< 2 Mbiri 22 >
1 Anthu a mu Yerusalemu anayika Ahaziya mwana wamngʼono kwambiri wa Yehoramu kukhala mfumu mʼmalo mwake, popeza gulu lankhondo limene linabwera ndi Aarabu ku misasa, linapha ana onse aakulu. Motero Ahaziya mwana wa Yehoramu mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
Derpå gjorde Jerusalems Indbyggere hans yngste Søn Ahazja til Konge i hans Sted, thi de ældre var dræbt af Røverskaren, der brød ind i Lejren sammen med Araberne. Således blev Ahazja, Jorams Søn, Konge i Juda.
2 Ahaziya anali wa zaka 22 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu chaka chimodzi. Dzina la amayi ake linali Ataliya, chidzukulu cha Omuri.
Ahazja var to og fyrretyve År gammel, da han blev Konge, og han herskede eet År i Jerusalem. Hans Moder hed Atalja og var Datter af Omri.
3 Nayenso anayenda mʼnjira ya banja la Ahabu, pakuti amayi ake anamulimbikitsa kuchita zolakwika.
Også han vandrede i Akabs Hus's Spor, thi hans Moder forledte ham til Ugudelighed ved sine Råd.
4 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga momwe banja la Ahabu linachitira, pakuti atamwalira abambo ake, iwo anakhala alangizi ake, kumene kunali kudziwononga kwake.
Han gjorde, hvad der var ondt i HERRENs Øjne, ligesom Akabs Hus, thi efter Faderens Død blev de hans Rådgivere, og det blev hans Fordærv.
5 Iyeyo anatsatiranso uphungu wawo pamene anapita ndi Yehoramu, mwana wa Ahabu, mfumu ya Israeli kukachita nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya Aramu ku Ramoti Giliyadi. Aaramu anavulaza Yehoramu,
Det var også efter deres Råd, han sammen med Akabs Søn, Kong Joram af Israel, drog i Krig mod Kong Hazael af Aram ved Ramot i Gilead. Men Aramæerne sårede Joram.
6 kotero iye anabwerera ku Yezireeli kuti akachire mabala amene anamuvulaza ku Ramoti pa nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya Aaramu. Ndipo Ahaziya, mwana wa Yehoramu mfumu ya Yuda anapita ku Yezireeli kukaona Yehoramu mwana wa Ahabu chifukwa anavulazidwa.
Så vendte Joram tilbage for i Jizre'el at søge Helbredelse for de Sår, man havde tilføjet ham ved Rama, da han kæmpede med Kong Hazael af Aram; og Jorams Søn, Kong Ahazja af Juda, drog ned for at se til Joram, Akabs Søn, i Jizre'el, fordi han lå syg.
7 Mulungu anakonza kuti Ahaziya akaphedwe pa ulendo wake wokacheza. Ahaziya atafika, iye ndi Yoramu anapita kukakumana ndi Yehu mwana wa Nimisi, amene Yehova anamudzoza kuti akawononge banja la Ahabu.
Men til Ahazjas Undergang var det tilskikket af Gud, at han skulde komme til Joram; thi da han var kommet derhen, gik han med Joram ud til Jehu, Nimsjis Søn, som HERREN havde salvet til at udrydde Akabs Hus.
8 Pamene Yehu ankalanga banja la Ahabu anapeza atsogoleri a ku Yuda ndiponso ana aamuna a abale ake a Ahaziya amene amatumikira Ahaziya, ndipo anawapha.
Og da Jehu fuldbyrdede Dommen over Akabs Hus, traf han på Judas Øverster og Ahazjas Brodersønner, der var i Ahazjas Tjeneste, og dræbte dem;
9 Kenaka anapita kukafunafuna Ahaziya, ndipo anthu ake anagwira Ahaziya pamene amabisala mu Samariya. Anabwera naye kwa Yehu ndipo anaphedwa. Iwo anamuyika mʼmanda, pakuti anati, “Iyeyu anali mwana wa Yehosafati amene anafunafuna Yehova ndi mtima wake wonse.” Kotero panalibe wamphamvu mʼbanja la Ahaziya kuti nʼkukhala mfumu.
derpå lod han Ahazja eftersøge, og man fangede ham, medens han holdt sig skjult i Samaria, ogbragte ham til Jehu, der lod ham dræbe. Så jordede de ham, thi de sagde: "Han var dog en Søn af Josafat, der søgte HERREN af hele sit Hjerte." Men af Ahazjas Hus var ingen stærk nok til at tage Magten.
10 Ataliya, amayi ake a Ahaziya, ataona kuti mwana wawo wafa, ananyamuka nakapha onse a banja laufumu la Yuda.
Da Atalja, Ahazjas Moder, fik at vide, at hendes Søn var død, tog hun sig for at udrydde hele den kongelige Slægt af Judas Hus.
11 Koma Yehoseba, mwana wamkazi wa mfumu Yehoramu, anatenga Yowasi mwana wa Ahaziya, momuba ndi kumuchotsa pakati pa ana aamuna a mfumu amene amati aphedwe ndipo anamuyika iye ndi mlezi wake mʼchipinda chogona. Motero Yehoseba, mwana wamkazi wa mfumu Yehoramu, mkazi wa wansembe Yehoyada, yemwe anali mlongo wake wa Ahaziya anamubisa mwanayo kuti Ataliya asamuphe.
Men Kongens Datter Josjab'at tog Ahazjas Søn Joas og fik ham hemmeligt af Vejen, så han ikke var imellem Kongesønnerne, der blev dræbt, og hun gemte ham og hans Amme i Sengekammeret. Således holdt Josjab'at, Kong Jorams Datter, Præsten Jojadas Hustru, der jo var Søster til Ahazja, ham skjult for Atalja, så hun ikke fik ham dræbt;
12 Mwanayo anakhala mobisala pamodzi ndi iwo mu Nyumba ya Mulungu kwa zaka zisanu ndi chimodzi muulamuliro wa Ataliya.
og han var i seks År skjult hos dem i HERRENs Hus, medens Atalja herskede i Landet.