< 2 Mbiri 20 >

1 Zitatha izi, Amowabu ndi Aamoni pamodzi ndi Ameuni ena anabwera kudzachita nkhondo ndi Yehosafati.
Añe izay, le nimb’eo hihotakotak’ am’Iehosafate o ana’ i Moabeo naho o ana’ i Amoneo, mitraok’ ami’ty ondaty ila’e.
2 Anthu ena anabwera kudzamuwuza Yehosafati kuti, “Gulu lalikulu kwambiri lankhondo likubwera kudzachita nanu nkhondo lochokera ku Edomu, ku mbali ina ya Nyanja. Gululi lafika kale ku Hazazoni Tamara” (ndiye kuti Eni-Gedi).
Le pok’ eo ty nitalily am’ Iehosafate ty hoe: Fa mb’atoa ty valobohòke boak’ alafe’ i riakey hirik’ Arame añe; le inao fa e Katsetsone-tamare iereo, e En-gedý ey henaneo.
3 Ndi mantha, Yehosafati anaganiza zofunsira kwa Yehova, ndipo analengeza kuti Ayuda onse asale zakudya.
Nihembañe amy zao t’Iehosafate, le nifahara’e tsoeke t’Iehovà vaho nanitsike Iehodà nitsèy lilitse.
4 Anthu a ku Yuda anabwera pamodzi kudzafuna thandizo kwa Yehova, ndipo anabweradi kuchokera ku mzinda uliwonse wa mu Yuda kudzafunafuna Yehova.
Nifanontoñe amy zao t’Iehoda, nipay imba am’ Iehovà; le boak’ amy ze hene rova’ Iehoda ty nivoria’ iareo hitsoeke Iehovà.
5 Yehosafati anayimirira pakati pa msonkhano wa Yuda ndi Yerusalemu, pa Nyumba ya Yehova patsogolo pa bwalo latsopano
Nijohañe amy fivori’ Iehoda naho Ierosalaimey t’Iehosafate, añ’ anjomba’ Iehovà aolo’ i kiririsa vaoy;
6 ndipo anati: “Inu Yehova, Mulungu wa makolo athu, kodi Inu sindinu Mulungu amene muli kumwamba? Inu mumalamulira maufumu onse a mitundu ya anthu. Mphamvu ndi nyonga zili mʼmanja mwanu, ndipo palibe amene angalimbane nanu.
nanao ty hoe; Ry Iehovà Andrianañaharen-droae’ay, tsy Ihe hao t’i Andrianañahare andindimoneñe ao? Tsy Ihe hao ty Mpifehe ze fonga fifehea’ o kilakila’ ondatio? Le am-pità’o ty hafatra­rañe naho ty haozarañe vaho tsy eo ty hahafitroatse ama’o.
7 Inu Mulungu wathu, kodi simunathamangitse nzika za dziko lino pamaso pa anthu anu Aisraeli ndipo munalipereka kwa zidzukulu za Abrahamu bwenzi lanu kwamuyaya?
Tsy Ihe hao, ry Andrianañahare’ay, ty nandroake o mpimoneñe an-tane atoio aolo’ ondati’o Israeleo vaho natolo’o amo tiri’ i Avrahame rañe’oo ho nainai’e donia?
8 Iwo akhala mʼdzikolo ndipo anamangira Dzina lanu malo opatulika, nʼkumati,
Aa le nimoneñe ao iereo vaho nandranjy toe-masiñe ho amy tahina’oy ami’ty hoe:
9 ‘Ngati tsoka litigwera kaya ndi lupanga lachiweruzo, kapena mliri, kapenanso njala, ife tidzayima pamaso panu patsogolo pa Nyumba ya Mulungu ino imene imatchedwa ndi Dzina lanu ndipo tidzalirira kwa inu mʼmasautso athu, ndipo Inu mudzatimvera ndi kutipulumutsa.’
Ie mifetsak’ ama’ay ty hankàñe, i fibaray, i zakay, ke angorosy, he hasalikoañe, le hijohañe añatrefa’ ty anjomba toy naho aolo’o eo zahay (amy te añ’anjomba atoy ty tahina’o) naho itoreova’ay ty haembera’aiy, le hijanjin-dRehe vaho handrombake.
10 “Koma tsopano pano pali anthu ochokera ku Amoni, Mowabu ndi Phiri la Seiri amene dziko lawo Inu simunawalole Aisraeli kuti alithire nkhondo pamene amabwera kuchokera ku Igupto. Kotero anatembenuka ndi kuwaleka ndipo sanawawononge.
