< 2 Mbiri 20 >
1 Zitatha izi, Amowabu ndi Aamoni pamodzi ndi Ameuni ena anabwera kudzachita nkhondo ndi Yehosafati.
After these things, the sons of Moab, and the sons of Ammon, and with them some from the Ammonites, gathered together so that they might fight against him.
2 Anthu ena anabwera kudzamuwuza Yehosafati kuti, “Gulu lalikulu kwambiri lankhondo likubwera kudzachita nanu nkhondo lochokera ku Edomu, ku mbali ina ya Nyanja. Gululi lafika kale ku Hazazoni Tamara” (ndiye kuti Eni-Gedi).
And messengers arrived and reported to Jehoshaphat, saying: “A great multitude has arrived against you, from those places that are across the sea, and from Syria. And behold, they are standing together at Hazazon-tamar, which is Engedi.”
3 Ndi mantha, Yehosafati anaganiza zofunsira kwa Yehova, ndipo analengeza kuti Ayuda onse asale zakudya.
Then Jehoshaphat, being terrified with fear, gave himself entirely to petitioning the Lord, and he proclaimed a fast for all of Judah.
4 Anthu a ku Yuda anabwera pamodzi kudzafuna thandizo kwa Yehova, ndipo anabweradi kuchokera ku mzinda uliwonse wa mu Yuda kudzafunafuna Yehova.
And Judah gathered together to pray to the Lord. Moreover, everyone from their cities came to beseech him.
5 Yehosafati anayimirira pakati pa msonkhano wa Yuda ndi Yerusalemu, pa Nyumba ya Yehova patsogolo pa bwalo latsopano
And when Jehoshaphat had stood up in the midst of the assembly of Judah and Jerusalem, in the house of the Lord, before the new atrium,
6 ndipo anati: “Inu Yehova, Mulungu wa makolo athu, kodi Inu sindinu Mulungu amene muli kumwamba? Inu mumalamulira maufumu onse a mitundu ya anthu. Mphamvu ndi nyonga zili mʼmanja mwanu, ndipo palibe amene angalimbane nanu.
he said: “O Lord, God of our fathers, you are God in heaven, and you rule over all the kingdoms of the Gentiles. In your hand is strength and power, and no one is able to withstand you.
7 Inu Mulungu wathu, kodi simunathamangitse nzika za dziko lino pamaso pa anthu anu Aisraeli ndipo munalipereka kwa zidzukulu za Abrahamu bwenzi lanu kwamuyaya?
Did not you, our God, put to death all the inhabitants of this land before your people Israel? And you gave it to the offspring of your friend Abraham, for all time.
8 Iwo akhala mʼdzikolo ndipo anamangira Dzina lanu malo opatulika, nʼkumati,
And they lived in it. And they built a Sanctuary to your name in it, saying:
9 ‘Ngati tsoka litigwera kaya ndi lupanga lachiweruzo, kapena mliri, kapenanso njala, ife tidzayima pamaso panu patsogolo pa Nyumba ya Mulungu ino imene imatchedwa ndi Dzina lanu ndipo tidzalirira kwa inu mʼmasautso athu, ndipo Inu mudzatimvera ndi kutipulumutsa.’
‘If evils will have fallen upon us, the sword of judgment, or pestilence, or famine, we will stand in your sight before this house, in which your name is invoked, and we will cry out to you in our tribulations. And you will heed us and accomplish our salvation.’
10 “Koma tsopano pano pali anthu ochokera ku Amoni, Mowabu ndi Phiri la Seiri amene dziko lawo Inu simunawalole Aisraeli kuti alithire nkhondo pamene amabwera kuchokera ku Igupto. Kotero anatembenuka ndi kuwaleka ndipo sanawawononge.
Now therefore, behold the sons of Ammon, and of Moab, and mount Seir, through whose lands you did not permit Israel to cross when they were departing from Egypt. Instead, they turned aside from them, and they did not put them to death.
11 Taonani, mmene akutibwezera ife pobwera kudzatithamangitsa mʼdziko limene inu munatipatsa ngati cholowa chathu.
They are doing the contrary, and they are striving to cast us from the possession which you delivered to us.
12 Inu Mulungu wathu, kodi simuwaweruza? Pakuti ife tilibe mphamvu zolimbana ndi gulu lalikulu lankhondo limene likutithira nkhondoli. Ife sitikudziwa choti tichite, koma maso athu ali pa Inu.”
Therefore, will you, our God, not judge them? Certainly, in us there is not enough strength so that we would be able to withstand this multitude, which rushes against us. But although we do not know what we ought to do, we have this alone remaining, that we direct our eyes to you.”
13 Anthu onse a Yuda, pamodzi ndi akazi awo ndi ana ndi makanda, anayima chilili pamaso pa Yehova.
Truly, all of Judah was standing before the Lord with their little ones and wives and children.
