< 2 Mbiri 23 >

1 Mʼchaka chachisanu ndi chiwiri Yehoyada anaonetsa mphamvu zake. Iye anachita pangano ndi olamulira magulu a anthu 100: Azariya mwana wa Yerohamu, Ismaeli mwana wa Yehohanani, Azariya mwana wa Obedi, Maaseya mwana wa Adaya ndi Elisafati mwana wa Zikiri.
و در سال هفتم، یهویاداع خویشتن راتقویت داده، بعضی از سرداران صده یعنی عزریا ابن یهورام و اسماعیل بن یهوحانان وعزریا ابن عوبید و معسیا ابن عدایا و الیشافاط بن زکری را با خود همداستان ساخت.۱
2 Iwo anayendayenda mʼdziko la Yuda ndipo anasonkhanitsa Alevi ndi atsogoleri a mabanja a Aisraeli ochokera mʼmizinda yonse. Atabwera ku Yerusalemu,
و ایشان دریهودا گردش کردند و لاویان را از جمیع شهرهای یهودا و روسای آبای اسرائیل را جمع کرده، به اورشلیم آمدند.۲
3 msonkhano wonse unachita pangano ndi mfumu mu Nyumba ya Mulungu. Yehoyada anawawuza kuti, “Mwana wa mfumu adzalamulira monga ananenera Yehova zokhudza ana a Davide.
و تمامی جماعت با پادشاه درخانه خدا عهد بستند. و او به ایشان گفت: «هماناپسر پادشاه سلطنت خواهد کرد، چنانکه خداونددرباره پسران داود گفته است.۳
4 Tsopano zimene muti muchite ndi izi: Limodzi mwa magawo atatu a ansembe ndi Alevi amene mudzakhale pa ntchito pa Sabata muzikalondera pa khomo,
و کاری که بایدبکنید این است: یک ثلث از شما که از کاهنان ولاویان در سبت داخل می‌شوید دربانهای آستانه‌ها باشید.۴
5 ndi limodzi la magawo atatu likakhale ku nyumba yaufumu ndipo limodzi la magawo atatu likakhale ku chipata cha Maziko ndipo anthu ena onse akakhale mʼmabwalo a Nyumba ya Yehova.
و ثلث دیگر به خانه پادشاه وثلثی به دروازه اساس و تمامی قوم در صحنهای خانه خداوند حاضر باشند.۵
6 Musalole aliyense kulowa mʼNyumba ya Yehova kupatula ansembe ndi Alevi amene akutumikira. Iwo atha kutero chifukwa apatulidwa koma anthu ena onse ayenera kumvera zimene Yehova walamula.
و کسی غیر ازکاهنان و لاویانی که به خدمت مشغول می‌باشند، داخل خانه خداوند نشود، اما ایشان داخل بشوند زیرا که مقدسند و تمامی قوم (خانه ) خداوند را حراست نمایند.۶
7 Alevi akhale mozungulira mfumu, munthu aliyense ali ndi chida chake mʼmanja. Aliyense amene alowe mʼNyumba ya Mulungu ayenera kuphedwa. Mukhale nayo pafupi mfumu kulikonse kumene izipita.”
و لاویان هرکس سلاح خود را به‌دست گرفته، پادشاه را از هرطرف احاطه نمایند و هر‌که به خانه درآید، کشته شود و چون پادشاه داخل شود یا بیرون رود، شما نزد او بمانید.»۷
8 Alevi ndi anthu onse a ku Yuda anachita monga momwe wansembe Yehoyada anawalamulira. Aliyense anatenga anthu ake amene ankagwira ntchito pa Sabata ndi amene amapita kukapuma, pakuti wansembe Yehoyada sanalole gulu lililonse kuti lipite.
پس لاویان و تمامی یهودا موافق هر‌چه یهویاداع کاهن امر فرمود عمل نمودند، و هر کدام کسان خود را خواه از آنانی که در روز سبت داخل می‌شدند و خواه از آنانی که در روز سبت بیرون می‌رفتند، برداشتند زیرا که یهویاداع کاهن فرقه هارا مرخص نفرمود.۸
9 Ndipo Yehoyada anapereka kwa atsogoleri a magulu a anthu 100 mikondo ndi zishango zazikulu ndi zazingʼono zimene zinali za Davide ndipo zinali mʼNyumba ya Mulungu.
و یهویاداع کاهن نیزه‌ها ومجنها و سپرها را که از آن داود پادشاه و در خانه خدا بود، به یوزباشیها داد.۹
10 Iye anayika anthu onse, aliyense ali ndi chida mʼdzanja lake mozungulira mfumu pafupi ndi guwa ndi Nyumba ya Mulungu, kuyambira mbali ya kummwera mpaka kumpoto kwa Nyumba ya Mulungu.
و تمامی قوم را که هر یک از ایشان سلاح خود را به‌دست گرفته بودند، از طرف راست خانه تا طرف چپ خانه به پهلوی مذبح و خانه، به اطراف پادشاه قرار داد.۱۰
11 Yehoyada ndi ana ake anatulutsa mwana wa mfumu ndipo anamumveka chipewa chaufumu ndipo anamupatsa Buku la Chipangano namulonga ufumu. Yehoyada ndi ana ake anamudzoza ndipo anafuwula kuti, “Ikhale ndi moyo wautali mfumu!”