Ie amy zao, vazohò o ana’ i Amoneo naho i Moabeo vaho i Vohi-Seirey, ie tsy nado’o ho tamè’ Israele niavotse an-tane Mitsraime añe, naho niary tsy nirotsa­heñe;
11 Taonani, mmene akutibwezera ife pobwera kudzatithamangitsa mʼdziko limene inu munatipatsa ngati cholowa chathu.
hehe ty atolo’ iareo ama’ay henaneo, ie mb’ etoa hañary anay amy fanaña’o natolo’o anay ho lovay.
12 Inu Mulungu wathu, kodi simuwaweruza? Pakuti ife tilibe mphamvu zolimbana ndi gulu lalikulu lankhondo limene likutithira nkhondoli. Ife sitikudziwa choti tichite, koma maso athu ali pa Inu.”
Ry Andria­nañahare’ay, Tsy Ihe hao ty hametsa-jaka am’ iereo? tsy ama’ay ty hafatrarañe hahafitroatse amo valobohòke jabajaba mb’ etoañe hiatreatre ama’aio, vaho tsy hai’ay ty hanoeñe, fe ama’o o fihaino’aio.
13 Anthu onse a Yuda, pamodzi ndi akazi awo ndi ana ndi makanda, anayima chilili pamaso pa Yehova.
Le fonga nijohañe añatrefa’ Iehovà t’Iehodà naho o keleia’eo, o vali’eo vaho o amori’eo.
14 Ndipo Mzimu wa Yehova unabwera pa Yahazieli mwana wa Zekariya, mwana wa Benaya, mwana wa Yeiyeli, mwana wa Mataniya Mlevi, chidzukulu cha Asafu, atayimirira mu msonkhano.
Aa le nivotrak’ am’ Iakaziele, ana’ i Zekarià, ana’ i Benaià, ana’ Ieiele, ana’ i Matanià nte-Levy amo ana’ i Asafeo, ty Arofo’ Iehovà añivo’ i fivoriy;
15 Iye anati, “Tamverani mfumu Yehosafati ndi onse amene amakhala mu Yuda ndi Yerusalemu! Zimene Yehova akunena kwa inu ndi izi: ‘Musaope kapena kutaya mtima chifukwa cha gulu lalikulu lankhondo ili. Pakuti nkhondoyi si yanu, koma ya Mulungu.
le hoe re: Mijanjiña, ry Iehoda naho o mpimone’ Ierosalaimeo naho ry Iehosafate mpanjaka; Hoe ty nafè’ Iehovà ama’ areo: Ko hembañe, ko miroreke ty amy valobohòke ra’e­lahiy; toe tsy anahareo i hotakotakey, fa an’ Andrianañahare.
16 Mawa mupite mukamenyane nawo. Adzakhala akubwera mokweza kudzera Njira ya Zizi, ndipo mukawapeza kumapeto kwa chigwa cha ku chipululu cha Yeruweli.
Mizotsoa mb’am’ iereo mb’eo hamaray; Inao! hionjomb’ am-pitroara’ i Zize iereo, le ho tendrek’ama’ areo amy figadoña’ i vavataney, aolo’ i fatrambei’ Ieroeley.
17 Sikudzafunika kuti Inu mumenyane nawo pa nkhondo imeneyi. Inu mukhale pa malo anu; imani molimba ndipo onani chipulumutso chimene Yehova adzakupatsani, Inu Yuda ndi Yerusalemu. Musaope, musataye mtima. Pitani kuti mukakumane nawo mawa, ndipo Yehova adzakhala nanu.’”
Tsy inahareo ty hialy amy hotakotakey, mijadoña eo, mijohaña an-kanintsiñe vaho isaho ty fandrombaha’ Iehovà, ry Iehodà naho Ierosala­ime, ko mirevendreveñe, ko mange­traketrake, miavota hiatreke iareo hamaray; fa hañimba anahareo t’Iehovà.
18 Yehosafati anaweramitsa nkhope yake ndi kugunda pansi, ndiponso anthu onse a Yuda ndi Yerusalemu anagwa pansi ndi kulambira Yehova.
Aa le nidròdreke, laharañe mb’ an-tane t’Iehosafate; le niba­bok’ añatrefa’ Iehovà iaby t’Ie­hoda naho o mpimone’ Ierosala­imeo, nitalaho am’ Iehovà.
