< 2 Mbiri 20 >

1 Zitatha izi, Amowabu ndi Aamoni pamodzi ndi Ameuni ena anabwera kudzachita nkhondo ndi Yehosafati.
After this the children of Moab, and the children of Ammon, and with them of the Ammonites, were gathered together to fight against Josaphat.
2 Anthu ena anabwera kudzamuwuza Yehosafati kuti, “Gulu lalikulu kwambiri lankhondo likubwera kudzachita nanu nkhondo lochokera ku Edomu, ku mbali ina ya Nyanja. Gululi lafika kale ku Hazazoni Tamara” (ndiye kuti Eni-Gedi).
And there came messengers, and told Josaphat, saying: There cometh a great multitude against thee from beyond the sea, and out of Syria, and behold they are in Asasonthamar, which is Engaddi.
3 Ndi mantha, Yehosafati anaganiza zofunsira kwa Yehova, ndipo analengeza kuti Ayuda onse asale zakudya.
And Josaphat being seized with fear betook himself wholly to pray to the Lord, and he proclaimed a fast for all Juda.
4 Anthu a ku Yuda anabwera pamodzi kudzafuna thandizo kwa Yehova, ndipo anabweradi kuchokera ku mzinda uliwonse wa mu Yuda kudzafunafuna Yehova.
And Juda gathered themselves together to pray to the Lord: and all came out of their cities to make supplication to him.
5 Yehosafati anayimirira pakati pa msonkhano wa Yuda ndi Yerusalemu, pa Nyumba ya Yehova patsogolo pa bwalo latsopano
And Josaphat stood in the midst of the assembly of Juda, and Jerusalem, in the house of the Lord before the new court,
6 ndipo anati: “Inu Yehova, Mulungu wa makolo athu, kodi Inu sindinu Mulungu amene muli kumwamba? Inu mumalamulira maufumu onse a mitundu ya anthu. Mphamvu ndi nyonga zili mʼmanja mwanu, ndipo palibe amene angalimbane nanu.
And said: O Lord God of our fathers, thou art God in heaven, and rulest over all the kingdoms and nations, in thy hand is strength and power, and no one can resist thee.
7 Inu Mulungu wathu, kodi simunathamangitse nzika za dziko lino pamaso pa anthu anu Aisraeli ndipo munalipereka kwa zidzukulu za Abrahamu bwenzi lanu kwamuyaya?
Didst not thou our God kill all the inhabitants of this land before thy people Israel, and gavest it to the seed of Abraham thy friend for ever?
8 Iwo akhala mʼdzikolo ndipo anamangira Dzina lanu malo opatulika, nʼkumati,
And they dwelt in it, and built in it a sanctuary to thy name, saying:
9 ‘Ngati tsoka litigwera kaya ndi lupanga lachiweruzo, kapena mliri, kapenanso njala, ife tidzayima pamaso panu patsogolo pa Nyumba ya Mulungu ino imene imatchedwa ndi Dzina lanu ndipo tidzalirira kwa inu mʼmasautso athu, ndipo Inu mudzatimvera ndi kutipulumutsa.’
If evils fall upon us, the sword of judgment, or pestilence, or famine, we will stand in thy presence before this house, in which thy name is called upon: and we will cry to thee in our afflictions, and thou wilt hear, and save us.
10 “Koma tsopano pano pali anthu ochokera ku Amoni, Mowabu ndi Phiri la Seiri amene dziko lawo Inu simunawalole Aisraeli kuti alithire nkhondo pamene amabwera kuchokera ku Igupto. Kotero anatembenuka ndi kuwaleka ndipo sanawawononge.
Now therefore behold the children of Ammon, and of Moab, and mount Seir, through whose lands thou didst not allow Israel to pass, when they came out of Egypt, but they turned aside from them, and slew them not,
11 Taonani, mmene akutibwezera ife pobwera kudzatithamangitsa mʼdziko limene inu munatipatsa ngati cholowa chathu.
Do the contrary, and endeavour to cast us out of the possession which thou hast delivered to us.
12 Inu Mulungu wathu, kodi simuwaweruza? Pakuti ife tilibe mphamvu zolimbana ndi gulu lalikulu lankhondo limene likutithira nkhondoli. Ife sitikudziwa choti tichite, koma maso athu ali pa Inu.”
O our God, wilt thou not then judge them? as for us we have not strength enough, to be able to resist this multitude, which cometh violently upon us. But as we know not what to do, we can only turn our eyes to thee.
13 Anthu onse a Yuda, pamodzi ndi akazi awo ndi ana ndi makanda, anayima chilili pamaso pa Yehova.
And all Juda stood before the Lord with their little ones, and their wives, and their children.
