< 2 Mbiri 22 >
1 Anthu a mu Yerusalemu anayika Ahaziya mwana wamngʼono kwambiri wa Yehoramu kukhala mfumu mʼmalo mwake, popeza gulu lankhondo limene linabwera ndi Aarabu ku misasa, linapha ana onse aakulu. Motero Ahaziya mwana wa Yehoramu mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
Les habitants de Jérusalem firent régner à sa place Achazia, son plus jeune fils, car la bande d'hommes qui était venue au camp avec les Arabes avait tué tous les plus âgés. Ainsi régna Achazia, fils de Joram, roi de Juda.
2 Ahaziya anali wa zaka 22 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu chaka chimodzi. Dzina la amayi ake linali Ataliya, chidzukulu cha Omuri.
Achazia avait quarante-deux ans lorsqu'il devint roi, et il régna un an à Jérusalem. Le nom de sa mère était Athalie, fille d'Omri.
3 Nayenso anayenda mʼnjira ya banja la Ahabu, pakuti amayi ake anamulimbikitsa kuchita zolakwika.
Il marchait aussi dans les voies de la maison d'Achab, car sa mère le conseillait dans sa méchanceté.
4 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga momwe banja la Ahabu linachitira, pakuti atamwalira abambo ake, iwo anakhala alangizi ake, kumene kunali kudziwononga kwake.
Il fit ce qui est mal aux yeux de l'Éternel, comme la maison d'Achab, car ils furent ses conseillers après la mort de son père, pour le détruire.
5 Iyeyo anatsatiranso uphungu wawo pamene anapita ndi Yehoramu, mwana wa Ahabu, mfumu ya Israeli kukachita nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya Aramu ku Ramoti Giliyadi. Aaramu anavulaza Yehoramu,
Il suivit aussi leurs conseils et alla avec Joram, fils d'Achab, roi d'Israël, à la guerre contre Hazaël, roi de Syrie, à Ramoth Galaad; et les Syriens blessèrent Joram.
6 kotero iye anabwerera ku Yezireeli kuti akachire mabala amene anamuvulaza ku Ramoti pa nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya Aaramu. Ndipo Ahaziya, mwana wa Yehoramu mfumu ya Yuda anapita ku Yezireeli kukaona Yehoramu mwana wa Ahabu chifukwa anavulazidwa.
Il revint se faire guérir à Jizreel des blessures qu'on lui avait faites à Rama, lorsqu'il combattait Hazaël, roi de Syrie. Azaria, fils de Joram, roi de Juda, descendit voir Joram, fils d'Achab, à Jizreel, car il était malade.
7 Mulungu anakonza kuti Ahaziya akaphedwe pa ulendo wake wokacheza. Ahaziya atafika, iye ndi Yoramu anapita kukakumana ndi Yehu mwana wa Nimisi, amene Yehova anamudzoza kuti akawononge banja la Ahabu.
Or, la destruction d'Achazia fut le fait de Dieu, en ce qu'il alla vers Joram; car, quand il fut arrivé, il sortit avec Joram contre Jéhu, fils de Nimshi, que l'Éternel avait oint pour exterminer la maison d'Achab.
8 Pamene Yehu ankalanga banja la Ahabu anapeza atsogoleri a ku Yuda ndiponso ana aamuna a abale ake a Ahaziya amene amatumikira Ahaziya, ndipo anawapha.
Lorsque Jéhu exerçait son jugement sur la maison d'Achab, il trouva les princes de Juda et les fils des frères d'Achazia au service d'Achazia, et il les tua.
9 Kenaka anapita kukafunafuna Ahaziya, ndipo anthu ake anagwira Ahaziya pamene amabisala mu Samariya. Anabwera naye kwa Yehu ndipo anaphedwa. Iwo anamuyika mʼmanda, pakuti anati, “Iyeyu anali mwana wa Yehosafati amene anafunafuna Yehova ndi mtima wake wonse.” Kotero panalibe wamphamvu mʼbanja la Ahaziya kuti nʼkukhala mfumu.
Il chercha Achazia, et on l'attrapa (il se cachait maintenant à Samarie), on l'amena à Jéhu et on le tua; puis on l'enterra, car on disait: « C'est le fils de Josaphat, qui cherchait Yahvé de tout son cœur. » La maison d'Achazia n'avait plus le pouvoir de détenir le royaume.
10 Ataliya, amayi ake a Ahaziya, ataona kuti mwana wawo wafa, ananyamuka nakapha onse a banja laufumu la Yuda.
Et quand Athalie, mère d'Achazia, vit que son fils était mort, elle se leva et fit périr toute la race royale de la maison de Juda.
11 Koma Yehoseba, mwana wamkazi wa mfumu Yehoramu, anatenga Yowasi mwana wa Ahaziya, momuba ndi kumuchotsa pakati pa ana aamuna a mfumu amene amati aphedwe ndipo anamuyika iye ndi mlezi wake mʼchipinda chogona. Motero Yehoseba, mwana wamkazi wa mfumu Yehoramu, mkazi wa wansembe Yehoyada, yemwe anali mlongo wake wa Ahaziya anamubisa mwanayo kuti Ataliya asamuphe.
Mais Joschabeath, fille du roi, prit Joas, fils d'Achazia, et le sauva furtivement du milieu des fils du roi qui avaient été tués, et le mit avec sa nourrice dans la chambre à coucher. Et Jéhoshabeath, fille du roi Joram, femme du prêtre Jehojada (car elle était la sœur d'Achazia), le cacha d'Athalie, afin qu'elle ne le tuât pas.
12 Mwanayo anakhala mobisala pamodzi ndi iwo mu Nyumba ya Mulungu kwa zaka zisanu ndi chimodzi muulamuliro wa Ataliya.
Il resta avec eux, caché dans la maison de Dieu, six ans pendant qu'Athalie régnait sur le pays.