19 Kenaka Alevi ena ochokera ku mabanja a Kohati ndi Kora anayimirira ndipo anatamanda Yehova Mulungu wa Israeli ndi mawu ofuwula kwambiri.
Nitroatse amy zao o nte-Levio, o anan-te-Kehàteo naho o anan-te-Koraheo handrenge Iehovà Andrianañahare’ Israele, am-pipoñafam-peo.
20 Mmamawa, ananyamuka kupita ku chipululu cha Tekowa. Akunyamuka, Yehosafati anayimirira ndipo anati, “Tandimverani ine anthu a Yuda ndi Yerusalemu! Khalani ndi chikhulupiriro mwa Yehova Mulungu wanu ndipo mudzatchinjirizidwa, khalani ndi chikhulupiriro mwa aneneri ake ndipo mudzapambana.”
Aa le nañaleñaleñe amy loak’ androy iereo, nionjomb’ an-diolio’ i Tekoà mb’eo; ie nañavelo iereo le nijohañe eo t’Iehosafate, nanao ty hoe; Janjiño iraho, ry Iehoda naho ry mpimone’ Ierosa­laimeo; iatò t’Iehovà Andrianañahare’ areo le hijadoñe; iantofo o mpitoki’eo le hahatafetetse.
21 Atafunsira kwa anthu, Yehosafati anasankha anthu oti ayimbire Yehova ndi kumutamanda chifukwa cha ulemerero wa chiyero chake pamene amapita ali patsogolo pa gulu la ankhondo, akunena kuti: “Yamikani Yehova pakuti chikondi chake ndi chosatha.”
Ie fa nisafiry am’ondatio le tinendre’e o hisabo amy Iehovào naho o handrenge am-pihaminañe miavakeo, hiaolo o lahindefoñeo, ami’ty hoe: Andriaño t’Iehovà, fa nainai’e ty fiferenaiña’e.
22 Atangoyamba kuyimba ndi kutamanda, Yehova anapereka mʼmanja mwawo anthu a ku Amoni ndi a ku Mowabu ndiponso a ku Phiri la Seiri amene amalimbana ndi Yuda, ndipo anagonjetsedwa.
Aa ie namototse nisabo naho nandrenge iereo, le nampipoha’ Iehovà mpamandroñe hanampoke o ana’ i Amone naho i Moabe naho o tam-bohi-Seire ho naname Iehodao, le zinevo iereo.
23 Anthu a ku Amoni ndi a ku Mowabu anawukira anthu ochokera ku Phiri la Seiri, ndipo anawawononga ndi kuwatheratu. Atatsiriza kuwapha anthu ochokera ku Seiri anamenyana wina ndi mnzake mpaka kuwonongana.
Amy te nitroatse amo mpimoneñe am-bohi-Seireio o ana’ i Amone naho Moabeo, nanjamañe naho nandrotsa­ke; aa ie fonga finongo’ iereo o mpimone’ i Seireo le songa nifanjamañe ka.
24 Anthu a ku Yuda atafika pa malo oyangʼanana ndi chipululu ndi kuona kumene kunali gulu lalikulu lankhondo, iwo anangoona mitembo yokhayokha itagona pansi ndipo palibe amene anathawa.
Aa ie niheo mb’amy fitilik’ abom-patrambeiy mb’eo t’Iehodà, le niisa’ iereo i valobohòkey; hehe te lolo avao ty nifitak’ an-tane eo, leo raike tsy nibotitsike.
25 Choncho Yehosafati ndi anthu ake anapita kukafunkha, ndipo pakati pawo anapeza katundu wambiri ndi zovala ndiponso zinthu zina zamtengowapatali kuposa zomwe akanatha kunyamula. Kunali katundu wambiri kotero kuti zinawatengera masiku atatu kuti amutenge.
Ie nivotrake eo t’Iehosafate naho ondati’eo hikopake, le tendreke te tsifotofoto ty vara naho ty lolo niravake vato soa vaho nangozie’ iereo, bey ta ty lefe-jinieñe; telo andro t’ie nangalake i kopakey ami’ty hamaro’e.
26 Tsiku lachinayi anasonkhana ku chigwa cha Beraka kumene anatamanda Yehova. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa chigwa cha Beraka mpaka lero.
Ie amy andro fahefatsey le nifanontoñe am-bavatane’ i Berakà ao nañandriañe Iehovà; aa le nitokaveñe ty hoe Vavatanem-Berakà ty añara’ i toetsey pak’ androany.