14 Ndipo Mzimu wa Yehova unabwera pa Yahazieli mwana wa Zekariya, mwana wa Benaya, mwana wa Yeiyeli, mwana wa Mataniya Mlevi, chidzukulu cha Asafu, atayimirira mu msonkhano.
But there was Jahaziel, the son of Zechariah, the son of Benaiah, the son of Jeiel, the son of Mattaniah, a Levite from the sons of Asaph, upon whom the Spirit of the Lord went, in the midst of the crowd.
15 Iye anati, “Tamverani mfumu Yehosafati ndi onse amene amakhala mu Yuda ndi Yerusalemu! Zimene Yehova akunena kwa inu ndi izi: ‘Musaope kapena kutaya mtima chifukwa cha gulu lalikulu lankhondo ili. Pakuti nkhondoyi si yanu, koma ya Mulungu.
And he said: “Pay attention, all of Judah, and you who live in Jerusalem, and you, king Jehoshaphat. Thus says the Lord to you: Do not be afraid. Neither should you be dismayed by this multitude. For the fight is not yours, but God’s.
16 Mawa mupite mukamenyane nawo. Adzakhala akubwera mokweza kudzera Njira ya Zizi, ndipo mukawapeza kumapeto kwa chigwa cha ku chipululu cha Yeruweli.
Tomorrow, you shall descend against them. For they will ascend along the incline named Ziz, and will find them at the summit of the torrent, which is opposite the wilderness of Jeruel.
17 Sikudzafunika kuti Inu mumenyane nawo pa nkhondo imeneyi. Inu mukhale pa malo anu; imani molimba ndipo onani chipulumutso chimene Yehova adzakupatsani, Inu Yuda ndi Yerusalemu. Musaope, musataye mtima. Pitani kuti mukakumane nawo mawa, ndipo Yehova adzakhala nanu.’”
It will not be you who will fight. Instead, only stand with confidence, and you will see the help of the Lord over you, O Judah and Jerusalem. Do not be afraid. Neither should you be dismayed. Tomorrow you shall go forth against them, and the Lord will be with you.”
18 Yehosafati anaweramitsa nkhope yake ndi kugunda pansi, ndiponso anthu onse a Yuda ndi Yerusalemu anagwa pansi ndi kulambira Yehova.
Then Jehoshaphat, and Judah, and all the inhabitants of Jerusalem fell prone on the ground before the Lord, and they adored him.
19 Kenaka Alevi ena ochokera ku mabanja a Kohati ndi Kora anayimirira ndipo anatamanda Yehova Mulungu wa Israeli ndi mawu ofuwula kwambiri.
And the Levites from the sons of Kohath, and from the sons of Korah, were praising the Lord, the God of Israel, with a great voice, on high.
20 Mmamawa, ananyamuka kupita ku chipululu cha Tekowa. Akunyamuka, Yehosafati anayimirira ndipo anati, “Tandimverani ine anthu a Yuda ndi Yerusalemu! Khalani ndi chikhulupiriro mwa Yehova Mulungu wanu ndipo mudzatchinjirizidwa, khalani ndi chikhulupiriro mwa aneneri ake ndipo mudzapambana.”
And when they had risen up in the morning, they went out through the desert of Tekoa. And as they were setting out, Jehoshaphat, standing in their midst, said: “Listen to me, men of Judah and all inhabitants of Jerusalem. Believe in the Lord your God, and you will be secure. Believe in his prophets, and everything will come to prosperity.”
21 Atafunsira kwa anthu, Yehosafati anasankha anthu oti ayimbire Yehova ndi kumutamanda chifukwa cha ulemerero wa chiyero chake pamene amapita ali patsogolo pa gulu la ankhondo, akunena kuti: “Yamikani Yehova pakuti chikondi chake ndi chosatha.”
And he gave counsel to the people. And he appointed the singing men of the Lord, so that they would praise him by their companies, and so that they would go before the army, and with one voice say: “Confess to the Lord. For his mercy is eternal.”
22 Atangoyamba kuyimba ndi kutamanda, Yehova anapereka mʼmanja mwawo anthu a ku Amoni ndi a ku Mowabu ndiponso a ku Phiri la Seiri amene amalimbana ndi Yuda, ndipo anagonjetsedwa.
And when they had begun to sing praises, the Lord turned their ambushes upon themselves, that is, those of the sons of Ammon, and of Moab, and of mount Seir, who had gone forth so that they might fight against Judah. And they were struck down.
23 Anthu a ku Amoni ndi a ku Mowabu anawukira anthu ochokera ku Phiri la Seiri, ndipo anawawononga ndi kuwatheratu. Atatsiriza kuwapha anthu ochokera ku Seiri anamenyana wina ndi mnzake mpaka kuwonongana.
For the sons of Ammon and of Moab rose up against the inhabitants of mount Seir, so that they might slay and destroy them. And when they had perpetrated this work, now also turning upon themselves, they cut one another with wounds.
