< 2 Mbiri 21 >

1 Yehosafati anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide. Ndipo Yehoramu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Torej Józafat je zaspal s svojimi očeti in bil s svojimi očeti pokopan v Davidovem mestu. Namesto njega je zakraljeval njegov sin Jehorám.
2 Abale ake a Yehoramu, ana aamuna a Yehosafati, anali Azariya, Yehieli, Zekariya, Azariyahu, Mikayeli ndi Sefatiya. Onsewa anali ana a Yehosafati mfumu ya Israeli.
Ta je imel brate, Józafatove sinove: Azarjája, Jehiéla, Zeharjája, Azarjája, Mihaela in Šefatjája. Vsi ti so bili sinovi Izraelovega kralja Józafata.
3 Abambo awo anawapatsa mphatso zambiri za siliva, golide ndi zinthu zina zamtengowapatali komanso mizinda yotetezedwa ya Yuda. Koma iye anapereka ufumu kwa Yehoramu chifukwa anali mwana wake woyamba kubadwa.
Njihov oče jim je dal veliko daril iz srebra in iz zlata in dragocenih stvari, z utrjenimi mesti v Judu, toda kraljestvo je dal Jehorámu, ker je bil prvorojenec.
4 Yehoramu atakhazikika pa ufumu wa abambo ake, iye anapha abale ake ndi lupanga pamodzi ndi atsogoleri ena a Israeli.
Torej ko je bil Jehorám dvignjen h kraljestvu svojega očeta, se je okrepil in vse svoje brate usmrtil z mečem in tudi številne izmed Izraelovih princev.
5 Yehoramu anali wa zaka 32 pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka zisanu ndi zitatu.
Jehorám je bil star dvaintrideset let, ko je začel kraljevati in v Jeruzalemu je kraljeval osem let.
6 Iye anayenda mʼnjira za mafumu a Israeli, monga mmene linachitira banja la Ahabu, pakuti anakwatira mwana wa Ahabu. Ndipo anachita zoyipa pamaso pa Yehova.
Hodil je po poti Izraelovih kraljev, podobno kakor je storila Ahábova hiša, kajti za ženo je imel Ahábovo hčer. Počel je to, kar je bilo zlo v Gospodovih očeh.
7 Komabe, chifukwa cha pangano limene Yehova anachita ndi Davide, Yehova sanafune kuwononga banja la Davide. Iye analonjeza kusungira nyale Davide ndi zidzukulu zake mpaka muyaya.
Vendar Gospod ni hotel uničiti Davidove hiše zaradi zaveze, ki jo je sklenil z Davidom in kakor je obljubil, da da luč njemu in njegovim sinovom na veke.
8 Pa nthawi ya Yehoramu, Edomu anawukira Yuda ndipo anadzisankhira mfumu.
V njegovih dneh so se Edómci spuntali izpod Judovega gospostva in si postavili kralja.
9 Choncho Yehoramu anapita kumeneko pamodzi ndi atsogoleri ake ndi magaleta ake onse. Aedomu anamuzungulira pamodzi ndi atsogoleri ake koma iye ananyamuka ndi kuthawa usiku.
Potem je Jehorám s svojimi princi odšel naprej in vsi njegovi bojni vozovi z njim. Ponoči je vstal in udaril Edomce, ki so obkolili njega in stotnike bojnih vozov.
10 Mpaka lero lino Edomu ndi wowukira ulamuliro wa Yuda. Pa nthawi yomweyi, mzinda wa Libina unawukiranso chifukwa Yehoramu anasiya Yehova, Mulungu wa makolo ake.
Tako so se Edómci spuntali izpod Judove roke do današnjega dne. Isti čas se je tudi Libna spuntala izpod njegove roke, ker je zapustil Gospoda, Boga svojih očetov.
11 Iye anamanganso malo opembedzerapo mafano mʼmapiri a Yuda ndipo anachititsa anthu a mu Yerusalemu kukhala osakhulupirika. Choncho anasocheretsa anthu a ku Yuda.
