< 2 Mbiri 23 >
1 Mʼchaka chachisanu ndi chiwiri Yehoyada anaonetsa mphamvu zake. Iye anachita pangano ndi olamulira magulu a anthu 100: Azariya mwana wa Yerohamu, Ismaeli mwana wa Yehohanani, Azariya mwana wa Obedi, Maaseya mwana wa Adaya ndi Elisafati mwana wa Zikiri.
Léta pak sedmého posilnil se Joiada, a pojal s sebou v smlouvu setníky, Azariáše syna Jerochamova, a Izmaele syna Jochananova, a Azariáše syna Obédova, a Maaseiáše syna Adaiášova, a Elizafata syna Zichri,
2 Iwo anayendayenda mʼdziko la Yuda ndipo anasonkhanitsa Alevi ndi atsogoleri a mabanja a Aisraeli ochokera mʼmizinda yonse. Atabwera ku Yerusalemu,
Kteříž obcházejíce zemi Judskou, shromáždili Levíty ze všech měst Judských, a přední z otcovských čeledí Izraelských, a přišli do Jeruzaléma.
3 msonkhano wonse unachita pangano ndi mfumu mu Nyumba ya Mulungu. Yehoyada anawawuza kuti, “Mwana wa mfumu adzalamulira monga ananenera Yehova zokhudza ana a Davide.
I učinilo všecko to shromáždění smlouvu v domě Božím s králem. Byl pak jim řekl Joiada: Aj, syn králův kralovati bude, jakož mluvil Hospodin o synech Davidových.
4 Tsopano zimene muti muchite ndi izi: Limodzi mwa magawo atatu a ansembe ndi Alevi amene mudzakhale pa ntchito pa Sabata muzikalondera pa khomo,
Tatoť jest věc, kterouž učiníte: Třetí díl vás, kteříž přicházíte v sobotu z kněží a z Levítů, budou vrátnými.
5 ndi limodzi la magawo atatu likakhale ku nyumba yaufumu ndipo limodzi la magawo atatu likakhale ku chipata cha Maziko ndipo anthu ena onse akakhale mʼmabwalo a Nyumba ya Yehova.
Třetí pak díl bude při domě královu, a třetí díl u brány přední, ale všecken lid bude v síních domu Hospodinova.
6 Musalole aliyense kulowa mʼNyumba ya Yehova kupatula ansembe ndi Alevi amene akutumikira. Iwo atha kutero chifukwa apatulidwa koma anthu ena onse ayenera kumvera zimene Yehova walamula.
Aniž kdo vcházej do domu Hospodinova kromě kněží a těch Levítů, kteříž konají služby. Ti ať vcházejí, nebo svatí jsou, všecken pak lid ať drží stráž Hospodinovu.
7 Alevi akhale mozungulira mfumu, munthu aliyense ali ndi chida chake mʼmanja. Aliyense amene alowe mʼNyumba ya Mulungu ayenera kuphedwa. Mukhale nayo pafupi mfumu kulikonse kumene izipita.”
I obstoupí Levítové krále vůkol, jeden každý maje braň svou v rukou svých, a kdož by koli všel do domu, ať umře. A buďte při králi, když bude vcházeti, i když bude vycházeti.
8 Alevi ndi anthu onse a ku Yuda anachita monga momwe wansembe Yehoyada anawalamulira. Aliyense anatenga anthu ake amene ankagwira ntchito pa Sabata ndi amene amapita kukapuma, pakuti wansembe Yehoyada sanalole gulu lililonse kuti lipite.
Tedy učinili Levítové a všecken Juda všecko, cožkoli přikázal Joiada kněz, a vzali jeden každý muže své, kteříž přicházeli v sobotu, a kteříž odcházeli v sobotu; nebo byl nepropustil Joiada kněz žádné střídy.
9 Ndipo Yehoyada anapereka kwa atsogoleri a magulu a anthu 100 mikondo ndi zishango zazikulu ndi zazingʼono zimene zinali za Davide ndipo zinali mʼNyumba ya Mulungu.
I dal Joiada kněz setníkům kopí a pavézy i štíty, kteříž byli krále Davida, jenž byli v domě Božím.
10 Iye anayika anthu onse, aliyense ali ndi chida mʼdzanja lake mozungulira mfumu pafupi ndi guwa ndi Nyumba ya Mulungu, kuyambira mbali ya kummwera mpaka kumpoto kwa Nyumba ya Mulungu.
A postavil všecken lid, (a jeden každý měl braň v ruce své), od pravé strany domu až do levé strany domu, proti oltáři a proti domu, při králi všudy vůkol.
11 Yehoyada ndi ana ake anatulutsa mwana wa mfumu ndipo anamumveka chipewa chaufumu ndipo anamupatsa Buku la Chipangano namulonga ufumu. Yehoyada ndi ana ake anamudzoza ndipo anafuwula kuti, “Ikhale ndi moyo wautali mfumu!”
