< 2 Mbiri 20 >

1 Zitatha izi, Amowabu ndi Aamoni pamodzi ndi Ameuni ena anabwera kudzachita nkhondo ndi Yehosafati.
Nogen tid efter hendte det at Moabs barn og Ammons barn og sammen med dem en del av me'unittene gjorde et krigstog mot Josafat.
2 Anthu ena anabwera kudzamuwuza Yehosafati kuti, “Gulu lalikulu kwambiri lankhondo likubwera kudzachita nanu nkhondo lochokera ku Edomu, ku mbali ina ya Nyanja. Gululi lafika kale ku Hazazoni Tamara” (ndiye kuti Eni-Gedi).
Folk kom med tidende derom til Josafat og sa: Det kommer en stor hær imot dig fra hin side havet, fra Syria; de er allerede i Haseson-Tamar, det er En-Gedi.
3 Ndi mantha, Yehosafati anaganiza zofunsira kwa Yehova, ndipo analengeza kuti Ayuda onse asale zakudya.
Da blev Josafat redd, og han v endte sig i bønn til Herren og lot utrope en faste over hele Juda.
4 Anthu a ku Yuda anabwera pamodzi kudzafuna thandizo kwa Yehova, ndipo anabweradi kuchokera ku mzinda uliwonse wa mu Yuda kudzafunafuna Yehova.
Og Juda samlet sig for å søke hjelp hos Herren; ja, fra alle Judas byer kom de for å søke Herren.
5 Yehosafati anayimirira pakati pa msonkhano wa Yuda ndi Yerusalemu, pa Nyumba ya Yehova patsogolo pa bwalo latsopano
Da stod Josafat frem blandt dem som var kommet sammen fra Juda og Jerusalem, i Herrens hus foran den nye forgård
6 ndipo anati: “Inu Yehova, Mulungu wa makolo athu, kodi Inu sindinu Mulungu amene muli kumwamba? Inu mumalamulira maufumu onse a mitundu ya anthu. Mphamvu ndi nyonga zili mʼmanja mwanu, ndipo palibe amene angalimbane nanu.
og sa: Herre, våre fedres Gud! Er det ikke du som er Gud i himmelen? Du råder over alle folkenes riker; i din hånd er kraft og velde, og det er ingen som kan holde stand mot dig.
7 Inu Mulungu wathu, kodi simunathamangitse nzika za dziko lino pamaso pa anthu anu Aisraeli ndipo munalipereka kwa zidzukulu za Abrahamu bwenzi lanu kwamuyaya?
Har ikke du, vår Gud, drevet dette lands innbyggere ut for ditt folk Israel og gitt det til din venn Abrahams efterkommere for alle tider?
8 Iwo akhala mʼdzikolo ndipo anamangira Dzina lanu malo opatulika, nʼkumati,
De bosatte sig der og bygget dig der en helligdom for ditt navn og sa:
9 ‘Ngati tsoka litigwera kaya ndi lupanga lachiweruzo, kapena mliri, kapenanso njala, ife tidzayima pamaso panu patsogolo pa Nyumba ya Mulungu ino imene imatchedwa ndi Dzina lanu ndipo tidzalirira kwa inu mʼmasautso athu, ndipo Inu mudzatimvera ndi kutipulumutsa.’
Om nogen ulykke kommer over oss, sverd, straffedom, pest eller hungersnød, så vil vi stille oss foran dette hus og for ditt åsyn, for ditt navn bor i dette hus, og vi vil rope til dig i vår trengsel, og du vil høre og frelse.
10 “Koma tsopano pano pali anthu ochokera ku Amoni, Mowabu ndi Phiri la Seiri amene dziko lawo Inu simunawalole Aisraeli kuti alithire nkhondo pamene amabwera kuchokera ku Igupto. Kotero anatembenuka ndi kuwaleka ndipo sanawawononge.
Se nu hvorledes Ammons barn og Moab og folket fra Se'ir-fjellet - disse folk som du ikke gav Israel lov til å trenge inn iblandt da de kom fra Egyptens land, så de bøide av og drog bort fra dem og ikke ødela dem -
11 Taonani, mmene akutibwezera ife pobwera kudzatithamangitsa mʼdziko limene inu munatipatsa ngati cholowa chathu.
se hvorledes de lønner oss! Nu kommer de og vil drive oss ut av din eiendom, som du har gitt oss i eie.
12 Inu Mulungu wathu, kodi simuwaweruza? Pakuti ife tilibe mphamvu zolimbana ndi gulu lalikulu lankhondo limene likutithira nkhondoli. Ife sitikudziwa choti tichite, koma maso athu ali pa Inu.”
Vår Gud! Vil du ikke holde dom over dem? For vi har ikke kraft nok til å motstå denne store hær som kommer imot oss, og vi vet ikke hvad vi skal gjøre; men til dig er våre øine vendt.
13 Anthu onse a Yuda, pamodzi ndi akazi awo ndi ana ndi makanda, anayima chilili pamaso pa Yehova.
Og hele Juda stod der for Herrens åsyn, endog deres små barn, deres hustruer og deres sønner.