Poleg tega je postavil visoke kraje po Judovih gorah in prebivalcem Jeruzalema storil, da zagrešijo prešuštvovanje in k temu zapeljal Juda.
12 Yehoramu analandira kalata yochokera kwa mneneri Eliya yonena kuti, “Yehova Mulungu wa Davide abambo ako akuti, ‘Iwe sunayende mʼnjira ya Yehosafati abambo ako kapena Asa mfumu ya Yuda.
In k njemu je prišlo pisanje preroka Elija, rekoč: ›Tako govori Gospod, Bog tvojega očeta Davida: ›Ker nisi hodil po poteh svojega očeta Józafata niti po poteh Judovega kralja Asája,
13 Koma wayenda mʼnjira za mafumu a Israeli ndipo watsogolera anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu kukhala osakhulupirika, monga linachitira banja la Ahabu. Waphanso abale ako, abale a banja la abambo ako, anthu amene anali abwino kuposa iweyo.
temveč si hodil po poti Izraelovih kraljev in si pripravil Juda in prebivalce Jeruzalema, da se vlačugajo, podobno vlačugarstvom Ahábove hiše in si tudi umoril svoje brate od hiše svojega očeta, ki so bili boljši kakor ti sam.
14 Kotero tsono Yehova ali pafupi kukantha anthu ako, ana ako, akazi ako ndi zinthu zako zonse, ndi chilango chachikulu.
Glej, z veliko nadlogo bo Gospod udaril tvoje ljudstvo, tvoje otroke, tvoje žene in vse tvoje dobrine,
15 Ndipo iwe udzadwala nthenda yoopsa yamʼmimba, mpaka nthendayo idzachititsa matumbo ako kutuluka.’”
ti pa boš imel veliko slabost z boleznijo svoje notranjosti, dokler tvoja notranjost ne zleze ven zaradi razloga bolezni dan za dnem.«
16 Yehova anamuutsira Yehoramuyo mkwiyo wa Afilisti ndi Aarabu amene amakhala pafupi ndi Akusi.
Poleg tega je Gospod zoper Jehoráma razvnel duha Filistejcev in Arabcev, ki so bili blizu Etiopijcev.
17 Iwo anathira nkhondo Yuda. Analowanso ndi kutenga katundu yense amene anamupeza mʼnyumba ya mfumu pamodzi ndi ana ake ndi akazi ake. Palibe mwana amene anatsala kupatula mwana wake wamngʼono kwambiri, Ahaziya.
Ti so prišli gor v Juda in vdrli vanj in odnesli vse imetje, ki je bilo najdeno v kraljevi hiši in tudi njegove sinove in njegove žene, tako da mu ni ostal sin razen Joaháza, najmlajšega izmed njegovih sinov.
18 Izi zonse zitachitika, Yehova anakantha Yehoramu ndi nthenda yamʼmimba imene inali yosachiritsika.
Po vsem tem ga je Gospod udaril v njegovi notranjosti z neozdravljivo boleznijo.
19 Patapita nthawi, kumapeto kwa chaka chachiwiri, matumbo ake anatuluka chifukwa cha nthendayo, ndipo anafa imfa yopweteka kwambiri. Anthu ake sanasonkhe moto kumuchitira ulemu, monga anachitira ndi makolo ake.
Pripetilo se je tekom časa, po koncu dveh let, da je njegova notranjost zlezla ven zaradi razloga njegove slabosti. Tako je umrl od hudih bolezni. Njegovo ljudstvo zanj ni naredilo nobenega sežiga [dišav], podobnega sežigu njegovim očetom.
20 Yehoramu anali wa zaka 32 pamene anakhala mfumu. Iyeyo analamulira mu Yerusalemu zaka zisanu ndi zitatu. Ndipo anamwalira popanda odandawula, nayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide, koma osati mʼmanda a mafumu.
Dvaintrideset let je bil star, ko je začel kraljevati in v Jeruzalemu je kraljeval osem let in odšel, brez da bi ga želeli. Vendar so ga pokopali v Davidovem mestu, toda ne v kraljevih mavzolejih.

< 2 Mbiri 21 >