A tak vyvedli syna králova, a vstavili na něj korunu královskou a ozdobu. I ustanovili jej králem, a pomazali ho Joiada a synové jeho, a říkali: Živ buď král!
12 Ataliya atamva phokoso la anthu akuthamanga ndi kukondwerera mfumu, anapita ku Nyumba ya Yehova komwe kunali anthuko.
V tom uslyševši Atalia hřmot sbíhajícího se lidu, a chválícího krále, vešla k lidu do domu Hospodinova.
13 Iye anayangʼana, ndipo anaona mfumu itayima pa chipilala chake chapakhomo. Atsogoleri ndi oyimba malipenga anali pafupi ndi mfumuyo, ndipo anthu onse a mʼderali amakondwerera ndi kuyimba malipenga ndiponso oyimba ndi zida amatsogolera matamando. Pamenepo Ataliya anangʼamba mkanjo wake ndipo anafuwula kuti, “Kuwukira! Kuwukira!”
A když pohleděla, a aj, král stál na místě vyšším, kudyž se vchází, a knížata i trubači podlé krále, a všecken lid země veselící se, a zvučící na trouby, a zpěváci s nástroji hudebnými, a ti, kteříž předčili v zpívání. Tedy roztrhla Atalia roucho své, a řekla: Spiknutí, spiknutí!
14 Wansembe Yehoyada anatumiza olamulira magulu a anthu 100 aja, amene amayangʼanira asilikali ndipo anawawuza kuti, “Mutulutseni ameneyu pakati pa mizere yanu ndipo muphe aliyense amene adzamutsata.” Pakuti ansembe anati, “Musamuphere mʼNyumba ya Mulungu wa Yehova,”
Ale Joiada kněz rozkázal vyjíti setníkům, hejtmanům vojska, řka jim: Vyveďte ji prostředkem řadů, a kdož by za ní šel, ať jest zabit mečem. Nebo byl řekl kněz: Nezabijejte jí v domě Hospodinově.
15 choncho anamugwira pamene amafika pa chipata cha Kavalo pa bwalo la nyumba yaufumu, ndipo anamuphera pamenepo.
A když se jí rozstoupili s obou stran, šla, kudy se chodí k bráně koňské k domu královskému, a tu ji zabili.
16 Tsono Yehoyada anachita pangano, iye mwini ndi anthu onse ndiponso mfumu kuti adzakhala anthu a Yehova.
Tedy Joiada učinil smlouvu mezi Hospodinem a mezi vším lidem, i mezi králem, aby byli lid Hospodinův.
17 Anthu onse anapita ku kachisi wa Baala ndipo anamugwetsa. Iwo anaphwanya maguwa ndi mafano ndi kupha Matani wansembe wa Baala patsogolo pa maguwawo.
Potom šel všecken lid do domu Bálova a zbořili jej i oltáře jeho, a obrazy stroskotali. Matana pak kněze Bálova zabili před oltáři.
18 Kenaka Yehoyada anayika ansembe, omwe anali Alevi kukhala oyangʼanira Nyumba ya Yehova, amene Davide anawapatsa ntchito yoti azipereka nsembe zopsereza kwa Yehova mʼNyumba ya Mulungu, monga zinalembedwa mʼmalamulo a Mose kuti azitero akukondwera ndi kuyimba monga Davide analamulira.
I uvedl zase Joiada úředníky domu Hospodinova pod moc kněží a Levítů, kteréž byl rozdělil David v domě Hospodinově, aby obětovali zápaly Hospodinu, (jakož psáno jest v zákoně Mojžíšově), s veselím a zpíváním podlé nařízení Davidova.
19 Ndipo anayika alonda a pa khomo pa zipata za Nyumba ya Yehova kuti aliyense amene ndi odetsedwa asalowe.
Postavil také vrátné u vrat domu Hospodinova, aby tam nevcházel poškvrněný jakoužkoli věcí.
20 Iye anatenga olamulira magulu a anthu 100, anthu otchuka, olamulira anthu ndi anthu onse a mʼderalo ndipo anabweretsa mfumu kuchokera ku Nyumba ya Mulungu. Iwo anapita ku nyumba yaufumu kudzera ku Chipata Chakumitu ndipo anayikira mfumu mpando wolemekezeka,
A pojav setníky a znamenitější, a ty, kteříž správu drželi nad lidem, i všecken lid země, provázel krále z domu Hospodinova. I šli branou hořejší do domu královského, a posadili krále na stolici královské.
21 ndipo anthu onse a mʼderali anakondwera. Tsono mu mzinda munali bata chifukwa Ataliya anaphedwa ndi lupanga.
I veselil se všecken lid země, a město se upokojilo, jakž Atalii zabili mečem.