< 2 Mbiri 22 >

1 Anthu a mu Yerusalemu anayika Ahaziya mwana wamngʼono kwambiri wa Yehoramu kukhala mfumu mʼmalo mwake, popeza gulu lankhondo limene linabwera ndi Aarabu ku misasa, linapha ana onse aakulu. Motero Ahaziya mwana wa Yehoramu mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
And the inhabitants of Jerusalem made Achazyahu his youngest son king in his stead; for the predatory band that was come with the Arabians to the camp had slain all the eldest. So became Achazyahu, the son of Jehoram the king of Judah, king.
2 Ahaziya anali wa zaka 22 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu chaka chimodzi. Dzina la amayi ake linali Ataliya, chidzukulu cha Omuri.
Forty and two years old was Achazyahu when he became king, and one year did he reign in Jerusalem: and his mother's name was Athalyahu the [grand-]daughter of 'Omri.
3 Nayenso anayenda mʼnjira ya banja la Ahabu, pakuti amayi ake anamulimbikitsa kuchita zolakwika.
Also he walked in the ways of the house of Achab; for his mother was his counsellor to act wickedly.
4 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga momwe banja la Ahabu linachitira, pakuti atamwalira abambo ake, iwo anakhala alangizi ake, kumene kunali kudziwononga kwake.
And he did what is evil in the eyes of the Lord like the house of Achab; for these were his counsellors after the death of his father to his destruction.
5 Iyeyo anatsatiranso uphungu wawo pamene anapita ndi Yehoramu, mwana wa Ahabu, mfumu ya Israeli kukachita nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya Aramu ku Ramoti Giliyadi. Aaramu anavulaza Yehoramu,
He walked also after their counsel, and went with Jehoram the son of Achab the king of Israel to war against Chazael the king of Syria at Ramoth-gil'ad: and the Syrians smote Joram.
6 kotero iye anabwerera ku Yezireeli kuti akachire mabala amene anamuvulaza ku Ramoti pa nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya Aaramu. Ndipo Ahaziya, mwana wa Yehoramu mfumu ya Yuda anapita ku Yezireeli kukaona Yehoramu mwana wa Ahabu chifukwa anavulazidwa.
And he returned to be healed in Yizre'el because of the wounds which had been given him at Ramah, when he fought with Chazael the king of Syria. And 'Azaryahu the son of Jehoram the king of Judah went down to see Jehoram the son of Achab at Yizre'el, because he was sick.
7 Mulungu anakonza kuti Ahaziya akaphedwe pa ulendo wake wokacheza. Ahaziya atafika, iye ndi Yoramu anapita kukakumana ndi Yehu mwana wa Nimisi, amene Yehova anamudzoza kuti akawononge banja la Ahabu.
But from God was the confusion of Achazyahu that he should come to Joram: and when he was come, he went out with Jehoram against Jehu the son of Nimshi, whom the Lord had anointed to cut off the house of Achab.
8 Pamene Yehu ankalanga banja la Ahabu anapeza atsogoleri a ku Yuda ndiponso ana aamuna a abale ake a Ahaziya amene amatumikira Ahaziya, ndipo anawapha.
And it came to pass, when Jehu was executing judgment on the house of Achab, that he found the princes of Judah, and the sons of the brothers of Achazyahu, that ministered to Achazyahu, and he slew them.
9 Kenaka anapita kukafunafuna Ahaziya, ndipo anthu ake anagwira Ahaziya pamene amabisala mu Samariya. Anabwera naye kwa Yehu ndipo anaphedwa. Iwo anamuyika mʼmanda, pakuti anati, “Iyeyu anali mwana wa Yehosafati amene anafunafuna Yehova ndi mtima wake wonse.” Kotero panalibe wamphamvu mʼbanja la Ahaziya kuti nʼkukhala mfumu.
And he sought Achazyahu, and they caught him while he was hiding himself in Samaria, and they brought him to Jehu, and they slew him, and buried him; because they said, He is son of Jehoshaphat, who sought the Lord with all his heart. And there was none of the house of Achazyahu who had sufficient power [to obtain] the kingdom.
10 Ataliya, amayi ake a Ahaziya, ataona kuti mwana wawo wafa, ananyamuka nakapha onse a banja laufumu la Yuda.
And when 'Athalyahu the mother of Achazyahu saw that her son was dead, she arose and exterminated all the royal seed of the house of Judah.
11 Koma Yehoseba, mwana wamkazi wa mfumu Yehoramu, anatenga Yowasi mwana wa Ahaziya, momuba ndi kumuchotsa pakati pa ana aamuna a mfumu amene amati aphedwe ndipo anamuyika iye ndi mlezi wake mʼchipinda chogona. Motero Yehoseba, mwana wamkazi wa mfumu Yehoramu, mkazi wa wansembe Yehoyada, yemwe anali mlongo wake wa Ahaziya anamubisa mwanayo kuti Ataliya asamuphe.
But Yehoshab'ath, the daughter of the king, took Joash the son of Achazyahu, and stole him away from the midst of the king's sons that were slain, and put him and his nurse into the bed-chamber. So did Yehoshab'ath, the daughter of king Jehoram, the wife of Yehoyada' the priest, —for she was the sister of Achazyahu, —hide him from 'Athalyahu, so that she slew him not.
12 Mwanayo anakhala mobisala pamodzi ndi iwo mu Nyumba ya Mulungu kwa zaka zisanu ndi chimodzi muulamuliro wa Ataliya.
And he was with them in the house of God hidden six years, while 'Athalyah was reigning over the land.

< 2 Mbiri 22 >