27 Tsono motsogozedwa ndi Yehosafati, anthu onse a Yuda ndi Yerusalemu anabwerera ku Yerusalemu mokondwera pakuti Yehova anawagonjetsera adani awo.
Songa nimpoly amy zao ze ondati’ Iehodà naho Ierosalaime, Iehosafate ty niaolo, nibalike mb’e Ierosalaime am-pirebehañe; ie nampirebehe’ Iehovà ty amo rafelahio.
28 Iwo analowa mu Yerusalemu ndipo anapita ku Nyumba ya Mulungu akuyimba azeze, apangwe ndi malipenga.
Aa le pok’ e Ierosalaime ao iereo reketse fikontsañañe naho marovany naho trompetra nimb’ añ’ anjomba’ Iehovà mb’eo.
29 Kuopsa kwa Mulungu kunali pa maufumu onse a mayiko amene anamva mmene Yehova anamenyera adani a Aisraeli.
Le nifetsak’ amo fifehea’ i taney iabio ty firevendreveñañe aman’Añahare, ie jinanjiñe te Iehovà ty nialy amo rafelahi’ Israeleo.
30 Ndipo ufumu wa Yehosafati unali pa mtendere pakuti Mulungu wake anamupatsa mpumulo ku mbali zonse.
Toe nianjiñe ty fifehea’ Iehosafate; amy te nampitofàn’ Añahare’e o añariary azeo.
31 Choncho Yehosafati analamulira Yuda. Iye anali wa zaka 35 pamene anakhala mfumu ya Yuda ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 25. Dzina la amayi ake linali Azuba mwana wa Sili.
Aa le nifehe Iehoda t’Iehosafate; niorotse nifehe amy tao’e faha telopolo-lime ambiy, le nifeleke e Ierosalaime ao roapolo taoñe lime amby, i Azobà ana’ i Silhý ty tahinan-drene’e.
32 Iye ankayenda mʼnjira za Asa abambo ake ndipo sanapatuke pa zimenezi pakuti anachita zolungama pamaso pa Yehova.
Nañavelo an-tsata’ i Asa, rae’e re, tsy nivike ama’e fa nanao ze fahiti’e am-pihaino’ Iehovà.
33 Komabe malo opembedzerapo mafano sanachotsedwe ndipo anthu sanaperekebe mitima yawo kwa Mulungu wa makolo awo.
Fe mboe tsy nafahañe añe o toets’ aboo; amy te tsy najado’ ondatio aman’ Añaharen-droae’ iareo o arofo’ iareoo.
34 Zochitika zina zokhudza ufumu wa Yehosafati, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la Yehu mwana wa Hanani, zomwe zikupezeka mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
Aa ty amo fitoloña’ Iehosafate ila’eo, ty valoha’e pak’ ampara’e, oniño t’ie misokitse amo enta’ Ieho ana’ i Kananý najoñe amy bokem-panjaka’ Israeleio.
35 Zitapita izi, Yehosafati mfumu ya Yuda inachita mgwirizano ndi Ahaziya mfumu ya Israeli, amene anachita zoyipa kwambiri.
Ie añe, nipiteke amy Ahkazià, mpanjaka’ Israele lo tsere­key, t’Iehosafate mpanjaka’ Iehoda;
36 Iye anagwirizana ndi Ahaziya kuti apange sitima zapamadzi zochitira malonda. Atazipanga zimenezi ku Ezioni-Geberi,
nirekets’ ama’e hamboatse sambo hionjoñe mb’e Tarsise mb’eo; le namboare’ iareo e Etsione-gebere ao i sambo rey.
37 Eliezara mwana wa Dodavahu wa ku Maresa ananenera motsutsana ndi Yehosafati ndipo anati, “Chifukwa chakuti wachita mgwirizano ndi Ahaziya, Yehova adzawononga zimene mwapangazo!” Sitima za pamadzizo zinawonongeka ndipo sizinapite nʼkomwe kumene zimakachita malonda.
Aa le nitoky amy Iehosafate t’i Eliezere, ana’ i Doda nte Maresà nanao ty hoe: Kanao nirekets’ amy Ahkazià irehe le fa nipozahe’ Iehovà o fitoloña’oo. Aa le nifoy iaby i sambo rey, tsy nahafionjoñe mb’e Tarsise.

< 2 Mbiri 20 >