< 2 Mbiri 23 >

1 Mʼchaka chachisanu ndi chiwiri Yehoyada anaonetsa mphamvu zake. Iye anachita pangano ndi olamulira magulu a anthu 100: Azariya mwana wa Yerohamu, Ismaeli mwana wa Yehohanani, Azariya mwana wa Obedi, Maaseya mwana wa Adaya ndi Elisafati mwana wa Zikiri.
А седме године ослободи се Јодај, и узе к себи стотнике Азарију сина Јероамовог и Исмаила сина Јоанановог и Азарију сина Овидовог и Масију сина Адајевог и Елисафата сина Зихријевог, и ухвати веру с њима,
2 Iwo anayendayenda mʼdziko la Yuda ndipo anasonkhanitsa Alevi ndi atsogoleri a mabanja a Aisraeli ochokera mʼmizinda yonse. Atabwera ku Yerusalemu,
Те пролазећи земљу Јудину сабраше Левите из свих градова Јудиних и главаре породица отачких у Израиљу, и дођоше у Јерусалим.
3 msonkhano wonse unachita pangano ndi mfumu mu Nyumba ya Mulungu. Yehoyada anawawuza kuti, “Mwana wa mfumu adzalamulira monga ananenera Yehova zokhudza ana a Davide.
И сав збор учини веру у дому Божјем с царем; и Јодај им рече: Ево, син ће царев царовати, као што је рекао Господ за синове Давидове.
4 Tsopano zimene muti muchite ndi izi: Limodzi mwa magawo atatu a ansembe ndi Alevi amene mudzakhale pa ntchito pa Sabata muzikalondera pa khomo,
Ово учините: трећина вас који долазите у суботу између свештеника и Левита нека буду вратари на прагу;
5 ndi limodzi la magawo atatu likakhale ku nyumba yaufumu ndipo limodzi la magawo atatu likakhale ku chipata cha Maziko ndipo anthu ena onse akakhale mʼmabwalo a Nyumba ya Yehova.
А друга трећина нека буде у царском двору; а остала трећина на вратима од темеља, а сав народ у тремовима дома Господњег.
6 Musalole aliyense kulowa mʼNyumba ya Yehova kupatula ansembe ndi Alevi amene akutumikira. Iwo atha kutero chifukwa apatulidwa koma anthu ena onse ayenera kumvera zimene Yehova walamula.
Нико да не улази у дом Господњи осим свештеника и оних Левита који служе; они нека улазе, јер су посвећени, а сав народ нека чини оно што је Господ заповедио да чини.
7 Alevi akhale mozungulira mfumu, munthu aliyense ali ndi chida chake mʼmanja. Aliyense amene alowe mʼNyumba ya Mulungu ayenera kuphedwa. Mukhale nayo pafupi mfumu kulikonse kumene izipita.”
И Левити нека опколе цара, сваки с оружјем својим у руци; и ко би год ушао у дом, да се погуби; и будите уз цара кад стане улазити и излазити.
8 Alevi ndi anthu onse a ku Yuda anachita monga momwe wansembe Yehoyada anawalamulira. Aliyense anatenga anthu ake amene ankagwira ntchito pa Sabata ndi amene amapita kukapuma, pakuti wansembe Yehoyada sanalole gulu lililonse kuti lipite.
И учинише Левити и сав народ Јудин све што заповеди свештеник Јодај; и узеше сваки своје људе који долажаху у суботу и који одлажаху у суботу; јер Јодај свештеник не отпусти редове.
9 Ndipo Yehoyada anapereka kwa atsogoleri a magulu a anthu 100 mikondo ndi zishango zazikulu ndi zazingʼono zimene zinali za Davide ndipo zinali mʼNyumba ya Mulungu.
И даде Јодај свештеник стотиницима копља и штитове и штитиће цара Давида што беху у дому Божијем.
10 Iye anayika anthu onse, aliyense ali ndi chida mʼdzanja lake mozungulira mfumu pafupi ndi guwa ndi Nyumba ya Mulungu, kuyambira mbali ya kummwera mpaka kumpoto kwa Nyumba ya Mulungu.
И постави сав народ све с оружјем у руку, од десне стране дома до леве према олтару и према дому, око цара.
11 Yehoyada ndi ana ake anatulutsa mwana wa mfumu ndipo anamumveka chipewa chaufumu ndipo anamupatsa Buku la Chipangano namulonga ufumu. Yehoyada ndi ana ake anamudzoza ndipo anafuwula kuti, “Ikhale ndi moyo wautali mfumu!”
