< 2 Mbiri 21 >
1 Yehosafati anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide. Ndipo Yehoramu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
And Jehoshaphat lieth with his fathers, and is buried with his fathers in the city of David, and Jehoram his son reigneth in his stead.
2 Abale ake a Yehoramu, ana aamuna a Yehosafati, anali Azariya, Yehieli, Zekariya, Azariyahu, Mikayeli ndi Sefatiya. Onsewa anali ana a Yehosafati mfumu ya Israeli.
And he hath brethren, sons of Jehoshaphat, Azariah, and Jehiel, and Zechariah, and Azariah, and Michael, and Shephatiah; all these [are] sons of Jehoshaphat king of Israel,
3 Abambo awo anawapatsa mphatso zambiri za siliva, golide ndi zinthu zina zamtengowapatali komanso mizinda yotetezedwa ya Yuda. Koma iye anapereka ufumu kwa Yehoramu chifukwa anali mwana wake woyamba kubadwa.
and their father giveth to them many gifts of silver and of gold, and of precious things, with fenced cities in Judah, and the kingdom he hath given to Jehoram, for He [is] the first-born.
4 Yehoramu atakhazikika pa ufumu wa abambo ake, iye anapha abale ake ndi lupanga pamodzi ndi atsogoleri ena a Israeli.
And Jehoram riseth up over the kingdom of his father, and strengtheneth himself, and slayeth all his brethren with the sword, and also — of the heads of Israel.
5 Yehoramu anali wa zaka 32 pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka zisanu ndi zitatu.
A son of thirty and two years [is] Jehoram in his reigning, and eight years he hath reigned in Jerusalem,
6 Iye anayenda mʼnjira za mafumu a Israeli, monga mmene linachitira banja la Ahabu, pakuti anakwatira mwana wa Ahabu. Ndipo anachita zoyipa pamaso pa Yehova.
and he walketh in the way of the kings of Israel, as did the house of Ahab, for a daughter of Ahab hath been to him for a wife, and he doth the evil thing in the eyes of Jehovah,
7 Komabe, chifukwa cha pangano limene Yehova anachita ndi Davide, Yehova sanafune kuwononga banja la Davide. Iye analonjeza kusungira nyale Davide ndi zidzukulu zake mpaka muyaya.
and Jehovah hath not been willing to destroy the house of David, for the sake of the covenant that He made with David, and as He had said to give to him a lamp, and to his sons — all the days.
8 Pa nthawi ya Yehoramu, Edomu anawukira Yuda ndipo anadzisankhira mfumu.
In his days hath Edom revolted from under the hand of Judah, and cause a king to reign over them;
9 Choncho Yehoramu anapita kumeneko pamodzi ndi atsogoleri ake ndi magaleta ake onse. Aedomu anamuzungulira pamodzi ndi atsogoleri ake koma iye ananyamuka ndi kuthawa usiku.
and Jehoram passeth over with his heads, and all the chariots with him, and it cometh to pass, he hath risen by night and smiteth the Edomites who are coming round against him, and the princes of the chariots,
10 Mpaka lero lino Edomu ndi wowukira ulamuliro wa Yuda. Pa nthawi yomweyi, mzinda wa Libina unawukiranso chifukwa Yehoramu anasiya Yehova, Mulungu wa makolo ake.
and Edom revolteth from under the hand of Judah unto this day; then doth Libnah revolt at that time from under his hand, because he hath forsaken Jehovah, God of his fathers,
11 Iye anamanganso malo opembedzerapo mafano mʼmapiri a Yuda ndipo anachititsa anthu a mu Yerusalemu kukhala osakhulupirika. Choncho anasocheretsa anthu a ku Yuda.
also, he hath made high places in the mountains of Judah, and causeth the inhabitants of Jerusalem to commit whoredom, and compelleth Judah.
12 Yehoramu analandira kalata yochokera kwa mneneri Eliya yonena kuti, “Yehova Mulungu wa Davide abambo ako akuti, ‘Iwe sunayende mʼnjira ya Yehosafati abambo ako kapena Asa mfumu ya Yuda.
And there cometh in unto him a writing from Elijah the prophet, saying, 'Thus said Jehovah, God of David thy father, Because that thou hast not walked in the ways of Jehoshaphat thy father, and in the ways of Asa king of Judah,
13 Koma wayenda mʼnjira za mafumu a Israeli ndipo watsogolera anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu kukhala osakhulupirika, monga linachitira banja la Ahabu. Waphanso abale ako, abale a banja la abambo ako, anthu amene anali abwino kuposa iweyo.
and thou dost walk in the way of the kings of Israel, and dost cause Judah and the inhabitants of Jerusalem to commit whoredom like the whoredoms of the house of Ahab, and also thy brethren, the house of thy father, who are better than thyself, thou hast slain;
14 Kotero tsono Yehova ali pafupi kukantha anthu ako, ana ako, akazi ako ndi zinthu zako zonse, ndi chilango chachikulu.
lo, Jehovah is smiting — a great smiting — among thy people, and among thy sons, and among thy wives, and among all thy goods —
15 Ndipo iwe udzadwala nthenda yoopsa yamʼmimba, mpaka nthendayo idzachititsa matumbo ako kutuluka.’”
and thou, with many sicknesses, with disease of thy bowels, till thy bowels come out, by the sickness, day by day.'
16 Yehova anamuutsira Yehoramuyo mkwiyo wa Afilisti ndi Aarabu amene amakhala pafupi ndi Akusi.
And Jehovah waketh up against Jehoram the spirit of the Philistines, and of the Arabians, who [are] beside the Cushim,
17 Iwo anathira nkhondo Yuda. Analowanso ndi kutenga katundu yense amene anamupeza mʼnyumba ya mfumu pamodzi ndi ana ake ndi akazi ake. Palibe mwana amene anatsala kupatula mwana wake wamngʼono kwambiri, Ahaziya.
and they come up into Judah, and rend it, and take captive all the substance that is found at the house of the king, and also his sons, and his wives, and there hath not been left to him a son except Jehoahaz the youngest of his sons.
18 Izi zonse zitachitika, Yehova anakantha Yehoramu ndi nthenda yamʼmimba imene inali yosachiritsika.
And after all this hath Jehovah plagued him in his bowels by a disease for which there is no healing,
19 Patapita nthawi, kumapeto kwa chaka chachiwiri, matumbo ake anatuluka chifukwa cha nthendayo, ndipo anafa imfa yopweteka kwambiri. Anthu ake sanasonkhe moto kumuchitira ulemu, monga anachitira ndi makolo ake.
and it cometh to pass, from days to days, and at the time of the going out of the end of two years, his bowels have gone out with his sickness, and he dieth of sore diseases, and his people have not made for him a burning like the burning of his fathers.
20 Yehoramu anali wa zaka 32 pamene anakhala mfumu. Iyeyo analamulira mu Yerusalemu zaka zisanu ndi zitatu. Ndipo anamwalira popanda odandawula, nayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide, koma osati mʼmanda a mafumu.
A son of thirty and two [years] was he in his reigning, and eight years he hath reigned in Jerusalem, and he goeth without desire, and they bury him in the city of David, and not in the graves of the kings.