ndipo Amaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Og hvad angaar hans Sønner og den svare Byrde, som var lagt paa ham, og Grundforbedringen af Guds Hus, se, om alt dette er skrevet i Kongernes Bogs Historie. Og hans Søn Amazia blev Konge i hans Sted.

< 2 Mbiri 24 >