< 2 Mbiri 22 >
1 Anthu a mu Yerusalemu anayika Ahaziya mwana wamngʼono kwambiri wa Yehoramu kukhala mfumu mʼmalo mwake, popeza gulu lankhondo limene linabwera ndi Aarabu ku misasa, linapha ana onse aakulu. Motero Ahaziya mwana wa Yehoramu mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
Och Jerusalems invånare gjorde Ahasja, hans yngste son, till konung efter honom; ty alla de äldre hade blivit dräpta av den rövarskara som med araberna hade kommit till lägret. Så blev då Ahasja, Jorams son, konung i Juda.
2 Ahaziya anali wa zaka 22 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu chaka chimodzi. Dzina la amayi ake linali Ataliya, chidzukulu cha Omuri.
Fyrtiotvå år gammal var Ahasja, är han blev konung, ock han regerade ett år i Jerusalem. Hans moder hette Atalja, Omris dotter.
3 Nayenso anayenda mʼnjira ya banja la Ahabu, pakuti amayi ake anamulimbikitsa kuchita zolakwika.
Också han vandrade på Ahabs hus' vägar, ty hans moder var hans rådgiverska i ogudaktighet.
4 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga momwe banja la Ahabu linachitira, pakuti atamwalira abambo ake, iwo anakhala alangizi ake, kumene kunali kudziwononga kwake.
Han gjorde vad ont var i HERRENS ögon likasom Ahabs hus; ty därifrån tog han, efter sin faders död, sina rådgivare, till sitt eget fördärv.
5 Iyeyo anatsatiranso uphungu wawo pamene anapita ndi Yehoramu, mwana wa Ahabu, mfumu ya Israeli kukachita nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya Aramu ku Ramoti Giliyadi. Aaramu anavulaza Yehoramu,
Det var ock deras råd han följde, när han drog åstad med Joram, Ahabs son, Israels konung, och stridde mot Hasael, konungen i Aram, vid Ramot i Gilead. Men Joram blev sårad av araméerna.
6 kotero iye anabwerera ku Yezireeli kuti akachire mabala amene anamuvulaza ku Ramoti pa nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya Aaramu. Ndipo Ahaziya, mwana wa Yehoramu mfumu ya Yuda anapita ku Yezireeli kukaona Yehoramu mwana wa Ahabu chifukwa anavulazidwa.
Då vände han tillbaka, för att i Jisreel låta hela sig från de sår som han hade fått vid Rama, i striden mot Hasael, konungen i Aram. Och Asarja, Jorams son, Juda konung, for ned för att besöka Joram, Ahabs son, i Jisreel, eftersom denne låg sjuk.
7 Mulungu anakonza kuti Ahaziya akaphedwe pa ulendo wake wokacheza. Ahaziya atafika, iye ndi Yoramu anapita kukakumana ndi Yehu mwana wa Nimisi, amene Yehova anamudzoza kuti akawononge banja la Ahabu.
Men till Ahasjas fördärv var det av Gud bestämt att han skulle komma till Joram. Ty när han hade kommit dit, for han med Joram för att möta Jehu, Nimsis son, som HERREN hade smort till att utrota Ahabs hus.
8 Pamene Yehu ankalanga banja la Ahabu anapeza atsogoleri a ku Yuda ndiponso ana aamuna a abale ake a Ahaziya amene amatumikira Ahaziya, ndipo anawapha.
Så hände sig att Jehu, när han utförde straffdomen över Ahabs hus, träffade på de Juda furstar och de brorsöner till Ahasja, som voro i Ahasjas tjänst, och dräpte dem.
9 Kenaka anapita kukafunafuna Ahaziya, ndipo anthu ake anagwira Ahaziya pamene amabisala mu Samariya. Anabwera naye kwa Yehu ndipo anaphedwa. Iwo anamuyika mʼmanda, pakuti anati, “Iyeyu anali mwana wa Yehosafati amene anafunafuna Yehova ndi mtima wake wonse.” Kotero panalibe wamphamvu mʼbanja la Ahaziya kuti nʼkukhala mfumu.
Sedan sökte han efter Ahasja; och man grep denne, där han höll sig gömd i Samaria, och förde honom till Jehu och dödade honom. Men därefter begrovo de honom, ty de sade: "Han var dock son till Josafat, som sökte HERREN av allt sitt hjärta." Och av Ahasjas hus fanns sedan ingen dom förmådde övertaga konungadömet.
10 Ataliya, amayi ake a Ahaziya, ataona kuti mwana wawo wafa, ananyamuka nakapha onse a banja laufumu la Yuda.
När nu Atalja, Ahasjas moder, förnam att hennes son var död, stod hon upp och förgjorde hela konungasläkten i Juda hus.
11 Koma Yehoseba, mwana wamkazi wa mfumu Yehoramu, anatenga Yowasi mwana wa Ahaziya, momuba ndi kumuchotsa pakati pa ana aamuna a mfumu amene amati aphedwe ndipo anamuyika iye ndi mlezi wake mʼchipinda chogona. Motero Yehoseba, mwana wamkazi wa mfumu Yehoramu, mkazi wa wansembe Yehoyada, yemwe anali mlongo wake wa Ahaziya anamubisa mwanayo kuti Ataliya asamuphe.
Men just när konungabarnen skulle dödas, tog konungadottern Josabeat Joas, Ahasjas son, och skaffade honom hemligen undan, i det att han förde honom jämte hans amma in i sovkammaren; där höll Josabeat, konung Jorams dotter, prästen Jojadas hustru -- som ju ock var Ahasjas syster -- honom dold för Atalja, så att denna icke fick döda honom.
12 Mwanayo anakhala mobisala pamodzi ndi iwo mu Nyumba ya Mulungu kwa zaka zisanu ndi chimodzi muulamuliro wa Ataliya.
Sedan var han hos dem i Guds hus, där han förblev gömd i sex år, medan Atalja regerade i landet.