< 2 Mbiri 23 >

1 Mʼchaka chachisanu ndi chiwiri Yehoyada anaonetsa mphamvu zake. Iye anachita pangano ndi olamulira magulu a anthu 100: Azariya mwana wa Yerohamu, Ismaeli mwana wa Yehohanani, Azariya mwana wa Obedi, Maaseya mwana wa Adaya ndi Elisafati mwana wa Zikiri.
La septième année, Joïada, s’étant affermi, prit avec lui comme alliés les centurions Azarias, fils de Jéroham, Ismaël, fils de Johanan, Azarias, fils d’Obed, Maasias, fils d’Adaïas, et Elisaphat, fils de Zechri.
2 Iwo anayendayenda mʼdziko la Yuda ndipo anasonkhanitsa Alevi ndi atsogoleri a mabanja a Aisraeli ochokera mʼmizinda yonse. Atabwera ku Yerusalemu,
Ils parcoururent Juda et, ayant rassemblé les lévites de toutes les villes de Juda et les chefs de famille d’Israël, ils vinrent à Jérusalem.
3 msonkhano wonse unachita pangano ndi mfumu mu Nyumba ya Mulungu. Yehoyada anawawuza kuti, “Mwana wa mfumu adzalamulira monga ananenera Yehova zokhudza ana a Davide.
Toute l’assemblée fit alliance avec le roi dans la maison de Dieu. Joïada leur dit: « Voici que le fils du roi va régner, comme Yahweh l’a déclaré à l’égard des fils de David.
4 Tsopano zimene muti muchite ndi izi: Limodzi mwa magawo atatu a ansembe ndi Alevi amene mudzakhale pa ntchito pa Sabata muzikalondera pa khomo,
Voici ce que vous ferez: Le tiers d’entre vous qui entre en service le jour du sabbat, prêtres et lévites, servira comme gardiens des portes;
5 ndi limodzi la magawo atatu likakhale ku nyumba yaufumu ndipo limodzi la magawo atatu likakhale ku chipata cha Maziko ndipo anthu ena onse akakhale mʼmabwalo a Nyumba ya Yehova.
un tiers servira à la maison du roi, et un tiers servira à la porte de Jésod; tout le peuple sera dans les parvis de la maison de Yahweh.
6 Musalole aliyense kulowa mʼNyumba ya Yehova kupatula ansembe ndi Alevi amene akutumikira. Iwo atha kutero chifukwa apatulidwa koma anthu ena onse ayenera kumvera zimene Yehova walamula.
Que personne n’entre dans la maison de Yahweh, excepté les prêtres et les lévites de service: eux peuvent y entrer, car ils sont saints; et tout le peuple doit garder l’observance de Yahweh.
7 Alevi akhale mozungulira mfumu, munthu aliyense ali ndi chida chake mʼmanja. Aliyense amene alowe mʼNyumba ya Mulungu ayenera kuphedwa. Mukhale nayo pafupi mfumu kulikonse kumene izipita.”
Les lévites entoureront le roi de toutes parts, chacun les armes à la main et, si quelqu’un entre dans la maison, qu’on le mette à mort; et vous serez près du roi quand il entrera et quand il sortira. »
8 Alevi ndi anthu onse a ku Yuda anachita monga momwe wansembe Yehoyada anawalamulira. Aliyense anatenga anthu ake amene ankagwira ntchito pa Sabata ndi amene amapita kukapuma, pakuti wansembe Yehoyada sanalole gulu lililonse kuti lipite.
Les lévites et tout Juda agirent selon tout ce qu’avait ordonné le prêtre Joïada. Ils prirent chacun leurs gens, ceux qui entraient en service et ceux qui sortaient de service le jour du sabbat; car le prêtre Joïada n’avait exempté aucune des divisions.
9 Ndipo Yehoyada anapereka kwa atsogoleri a magulu a anthu 100 mikondo ndi zishango zazikulu ndi zazingʼono zimene zinali za Davide ndipo zinali mʼNyumba ya Mulungu.
Le prêtre Joïada remit aux centurions les lances et les boucliers, grands et petits, qui avaient appartenu au roi David, et qui se trouvaient dans la maison de Dieu.
10 Iye anayika anthu onse, aliyense ali ndi chida mʼdzanja lake mozungulira mfumu pafupi ndi guwa ndi Nyumba ya Mulungu, kuyambira mbali ya kummwera mpaka kumpoto kwa Nyumba ya Mulungu.
Il fit placer tout le peuple, chacun son arme à la main, depuis le côté droit de la maison jusqu’au côté gauche de la maison, près de l’autel et près de la maison, de manière à entourer le roi.
11 Yehoyada ndi ana ake anatulutsa mwana wa mfumu ndipo anamumveka chipewa chaufumu ndipo anamupatsa Buku la Chipangano namulonga ufumu. Yehoyada ndi ana ake anamudzoza ndipo anafuwula kuti, “Ikhale ndi moyo wautali mfumu!”
