< 2 Mbiri 23 >

1 Mʼchaka chachisanu ndi chiwiri Yehoyada anaonetsa mphamvu zake. Iye anachita pangano ndi olamulira magulu a anthu 100: Azariya mwana wa Yerohamu, Ismaeli mwana wa Yehohanani, Azariya mwana wa Obedi, Maaseya mwana wa Adaya ndi Elisafati mwana wa Zikiri.
А в седмата година Иодай се усили като взе стотниците Азария, Ероамовия син, Исмаила Иоанановия син, Азария Овидовия син, Маасия Адаиевия син и Елисафата Зехриевия син, та направи завет с тях.
2 Iwo anayendayenda mʼdziko la Yuda ndipo anasonkhanitsa Alevi ndi atsogoleri a mabanja a Aisraeli ochokera mʼmizinda yonse. Atabwera ku Yerusalemu,
И обходиха Юда та събраха левитите от всичките Юдови градове, и началниците на Израилевите бащини домове, и дойдоха в Ерусалим.
3 msonkhano wonse unachita pangano ndi mfumu mu Nyumba ya Mulungu. Yehoyada anawawuza kuti, “Mwana wa mfumu adzalamulira monga ananenera Yehova zokhudza ana a Davide.
Тогава цялото събрание направи завет с царя в Божия дом. И Иодай им каза: Ето, царският син ще се възцари, както е говорил Господ за Давидовите потомци.
4 Tsopano zimene muti muchite ndi izi: Limodzi mwa magawo atatu a ansembe ndi Alevi amene mudzakhale pa ntchito pa Sabata muzikalondera pa khomo,
Ето какво трябва да направите: една трета от вас, от свещениците и от левитите, които постъпват на служба в съботата, нека стоят вратари при вратите,
5 ndi limodzi la magawo atatu likakhale ku nyumba yaufumu ndipo limodzi la magawo atatu likakhale ku chipata cha Maziko ndipo anthu ena onse akakhale mʼmabwalo a Nyumba ya Yehova.
една трета в царската къща, и една трета при портата на основата; а всичките люде да бъдат в дворовете на Господния дом.
6 Musalole aliyense kulowa mʼNyumba ya Yehova kupatula ansembe ndi Alevi amene akutumikira. Iwo atha kutero chifukwa apatulidwa koma anthu ena onse ayenera kumvera zimene Yehova walamula.
И никой да не влиза в Господния дом, освен свещениците и ония от левитите, които служат; те нека влизат, защото са свети; а всичките люде да пазят заръчаното от Господа,
7 Alevi akhale mozungulira mfumu, munthu aliyense ali ndi chida chake mʼmanja. Aliyense amene alowe mʼNyumba ya Mulungu ayenera kuphedwa. Mukhale nayo pafupi mfumu kulikonse kumene izipita.”
И левитите да окръжават царя, като има всеки оръжията си в ръка; и който би влязъл в дома, да бъде убит; и да бъдете с царя при влизането му и при излизането му.
8 Alevi ndi anthu onse a ku Yuda anachita monga momwe wansembe Yehoyada anawalamulira. Aliyense anatenga anthu ake amene ankagwira ntchito pa Sabata ndi amene amapita kukapuma, pakuti wansembe Yehoyada sanalole gulu lililonse kuti lipite.
И тъй, левитите и целият Юда извършиха всичко според както заповяда свещеник Иодай, и взеха всеки мъжете си - ония, които щяха да постъпят на служба в събота, и ония, които щяха да оставят службата в съботата; защото свещеник Иодай не разпущаше отредите.
9 Ndipo Yehoyada anapereka kwa atsogoleri a magulu a anthu 100 mikondo ndi zishango zazikulu ndi zazingʼono zimene zinali za Davide ndipo zinali mʼNyumba ya Mulungu.
И свещеник Иодай даде на стотниците цар Давидовите копия и щитчетата и щитове, които бяха в Божия дом.
10 Iye anayika anthu onse, aliyense ali ndi chida mʼdzanja lake mozungulira mfumu pafupi ndi guwa ndi Nyumba ya Mulungu, kuyambira mbali ya kummwera mpaka kumpoto kwa Nyumba ya Mulungu.
И постави всичките люде около царя, всеки мъж с оръжията му в ръка, от дясната страна на дома до лявата страна на дома, край олтара и край храма.
11 Yehoyada ndi ana ake anatulutsa mwana wa mfumu ndipo anamumveka chipewa chaufumu ndipo anamupatsa Buku la Chipangano namulonga ufumu. Yehoyada ndi ana ake anamudzoza ndipo anafuwula kuti, “Ikhale ndi moyo wautali mfumu!”