14 Ndipo Mzimu wa Yehova unabwera pa Yahazieli mwana wa Zekariya, mwana wa Benaya, mwana wa Yeiyeli, mwana wa Mataniya Mlevi, chidzukulu cha Asafu, atayimirira mu msonkhano.
And Jahaziel the son of Zacharias, the son of Banaias, the son of Jehiel, the son of Mathanias, a Levite of the sons of Asaph, was there, upon whom the spirit of the Lord came in the midst of the multitude,
15 Iye anati, “Tamverani mfumu Yehosafati ndi onse amene amakhala mu Yuda ndi Yerusalemu! Zimene Yehova akunena kwa inu ndi izi: ‘Musaope kapena kutaya mtima chifukwa cha gulu lalikulu lankhondo ili. Pakuti nkhondoyi si yanu, koma ya Mulungu.
And he said: Attend ye, all Juda, and you that dwell in Jerusalem, and thou king Josaphat: Thus saith the Lord to you: Fear ye not, and be not dismayed at this multitude: for the battle is not yours, but God’s.
16 Mawa mupite mukamenyane nawo. Adzakhala akubwera mokweza kudzera Njira ya Zizi, ndipo mukawapeza kumapeto kwa chigwa cha ku chipululu cha Yeruweli.
Tomorrow you shall go down against them: for they will come up by the ascent named Sis, and you shall find them at the head of the torrent, which is over against the wilderness of Jeruel.
17 Sikudzafunika kuti Inu mumenyane nawo pa nkhondo imeneyi. Inu mukhale pa malo anu; imani molimba ndipo onani chipulumutso chimene Yehova adzakupatsani, Inu Yuda ndi Yerusalemu. Musaope, musataye mtima. Pitani kuti mukakumane nawo mawa, ndipo Yehova adzakhala nanu.’”
It shall not be you that shall fight, but only stand with confidence, and you shall see the help of the Lord over you, O Juda, and Jerusalem: fear ye not, nor be you dismayed: tomorrow you shall go out against them, and the Lord will be with you.
18 Yehosafati anaweramitsa nkhope yake ndi kugunda pansi, ndiponso anthu onse a Yuda ndi Yerusalemu anagwa pansi ndi kulambira Yehova.
Then Josaphat, and Juda, and all the inhabitants of Jerusalem fell hat on the ground before the Lord, and adored him.
19 Kenaka Alevi ena ochokera ku mabanja a Kohati ndi Kora anayimirira ndipo anatamanda Yehova Mulungu wa Israeli ndi mawu ofuwula kwambiri.
And the Levites of the sons of Caath, and of the sons of Core praised the Lord the God of Israel with a loud voice, on high.
20 Mmamawa, ananyamuka kupita ku chipululu cha Tekowa. Akunyamuka, Yehosafati anayimirira ndipo anati, “Tandimverani ine anthu a Yuda ndi Yerusalemu! Khalani ndi chikhulupiriro mwa Yehova Mulungu wanu ndipo mudzatchinjirizidwa, khalani ndi chikhulupiriro mwa aneneri ake ndipo mudzapambana.”
And they rose early in the morning, and went out through the desert of Thecua: and as they were marching, Josaphat standing in the midst of them, said: Hear me, ye men of Juda, and all the inhabitants of Jerusalem: believe in the Lord your God, and you shall be secure: believe his prophets, and all things shall succeed well.
21 Atafunsira kwa anthu, Yehosafati anasankha anthu oti ayimbire Yehova ndi kumutamanda chifukwa cha ulemerero wa chiyero chake pamene amapita ali patsogolo pa gulu la ankhondo, akunena kuti: “Yamikani Yehova pakuti chikondi chake ndi chosatha.”
And he gave counsel to the people, and appointed the singing men of the Lord, to praise him by their companies, and to go before the army, and with one voice to say: Give glory to the Lord, for his mercy endureth for ever.
22 Atangoyamba kuyimba ndi kutamanda, Yehova anapereka mʼmanja mwawo anthu a ku Amoni ndi a ku Mowabu ndiponso a ku Phiri la Seiri amene amalimbana ndi Yuda, ndipo anagonjetsedwa.
And when they began to sing praises, the Lord turned their ambushments upon themselves, that is to say, of the children of Ammon, and of Moab, and of mount Seir, who were come out to fight against Juda, and they were slain.
23 Anthu a ku Amoni ndi a ku Mowabu anawukira anthu ochokera ku Phiri la Seiri, ndipo anawawononga ndi kuwatheratu. Atatsiriza kuwapha anthu ochokera ku Seiri anamenyana wina ndi mnzake mpaka kuwonongana.
For the children of Ammon, and of Moab, rose up against the inhabitants of mount Seir, to kill and destroy them: and when they had made an end of them, they turned also against one another, and destroyed one another.