و پسر پادشاه را بیرون آورده، تاج را بر سرش گذاشتند و شهادت نامه را به او داده، او را به پادشاهی نصب کردند، و یهویاداع و پسرانش، اورا مسح نموده، گفتند: «پادشاه زنده بماند.»۱۱
12 Ataliya atamva phokoso la anthu akuthamanga ndi kukondwerera mfumu, anapita ku Nyumba ya Yehova komwe kunali anthuko.
اما چون عتلیا آواز قوم را که می‌دویدند وپادشاه را مدح می‌کردند شنید، نزد قوم به خانه خداوند داخل شد.۱۲
13 Iye anayangʼana, ndipo anaona mfumu itayima pa chipilala chake chapakhomo. Atsogoleri ndi oyimba malipenga anali pafupi ndi mfumuyo, ndipo anthu onse a mʼderali amakondwerera ndi kuyimba malipenga ndiponso oyimba ndi zida amatsogolera matamando. Pamenepo Ataliya anangʼamba mkanjo wake ndipo anafuwula kuti, “Kuwukira! Kuwukira!”
و دید که اینک پادشاه به پهلوی ستون خود نزد مدخل ایستاده است، وسروران و کرنانوازان نزد پادشاه می‌باشند وتمامی قوم زمین شادی می‌کنند و کرناها رامی نوازند و مغنیان با آلات موسیقی و پیشوایان تسبیح. آنگاه عتلیا لباس خود را دریده، صدا زدکه «خیانت، خیانت!»۱۳
14 Wansembe Yehoyada anatumiza olamulira magulu a anthu 100 aja, amene amayangʼanira asilikali ndipo anawawuza kuti, “Mutulutseni ameneyu pakati pa mizere yanu ndipo muphe aliyense amene adzamutsata.” Pakuti ansembe anati, “Musamuphere mʼNyumba ya Mulungu wa Yehova,”
و یهویاداع کاهن، یوزباشیها را که سرداران فوج بودند امر فرموده، به ایشان گفت: «او را از میان صفها بیرون کنید، وهر‌که از عقب او برود، به شمشیر کشته شود.» زیرا کاهن فرموده بود که او را در خانه خداوندمکشید.۱۴
15 choncho anamugwira pamene amafika pa chipata cha Kavalo pa bwalo la nyumba yaufumu, ndipo anamuphera pamenepo.
پس او را راه دادند و چون به دهنه دروازه اسبان، نزد خانه پادشاه رسید، او را درآنجا کشتند.۱۵
16 Tsono Yehoyada anachita pangano, iye mwini ndi anthu onse ndiponso mfumu kuti adzakhala anthu a Yehova.
و یهویاداع در میان خود و تمامی قوم وپادشاه، عهد بست تا قوم خداوند باشند.۱۶
17 Anthu onse anapita ku kachisi wa Baala ndipo anamugwetsa. Iwo anaphwanya maguwa ndi mafano ndi kupha Matani wansembe wa Baala patsogolo pa maguwawo.
وتمامی قوم به خانه بعل رفته، آن را منهدم ساختندو مذبح هایش و تماثیلش را شکستند و کاهن بعل متان را روبه‌روی مذبحها کشتند.۱۷
18 Kenaka Yehoyada anayika ansembe, omwe anali Alevi kukhala oyangʼanira Nyumba ya Yehova, amene Davide anawapatsa ntchito yoti azipereka nsembe zopsereza kwa Yehova mʼNyumba ya Mulungu, monga zinalembedwa mʼmalamulo a Mose kuti azitero akukondwera ndi kuyimba monga Davide analamulira.
و یهویاداع باشادمانی و نغمه سرایی برحسب امر داود، وظیفه های خانه خداوند را به‌دست کاهنان ولاویان سپرد، چنانکه داود ایشان را بر خانه خداوند تقسیم کرده بود تا موافق آنچه در تواره موسی مکتوب است، قربانی های سوختنی خداوند را بگذرانند.۱۸
19 Ndipo anayika alonda a pa khomo pa zipata za Nyumba ya Yehova kuti aliyense amene ndi odetsedwa asalowe.
و دربانان را به دروازه های خانه خداوند قرار داد تا کسی‌که به هر جهتی نجس باشد، داخل نشود.۱۹
20 Iye anatenga olamulira magulu a anthu 100, anthu otchuka, olamulira anthu ndi anthu onse a mʼderalo ndipo anabweretsa mfumu kuchokera ku Nyumba ya Mulungu. Iwo anapita ku nyumba yaufumu kudzera ku Chipata Chakumitu ndipo anayikira mfumu mpando wolemekezeka,
ویوزباشیها و نجبا و حاکمان قوم و تمامی قوم زمین را برداشت و پادشاه را از خانه خداوند به زیر آورد و او را از دروازه اعلی به خانه پادشاه درآورده، او را بر کرسی سلطنت نشانید.۲۰
21 ndipo anthu onse a mʼderali anakondwera. Tsono mu mzinda munali bata chifukwa Ataliya anaphedwa ndi lupanga.
وتمامی قوم زمین شادی کردند و شهر آرامی یافت و عتلیا را به شمشیر کشتند.۲۱

< 2 Mbiri 23 >