Тогава изведоха царския син, та положиха на него короната и му връчиха божественото заявление, и направиха го цар. И Иодай и синовете му го помазаха и казаха: Да живее царят!
12 Ataliya atamva phokoso la anthu akuthamanga ndi kukondwerera mfumu, anapita ku Nyumba ya Yehova komwe kunali anthuko.
А Годолия, като чу вика от людете, които се стичаха и хвалеха царя, дойде при людете в Господния дом,
13 Iye anayangʼana, ndipo anaona mfumu itayima pa chipilala chake chapakhomo. Atsogoleri ndi oyimba malipenga anali pafupi ndi mfumuyo, ndipo anthu onse a mʼderali amakondwerera ndi kuyimba malipenga ndiponso oyimba ndi zida amatsogolera matamando. Pamenepo Ataliya anangʼamba mkanjo wake ndipo anafuwula kuti, “Kuwukira! Kuwukira!”
и погледна, и, ето, царят стоеше при стълба си във входа и военачалниците и тръбите при царя, и всичките люде от страната са радваха и свиреха с тръбите, а певците и ония, които бяха изкусни да псалмопеят, свиреха с музикалните инструменти. Тогава Годолия раздра дрехите си и извика: Заговор! заговор!
14 Wansembe Yehoyada anatumiza olamulira magulu a anthu 100 aja, amene amayangʼanira asilikali ndipo anawawuza kuti, “Mutulutseni ameneyu pakati pa mizere yanu ndipo muphe aliyense amene adzamutsata.” Pakuti ansembe anati, “Musamuphere mʼNyumba ya Mulungu wa Yehova,”
И свещеник Иодай изведе стотниците, поставени над силите, та им рече: Изведете я вън от редовете, и който би я последвал, да бъде убит с меч; защото свещеникът беше казал: Да не я убиете в Господния дом.
15 choncho anamugwira pamene amafika pa chipata cha Kavalo pa bwalo la nyumba yaufumu, ndipo anamuphera pamenepo.
И така отстъпиха й място: и когато стигна до входа на царската къща, убиха я там.
16 Tsono Yehoyada anachita pangano, iye mwini ndi anthu onse ndiponso mfumu kuti adzakhala anthu a Yehova.
Тогава Иодай направи завет между себе си и всичките люде и царя, че ще бъдат Господни люде.
17 Anthu onse anapita ku kachisi wa Baala ndipo anamugwetsa. Iwo anaphwanya maguwa ndi mafano ndi kupha Matani wansembe wa Baala patsogolo pa maguwawo.
И всичките люде влязоха във Вааловото капище, та го събориха, жертвениците му и кумирите му изпотрошиха, а Вааловият жрец, Матан, убиха пред жертвениците.
18 Kenaka Yehoyada anayika ansembe, omwe anali Alevi kukhala oyangʼanira Nyumba ya Yehova, amene Davide anawapatsa ntchito yoti azipereka nsembe zopsereza kwa Yehova mʼNyumba ya Mulungu, monga zinalembedwa mʼmalamulo a Mose kuti azitero akukondwera ndi kuyimba monga Davide analamulira.
И Иодай постави службите на Господния дом в ръцете на левитските свещеници, които Давид беше разпределил из Господния дом, за да принасят Господните всеизгаряния, според както е писано в Моисеевия закон, с веселие и с песни според Давидовата наредба.
19 Ndipo anayika alonda a pa khomo pa zipata za Nyumba ya Yehova kuti aliyense amene ndi odetsedwa asalowe.
Постави и вратарите при портите на Господния дом, да не би да влиза някой нечист от какво да е нещо.
20 Iye anatenga olamulira magulu a anthu 100, anthu otchuka, olamulira anthu ndi anthu onse a mʼderalo ndipo anabweretsa mfumu kuchokera ku Nyumba ya Mulungu. Iwo anapita ku nyumba yaufumu kudzera ku Chipata Chakumitu ndipo anayikira mfumu mpando wolemekezeka,
Тогава, като взе стотниците, високопоставените, началниците на людете, и всичките люде от страната, изведоха царя от Господния дом; и като заминаха през горната порта в царската къща, поставиха царя на царския престол.
21 ndipo anthu onse a mʼderali anakondwera. Tsono mu mzinda munali bata chifukwa Ataliya anaphedwa ndi lupanga.
Така всичките люде от страната се зарадваха, и градът се успокои; а Готолия убиха с меч.

< 2 Mbiri 23 >