Тада изведоше сина царевог, и метнуше му на главу венац, и дадоше му сведочанство, и зацарише га, и Јодај и синови његови помазаше га и рекоше: Да живи цар!
12 Ataliya atamva phokoso la anthu akuthamanga ndi kukondwerera mfumu, anapita ku Nyumba ya Yehova komwe kunali anthuko.
А кад Готолија чу вику народа који се стецаше и хваљаше цара, дође к народу у дом Господњи.
13 Iye anayangʼana, ndipo anaona mfumu itayima pa chipilala chake chapakhomo. Atsogoleri ndi oyimba malipenga anali pafupi ndi mfumuyo, ndipo anthu onse a mʼderali amakondwerera ndi kuyimba malipenga ndiponso oyimba ndi zida amatsogolera matamando. Pamenepo Ataliya anangʼamba mkanjo wake ndipo anafuwula kuti, “Kuwukira! Kuwukira!”
И погледа, и гле, цар стајаше код свог ступа на уласку, а кнезови и трубе око цара, и сав народ земаљски радоваше се и трубе трубљаху и певачи певаху уз оруђа музичка и они који почињаху у певању. Тада раздре Готолија хаљине своје и повика: Буна! Буна!
14 Wansembe Yehoyada anatumiza olamulira magulu a anthu 100 aja, amene amayangʼanira asilikali ndipo anawawuza kuti, “Mutulutseni ameneyu pakati pa mizere yanu ndipo muphe aliyense amene adzamutsata.” Pakuti ansembe anati, “Musamuphere mʼNyumba ya Mulungu wa Yehova,”
А Јодај свештеник заповеди да изађу стотиници који беху над војском, и рече им: Изведите је из врста напоље, и ко пође за њом нека се погуби мачем; јер рече свештеник: Немојте је убити у дому Господњем.
15 choncho anamugwira pamene amafika pa chipata cha Kavalo pa bwalo la nyumba yaufumu, ndipo anamuphera pamenepo.
И начинише јој место, те отиде како се иде вратима коњским у дом царев, и онде је погубише.
16 Tsono Yehoyada anachita pangano, iye mwini ndi anthu onse ndiponso mfumu kuti adzakhala anthu a Yehova.
Тада Јодај учини веру међу собом и свим народом и царем да ће бити народ Господњи.
17 Anthu onse anapita ku kachisi wa Baala ndipo anamugwetsa. Iwo anaphwanya maguwa ndi mafano ndi kupha Matani wansembe wa Baala patsogolo pa maguwawo.
Потом сав народ отиде у дом Валов, и раскопаше га, и олтаре његове и ликове његове изломише, а Матана, свештеника Валовог, убише пред олтарима.
18 Kenaka Yehoyada anayika ansembe, omwe anali Alevi kukhala oyangʼanira Nyumba ya Yehova, amene Davide anawapatsa ntchito yoti azipereka nsembe zopsereza kwa Yehova mʼNyumba ya Mulungu, monga zinalembedwa mʼmalamulo a Mose kuti azitero akukondwera ndi kuyimba monga Davide analamulira.
И Јодај уреди опет службу у дому Господњем међу свештеницима и Левитима, које Давид беше одредио дому Господњем, да би приносили жртве паљенице Господу, као што пише у закону Мојсијевом, с весељем и песмама по наредби Давидовој.
19 Ndipo anayika alonda a pa khomo pa zipata za Nyumba ya Yehova kuti aliyense amene ndi odetsedwa asalowe.
Постави и вратаре на вратима дома Господњег да не би улазио нечист ода шта му драго.
20 Iye anatenga olamulira magulu a anthu 100, anthu otchuka, olamulira anthu ndi anthu onse a mʼderalo ndipo anabweretsa mfumu kuchokera ku Nyumba ya Mulungu. Iwo anapita ku nyumba yaufumu kudzera ku Chipata Chakumitu ndipo anayikira mfumu mpando wolemekezeka,
И узе стотинике и знатније људе и који управљаху народом, сав народ земаљски, и изведе цара из дома Господњег и уђоше високим вратима у дом царски, и посадише цара на царски престо.
21 ndipo anthu onse a mʼderali anakondwera. Tsono mu mzinda munali bata chifukwa Ataliya anaphedwa ndi lupanga.
И радоваше се сав народ земаљски, и град се умири, кад Готолију убише мачем.

< 2 Mbiri 23 >