14 Ndipo Mzimu wa Yehova unabwera pa Yahazieli mwana wa Zekariya, mwana wa Benaya, mwana wa Yeiyeli, mwana wa Mataniya Mlevi, chidzukulu cha Asafu, atayimirira mu msonkhano.
Da kom Herrens Ånd midt i forsamlingen over levitten Jahasiel, sønn av Sakarja, sønn av Benaja, sønn av Je'iel, sønn av Mattanja, en av Asafs sønner,
15 Iye anati, “Tamverani mfumu Yehosafati ndi onse amene amakhala mu Yuda ndi Yerusalemu! Zimene Yehova akunena kwa inu ndi izi: ‘Musaope kapena kutaya mtima chifukwa cha gulu lalikulu lankhondo ili. Pakuti nkhondoyi si yanu, koma ya Mulungu.
Og han sa: Hør efter, hele Juda og I Jerusalems innbyggere og du kong Josafat! Så sier Herren til eder: Frykt ikke og reddes ikke for denne store hær! For dette er ikke eders krig, men Guds.
16 Mawa mupite mukamenyane nawo. Adzakhala akubwera mokweza kudzera Njira ya Zizi, ndipo mukawapeza kumapeto kwa chigwa cha ku chipululu cha Yeruweli.
Dra ned mot dem imorgen! Da drar de opefter Hassis-bakken, Og I kommer til å møte dem ved enden av dalen midt imot Jeruelørkenen.
17 Sikudzafunika kuti Inu mumenyane nawo pa nkhondo imeneyi. Inu mukhale pa malo anu; imani molimba ndipo onani chipulumutso chimene Yehova adzakupatsani, Inu Yuda ndi Yerusalemu. Musaope, musataye mtima. Pitani kuti mukakumane nawo mawa, ndipo Yehova adzakhala nanu.’”
Men det er ikke I som skal stride her; I skal bare stille eder op og stå og se på hvorledes Herren frelser eder, I fra Juda og Jerusalem! Frykt ikke og reddes ikke! Dra ut imot dem imorgen, og Herren skal være med eder.
18 Yehosafati anaweramitsa nkhope yake ndi kugunda pansi, ndiponso anthu onse a Yuda ndi Yerusalemu anagwa pansi ndi kulambira Yehova.
Da bøide Josafat sig med ansiktet til jorden, og hele Juda og alle Jerusalems innbyggere falt ned for Herrens åsyn og tilbad Herren.
19 Kenaka Alevi ena ochokera ku mabanja a Kohati ndi Kora anayimirira ndipo anatamanda Yehova Mulungu wa Israeli ndi mawu ofuwula kwambiri.
Og de levitter som hørte til kahatittenes og korahittenes barn, reiste sig og lovet Herren, Israels Gud, med høi og lydelig røst.
20 Mmamawa, ananyamuka kupita ku chipululu cha Tekowa. Akunyamuka, Yehosafati anayimirira ndipo anati, “Tandimverani ine anthu a Yuda ndi Yerusalemu! Khalani ndi chikhulupiriro mwa Yehova Mulungu wanu ndipo mudzatchinjirizidwa, khalani ndi chikhulupiriro mwa aneneri ake ndipo mudzapambana.”
Morgenen efter tok de tidlig ut og drog avsted til Tekoa-ørkenen; og med det samme de drog ut, stod Josafat frem og sa: Hør på mig, Juda og I Jerusalems innbyggere! Tro på Herren eders Gud, så skal I holde stand! Tro på hans profeter, så skal I ha lykke med eder!
21 Atafunsira kwa anthu, Yehosafati anasankha anthu oti ayimbire Yehova ndi kumutamanda chifukwa cha ulemerero wa chiyero chake pamene amapita ali patsogolo pa gulu la ankhondo, akunena kuti: “Yamikani Yehova pakuti chikondi chake ndi chosatha.”
Og han rådførte sig med folket og stilte op sangere som skulde love Herren i hellig skrud mens de drog ut foran den væbnede hær, og si: Lov Herren, for hans miskunnhet varer evindelig!
22 Atangoyamba kuyimba ndi kutamanda, Yehova anapereka mʼmanja mwawo anthu a ku Amoni ndi a ku Mowabu ndiponso a ku Phiri la Seiri amene amalimbana ndi Yuda, ndipo anagonjetsedwa.
Og straks de begynte med sine fryderop og lovsanger, lot Herren en flokk bakfra komme over Ammons barn, Moab og folket fra Se'ir-fjellet, som var kommet mot Juda, og de blev slått.
23 Anthu a ku Amoni ndi a ku Mowabu anawukira anthu ochokera ku Phiri la Seiri, ndipo anawawononga ndi kuwatheratu. Atatsiriza kuwapha anthu ochokera ku Seiri anamenyana wina ndi mnzake mpaka kuwonongana.
Og Ammons barn og Moab vendte sig mot folket fra Se'ir-fjellet og hugg dem ned og ødela dem; og da de hadde gjort ende på folket fra Se'ir, hjalp de hverandre med innbyrdes ødeleggelse.