24 Anthu a ku Yuda atafika pa malo oyangʼanana ndi chipululu ndi kuona kumene kunali gulu lalikulu lankhondo, iwo anangoona mitembo yokhayokha itagona pansi ndipo palibe amene anathawa.
Then, when Judah had gone to the high point that looks out toward the desert, they saw, from far away, the entire wide region filled with dead bodies. Neither was there anyone who was left alive and had been able to escape death.
25 Choncho Yehosafati ndi anthu ake anapita kukafunkha, ndipo pakati pawo anapeza katundu wambiri ndi zovala ndiponso zinthu zina zamtengowapatali kuposa zomwe akanatha kunyamula. Kunali katundu wambiri kotero kuti zinawatengera masiku atatu kuti amutenge.
Therefore, Jehoshaphat went, and all the people with him, in order to take away the spoils of the dead. And they found, among the dead bodies, diverse equipment, and also garments, and very precious vessels. And they despoiled these, to such an extent that they were unable to carry everything. Neither could they, over three days, take away the spoils because of the magnitude of the plunder.
26 Tsiku lachinayi anasonkhana ku chigwa cha Beraka kumene anatamanda Yehova. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa chigwa cha Beraka mpaka lero.
Then, on the fourth day, they were gathered together in the Valley of Blessing. For they had blessed the Lord there, and therefore they called that place the Valley of Blessing, even to the present day.
27 Tsono motsogozedwa ndi Yehosafati, anthu onse a Yuda ndi Yerusalemu anabwerera ku Yerusalemu mokondwera pakuti Yehova anawagonjetsera adani awo.
And every man of Judah, and the inhabitants of Jerusalem, returned, with Jehoshaphat before them, to Jerusalem, with great rejoicing. For the Lord had granted to them gladness concerning their enemies.
28 Iwo analowa mu Yerusalemu ndipo anapita ku Nyumba ya Mulungu akuyimba azeze, apangwe ndi malipenga.
And they entered into Jerusalem with psalteries, and harps, and trumpets, into the house of the Lord.
29 Kuopsa kwa Mulungu kunali pa maufumu onse a mayiko amene anamva mmene Yehova anamenyera adani a Aisraeli.
Then the fear of the Lord fell upon all the kingdoms of the lands, when they had heard that the Lord had fought against the enemies of Israel.
30 Ndipo ufumu wa Yehosafati unali pa mtendere pakuti Mulungu wake anamupatsa mpumulo ku mbali zonse.
And the kingdom of Jehoshaphat was quiet. And God granted to him peace on all sides.
31 Choncho Yehosafati analamulira Yuda. Iye anali wa zaka 35 pamene anakhala mfumu ya Yuda ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 25. Dzina la amayi ake linali Azuba mwana wa Sili.
And so Jehoshaphat reigned over Judah. And he was thirty-five years old when he had begun to reign. Then he reigned for twenty-five years in Jerusalem. And the name of his mother was Azubah, the daughter of Shilhi.
32 Iye ankayenda mʼnjira za Asa abambo ake ndipo sanapatuke pa zimenezi pakuti anachita zolungama pamaso pa Yehova.
And he walked in the way of his father, Asa, and he did not decline from it, doing the things that were pleasing before the Lord.
33 Komabe malo opembedzerapo mafano sanachotsedwe ndipo anthu sanaperekebe mitima yawo kwa Mulungu wa makolo awo.
Yet truly, he did not take away the high places, and the people still had not directed their heart to the Lord, the God of their fathers.
34 Zochitika zina zokhudza ufumu wa Yehosafati, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la Yehu mwana wa Hanani, zomwe zikupezeka mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
But the rest of the acts of Jehoshaphat, the first and the last, have been written in the words of Jehu, the son of Hanani, which he digested into the books of the kings of Israel.
35 Zitapita izi, Yehosafati mfumu ya Yuda inachita mgwirizano ndi Ahaziya mfumu ya Israeli, amene anachita zoyipa kwambiri.
After these things, Jehoshaphat, the king of Judah, formed a friendship with Ahaziah, the king of Israel, whose works were very impious.
36 Iye anagwirizana ndi Ahaziya kuti apange sitima zapamadzi zochitira malonda. Atazipanga zimenezi ku Ezioni-Geberi,
And he was a partner in the making of ships, which would go to Tarshish. And they made the fleet at Eziongeber.
37 Eliezara mwana wa Dodavahu wa ku Maresa ananenera motsutsana ndi Yehosafati ndipo anati, “Chifukwa chakuti wachita mgwirizano ndi Ahaziya, Yehova adzawononga zimene mwapangazo!” Sitima za pamadzizo zinawonongeka ndipo sizinapite nʼkomwe kumene zimakachita malonda.
Then Eliezer, the son of Dodavahu, from Mareshah, prophesied to Jehoshaphat, saying: “Because you have made a pact with Ahaziah, the Lord has struck your works, and the ships have been broken, and they have not been able to go to Tarshish.”