On fit avancer le fils du roi, on mit sur lui le diadème et le témoignage, et on l’établit roi. Et Joïada et ses fils l’oignirent, et ils dirent: « Vive le roi! »
12 Ataliya atamva phokoso la anthu akuthamanga ndi kukondwerera mfumu, anapita ku Nyumba ya Yehova komwe kunali anthuko.
Lorsqu’Athalie entendit le bruit du peuple, courant et acclamant le roi, elle vint vers le peuple, à la maison de Yahweh.
13 Iye anayangʼana, ndipo anaona mfumu itayima pa chipilala chake chapakhomo. Atsogoleri ndi oyimba malipenga anali pafupi ndi mfumuyo, ndipo anthu onse a mʼderali amakondwerera ndi kuyimba malipenga ndiponso oyimba ndi zida amatsogolera matamando. Pamenepo Ataliya anangʼamba mkanjo wake ndipo anafuwula kuti, “Kuwukira! Kuwukira!”
Elle regarda, et voici que le roi se tenait sur son estrade à l’entrée; près du roi étaient les chefs et les trompettes, et tout le peuple du pays était dans la joie; on sonnait des trompettes, et les chantres avec les instruments de musique donnaient des instructions pour les hymnes de louange. Athalie déchira ses vêtements et dit: « Conspiration! Conspiration! »
14 Wansembe Yehoyada anatumiza olamulira magulu a anthu 100 aja, amene amayangʼanira asilikali ndipo anawawuza kuti, “Mutulutseni ameneyu pakati pa mizere yanu ndipo muphe aliyense amene adzamutsata.” Pakuti ansembe anati, “Musamuphere mʼNyumba ya Mulungu wa Yehova,”
Alors le prêtre Joïada fit sortir les centurions, qui étaient à la tête de l’armée, et leur dit: « Faites-la sortir entre les rangs, et que quiconque la suivra soit mis à mort par l’épée! » Car le prêtre avait dit: « Ne la mettez pas à mort dans la maison de Yahweh. »
15 choncho anamugwira pamene amafika pa chipata cha Kavalo pa bwalo la nyumba yaufumu, ndipo anamuphera pamenepo.
On lui fit place des deux côtés, et elle se rendit à l’entrée de la porte des chevaux, vers la maison du roi, et c’est là qu’ils la mirent à mort.
16 Tsono Yehoyada anachita pangano, iye mwini ndi anthu onse ndiponso mfumu kuti adzakhala anthu a Yehova.
Joïada conclut entre lui, tout le peuple et le roi une alliance par laquelle ils devaient être le peuple de Yahweh.
17 Anthu onse anapita ku kachisi wa Baala ndipo anamugwetsa. Iwo anaphwanya maguwa ndi mafano ndi kupha Matani wansembe wa Baala patsogolo pa maguwawo.
Et tout le peuple entra dans la maison de Baal, et ils la démolirent; ils brisèrent ses autels et ses images, et ils tuèrent devant les autels Mathan, prêtre de Baal.
18 Kenaka Yehoyada anayika ansembe, omwe anali Alevi kukhala oyangʼanira Nyumba ya Yehova, amene Davide anawapatsa ntchito yoti azipereka nsembe zopsereza kwa Yehova mʼNyumba ya Mulungu, monga zinalembedwa mʼmalamulo a Mose kuti azitero akukondwera ndi kuyimba monga Davide analamulira.
Joïada mit des gardiens dans la maison de Yahweh, sous l’autorité des prêtres et des lévites, que David avait distribués dans la maison de Yahweh pour qu’ils offrissent des holocaustes à Yahweh, comme il est écrit dans la loi de Moïse, au milieu des réjouissances et des chants, d’après les ordonnances de David.
19 Ndipo anayika alonda a pa khomo pa zipata za Nyumba ya Yehova kuti aliyense amene ndi odetsedwa asalowe.
Il établit les portiers aux portes de la maison de Yahweh, afin qu’il n’y entrât aucune personne souillée en quelque manière.
20 Iye anatenga olamulira magulu a anthu 100, anthu otchuka, olamulira anthu ndi anthu onse a mʼderalo ndipo anabweretsa mfumu kuchokera ku Nyumba ya Mulungu. Iwo anapita ku nyumba yaufumu kudzera ku Chipata Chakumitu ndipo anayikira mfumu mpando wolemekezeka,
Il prit les centurions, les hommes considérés, ceux qui avaient autorité sur le peuple et tout le peuple du pays, et il fit descendre le roi de la maison de Yahweh. Ils entrèrent dans la maison du roi par la porte supérieure, et ils firent asseoir le roi sur le trône de la royauté.
21 ndipo anthu onse a mʼderali anakondwera. Tsono mu mzinda munali bata chifukwa Ataliya anaphedwa ndi lupanga.
Tout le peuple du pays se réjouit, et la ville fut tranquille; on fit mourir Athalie par l’épée.

< 2 Mbiri 23 >