< 2 Mbiri 21 >

1 Yehosafati anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide. Ndipo Yehoramu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Potom poèinu Josafat kod otaca svojih, i bi pogreben kod otaca svojih u gradu Davidovu; a na njegovo se mjesto zacari Joram sin njegov.
2 Abale ake a Yehoramu, ana aamuna a Yehosafati, anali Azariya, Yehieli, Zekariya, Azariyahu, Mikayeli ndi Sefatiya. Onsewa anali ana a Yehosafati mfumu ya Israeli.
A braæa mu, sinovi Josafatovi, bijahu: Azarija i Jehilo i Zaharija i Azarija i Mihailo i Sefatija; ti svi bijahu sinovi Josafata cara Izrailjeva.
3 Abambo awo anawapatsa mphatso zambiri za siliva, golide ndi zinthu zina zamtengowapatali komanso mizinda yotetezedwa ya Yuda. Koma iye anapereka ufumu kwa Yehoramu chifukwa anali mwana wake woyamba kubadwa.
I otac im dade velike darove, srebra i zlata i zaklada s tvrdijem gradovima u zemlji Judinoj; carstvo pak dade Joramu, jer bješe prvenac.
4 Yehoramu atakhazikika pa ufumu wa abambo ake, iye anapha abale ake ndi lupanga pamodzi ndi atsogoleri ena a Israeli.
A Joram stupiv na carstvo oca svojega i utvrdiv se, pobi svu braæu svoju maèem i neke knezove Izrailjeve.
5 Yehoramu anali wa zaka 32 pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka zisanu ndi zitatu.
Imaše Joram trideset i dvije godine kad se zacari, i carova osam godina u Jerusalimu.
6 Iye anayenda mʼnjira za mafumu a Israeli, monga mmene linachitira banja la Ahabu, pakuti anakwatira mwana wa Ahabu. Ndipo anachita zoyipa pamaso pa Yehova.
I hoðaše putem careva Izrailjevijeh, kao što èinjaše dom Ahavov, jer se oženi kæerju Ahavovom; i èinjaše što je zlo pred Gospodom.
7 Komabe, chifukwa cha pangano limene Yehova anachita ndi Davide, Yehova sanafune kuwononga banja la Davide. Iye analonjeza kusungira nyale Davide ndi zidzukulu zake mpaka muyaya.
Ali Gospod ne htje zatrti doma Davidova radi zavjeta koji uèini s Davidom i što mu bješe rekao da æe dati vidjelo njemu i sinovima njegovijem uvijek.
8 Pa nthawi ya Yehoramu, Edomu anawukira Yuda ndipo anadzisankhira mfumu.
Za njegova vremena odvrže se Edom da ne bude pod Judom, i postaviše sebi cara.
9 Choncho Yehoramu anapita kumeneko pamodzi ndi atsogoleri ake ndi magaleta ake onse. Aedomu anamuzungulira pamodzi ndi atsogoleri ake koma iye ananyamuka ndi kuthawa usiku.
Zato otide Joram s vojvodama svojim i sa svijem kolima svojim; i usta noæu, te pobi Edomce koji ga bijahu opkolili, i zapovjednike od kola.
10 Mpaka lero lino Edomu ndi wowukira ulamuliro wa Yuda. Pa nthawi yomweyi, mzinda wa Libina unawukiranso chifukwa Yehoramu anasiya Yehova, Mulungu wa makolo ake.
Ipak se odvrgoše Edomci da ne budu pod Judom do danas. U isto vrijeme odvrže se i Livna da ne bude pod njim, jer ostavi Gospoda Boga otaca svojih.
11 Iye anamanganso malo opembedzerapo mafano mʼmapiri a Yuda ndipo anachititsa anthu a mu Yerusalemu kukhala osakhulupirika. Choncho anasocheretsa anthu a ku Yuda.
Još i visine naèini po brdima Judinijem, i navede na preljubu Jerusalimljane i prelasti Judu.
12 Yehoramu analandira kalata yochokera kwa mneneri Eliya yonena kuti, “Yehova Mulungu wa Davide abambo ako akuti, ‘Iwe sunayende mʼnjira ya Yehosafati abambo ako kapena Asa mfumu ya Yuda.
Tada mu doðe knjiga od Ilije proroka, gdje mu govoraše: ovako veli Gospod Bog Davida oca tvojega: što nijesi hodio putovima Josafata oca svojega i putovima Ase cara Judina,
13 Koma wayenda mʼnjira za mafumu a Israeli ndipo watsogolera anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu kukhala osakhulupirika, monga linachitira banja la Ahabu. Waphanso abale ako, abale a banja la abambo ako, anthu amene anali abwino kuposa iweyo.
Nego si hodio putem careva Izrailjevijeh i naveo si na preljubu Judu i Jerusalimljane, kao što je dom Ahavov naveo na preljubu Izrailja, i još si pobio braæu svoju, dom oca svojega, bolje od sebe,
14 Kotero tsono Yehova ali pafupi kukantha anthu ako, ana ako, akazi ako ndi zinthu zako zonse, ndi chilango chachikulu.
Evo, Gospod æe udariti velikim zlom narod tvoj i sinove tvoje i žene tvoje i sve što imaš.
15 Ndipo iwe udzadwala nthenda yoopsa yamʼmimba, mpaka nthendayo idzachititsa matumbo ako kutuluka.’”
I ti æeš bolovati teško, od bolesti u crijevima, da æe ti crijeva izaæi od bolesti, koja æe trajati dvije godine.
16 Yehova anamuutsira Yehoramuyo mkwiyo wa Afilisti ndi Aarabu amene amakhala pafupi ndi Akusi.
I tako podiže Gospod na Jorama duh Filistejima i Arapima koji žive od Etiopljana.
17 Iwo anathira nkhondo Yuda. Analowanso ndi kutenga katundu yense amene anamupeza mʼnyumba ya mfumu pamodzi ndi ana ake ndi akazi ake. Palibe mwana amene anatsala kupatula mwana wake wamngʼono kwambiri, Ahaziya.
I oni došavši na zemlju Judinu prodriješe u nju, i odnesoše sve blago što se naðe u domu carevu, i sinove njegove i žene njegove, da mu ne osta nijedan sin osim Joahaza najmlaðega sina njegova.
18 Izi zonse zitachitika, Yehova anakantha Yehoramu ndi nthenda yamʼmimba imene inali yosachiritsika.
I poslije svega toga udari ga Gospod bolešæu u crijevima, kojoj ne bješe lijeka.
19 Patapita nthawi, kumapeto kwa chaka chachiwiri, matumbo ake anatuluka chifukwa cha nthendayo, ndipo anafa imfa yopweteka kwambiri. Anthu ake sanasonkhe moto kumuchitira ulemu, monga anachitira ndi makolo ake.
I dan po dan prolažaše, i kad se navršiše dvije godine, izidoše mu crijeva s bolešæu i umrije od teških bolova, i narod mu ne pali mirisa kao što je èinio ocima njegovijem.
20 Yehoramu anali wa zaka 32 pamene anakhala mfumu. Iyeyo analamulira mu Yerusalemu zaka zisanu ndi zitatu. Ndipo anamwalira popanda odandawula, nayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide, koma osati mʼmanda a mafumu.
Imaše trideset i dvije godine kad poèe carovati, i carova osam godina u Jerusalimu, i preminu da niko ne zažali za njim; i pogreboše ga u gradu Davidovu, ali ne u grobu carskom.

< 2 Mbiri 21 >