24 Anthu a ku Yuda atafika pa malo oyangʼanana ndi chipululu ndi kuona kumene kunali gulu lalikulu lankhondo, iwo anangoona mitembo yokhayokha itagona pansi ndipo palibe amene anathawa.
And when Juda came to the watch tower, that looketh toward the desert, they saw afar off all the country, for a great space, full of dead bodies, and that no one was left that could escape death.
25 Choncho Yehosafati ndi anthu ake anapita kukafunkha, ndipo pakati pawo anapeza katundu wambiri ndi zovala ndiponso zinthu zina zamtengowapatali kuposa zomwe akanatha kunyamula. Kunali katundu wambiri kotero kuti zinawatengera masiku atatu kuti amutenge.
Then Josaphat came, and all the people with him to take away the spoils of the dead, and they found among the dead bodies, stuff of various kinds, and garments, and most precious vessels: and they took them for themselves, insomuch that they could not carry all, nor in three days take away the spoils, the booty was so great.
26 Tsiku lachinayi anasonkhana ku chigwa cha Beraka kumene anatamanda Yehova. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa chigwa cha Beraka mpaka lero.
And on the fourth day they were assembled in the valley of Blessing: for there they blessed the Lord, and therefore they called that place the valley of Blessing until this day.
27 Tsono motsogozedwa ndi Yehosafati, anthu onse a Yuda ndi Yerusalemu anabwerera ku Yerusalemu mokondwera pakuti Yehova anawagonjetsera adani awo.
And every man of Juda, and the inhabitants of Jerusalem returned, and Josaphat at their head, into Jerusalem with great joy, because the Lord had made them rejoice over their enemies.
28 Iwo analowa mu Yerusalemu ndipo anapita ku Nyumba ya Mulungu akuyimba azeze, apangwe ndi malipenga.
And they came into Jerusalem with psalteries, and harps, and trumpets into the house of the Lord.
29 Kuopsa kwa Mulungu kunali pa maufumu onse a mayiko amene anamva mmene Yehova anamenyera adani a Aisraeli.
And the fear of the Lord fell upon all the kingdoms of the lands when they heard that the Lord had fought against the enemies of Israel.
30 Ndipo ufumu wa Yehosafati unali pa mtendere pakuti Mulungu wake anamupatsa mpumulo ku mbali zonse.
And the kingdom of Josaphat was quiet, and God gave him peace round about.
31 Choncho Yehosafati analamulira Yuda. Iye anali wa zaka 35 pamene anakhala mfumu ya Yuda ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 25. Dzina la amayi ake linali Azuba mwana wa Sili.
And Josaphat reigned over Juda, and he was five and thirty years old when he began to reign: and he reigned five and twenty years in Jerusalem: and the name of his mother was Azuba the daughter of Selahi.
32 Iye ankayenda mʼnjira za Asa abambo ake ndipo sanapatuke pa zimenezi pakuti anachita zolungama pamaso pa Yehova.
And he walked in the way of his father Asa, and departed not from it, doing the things that were pleasing before the Lord.
33 Komabe malo opembedzerapo mafano sanachotsedwe ndipo anthu sanaperekebe mitima yawo kwa Mulungu wa makolo awo.
But yet he took not away the high places, and the people had not yet turned their heart to the Lord the God of their fathers.
34 Zochitika zina zokhudza ufumu wa Yehosafati, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la Yehu mwana wa Hanani, zomwe zikupezeka mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
But the rest of the acts of Josaphat, first and last, are written in the words of Jehu the son of Hanani, which he digested into the books of the kings of Israel.
35 Zitapita izi, Yehosafati mfumu ya Yuda inachita mgwirizano ndi Ahaziya mfumu ya Israeli, amene anachita zoyipa kwambiri.
After these things Josaphat king of Juda made friendship with Ochozias king of Israel, whose works were very wicked.
36 Iye anagwirizana ndi Ahaziya kuti apange sitima zapamadzi zochitira malonda. Atazipanga zimenezi ku Ezioni-Geberi,
And he was partner with him in making ships, to go to Tharsis: and they made the ships in Asiongaber.
37 Eliezara mwana wa Dodavahu wa ku Maresa ananenera motsutsana ndi Yehosafati ndipo anati, “Chifukwa chakuti wachita mgwirizano ndi Ahaziya, Yehova adzawononga zimene mwapangazo!” Sitima za pamadzizo zinawonongeka ndipo sizinapite nʼkomwe kumene zimakachita malonda.
And Eliezer the son of Dodau of Maresa prophesied to Josaphat, saying: Because thou hast made a league with Ochozias, the Lord hath destroyed thy works, and the ships are broken, and they could not go to Tharsis.

< 2 Mbiri 20 >