24 Anthu a ku Yuda atafika pa malo oyangʼanana ndi chipululu ndi kuona kumene kunali gulu lalikulu lankhondo, iwo anangoona mitembo yokhayokha itagona pansi ndipo palibe amene anathawa.
Da Juda kom op på høiden hvorfra en kunde se ut over ørkenen, og så sig om efter hæren, fikk de se dem ligge døde på jorden, og ingen var sloppet unda.
25 Choncho Yehosafati ndi anthu ake anapita kukafunkha, ndipo pakati pawo anapeza katundu wambiri ndi zovala ndiponso zinthu zina zamtengowapatali kuposa zomwe akanatha kunyamula. Kunali katundu wambiri kotero kuti zinawatengera masiku atatu kuti amutenge.
Josafat og hans folk drog dit for å plyndre, og de fant der både gods og døde kropper og kostbare ting i mengde, og det hærfang de tok, var så stort at de ikke kunde bære det; i tre dager holdt de på med å plyndre, så meget hærfang var det.
26 Tsiku lachinayi anasonkhana ku chigwa cha Beraka kumene anatamanda Yehova. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa chigwa cha Beraka mpaka lero.
Den fjerde dag samlet de sig i Lovprisnings-dalen. Der lovet de Herren; derfor heter dette sted Lovprisnings-dalen den dag idag.
27 Tsono motsogozedwa ndi Yehosafati, anthu onse a Yuda ndi Yerusalemu anabwerera ku Yerusalemu mokondwera pakuti Yehova anawagonjetsera adani awo.
Så vendte alle Judas og Jerusalems menn om med Josafat foran og drog glade tilbake til Jerusalem; for Herren hadde unt dem den glede å vinne over sine fiender.
28 Iwo analowa mu Yerusalemu ndipo anapita ku Nyumba ya Mulungu akuyimba azeze, apangwe ndi malipenga.
De drog inn i Jerusalem til Herrens hus med harper og citarer og trompeter.
29 Kuopsa kwa Mulungu kunali pa maufumu onse a mayiko amene anamva mmene Yehova anamenyera adani a Aisraeli.
Og frykt for Gud kom over alle riker rundt i landene, da de hørte at Herren hadde stridt mot Israels fiender.
30 Ndipo ufumu wa Yehosafati unali pa mtendere pakuti Mulungu wake anamupatsa mpumulo ku mbali zonse.
Og Josafats rike hadde nu fred, fordi hans Gud lot ham få ro på alle kanter.
31 Choncho Yehosafati analamulira Yuda. Iye anali wa zaka 35 pamene anakhala mfumu ya Yuda ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 25. Dzina la amayi ake linali Azuba mwana wa Sili.
Således regjerte Josafat over Juda. Han var fem og tretti år gammel da han blev konge, og regjerte fem og tyve år i Jerusalem. Hans mor hette Asuba og var datter av Silhi.
32 Iye ankayenda mʼnjira za Asa abambo ake ndipo sanapatuke pa zimenezi pakuti anachita zolungama pamaso pa Yehova.
Han vandret på sin far Asas vei og vek ikke fra den, men gjorde hvad rett var i Herrens øine.
33 Komabe malo opembedzerapo mafano sanachotsedwe ndipo anthu sanaperekebe mitima yawo kwa Mulungu wa makolo awo.
Dog blev offerhaugene ikke nedlagt, og folket hadde ennu ikke vendt sitt hjerte til sine fedres Gud.
34 Zochitika zina zokhudza ufumu wa Yehosafati, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la Yehu mwana wa Hanani, zomwe zikupezeka mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
Hvad som ellers er å fortelle om Josafat, både i hans første og i hans senere dager, det er opskrevet i Jehus, Hananis sønns krønike, som er optatt i boken om Israels konger.
35 Zitapita izi, Yehosafati mfumu ya Yuda inachita mgwirizano ndi Ahaziya mfumu ya Israeli, amene anachita zoyipa kwambiri.
Siden inngikk Josafat, Judas konge, en overenskomst med Akasja, Israels konge, han som bar sig så ugudelig at.
36 Iye anagwirizana ndi Ahaziya kuti apange sitima zapamadzi zochitira malonda. Atazipanga zimenezi ku Ezioni-Geberi,
Han kom overens med ham om å bygge skiber som skulde gå til Tarsis; og de bygget skiber i Esjon-Geber.
37 Eliezara mwana wa Dodavahu wa ku Maresa ananenera motsutsana ndi Yehosafati ndipo anati, “Chifukwa chakuti wachita mgwirizano ndi Ahaziya, Yehova adzawononga zimene mwapangazo!” Sitima za pamadzizo zinawonongeka ndipo sizinapite nʼkomwe kumene zimakachita malonda.
Da spådde Elieser, Dodavas sønn, fra Maresa, mot Josafat og sa: Fordi du har inngått forbund med Akasja, skal Herren la ditt foretagende bli til intet. Og nogen av skibene forliste, så de ikke kunde gå til Tarsis.

< 2 Mbiri 20 >